< Numeri 31 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
The Lord told Moses,
2 “Uwabwezere zoyipa Amidiyani chifukwa cha zimene anachitira Aisraeli. Ukatha kuchita zimenezi, iwe udzamwalira.”
“Punish the Midianites because of what they did to the Israelites. After that you will join your forefathers in death.”
3 Ndipo Mose anati kwa Aisraeli, “Perekani zida kwa ena mwa anthu anu kuti akamenyane ndi Amidiyani ndi kuwabwezera choyipa mʼmalo mwa Yehova.
Moses instructed the people, “Have some of your men get ready for battle, so they can go and attack the Midianites and carry out the Lord's punishment on them.
4 Mutumize ku nkhondoko amuna 1,000 kuchokera ku fuko lililonse la Aisraeli.”
You are to contribute one thousand men from each Israelite tribe.”
5 Choncho amuna okwana 12,000 anatenga zida kukonzekera nkhondo, anthu 1,000 kuchokera ku fuko lililonse la Aisraeli.
So one thousand men were chosen from each Israelite tribe, making twelve thousand troops ready for battle.
6 Mose anawatumiza ku nkhondo, anthu 1,000 kuchokera ku fuko lililonse pamodzi ndi Finehasi mwana wa Eliezara wansembe amene ananyamula zipangizo zochokera ku malo wopatulika ndi malipenga okaliza.
Moses sent them into battle, one thousand from each tribe, together with Phinehas, son of Eleazar the priest. He carried with him the holy objects from the sanctuary and the trumpets used for giving signals.
7 Iwo anamenyana ndi Amidiyani monga momwe Yehova analamulira Mose ndipo anapha mwamuna aliyense.
They attacked the Midianites, as the Lord had told Moses to do, and they killed all the men.
8 Mwa anthu ophedwawo munali Evi, Rekemu, Zuri, Huri ndi Reba, mafumu asanu a Amidiyani. Ndipo anaphanso ndi lupanga Balaamu mwana wa Beori.
Among those killed were the five kings of Midian, Evi, Rekem, Zur, Hur, and Reba. They also killed Balaam, son of Beor, with the sword.
9 Aisraeli anagwira ukapolo amayi a Chimidiyani ndi ana awo ndipo analandanso ngʼombe, ziweto zawo zina zonse ndi katundu wawo yense.
The Israelites captured the Midianite women and children, and they took as plunder all their herds, flocks, and possessions.
10 Anawotcha mizinda yonse imene Amidiyani ankakhalamo pamodzi ndi misasa yawo yonse.
They set fire to all the Midianite towns and camps where they had lived,
11 Anatenga zonse zimene analanda ku nkhondoko, anthu ndi zoweta zomwe.
and carried away all the plunder and loot, including people and animals.
12 Ndipo anabwera nawo akapolowo ndi zolanda ku nkhondozo kwa Mose ndi kwa wansembe Eliezara ndi kwa gulu lonse la Aisraeli ku misasa yawo ku chigwa cha Mowabu, mʼmbali mwa mtsinje wa Yorodani ku Yeriko.
They brought the prisoners, loot, and plunder to Moses, to Eleazar the priest, and to the rest of the Israelites where they were camped on the plains of Moab, beside the Jordan opposite Jericho.
13 Mose, wansembe Eliezara ndi atsogoleri onse a gululo anapita kukakumana nawo kunja kwa misasa.
Moses, Eleazar the priest, and all the Israelite leaders went out of the camp to meet them.
14 Mose anakwiya nawo akuluakulu a magulu a ankhondowo: olamulira 1,000 ndi olamulira 100, amene ankachokera ku nkhondo.
Moses was angry with the army officers, the commanders of thousands and commanders of hundreds, who returned from the battle.
15 Iye anafunsa kuti, “Kodi nʼchifukwa chiyani mwawaleka amoyo amayi onsewa?”
“Why did you let all the women live?” he asked them.
16 Paja iwo ndi amene ankatsatira uphungu wa Balaamu ndiponso ndi amene anachititsa Aisraeli kuti asiye Yehova pa zimene zinachitika ku Peori, kotero mliri unagwera anthu a Yehova.
“You realize that these were the women seduced the Israelite men, leading them to be unfaithful to the Lord at Peor, following Balaam's advice! That's why the Lord's people suffered from the plague!
17 Tsopano iphani munthu wamwamuna aliyense. Ndiponso iphani mayi aliyense amene anagonapo ndi mwamuna,
So go and kill all the boys and every woman who has had slept with a man.
18 koma sungani mtsikana aliyense amene sanagonepo ndi mwamuna.
Let all the girls who are virgins live. They are yours.
19 “Inu nonse amene mwaphapo wina wake, kapena kukhudza aliyense amene anaphedwa mukhale kunja kwa msasa masiku asanu ndi awiri. Pa tsiku lachitatu mudziyeretse nokha pamodzi ndi akapolo anu.
All those of you who killed someone or touched a dead body must stay outside the camp for seven days. Purify yourselves and your prisoners on the third day and the seventh day.
20 Muyeretsenso zovala zanu ndi china chilichonse chopangidwa ndi chikopa, ubweya wa mbuzi kapenanso ndi mtengo.”
Also purify all your clothing garment and anything made of leather, goat's hair, or wood.”
21 Tsono wansembe Eliezara anati kwa asilikali amene anapita ku nkhondo aja, “Lamulo limene Yehova anapereka kwa Mose ndi ili:
Eleazar the priest told the soldiers who had gone into battle, “These are the legal regulations that the Lord has ordered Moses to be carried out:
22 Golide, siliva, mkuwa, chitsulo, chiwaya, mtovu
All that's made of gold, silver, bronze, iron, tin, and lead—
23 ndi china chilichonse chimene sichingapse ndi moto muchidutsitse pa moto, ndipo chidzayeretsedwa. Komanso chiyeretsedwe ndi madzi oyeretsa. Ndipo chilichonse chimene chingapse ndi moto muchidutsitse mʼmadzimo.
anything that doesn't burn—must be put through fire to make it clean. But it still has to be purified using water of purification. Anything that burns must be put through the water.
24 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muchape zovala zanu ndipo mudzayera. Mukatero mutha kulowa mu msasa.”
Wash your clothes on the seventh day and you will be clean. Then you can enter the camp.”
25 Yehova anawuza Mose kuti,
The Lord told Moses,
26 “Iwe ndi wansembe Eliezara ndiponso akuluakulu a mabanja a anthuwa, muwerenge anthu onse ndi ziweto zomwe zinagwidwa ku nkhondo.
“You, Eleazar the priest, and the Israelite family leaders are to take a record of the people and animals that were captured.
27 Mugawe zolanda ku nkhondozo magawo awiri, lina la ankhondo amene anapita ku nkhondo, lina la anthu onse.
Then divide them between the troops who went into battle and the rest of the Israelites.
28 Pa gawo la ankhondowo, mutengeko gawo la Yehova, pa zofunkha 500 zilizonse mutengeko chimodzi, pa akapolo, ngʼombe, bulu ndi nkhosa.
Take as a contribution to the Lord from what is allocated to the troops who went into battle one out of every five hundred people, cattle, donkeys, or sheep.
29 Utenge zimenezo pa theka la gawo la ankhondowo ndipo upereke kwa wansembe Eliezara kuti zikhale zopereka zanu kwa Yehova.
Take this from their half share and give it to Eleazar the priest as an offering to the Lord.
30 Kuchokera pa theka la gawo la Aisraeli, utengeko cholanda chimodzi pa makumi asanu aliwonse, pa anthu, ngʼombe, abulu, nkhosa, mbuzi kapena zoweta zina. Uzipereke kwa Alevi amene ntchito yawo ndi yosamalira tenti ya Yehova.”
From the Israelites; half share, take one out of every fifty people, cattle, donkeys, or sheep, or other animals, and give them to the Levites who take care of the Lord's Tabernacle.”
31 Ndipo Mose ndi wansembe Eliezara anachita monga Yehova analamulira Mose.
Moses and Eleazar the priest did as the Lord had ordered Moses.
32 Zotsala pa zolanda ku nkhondo zimene ankhondowo anatenga zinali nkhosa 675,000,
This was the list of plunder remaining that had been looted by the troops: 675,000 sheep,
33 Ngʼombe 72,000,
72,000 cattle,
34 abulu 61,000,
61,000 donkeys,
35 ndi atsikana omwe sanagonepo ndi mwamuna 32,000.
and 32,000 virgins.
36 Gawo la ankhondo amene anapita ku nkhondo linali: nkhosa 337,500,
This was the half share for those who had gone to fight: 337,500 sheep,
37 mwa zimenezi gawo la Yehova linali 675;
with a contribution for the Lord of 675,
38 ngʼombe zinalipo 36,000 ndipo gawo la Yehova linali 72;
36,000 cattle, with a Lord's contribution of 72,
39 abulu analipo 30,500 ndipo gawo la Yehova linali 61;
30,500 donkeys, with a Lord's contribution of 61,
40 anthu analipo 16,000 ndipo gawo la Yehova linali 32.
and 16,000 people, with a Lord's contribution of 32.
41 Mose anapereka kwa wansembe Eliezara gawo limene linali loyenera kupereka kwa Yehova monga momwe Yehova analamulira Mose.
Moses gave the contribution to Eleazar the priest as an offering to the Lord as the Lord had ordered Moses.
42 Pa gawo la Aisraeli, Mose anapatula theka limodzi kuchotsa pa zolanda ku nkhondo zonse zimene zinabwera ndi ankhondo aja.
The Israelites' half share left after Moses had given the half share to the troops who had gone to fight,
43 Tsono gawo la Aisraeli linali ili: nkhosa 337,500,
consisted of: 337,500 sheep,
44 ngʼombe 36,000,
36,000 cattle,
45 abulu 30,500,
30,500 donkeys,
46 anthu 16,000.
and 16,000 people.
47 Kuchoka pa gawo la Aisraelilo, Mose anatengapo chimodzi pa zolanda ku nkhondo makumi asanu aliwonse, anthu ndi nyama, ndipo anazipereka kwa Alevi amene ankayangʼanira tenti ya Yehova monga Yehova analamulira Mose.
Moses took from the Israelites' half one out of every fifty people and animals and gave them the Levites who take care of the Lord's Tabernacle, as the Lord had ordered him.
48 Pamenepo omwe ankayangʼanira magulu a ankhondo olamulira 1,000 ndi olamulira 100 anabwera kwa Mose,
The army officers, the commanders of thousands and commanders of hundreds, came to Moses
49 iwo anati kwa iye, “Ife anthu anu tawerenga ankhondo amene timawalamulira. Palibe munthu ndi mmodzi yemwe amene wasowa.
and told him, “We, your servants, have checked the troops we command and not a single man is missing.
50 Ndipo tabweretsa zopereka kwa Yehova zimene munthu aliyense anapeza: ziwiya zagolide, zibangiri, zigwinjiri, mphete zosindikizira, ndolo ndi mikanda kuti tichitire mwambo wopepesera machimo pamaso pa Yehova.”
So we have brought the Lord an offering of the gold objects each man received—armlets, bracelets, rings, earrings, and necklaces—in order that we may be right before the Lord.”
51 Ndipo Mose ndi wansembe Eliezara analandira kuchokera kwa atsogoleriwo golide pamodzi ndi zipangizo zonse zosula.
Moses and Eleazar the priest accepted from them all the objects made out of gold.
52 Golide yense wochokera kwa atsogoleri a 1,000 ndi atsogoleri a 100 zomwe Mose ndi Eliezara anapereka ngati mphatso kwa Yehova zinali zolemera makilogalamu 200.
The gold that the commanders of thousands and of hundreds gave as an offering to the Lord weighed in total 16,750 shekels.
53 Wankhondo aliyense anatenga zomwe analanda yekha ku nkhondo.
(The men who had fought in the battle had each taken plunder for himself.)
54 Mose ndi Eliezara wansembe analandira golide kuchokera kwa atsogoleri a 1,000 ndi atsogoleri a 100 ndi kukamuyika mu tenti ya msonkhano ngati chikumbutso cha Aisraeli pamaso pa Yehova.
Moses and Eleazar the priest accepted the gold from the commanders of thousands and of hundreds and took it into the Tent of Meeting as a memorial offering for the Israelites in the presence of the Lord.

< Numeri 31 >