< Numeri 31 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
And he spoke Yahweh to Moses saying.
2 “Uwabwezere zoyipa Amidiyani chifukwa cha zimene anachitira Aisraeli. Ukatha kuchita zimenezi, iwe udzamwalira.”
Avenge [the] vengeance of [the] people of Israel from with the Midianites (after *L(P)*) you will be gathered to people your.
3 Ndipo Mose anati kwa Aisraeli, “Perekani zida kwa ena mwa anthu anu kuti akamenyane ndi Amidiyani ndi kuwabwezera choyipa mʼmalo mwa Yehova.
And he spoke Moses to the people saying be equipped from with you men for war so they may be on Midian to give [the] vengeance of Yahweh on Midian.
4 Mutumize ku nkhondoko amuna 1,000 kuchokera ku fuko lililonse la Aisraeli.”
One thousand to the tribe one thousand to the tribe for all [the] tribes of Israel you will send out to war.
5 Choncho amuna okwana 12,000 anatenga zida kukonzekera nkhondo, anthu 1,000 kuchokera ku fuko lililonse la Aisraeli.
And they were selected from [the] thousands of Israel one thousand to the tribe two [plus] ten thousand armed [men] of war.
6 Mose anawatumiza ku nkhondo, anthu 1,000 kuchokera ku fuko lililonse pamodzi ndi Finehasi mwana wa Eliezara wansembe amene ananyamula zipangizo zochokera ku malo wopatulika ndi malipenga okaliza.
And he sent them Moses one thousand to the tribe to war them and Phinehas [the] son of Eleazar the priest to war and [the] vessels of the holy place and [the] trumpets of the alarm [were] in hand his.
7 Iwo anamenyana ndi Amidiyani monga momwe Yehova analamulira Mose ndipo anapha mwamuna aliyense.
And they waged war on Midian just as he had commanded Yahweh Moses and they killed every male.
8 Mwa anthu ophedwawo munali Evi, Rekemu, Zuri, Huri ndi Reba, mafumu asanu a Amidiyani. Ndipo anaphanso ndi lupanga Balaamu mwana wa Beori.
And [the] kings of Midian they killed with slain [ones] their Evi and Rekem and Zur and Hur and Reba [the] five [the] kings of Midian and Balaam [the] son of Beor they killed with the sword.
9 Aisraeli anagwira ukapolo amayi a Chimidiyani ndi ana awo ndipo analandanso ngʼombe, ziweto zawo zina zonse ndi katundu wawo yense.
And they took captive [the] people of Israel [the] women of Midian and little one[s] their and all cattle their and all livestock their and all wealth their they plundered.
10 Anawotcha mizinda yonse imene Amidiyani ankakhalamo pamodzi ndi misasa yawo yonse.
And all cities their in dwelling places their and all encampments their they burned with fire.
11 Anatenga zonse zimene analanda ku nkhondoko, anthu ndi zoweta zomwe.
And they took all the plunder and all the booty among humankind and among the livestock.
12 Ndipo anabwera nawo akapolowo ndi zolanda ku nkhondozo kwa Mose ndi kwa wansembe Eliezara ndi kwa gulu lonse la Aisraeli ku misasa yawo ku chigwa cha Mowabu, mʼmbali mwa mtsinje wa Yorodani ku Yeriko.
And they brought to Moses and to Eleazar the priest and to [the] congregation of [the] people of Israel the captive[s] and the booty and the plunder to the camp to [the] plains of Moab which [were] at [the] Jordan of Jericho.
13 Mose, wansembe Eliezara ndi atsogoleri onse a gululo anapita kukakumana nawo kunja kwa misasa.
And they went out Moses and Eleazar the priest and all [the] leaders of the congregation to meet them to from [the] outside of the camp.
14 Mose anakwiya nawo akuluakulu a magulu a ankhondowo: olamulira 1,000 ndi olamulira 100, amene ankachokera ku nkhondo.
And he was angry Moses towards [the] officers of the army [the] commanders of the thousands and [the] commanders of the hundreds who were coming from [the] war of the battle.
15 Iye anafunsa kuti, “Kodi nʼchifukwa chiyani mwawaleka amoyo amayi onsewa?”
And he said to them Moses ¿ have you let live every female.
16 Paja iwo ndi amene ankatsatira uphungu wa Balaamu ndiponso ndi amene anachititsa Aisraeli kuti asiye Yehova pa zimene zinachitika ku Peori, kotero mliri unagwera anthu a Yehova.
There! they they were to [the] people of Israel by [the] word of Balaam to offer unfaithfulness in Yahweh on [the] matter of Peor and it was the plague among [the] congregation of Yahweh.
17 Tsopano iphani munthu wamwamuna aliyense. Ndiponso iphani mayi aliyense amene anagonapo ndi mwamuna,
And therefore kill every male among the little one[s] and every woman [who has] known a man to [the] lying of a male kill.
18 koma sungani mtsikana aliyense amene sanagonepo ndi mwamuna.
And all the little one[s] among the women who not they have known lying of a male preserve alive for yourselves.
19 “Inu nonse amene mwaphapo wina wake, kapena kukhudza aliyense amene anaphedwa mukhale kunja kwa msasa masiku asanu ndi awiri. Pa tsiku lachitatu mudziyeretse nokha pamodzi ndi akapolo anu.
And you encamp from [the] outside of the camp seven days any [one who] has killed anyone and any - [one who] has touched the [one] slain you will purify yourselves on the day third and on the day seventh you and captive[s] your.
20 Muyeretsenso zovala zanu ndi china chilichonse chopangidwa ndi chikopa, ubweya wa mbuzi kapenanso ndi mtengo.”
And every garment and every article of hide and every product of goat hair and every article of wood you will purify yourselves.
21 Tsono wansembe Eliezara anati kwa asilikali amene anapita ku nkhondo aja, “Lamulo limene Yehova anapereka kwa Mose ndi ili:
And he said Eleazar the priest to [the] men of the army who had gone to the battle this [is] [the] statute of the law which he commanded Yahweh Moses.
22 Golide, siliva, mkuwa, chitsulo, chiwaya, mtovu
Only the gold and the silver the bronze the iron the tin and the lead.
23 ndi china chilichonse chimene sichingapse ndi moto muchidutsitse pa moto, ndipo chidzayeretsedwa. Komanso chiyeretsedwe ndi madzi oyeretsa. Ndipo chilichonse chimene chingapse ndi moto muchidutsitse mʼmadzimo.
Every thing which it will go in the fire you will make pass in the fire and it will be pure nevertheless by [the] water of impurity it will purify itself and all that not it will go in the fire you will make pass in the water.
24 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muchape zovala zanu ndipo mudzayera. Mukatero mutha kulowa mu msasa.”
And you will wash clothes your on the day seventh and you will be pure and after you will come to the camp.
25 Yehova anawuza Mose kuti,
And he said Yahweh to Moses saying.
26 “Iwe ndi wansembe Eliezara ndiponso akuluakulu a mabanja a anthuwa, muwerenge anthu onse ndi ziweto zomwe zinagwidwa ku nkhondo.
Lift up [the] head of [the] booty of captivity among humankind and among the livestock you and Eleazar the priest and [the] leaders of [the] fathers of the congregation.
27 Mugawe zolanda ku nkhondozo magawo awiri, lina la ankhondo amene anapita ku nkhondo, lina la anthu onse.
And you will divide the booty between [those] skilled of the battle who went out to war and between all the congregation.
28 Pa gawo la ankhondowo, mutengeko gawo la Yehova, pa zofunkha 500 zilizonse mutengeko chimodzi, pa akapolo, ngʼombe, bulu ndi nkhosa.
And you will raise a tax for Yahweh from with [the] men of war who went out to war one person from [the] five hundred from humankind and from the cattle and from the donkeys and from the sheep.
29 Utenge zimenezo pa theka la gawo la ankhondowo ndipo upereke kwa wansembe Eliezara kuti zikhale zopereka zanu kwa Yehova.
From half their you will take [it] and you will give [it] to Eleazar the priest [the] contribution of Yahweh.
30 Kuchokera pa theka la gawo la Aisraeli, utengeko cholanda chimodzi pa makumi asanu aliwonse, pa anthu, ngʼombe, abulu, nkhosa, mbuzi kapena zoweta zina. Uzipereke kwa Alevi amene ntchito yawo ndi yosamalira tenti ya Yehova.”
And from [the] half of [the] people of Israel you will take - one - [person] drawn from the fifty from humankind from the cattle from the donkeys and from the sheep from all the livestock and you will give them to the Levites [who] keep [the] service of [the] tabernacle of Yahweh.
31 Ndipo Mose ndi wansembe Eliezara anachita monga Yehova analamulira Mose.
And he did Moses and Eleazar the priest just as he had commanded Yahweh Moses.
32 Zotsala pa zolanda ku nkhondo zimene ankhondowo anatenga zinali nkhosa 675,000,
And it was the booty [the] remainder of the plunder which they had plundered [the] people of the army sheep six hundred thousand and seventy thousand and five thousand.
33 Ngʼombe 72,000,
And cattle two and seventy thousand.
34 abulu 61,000,
And donkeys one and sixty thousand.
35 ndi atsikana omwe sanagonepo ndi mwamuna 32,000.
And [the] person[s] of humankind from the women who not they had known lying of a male every person two and thirty thousand.
36 Gawo la ankhondo amene anapita ku nkhondo linali: nkhosa 337,500,
And it was the half [the] portion of those [who] had gone out in the army [the] number of the sheep [was] three hundred thousand and thirty thousand and seven thousand and five hundred.
37 mwa zimenezi gawo la Yehova linali 675;
And it was the tax for Yahweh from the sheep six hundred five and seventy.
38 ngʼombe zinalipo 36,000 ndipo gawo la Yehova linali 72;
And the cattle [were] six and thirty thousand and tax their for Yahweh [was] two and seventy.
39 abulu analipo 30,500 ndipo gawo la Yehova linali 61;
And donkeys [were] thirty thousand and five hundred and tax their for Yahweh [was] one and sixty.
40 anthu analipo 16,000 ndipo gawo la Yehova linali 32.
And [the] person[s] of humankind [were] six-teen thousand and tax their for Yahweh [was] two and thirty person[s].
41 Mose anapereka kwa wansembe Eliezara gawo limene linali loyenera kupereka kwa Yehova monga momwe Yehova analamulira Mose.
And he gave Moses [the] tax of [the] contribution of Yahweh to Eleazar the priest just as he had commanded Yahweh Moses.
42 Pa gawo la Aisraeli, Mose anapatula theka limodzi kuchotsa pa zolanda ku nkhondo zonse zimene zinabwera ndi ankhondo aja.
And from [the] half of [the] people of Israel which he had divided Moses from the men who had gone to war.
43 Tsono gawo la Aisraeli linali ili: nkhosa 337,500,
And it was [the] half of the congregation from the sheep three hundred thousand and thirty thousand seven thousand and five hundred.
44 ngʼombe 36,000,
And cattle six and thirty thousand.
45 abulu 30,500,
And donkeys thirty thousand and five hundred.
46 anthu 16,000.
And person[s] of humankind six-teen thousand.
47 Kuchoka pa gawo la Aisraelilo, Mose anatengapo chimodzi pa zolanda ku nkhondo makumi asanu aliwonse, anthu ndi nyama, ndipo anazipereka kwa Alevi amene ankayangʼanira tenti ya Yehova monga Yehova analamulira Mose.
And he took Moses from [the] half of [the] people of Israel those drawn one from the fifty from humankind and from the livestock and he gave them to the Levites [who] keep [the] service of [the] tabernacle of Yahweh just as he had commanded Yahweh Moses.
48 Pamenepo omwe ankayangʼanira magulu a ankhondo olamulira 1,000 ndi olamulira 100 anabwera kwa Mose,
And they drew near to Moses the officers who [were] of [the] thousands of the army [the] commanders of the thousands and [the] commanders of the hundreds.
49 iwo anati kwa iye, “Ife anthu anu tawerenga ankhondo amene timawalamulira. Palibe munthu ndi mmodzi yemwe amene wasowa.
And they said to Moses servants your they have lifted up [the] head of [the] men of war who [were] in hand our and not he is missing from us anyone.
50 Ndipo tabweretsa zopereka kwa Yehova zimene munthu aliyense anapeza: ziwiya zagolide, zibangiri, zigwinjiri, mphete zosindikizira, ndolo ndi mikanda kuti tichitire mwambo wopepesera machimo pamaso pa Yehova.”
And we have brought near [the] offering of Yahweh everyone [that] which he found an article of gold an armlet and a bracelet a signet-ring an earring and an ornament to make atonement on selves our before Yahweh.
51 Ndipo Mose ndi wansembe Eliezara analandira kuchokera kwa atsogoleriwo golide pamodzi ndi zipangizo zonse zosula.
And he took Moses and Eleazar the priest the gold from with them every article of work.
52 Golide yense wochokera kwa atsogoleri a 1,000 ndi atsogoleri a 100 zomwe Mose ndi Eliezara anapereka ngati mphatso kwa Yehova zinali zolemera makilogalamu 200.
And it was - all [the] gold of the contribution which they raised for Yahweh six-teen thousand seven hundred and fifty shekel[s] from with [the] commanders of the thousands and from with [the] commanders of the hundreds.
53 Wankhondo aliyense anatenga zomwe analanda yekha ku nkhondo.
[the] men of The army they had taken plunder everyone for himself.
54 Mose ndi Eliezara wansembe analandira golide kuchokera kwa atsogoleri a 1,000 ndi atsogoleri a 100 ndi kukamuyika mu tenti ya msonkhano ngati chikumbutso cha Aisraeli pamaso pa Yehova.
And he took Moses and Eleazar the priest the gold from with [the] commanders of the thousands and the hundreds and they brought it into [the] tent of meeting a memorial for [the] people of Israel before Yahweh.

< Numeri 31 >