< Numeri 32 >
1 Arubeni ndi Agadi amene anali ndi ngʼombe zambiri ndi ziweto zina anaona dziko la Yazeri ndi la Giliyadi kuti linali labwino kwa ziwetozo.
Rubeniterne og Gaditerne havde meget Kvæg i store mængder. Da de nu saa Ja'zers Land og Gileads Land, fandt de, at Stedet egnede sig til Kvægavl.
2 Choncho Arubeni ndi Agadi anapita kwa Mose ndi kwa wansembe Eliezara ndi kwa atsogoleri a anthu ndi kunena kuti,
Derfor kom Gaditerne og Rubeniterne og sagde til Moses og Præsten Eleazar og Menighedens Øverste:
3 “Ataroti, Diboni, Yazeri, Nimira, Hesiboni, Eleali, Sebamu, Nebo ndi Beoni,
»Atarot, Dibon, Ja'zer, Nimra, Hesjbon, El'ale, Sebam, Nebo og Beon,
4 dziko lomwe Yehova anagonjetsa pamaso pa Aisraeli, ndiwo malo woyenera ziweto, ndipo atumiki anufe tili ndi ziweto.
det Land, HERREN har erobret for Israels Menighed, er et Land, der egner sig til Kvægavl, og dine Trælle ejer Hjorde.«
5 Iwo anati, ‘Ngati tapeza ufulu pamaso panu atumiki anufe, mutipatse dziko limeneli kuti likhale lathu. Tisawoloke nanu Yorodani.’”
Og de sagde: »Dersom vi har fundet Naade for dine Øjne, saa lad dine Trælle faa dette Land i Eje; før os ikke over Jordan!«
6 Ndipo Mose anati kwa Agadi ndi Arubeni, “Kodi anthu a mtundu wanu apite ku nkhondo inu mutangokhala kuno?
Men Moses sagde til Gaditerne og Rubeniterne: »Skal eders Brødre drage i Krig, medens I bliver boende her?
7 Chifukwa chiyani mukufowoketsa Aisraeli kupita mʼdziko limene Yehova wawapatsa?
Og hvorfor vil I betage Israeliterne Modet til at drage over til det Land, HERREN har givet dem?
8 Izi ndi zimene makolo anu anachita pamene ndinawatuma kuchokera ku Kadesi kukaona dzikolo.
Det gjorde eders Fædre, da jeg fra Kadesj-Barnea sendte dem hen for at se paa Landet;
9 Atapita ku chigwa cha Esikolo, ndi kuliona dzikolo, anafowoketsa Aisraeli kuti asalowe mʼdziko limene Yehova anawapatsa.
da de var draget op til Esjkoldalen og havde set paa Landet, det og de Israeliterne Modet til at drage ind i det Land, HERREN havde givet dem.
10 Yehova anakwiya tsiku limenelo ndipo analumbira kuti,
Men HERRENS Vrede blussede den Gang op, og han svor:
11 ‘Chifukwa sananditsatire ndi mtima wonse, palibe ndi mmodzi yemwe mwa amuna a zaka makumi awiri kapena kuposa pamenepo, amene anachokera ku Igupto, amene adzaone dziko limene ndinalonjeza mwa lumbiro kwa Abrahamu, Isake ndi Yakobo.
De Mænd, der er draget op fra Ægypten, fra Tyveaarsalderen og opefter, skal ikke faa det Land at se, jeg tilsvor Abraham, Isak og Jakob, fordi de ikke viste mig fuld Lydighed,
12 Palibe ndi mmodzi yemwe kupatula Kalebe mwana wa Yefune, Mkeni, ndi Yoswa mwana wa Nuni chifukwa anatsatira Yehova ndi mtima wonse.’
med Undtagelse af Kenizziten Kaleb, Jefunnes Søn, og Josua, Nuns Søn, thi de viste HERREN fuld Lydighed!
13 Yehova anakwiyira Aisraeli kwambiri ndipo anawachititsa kuyenda mʼchipululu zaka makumi anayi, mpaka mʼbado wonse wa anthu amene anachita choyipa pamaso pake unatha.
Og HERRENS Vrede blussede op mod Israel, og han lod dem vanke om i Ørkenen i fyrretyve Aar, indtil hele den Slægt var gaaet til Grunde, der gjorde, hvad der var ondt i HERRENS Øjne.
14 “Ndipo onani tsopano, inu mʼbado wochimwa, mwalowa mʼmalo mwa makolo anu ndipo mwachititsa kuti Yehova akwiyire Israeli kwambiri.
Og se, I træder nu i eders Fædres Fodspor, en Yngel af Syndere, for yderligere at øge HERRENS Vrede mod Israel!
15 Ngati muleka kumutsata, Iye adzawasiyiranso anthu onsewa mʼchipululu ndipo mudzawonongetsa anthu onsewa.”
Naar I viger bort fra ham, vil han lade det blive endnu længer i Ørkenen, og I bringer Fordærvelse over hele dette Folk.«
16 Ndipo iwo anabwera kwa Mose namuwuza kuti, “Ife tikufuna kumanga makola a ziweto zathu kuno ndi mizinda yokhalamo akazi athu ndi ana athu.
Da traadte de frem for ham og sagde: »Vi vil kun bygge Kvægfolde til vore Hjorde her og Byer til vore Familier;
17 Koma ndife okonzeka kutenga zida za nkhondo ndi kupita pamodzi ndi Aisraeli mpaka titakawafikitsa ku malo awo. Panopa, akazi ndi ana athu akhala mʼmizinda yotetezedwa, kuwateteza kwa anthu okhala mʼdzikoli.
men selv vil vi ruste os til Kamp og drage i Spidsen for Israeliterne, til vi har bragt dem hen til deres Sted; imens skal vore Familier blive i de befæstede Byer i Ly for Landets Indbyggere.
18 Sitidzabwerera ku midzi yathu mpaka Mwisraeli aliyense atalandira cholowa chake.
Vi vil ikke vende tilbage til vore Huse, før enhver af Israeliterne har faaet sin Arvelod;
19 Sitidzalandira cholowa chilichonse pamodzi nawo ku tsidya lina la Yorodani, chifukwa cholowa chathu tachipezera ku tsidya lino la kummawa kwa Yorodani.”
thi vi vil ikke have Arvelod sammen med dem paa den anden Side af Jordan og længere borte, eftersom vi har faaet vor Arvelod her paa denne Side af Jordan paa Østsiden.«
20 Tsono Mose anati kwa anthuwo, “Ngati inu mudzachita zimenezi, kutenga zida zankhondo pamaso pa Yehova kuti muchite nkhondo,
Da sagde Moses til dem: »Hvis I gør det, hvis I ruster eder til Kamp for HERRENS Aasyn,
21 ndipo ngati nonsenu mudzapita ndi zida kuwoloka Yorodani pamaso pa Yehova mpaka atachotsa adani ake pamaso pake,
hvis alle eders kamprustede Mænd overskrider Jordan for HERRENS Aasyn og bliver der, indtil han har jaget sine Fjender bort fra sit Aasyn,
22 dzikolo nʼkugonja pamaso pa Yehova, mudzabwera ndi kukhala mfulu pamaso pa Yehova ndi Aisraeli. Ndipo dziko lino lidzakhala lanu pamaso pa Yehova.
og hvis I først vender tilbage, naar Landet er undertvunget for HERRENS Aasyn, skal I være sagesløse over for HERREN og Israel, og saa skal Landet her blive eders Ejendom for HERRENS Aasyn.
23 “Koma mukalephera kuchita izi, mudzakhala mukuchimwira Yehova. Ndipo dziwani kuti tchimo lanu lidzakupezani.
Men hvis I ikke gør det, se, da synder I mod HERREN, og da skal I faa eders Synd at mærke, den skal nok finde eder.
24 Amangireni akazi ndi ana anu mizinda, mangani makola a ziweto zanu, koma chitani zomwe mwalonjeza.”
Byg eder Byer til eders Familier og Folde til eders Smaakvæg og gør, som I har sagt!«
25 Agadi ndi Arubeni anati kwa Mose, “Ife antchito anu tidzachita monga mbuye wathu mwalamulira.
Da sagde Gaditerne og Rubeniterne til Moses: »Dine Trælle vil gøre, som min Herre byder;
26 Ana ndi akazi athu, ziweto zathu zina ndi ngʼombe zidzatsala kuno ku mizinda ya Giliyadi,
vore Børn, Kvinder, Hjorde og alt vort Kvæg skal blive der i Gileads Byer,
27 koma antchito anufe, mwamuna aliyense amene ali ndi chida cha nkhondo, adzawoloka kukamenya nkhondo pamaso pa Yehova monga mbuye wathu wanenera.”
men dine Trælle vil drage over og tage Del i Krigen, saa mange som er rustet til Kamp for HERRENS Aasyn, saaledes som min Herre har sagt.«
28 Choncho Mose anapereka malamulo awa kwa wansembe Eliezara, kwa Yoswa mwana wa Nuni ndi kwa akulu a mafuko a Aisraeli.
Saa gav Moses Præsten Eleazar og Josua, Nuns Søn, og Overhovederne for de israelitiske Stammers Fædrenehuse Befaling om dem,
29 Mose anawawuza kuti, ngati Agadi ndi Arubeni, mwamuna aliyense wokonzekera nkhondo, awoloka Yorodani pamodzi ndi inu pamaso pa Yehova, ndipo dzikolo nʼkugonjetsedwa pamaso panu, mudzawapatse dziko la Giliyadi kukhala lawo.
og Moses sagde til dem: »Hvis Gaditerne og Rubeniterne, saa mange som er rustet til Kamp for HERRENS Aasyn, gaar over Jordan sammen med eder og Landet bliver eder underlagt, skal I give dem Gilead i Eje;
30 Koma ngati sawoloka pamodzi nanu ndi zida zankhondo, ayenera kulandira cholowa chawo pamodzi ndi inu ku Kanaani.
men hvis de ikke gaar over sammen med eder, rustede til Kamp, skal de have Bopæl anvist blandt eder i Kana'ans Land.«
31 Agadi ndi Arubeni anayankha kuti, “Antchito anu adzachita zimene Yehova wanena.
Da svarede Gaditerne og Rubeniterne: »Hvad HERREN har talt til dine Trælle, vil vi gøre;
32 Tidzawoloka pamaso pa Yehova ndipo tidzalowa mu Kanaani ndi zida zankhondo, koma cholowa chathu chidzakhala ku tsidya lino la Yorodani.”
vi vil, rustede til Kamp for HERRENS Øjne, drage over til Kana'ans Land, men vor Arvelod paa den anden Side af Jordan bliver i vort Eje.«
33 Choncho Mose anapatsa Agadi, Arubeni ndi theka la fuko la Manase mwana wa Yosefe dziko la Sihoni mfumu ya Aamori ndi dziko la Ogi, mfumu ya ku Basani, dziko lonse, mizinda yake ndi midzi yowazungulira.
Da gav Moses Gaditerne, Rubeniterne og Josefs Søn Manasses halve Stamme Amoriterkongen Sihons Kongerige og Kong Og af Basans Kongerige, Landet med Byerne og deres Omraade, Landets Byer rundt om.
34 Agadi anamanga Diboni, Ataroti, Aroeri,
Saa byggede Gaditerne Dibon, Atarot, Aroer.
35 Atiroti-Sofani, Yazeri, Yogibeha,
Atarot-Sjofan, Ja'zer, Jogbeha,
36 Beti-Nimira ndi Beti-Harani mizinda ya malinga. Anamanganso makola a ziweto zawo.
Bet-Nimra, Bet-Haran, befæstede Byer, og Kvægfolde;
37 Ndipo Arubeni anamanga Hesiboni, Eleali, Kiriataimu,
og Rubeniterne byggede Hesjbon, El'ale og Kirjatajim,
38 Nebo ndi Baala-Meoni (mayina awa anasinthidwa) ndi Sibima. Anapereka mayina ku mizinda ina yomwe anamangayo.
Nebo og Ba'al-Meon, hvis Navne ændredes, og Sibma; og de opkaldte Byerne, som de byggede, efter deres Navne.
39 Zidzukulu za Makiri mwana wa Manase zinapita ku Giliyadi kulanda mzindawo ndi kuthamangitsira kunja Aamori omwe anali kumeneko.
Og Manasses Søn Makirs Sønner drog til Gilead og erobrede det og drev de der boende Amoriter bort;
40 Tsono Mose anapereka Giliyadi kwa Amakiri, ana a Manase, ndipo anakhala kumeneko.
og Moses overdrog Gilead til Manasses Søn Makir, og han bosatte sig der;
41 Yairi, mwana wa Manase analanda midzi yambiri ya Giliyadi ndi kuyitcha kuti Havoti-Yairi.
men Manasses Søn Ja'ir drog hen og erobrede deres Teltbyer og kaldte dem Ja'irs Teltbyer.
42 Ndipo Noba analanda Kenati ndi midzi yozungulira ndi kuyitcha Noba, kutengera dzina la iye mwini.
Og Noba drog hen og erobrede Kenat med tilhørende Smaabyer og kaldte det Noba efter sit eget Navn.