< Numeri 31 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
INkosi yasikhuluma kuMozisi isithi:
2 “Uwabwezere zoyipa Amidiyani chifukwa cha zimene anachitira Aisraeli. Ukatha kuchita zimenezi, iwe udzamwalira.”
Phindisela impindiselo yabantwana bakoIsrayeli kumaMidiyani; emva kwalokho ubuthelwe ebantwini bakini.
3 Ndipo Mose anati kwa Aisraeli, “Perekani zida kwa ena mwa anthu anu kuti akamenyane ndi Amidiyani ndi kuwabwezera choyipa mʼmalo mwa Yehova.
UMozisi wakhuluma ebantwini esithi: Abanye benu kabahlomele impi ukuze bamelane lamaMidiyani, benze impindiselo yeNkosi kumaMidiyani.
4 Mutumize ku nkhondoko amuna 1,000 kuchokera ku fuko lililonse la Aisraeli.”
Thumelani empini abayinkulungwane kuleso lalesosizwe, kuzo zonke izizwe zakoIsrayeli.
5 Choncho amuna okwana 12,000 anatenga zida kukonzekera nkhondo, anthu 1,000 kuchokera ku fuko lililonse la Aisraeli.
Kwasekunikelwa kuvela ezinkulungwaneni zakoIsrayeli inkulungwane ngesizwe, inkulungwane ezilitshumi lambili zihlomele impi.
6 Mose anawatumiza ku nkhondo, anthu 1,000 kuchokera ku fuko lililonse pamodzi ndi Finehasi mwana wa Eliezara wansembe amene ananyamula zipangizo zochokera ku malo wopatulika ndi malipenga okaliza.
UMozisi wasezithumela empini, inkulungwane ngesizwe, zona loPhinehasi indodana kaEleyazare umpristi, ukuya empini, belempahla ezingcwele lempondo zokuhlaba umkhosi esandleni sakhe.
7 Iwo anamenyana ndi Amidiyani monga momwe Yehova analamulira Mose ndipo anapha mwamuna aliyense.
Basebesilwa bemelene lamaMidiyani, njengokulaya kweNkosi kuMozisi, babulala bonke abesilisa.
8 Mwa anthu ophedwawo munali Evi, Rekemu, Zuri, Huri ndi Reba, mafumu asanu a Amidiyani. Ndipo anaphanso ndi lupanga Balaamu mwana wa Beori.
Babulala njalo amakhosi eMidiyani, ngaphandle kwababuleweyo, oEvi loRekemi loZuri loHuri loReba, amakhosi amahlanu eMidiyani; loBalami indodana kaBeyori bambulala ngenkemba.
9 Aisraeli anagwira ukapolo amayi a Chimidiyani ndi ana awo ndipo analandanso ngʼombe, ziweto zawo zina zonse ndi katundu wawo yense.
Abantwana bakoIsrayeli basebethumba abesifazana bamaMidiyani labantwanyana babo, baphanga inkomo zawo zonke, lezimvu zawo zonke, layo yonke inotho yawo.
10 Anawotcha mizinda yonse imene Amidiyani ankakhalamo pamodzi ndi misasa yawo yonse.
Batshisa ngomlilo yonke imizi ayehlala kiyo, lazo zonke izinqaba zawo.
11 Anatenga zonse zimene analanda ku nkhondoko, anthu ndi zoweta zomwe.
Bathatha yonke impango lakho konke okuthunjiweyo, kwabantu lokwezifuyo,
12 Ndipo anabwera nawo akapolowo ndi zolanda ku nkhondozo kwa Mose ndi kwa wansembe Eliezara ndi kwa gulu lonse la Aisraeli ku misasa yawo ku chigwa cha Mowabu, mʼmbali mwa mtsinje wa Yorodani ku Yeriko.
baletha abathunjiweyo lempango lokuthunjiweyo kuMozisi lakuEleyazare umpristi, lakunhlangano yabantwana bakoIsrayeli, enkambeni emagcekeni akoMowabi, aseJordani eJeriko.
13 Mose, wansembe Eliezara ndi atsogoleri onse a gululo anapita kukakumana nawo kunja kwa misasa.
UMozisi loEleyazare umpristi leziphathamandla zonke zenhlangano basebephuma ukubahlangabeza ngaphandle kwenkamba.
14 Mose anakwiya nawo akuluakulu a magulu a ankhondowo: olamulira 1,000 ndi olamulira 100, amene ankachokera ku nkhondo.
UMozisi wasethukuthelela induna zebutho, induna zezinkulungwane lenduna zamakhulu ezazivela ebuthweni lempi.
15 Iye anafunsa kuti, “Kodi nʼchifukwa chiyani mwawaleka amoyo amayi onsewa?”
UMozisi wasesithi kuzo: Liyekele yini abesifazana bonke ukuthi baphile?
16 Paja iwo ndi amene ankatsatira uphungu wa Balaamu ndiponso ndi amene anachititsa Aisraeli kuti asiye Yehova pa zimene zinachitika ku Peori, kotero mliri unagwera anthu a Yehova.
Khangelani, yilaba abenza abantwana bakoIsrayeli, ngeseluleko sikaBalami, ukuthi benze isiphambeko eNkosini endabeni yePeyori, kwaze kwaba lenhlupheko phakathi kwenhlangano yeNkosi.
17 Tsopano iphani munthu wamwamuna aliyense. Ndiponso iphani mayi aliyense amene anagonapo ndi mwamuna,
Ngakho-ke bulalani wonke owesilisa ebantwanyaneni, libulale wonke owesifazana owazi indoda ngokulala lendoda;
18 koma sungani mtsikana aliyense amene sanagonepo ndi mwamuna.
kodwa bonke abantwanyana abesifazana abangazanga indoda ngokulala layo, libayekele baphile, babe ngabenu.
19 “Inu nonse amene mwaphapo wina wake, kapena kukhudza aliyense amene anaphedwa mukhale kunja kwa msasa masiku asanu ndi awiri. Pa tsiku lachitatu mudziyeretse nokha pamodzi ndi akapolo anu.
Lina-ke, misani inkamba ngaphandle kwenkamba insuku eziyisikhombisa, loba ngubani obulele umuntu, laloba ngubani othinte obuleweyo, lizihlambulule lina labathunjiweyo benu ngosuku lwesithathu langosuku lwesikhombisa,
20 Muyeretsenso zovala zanu ndi china chilichonse chopangidwa ndi chikopa, ubweya wa mbuzi kapenanso ndi mtengo.”
lihlambulule sonke isembatho, layo yonke into eyenziweyo ngesikhumba, lakho konke okwenziweyo ngoboya bembuzi, layo yonke into eyenziweyo ngesihlahla.
21 Tsono wansembe Eliezara anati kwa asilikali amene anapita ku nkhondo aja, “Lamulo limene Yehova anapereka kwa Mose ndi ili:
UEleyazare umpristi wasesithi kumadoda empi ayephume impi: Lesi yisimiso somlayo iNkosi emlaye ngaso uMozisi:
22 Golide, siliva, mkuwa, chitsulo, chiwaya, mtovu
Kuphela igolide, lesiliva, ithusi, insimbi, ithini, lomnuso,
23 ndi china chilichonse chimene sichingapse ndi moto muchidutsitse pa moto, ndipo chidzayeretsedwa. Komanso chiyeretsedwe ndi madzi oyeretsa. Ndipo chilichonse chimene chingapse ndi moto muchidutsitse mʼmadzimo.
yonke into engahlala emlilweni lizayidlulisa emlilweni, ihlambuluke; loba kunjalo izahlanjululwa ngamanzi okwehlukanisa. Lakho konke okungahlali emlilweni lizakudlulisa emanzini.
24 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muchape zovala zanu ndipo mudzayera. Mukatero mutha kulowa mu msasa.”
Njalo lizahlamba izembatho zenu ngosuku lwesikhombisa, lihlambuluke, lemva kwalokho lingene enkambeni.
25 Yehova anawuza Mose kuti,
INkosi yasikhuluma kuMozisi isithi:
26 “Iwe ndi wansembe Eliezara ndiponso akuluakulu a mabanja a anthuwa, muwerenge anthu onse ndi ziweto zomwe zinagwidwa ku nkhondo.
Thatha inani lonke lempango lokuthunjiweyo, okwabantu lokwezifuyo, wena, loEleyazare umpristi, lenhloko zaboyise zenhlangano;
27 Mugawe zolanda ku nkhondozo magawo awiri, lina la ankhondo amene anapita ku nkhondo, lina la anthu onse.
yehlukanisa impango ibe zingxenye ezimbili, phakathi kwabahlanganyela empini baphuma impi lenhlangano yonke.
28 Pa gawo la ankhondowo, mutengeko gawo la Yehova, pa zofunkha 500 zilizonse mutengeko chimodzi, pa akapolo, ngʼombe, bulu ndi nkhosa.
Njalo thelisela iNkosi umthelo emadodeni empi ayephumele impi, umphefumulo owodwa phakathi kwamakhulu amahlanu, owabantu, lowenkomo, lowabobabhemi, lowezimvu,
29 Utenge zimenezo pa theka la gawo la ankhondowo ndipo upereke kwa wansembe Eliezara kuti zikhale zopereka zanu kwa Yehova.
likuthathe kungxenye yawo eyodwa kwezimbili, njalo ukunike uEleyazare umpristi kube ngumnikelo wokuphakanyiswa weNkosi.
30 Kuchokera pa theka la gawo la Aisraeli, utengeko cholanda chimodzi pa makumi asanu aliwonse, pa anthu, ngʼombe, abulu, nkhosa, mbuzi kapena zoweta zina. Uzipereke kwa Alevi amene ntchito yawo ndi yosamalira tenti ya Yehova.”
Lengxenyeni eyodwa kwezimbili yabantwana bakoIsrayeli thatha isabelo esisodwa kwezingamatshumi amahlanu, esabantu, esezinkomo, esabobabhemi, lesezimvu, kuso sonke isifuyo, ukunike amaLevi alondoloza imfanelo yethabhanekele leNkosi.
31 Ndipo Mose ndi wansembe Eliezara anachita monga Yehova analamulira Mose.
UMozisi loEleyazare umpristi basebesenza njengokulaya kweNkosi kuMozisi.
32 Zotsala pa zolanda ku nkhondo zimene ankhondowo anatenga zinali nkhosa 675,000,
Lempango eyayisele lokuthunjiweyo abantu bempi abakuthumbayo yayiyizimvu ezizinkulungwane ezingamakhulu ayisithupha lamatshumi ayisikhombisa lanhlanu,
33 Ngʼombe 72,000,
lenkomo ezizinkulungwane ezingamatshumi ayisikhombisa lambili,
34 abulu 61,000,
labobabhemi abazinkulungwane ezingamatshumi ayisithupha lanye,
35 ndi atsikana omwe sanagonepo ndi mwamuna 32,000.
lemiphefumulo yabantu besifazana abangazanga ukulala lendoda, bonke abantu babeyizinkulungwane ezingamatshumi amathathu lambili.
36 Gawo la ankhondo amene anapita ku nkhondo linali: nkhosa 337,500,
Lengxenye, isabelo sababephumele impi, ngenani, yayiyizimvu ezizinkulungwane ezingamakhulu amathathu lamatshumi amathathu lesikhombisa lamakhulu amahlanu;
37 mwa zimenezi gawo la Yehova linali 675;
lomthelo eNkosini wezimvu wawungamakhulu ayisithupha lamatshumi ayisikhombisa lanhlanu.
38 ngʼombe zinalipo 36,000 ndipo gawo la Yehova linali 72;
Lenkomo zazizinkulungwane ezingamatshumi amathathu lesithupha; lomthelo wazo eNkosini wawungamatshumi ayisikhombisa lambili.
39 abulu analipo 30,500 ndipo gawo la Yehova linali 61;
Labobabhemi babeyizinkulungwane ezingamatshumi amathathu lamakhulu amahlanu; lomthelo wabo eNkosini wawungamatshumi ayisithupha lanye.
40 anthu analipo 16,000 ndipo gawo la Yehova linali 32.
Lemiphefumulo yabantu yayizinkulungwane ezilitshumi lesithupha; lomthelo wayo eNkosini wawungabantu abangamatshumi amathathu lambili.
41 Mose anapereka kwa wansembe Eliezara gawo limene linali loyenera kupereka kwa Yehova monga momwe Yehova analamulira Mose.
UMozisi wasenika umthelo, umnikelo wokuphakanyiswa weNkosi, kuEleyazare umpristi, njengalokho iNkosi yamlaya uMozisi.
42 Pa gawo la Aisraeli, Mose anapatula theka limodzi kuchotsa pa zolanda ku nkhondo zonse zimene zinabwera ndi ankhondo aja.
Lokwengxenye yabantwana bakoIsrayeli, uMozisi ayehlukanise ivela emadodeni ayelwe impi.
43 Tsono gawo la Aisraeli linali ili: nkhosa 337,500,
Lengxenye engeyenhlangano, eyezimvu, yayizinkulungwane ezingamakhulu amathathu lamatshumi amathathu lesikhombisa lamakhulu amahlanu,
44 ngʼombe 36,000,
lenkomo ezizinkulungwane ezingamatshumi amathathu lesithupha,
45 abulu 30,500,
labobabhemi abazinkulungwane ezingamatshumi amathathu lamakhulu amahlanu,
46 anthu 16,000.
lemiphefumulo yabantu abayizinkulungwane ezilitshumi lesithupha.
47 Kuchoka pa gawo la Aisraelilo, Mose anatengapo chimodzi pa zolanda ku nkhondo makumi asanu aliwonse, anthu ndi nyama, ndipo anazipereka kwa Alevi amene ankayangʼanira tenti ya Yehova monga Yehova analamulira Mose.
Lakuyo ingxenye yabantwana bakoIsrayeli uMozisi wathatha isabelo esisodwa kwezingatshumini amahlanu, esabantu lesezifuyo, wakunika amaLevi ayelondoloza imfanelo yethabhanekele leNkosi, njengokulaya kweNkosi kuMozisi.
48 Pamenepo omwe ankayangʼanira magulu a ankhondo olamulira 1,000 ndi olamulira 100 anabwera kwa Mose,
Iziphathamandla ezaziphezu kwezinkulungwane zebutho, izinduna zezinkulungwane lezinduna zamakhulu, zasezisondela kuMozisi,
49 iwo anati kwa iye, “Ife anthu anu tawerenga ankhondo amene timawalamulira. Palibe munthu ndi mmodzi yemwe amene wasowa.
zathi kuMozisi: Izinceku zakho sezithethe inani lonke lamadoda empi ayengaphansi kwesandla sethu; njalo kakulamuntu ongekho kithi.
50 Ndipo tabweretsa zopereka kwa Yehova zimene munthu aliyense anapeza: ziwiya zagolide, zibangiri, zigwinjiri, mphete zosindikizira, ndolo ndi mikanda kuti tichitire mwambo wopepesera machimo pamaso pa Yehova.”
Ngakho silethile umnikelo weNkosi, ngulowo lalowo awutholileyo, izinto zegolide, izigqizo, lamasongo, izindandatho, amacici, lezigqizo zentanyeni, ukwenzela imiphefumulo yethu inhlawulo yokuthula phambi kweNkosi.
51 Ndipo Mose ndi wansembe Eliezara analandira kuchokera kwa atsogoleriwo golide pamodzi ndi zipangizo zonse zosula.
UMozisi loEleyazare umpristi basebesemukela igolide kuzo, zonke izinto ezenziwe ngobungcitshi.
52 Golide yense wochokera kwa atsogoleri a 1,000 ndi atsogoleri a 100 zomwe Mose ndi Eliezara anapereka ngati mphatso kwa Yehova zinali zolemera makilogalamu 200.
Lalo lonke igolide lomnikelo abalinikela eNkosini, livela ezinduneni zezinkulungwane lezinduneni zamakhulu lalingamashekeli azinkulungwane ezilitshumi lesithupha lamakhulu ayisikhombisa lamatshumi amahlanu.
53 Wankhondo aliyense anatenga zomwe analanda yekha ku nkhondo.
Amadoda empi ayethethe impango, yileyo laleyo engeyayo.
54 Mose ndi Eliezara wansembe analandira golide kuchokera kwa atsogoleri a 1,000 ndi atsogoleri a 100 ndi kukamuyika mu tenti ya msonkhano ngati chikumbutso cha Aisraeli pamaso pa Yehova.
UMozisi loEleyazare umpristi basebesemukela igolide enduneni zezinkulungwane lezamakhulu, baliletha ethenteni lenhlangano, kube yisikhumbuzo kubantwana bakoIsrayeli phambi kweNkosi.

< Numeri 31 >