< Numeri 31 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
Entonces el SEÑOR dijo a Moisés:
2 “Uwabwezere zoyipa Amidiyani chifukwa cha zimene anachitira Aisraeli. Ukatha kuchita zimenezi, iwe udzamwalira.”
Da a los madianitas el castigo por el mal que hicieron a los hijos de Israel: y después de eso serás recogido a tu pueblo, morirás.
3 Ndipo Mose anati kwa Aisraeli, “Perekani zida kwa ena mwa anthu anu kuti akamenyane ndi Amidiyani ndi kuwabwezera choyipa mʼmalo mwa Yehova.
Entonces Moisés dijo al pueblo: Que los hombres de entre ustedes estén armados para la guerra para poner en práctica el castigo de Madián el Señor.
4 Mutumize ku nkhondoko amuna 1,000 kuchokera ku fuko lililonse la Aisraeli.”
De cada tribu de Israel envía mil a la guerra.
5 Choncho amuna okwana 12,000 anatenga zida kukonzekera nkhondo, anthu 1,000 kuchokera ku fuko lililonse la Aisraeli.
Así, de los miles de Israel se tomaron mil de cada tribu, doce mil hombres armados para la guerra.
6 Mose anawatumiza ku nkhondo, anthu 1,000 kuchokera ku fuko lililonse pamodzi ndi Finehasi mwana wa Eliezara wansembe amene ananyamula zipangizo zochokera ku malo wopatulika ndi malipenga okaliza.
Y Moisés los envió a la guerra, mil de cada tribu, y con ellos Finees, el hijo del sacerdote Eleazar, tomando en sus manos los vasos del lugar santo y los cuernos para hacer sonar la nota de la guerra.
7 Iwo anamenyana ndi Amidiyani monga momwe Yehova analamulira Mose ndipo anapha mwamuna aliyense.
E hicieron guerra contra Madián, como el Señor le dio órdenes a Moisés; y matan a todos los varones.
8 Mwa anthu ophedwawo munali Evi, Rekemu, Zuri, Huri ndi Reba, mafumu asanu a Amidiyani. Ndipo anaphanso ndi lupanga Balaamu mwana wa Beori.
Ellos mataron a los reyes de Madián con el resto, Evi y Requem y Zur y Hur y Reba, los cinco reyes de Midian; y Balaam, el hijo de Beor, los mataron con la espada.
9 Aisraeli anagwira ukapolo amayi a Chimidiyani ndi ana awo ndipo analandanso ngʼombe, ziweto zawo zina zonse ndi katundu wawo yense.
Las mujeres de Midian con sus pequeños los hijos de Israel tomaron prisioneras; y tomaron para sí todos sus ganados y sus rebaños y todos sus bienes;
10 Anawotcha mizinda yonse imene Amidiyani ankakhalamo pamodzi ndi misasa yawo yonse.
Y después de quemar todos sus pueblos y todos sus campamentos de tiendas,
11 Anatenga zonse zimene analanda ku nkhondoko, anthu ndi zoweta zomwe.
Se fueron con los bienes que habían tomado, hombre y bestia.
12 Ndipo anabwera nawo akapolowo ndi zolanda ku nkhondozo kwa Mose ndi kwa wansembe Eliezara ndi kwa gulu lonse la Aisraeli ku misasa yawo ku chigwa cha Mowabu, mʼmbali mwa mtsinje wa Yorodani ku Yeriko.
Y los prisioneros y los bienes y todo lo que habían tomado, llevaron a Moisés y al sacerdote Eleazar y al pueblo de Israel, al campamento de tiendas de campaña en las tierras bajas de Moab, junto al Jordán en Jericó.
13 Mose, wansembe Eliezara ndi atsogoleri onse a gululo anapita kukakumana nawo kunja kwa misasa.
Entonces Moisés y el sacerdote Eleazar y los jefes de la gente salieron a ellos antes de entrar en el campamento de la tienda.
14 Mose anakwiya nawo akuluakulu a magulu a ankhondowo: olamulira 1,000 ndi olamulira 100, amene ankachokera ku nkhondo.
Y Moisés se enojó con los jefes del ejército, los capitanes de miles y los capitanes de cientos que habían regresado de la guerra.
15 Iye anafunsa kuti, “Kodi nʼchifukwa chiyani mwawaleka amoyo amayi onsewa?”
Y Moisés les dijo: ¿Por qué habéis salvado a todas las mujeres?
16 Paja iwo ndi amene ankatsatira uphungu wa Balaamu ndiponso ndi amene anachititsa Aisraeli kuti asiye Yehova pa zimene zinachitika ku Peori, kotero mliri unagwera anthu a Yehova.
Fueron éstas quienes, por él consejo Balaam, fueron la causa del pecado de Israel contra el Señor en la cuestión de Baal-Peor, debido a la enfermedad que afectó a la gente del Señor.
17 Tsopano iphani munthu wamwamuna aliyense. Ndiponso iphani mayi aliyense amene anagonapo ndi mwamuna,
Así que ahora da muerte a cada hijo varón, y a toda mujer que haya tenido relaciones sexuales con un hombre.
18 koma sungani mtsikana aliyense amene sanagonepo ndi mwamuna.
Pero todas las niñas que no han tenido relaciones sexuales con hombres, pueden quedarse con ustedes.
19 “Inu nonse amene mwaphapo wina wake, kapena kukhudza aliyense amene anaphedwa mukhale kunja kwa msasa masiku asanu ndi awiri. Pa tsiku lachitatu mudziyeretse nokha pamodzi ndi akapolo anu.
Ustedes mismos deberán mantenerse fuera del campamento de la tienda durante siete días, cualquiera de ustedes que haya matado a una persona o se haya acercado a un cadáver; y en el tercer día y en el séptimo día hagan que ustedes y sus prisioneros se purifiquen.
20 Muyeretsenso zovala zanu ndi china chilichonse chopangidwa ndi chikopa, ubweya wa mbuzi kapenanso ndi mtengo.”
Y toda ropa, y cualquier cosa hecha de cuero o pelo de cabra o madera, debes limpiarla.
21 Tsono wansembe Eliezara anati kwa asilikali amene anapita ku nkhondo aja, “Lamulo limene Yehova anapereka kwa Mose ndi ili:
Entonces el sacerdote Eleazar dijo a los hombres de guerra que habían estado en la lucha: Esta es la ley, de la ley que el Señor ha dado a Moisés:
22 Golide, siliva, mkuwa, chitsulo, chiwaya, mtovu
Más oro y plata y latón, hierro y estaño y plomo.
23 ndi china chilichonse chimene sichingapse ndi moto muchidutsitse pa moto, ndipo chidzayeretsedwa. Komanso chiyeretsedwe ndi madzi oyeretsa. Ndipo chilichonse chimene chingapse ndi moto muchidutsitse mʼmadzimo.
Y cualquier cosa que pueda ser calentada, es pasar por el fuego y ser limpiada; pero además se debe poner en el agua de la purificación, y cualquier cosa que no pase por el fuego se debe poner en el agua.
24 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muchape zovala zanu ndipo mudzayera. Mukatero mutha kulowa mu msasa.”
Y en el séptimo día, después de lavar tu ropa, estarás limpio, y luego podrás entrar en el campamento de la tienda.
25 Yehova anawuza Mose kuti,
Y él Señor dijo a Moisés:
26 “Iwe ndi wansembe Eliezara ndiponso akuluakulu a mabanja a anthuwa, muwerenge anthu onse ndi ziweto zomwe zinagwidwa ku nkhondo.
Obtenga una cuenta de todo lo que se tomó en la guerra, del hombre y de la bestia, tú y el sacerdote Eleazar y los jefes de las familias de la gente.
27 Mugawe zolanda ku nkhondozo magawo awiri, lina la ankhondo amene anapita ku nkhondo, lina la anthu onse.
Y ​​que la división se haga en dos partes, una para los hombres de guerra que salieron a la lucha, y otra para todo el pueblo.
28 Pa gawo la ankhondowo, mutengeko gawo la Yehova, pa zofunkha 500 zilizonse mutengeko chimodzi, pa akapolo, ngʼombe, bulu ndi nkhosa.
Y de los hombres de guerra que salieron, se ofrezca al Señor uno de cada quinientos, de las personas, y de los becerros, asnos y ovejas.
29 Utenge zimenezo pa theka la gawo la ankhondowo ndipo upereke kwa wansembe Eliezara kuti zikhale zopereka zanu kwa Yehova.
Toma esto de su parte y dáselo al sacerdote Eleazar como ofrenda para ser elevado al Señor.
30 Kuchokera pa theka la gawo la Aisraeli, utengeko cholanda chimodzi pa makumi asanu aliwonse, pa anthu, ngʼombe, abulu, nkhosa, mbuzi kapena zoweta zina. Uzipereke kwa Alevi amene ntchito yawo ndi yosamalira tenti ya Yehova.”
Y de la parte dada a los hijos de Israel, toma uno de cada cincuenta, de las personas, y de los bueyes y asnos y ovejas, y dáselo a los levitas que tienen el cuidado de la Casa de los Señor.
31 Ndipo Mose ndi wansembe Eliezara anachita monga Yehova analamulira Mose.
Entonces Eleazar y Moisés hicieron lo que el Señor le había ordenado a Moisés.
32 Zotsala pa zolanda ku nkhondo zimene ankhondowo anatenga zinali nkhosa 675,000,
Las bestias capturadas, además de lo que los guerreros tomaron para sí, eran seiscientas setenta y cinco mil ovejas,
33 Ngʼombe 72,000,
Y setenta y dos mil bueyes,
34 abulu 61,000,
Y sesenta y un mil asnos;
35 ndi atsikana omwe sanagonepo ndi mwamuna 32,000.
Y treinta y dos mil personas, es decir, mujeres que nunca habían tenido relaciones sexuales con un hombre.
36 Gawo la ankhondo amene anapita ku nkhondo linali: nkhosa 337,500,
Y la mitad entregada a los hombres que fueron a la guerra, fue de trescientos treinta y siete mil quinientas ovejas.
37 mwa zimenezi gawo la Yehova linali 675;
De los cuales la parte del Señor era seiscientos setenta y cinco.
38 ngʼombe zinalipo 36,000 ndipo gawo la Yehova linali 72;
El número de bueyes era treinta y seis mil, de los cuales la parte del Señor era setenta y dos;
39 abulu analipo 30,500 ndipo gawo la Yehova linali 61;
El número de asnos fue treinta mil quinientos, de los cuales la parte del Señor era sesenta y uno.
40 anthu analipo 16,000 ndipo gawo la Yehova linali 32.
Y el número de personas era dieciséis mil, de las cuales la parte del Señor era treinta y dos personas.
41 Mose anapereka kwa wansembe Eliezara gawo limene linali loyenera kupereka kwa Yehova monga momwe Yehova analamulira Mose.
Entonces Moisés dio la parte del Señor, que se levantó como ofrenda, al sacerdote Eleazar, como el Señor le había dado órdenes a Moisés.
42 Pa gawo la Aisraeli, Mose anapatula theka limodzi kuchotsa pa zolanda ku nkhondo zonse zimene zinabwera ndi ankhondo aja.
Y de la mitad dada a los hijos de Israel, que Moisés había mantenido separada de la que se daba a los combatientes,
43 Tsono gawo la Aisraeli linali ili: nkhosa 337,500,
La mitad del pueblo era trescientos treinta y siete mil quinientas ovejas,
44 ngʼombe 36,000,
Y treinta y seis mil bueyes.
45 abulu 30,500,
Y treinta mil quinientos asnos,
46 anthu 16,000.
Y dieciséis mil personas;
47 Kuchoka pa gawo la Aisraelilo, Mose anatengapo chimodzi pa zolanda ku nkhondo makumi asanu aliwonse, anthu ndi nyama, ndipo anazipereka kwa Alevi amene ankayangʼanira tenti ya Yehova monga Yehova analamulira Mose.
Incluso de la mitad de los hijos de Israel, Moisés tomó uno de cada cincuenta hombres y bestias, y se los dio a los levitas que cuidaban de la Tienda del Señor; como el SEÑOR dio órdenes a Moisés.
48 Pamenepo omwe ankayangʼanira magulu a ankhondo olamulira 1,000 ndi olamulira 100 anabwera kwa Mose,
Entonces los hombres en autoridad sobre los miles del ejército, los capitanes de miles y los capitanes de cientos vinieron a Moisés.
49 iwo anati kwa iye, “Ife anthu anu tawerenga ankhondo amene timawalamulira. Palibe munthu ndi mmodzi yemwe amene wasowa.
Y le dijeron: Tus siervos han tomado nota del número de todos los combatientes bajo nuestras órdenes, y todos están presentes;
50 Ndipo tabweretsa zopereka kwa Yehova zimene munthu aliyense anapeza: ziwiya zagolide, zibangiri, zigwinjiri, mphete zosindikizira, ndolo ndi mikanda kuti tichitire mwambo wopepesera machimo pamaso pa Yehova.”
Y aquí tenemos una ofrenda para el Señor de lo que cada hombre tomó en la guerra, adornos de oro, cadenas para las piernas y anillos para los brazos, anillos para los dedos, aretes y adornos para el cuello, para hacer nuestra Almas libres del pecado delante del Señor.
51 Ndipo Mose ndi wansembe Eliezara analandira kuchokera kwa atsogoleriwo golide pamodzi ndi zipangizo zonse zosula.
Y Moisés y el sacerdote Eleazar les quitaron el oro, y todos los ornamentos trabajados.
52 Golide yense wochokera kwa atsogoleri a 1,000 ndi atsogoleri a 100 zomwe Mose ndi Eliezara anapereka ngati mphatso kwa Yehova zinali zolemera makilogalamu 200.
Y el oro que los capitanes de miles y los capitanes de cientos dieron, como ofrenda para ser levantados delante del Señor, llegó a dieciséis mil setecientos cincuenta siclos.
53 Wankhondo aliyense anatenga zomwe analanda yekha ku nkhondo.
Porque cada hombre del ejército había tomado bienes para sí mismo en la guerra.
54 Mose ndi Eliezara wansembe analandira golide kuchokera kwa atsogoleri a 1,000 ndi atsogoleri a 100 ndi kukamuyika mu tenti ya msonkhano ngati chikumbutso cha Aisraeli pamaso pa Yehova.
Entonces Moisés y el sacerdote Eleazar tomaron el oro dado por los capitanes de miles y capitanes de cientos, y lo llevaron a la Tienda de la reunión, para ser una señal en memoria de los hijos de Israel ante el Señor.

< Numeri 31 >