< Numeri 30 >
1 Mose anawuza Aisraeli onse zonse zimene Yehova anamulamula. Iye anati, “Zimene Yehova walamula ndi izi:
and to speak: speak Moses to(wards) head: leader [the] tribe to/for son: descendant/people Israel to/for to say this [the] word which to command LORD
2 Munthu wamwamuna ngati walonjeza kwa Yehova kapena kulumbira kuti adzachita zimene walumbirazo, asaphwanye mawuwo koma ayenera kuchita chilichonse chimene wanena.
man for to vow vow to/for LORD or to swear oath to/for to bind injunction upon soul: myself his not to profane/begin: profane word his like/as all [the] to come out: speak from lip his to make: do
3 “Pamene munthu wamkazi amene akukhalabe mʼnyumba ya abambo ake alumbira kwa Yehova kuti adzachita zimene walonjeza pa ubwana wake,
and woman for to vow vow to/for LORD and to bind injunction in/on/with house: household father her in/on/with youth her
4 abambo ake namva kulumbira kwakeko kapena kulonjeza kwake kuti adzachitadi, ndipo abambo akewo wosayankhula kanthu, mkaziyo achitedi zomwe analumbirazo. Ayenera kudzachita zonse zimene walonjeza zija.
and to hear: hear father her [obj] vow her and injunction her which to bind upon soul: myself her and be quiet to/for her father her and to arise: establish all vow her and all injunction which to bind upon soul: myself her to arise: establish
5 Koma ngati abambo akewo amva kulumbira kwake ndi kumukaniza, palibe lamulo lomukakamiza mkaziyo kuchita zimene walonjeza. Yehova adzamukhululukira chifukwa abambo ake anamukaniza.
and if to forbid father her [obj] her in/on/with day to hear: hear he all vow her and injunction her which to bind upon soul: myself her not to arise: establish and LORD to forgive to/for her for to forbid father her [obj] her
6 “Ngati akwatiwa atalumbira kale kapena ngati alonjeza mofulumira ndi pakamwa pake,
and if to be to be to/for man: husband and vow her upon her or rash word lips her which to bind upon soul: myself her
7 mwamuna wake ndi kumva kulumbira kwakeko koma wosanenapo kanthu, mkaziyo achitedi zomwe walumbirazo. Achite ndithu zomwe walonjeza zija.
and to hear: hear man: husband her in/on/with day to hear: hear he and be quiet to/for her and to arise: establish vow her and injunction her which to bind upon soul: myself her to arise: establish
8 Koma ngati mwamuna wake amuletsa atamva kulumbira kwakeko, pamenepo amumasula mayiyo ku zimene analumbira komanso ku zimene analonjeza mosaganiza bwinozo ndipo Yehova adzamukhululukira.
and if in/on/with day to hear: hear man: husband her to forbid [obj] her and to break [obj] vow her which upon her and [obj] rash word lips her which to bind upon soul: myself her and LORD to forgive to/for her
9 “Mayi wamasiye kapena wosiyidwa ukwati akalumbira kapena kulonjeza kuti adzachita kanthu kalikonse, ayenera kukachitadi.
and vow widow and to drive out: divorce all which to bind upon soul: myself her to arise: establish upon her
10 “Koma ngati mayi wokwatiwa alumbira nalonjeza kuti adzachitadi zimene walonjeza,
and if house: household man: husband her to vow or to bind injunction upon soul: myself her in/on/with oath
11 mwamuna wake ndi kumva kulumbira kwakeko koma osayankhulapo kanthu, osamuletsa, ayenera kuchitadi zonse zimene walumbira ndi zonse zimene walonjeza.
and to hear: hear man: husband her and be quiet to/for her not to forbid [obj] her and to arise: establish all vow her and all injunction which to bind upon soul: myself her to arise: establish
12 Koma ngati mwamuna wake amva ndi kumuletsa kuti asachite zomwe walumbirazo, palibe lamulo lomukakamiza mayiyo kuchita zomwe walumbirazo kapenanso zimene walonjeza. Popeza mwamuna wake wamuletsa, Yehova adzamukhululukira mayiyo.
and if to break to break [obj] them man: husband her in/on/with day to hear: hear he all exit lips her to/for vow her and to/for injunction soul: myself her not to arise: establish man: husband her to break them and LORD to forgive to/for her
13 Mwamuna wake ali ndi mphamvu zovomereza kapena kukana zimene mayiyo walumbira kapena zimene walonjeza zokhudza kudzilanga yekha.
all vow and all oath injunction to/for to afflict soul: myself man: husband her to arise: establish him and man: husband her to break him
14 Ndipo ngati mmawa mwake ndi masiku otsatira mwamuna wake sanenapo kanthu atamva zimenezi, mayiyo achitedi zimene walumbira kapena zimene walonjeza. Mwamunayo wavomereza zimenezo, chifukwa sanamuwuze kanthu mayiyo pa tsiku limene anamva akulonjeza kapena kulumbira.
and if be quiet be quiet to/for her man: husband her from day to(wards) day and to arise: establish [obj] all vow her or [obj] all injunction her which upon her to arise: establish [obj] them for be quiet to/for her in/on/with day to hear: hear he
15 Koma ngati mwamunayo amukaniza patapita kanthawi atazimva kale, iyeyo ndiye wochimwa mʼmalo mwa mayiyo.”
and if to break to break [obj] them after to hear: hear he and to lift: guilt [obj] iniquity: crime her
16 Awa ndiwo malamulo amene Yehova analamula Mose za mwamuna ndi mkazi wake, ndiponso abambo ndi mwana wawo wamkazi amene akanali mtsikana wokhalabe mʼnyumba ya abambo akewo.
these [the] statute: decree which to command LORD [obj] Moses between man to/for woman: wife his between father to/for daughter his in/on/with youth her house: household father her