< Numeri 3 >
1 Iyi ndi mbiri ya banja la Aaroni ndi Mose pa nthawi yomwe Yehova anayankhula ndi Mose pa phiri la Sinai.
Lezi yizizukulwane zika-Aroni lezikaMosi ngesikhathi sokukhuluma kukaThixo kuMosi entabeni yaseSinayi.
2 Mayina a ana aamuna a Aaroni anali Nadabu, woyamba kubadwa, Abihu, Eliezara ndi Itamara.
Amabizo amadodana ka-Aroni kwakunguNadabi izibulo lo-Abhihu, u-Eliyazari kanye lo-Ithamari.
3 Amenewa ndi mayina a ana aamuna a Aaroni, ansembe odzozedwa omwe anapatulidwa kuti azitumikira ngati ansembe.
La ngamabizo amadodana ka-Aroni, agcotshwayo abekwa ukuba ngabaphristi.
4 Koma Nadabu ndi Abihu, anagwa nafa pamaso pa Yehova pamene ankapereka nsembe ndi moto wachilendo pamaso pa Yehova mʼchipululu cha Sinai. Iwowo analibe ana aamuna. Choncho Eliezara ndi Itamara ndiwo amene ankatumikira ngati ansembe nthawi imene Aaroni abambo awo anali moyo.
Kodwa, uNadabi lo-Abhihu bafa phambi kukaThixo ngenxa yokunikela ngomlilo ongemukelekiyo kuThixo enkangala yaseSinayi. Babengelamadodana; kungakho u-Eliyazari lo-Ithamari babangabaphristi ngesikhathi uyise u-Aroni esaphila.
6 “Bweretsa fuko la Levi ndipo ulipereke kwa Aaroni wansembe kuti lizimutumikira.
“Letha abesizwe sikaLevi ubethule ku-Aroni umphristi ukuze bamncedise.
7 Azigwira ntchito yothandiza iyeyo ndi gulu lonse ku tenti ya msonkhano pogwira ntchito ya ku Chihema.
Bazamsebenzela yena kanye lesizwana sonke ethenteni lokuhlangana beqhuba umsebenzi wethabanikeli.
8 Azisamalira zipangizo zonse za mu tenti ya msonkhano, ndipo azigwirira ntchito Aisraeli potumikira mu tenti.
Bazalondoloza yonke impahla yethente lokuhlangana, benzele abako-Israyeli imisebenzi nxa besenza inkonzo ethabanikeleni.
9 Pereka Alevi kwa Aaroni ndi kwa ana ake aamuna. Amenewa ndiwo Aisraeli amene aperekedwa kwa iye kwathunthu.
Yethula abaLevi ku-Aroni lakumadodana akhe; bangabako-Israyeli okumele bethulwe ngokugcweleyo kuye.
10 Usankhe Aaroni ndi ana ake aamuna kuti azitumikira pa ntchito ya unsembe. Koma wina aliyense woyandikira malo opatulika aphedwe.”
Khetha u-Aroni lamadodana akhe ukuthi babe ngabaphristi; loba ngubani omunye ozasondela endaweni engcwele kumele abulawe.”
11 Yehova anawuzanso Mose kuti,
UThixo waphinda wathi kuMosi,
12 “Pakati pa Aisraeli onse ndatenga Alevi kulowa mʼmalo mwa mwana wamwamuna aliyense woyamba kubadwa kwa amayi a Chiisraeli. Alevi ndi anga,
“AbaLevi sengibakhetha phakathi kwabako-Israyeli esikhundleni samazibulo angabafana esizweni sonke sako-Israyeli. AbaLevi ngabami,
13 pakuti ana onse oyamba kubadwa ndi anga. Nditakantha ana onse oyamba kubadwa mu Igupto, ndinadzipatulira ndekha mwana aliyense woyamba kubadwa mu Israeli, wa munthu ndi nyama. Azikhala anga. Ine ndine Yehova.”
njengoba wonke amazibulo engawami. Ekubulaleni kwami wonke amazibulo aseGibhithe, ngazehlukanisela wonke amazibulo ako-Israyeli, awabantu loba awezinyamazana. Kumele abe ngawami. Mina nginguThixo.”
14 Yehova anawuza Mose mʼchipululu cha Sinai kuti,
UThixo wathi kuMosi eNkangala yaseSinayi,
15 “Werenga Alevi monga mwa mabanja awo ndi mafuko awo. Werenga mwamuna aliyense kuyambira wa mwezi umodzi kapena kupitirirapo.”
“Bala abaLevi ngezindlu zabo langosendo lwabo. Bala bonke abesilisa kusukela kwabalenyanga eyodwa bezelwe kusiya phezulu.”
16 Choncho Mose anawawerenga potsatira zomwe Yehova anamulamulira.
Ngakho uMosi wababala, njengokulaywa kwakhe yilizwi likaThixo.
17 Mayina a ana aamuna a Levi ndi awa: Geresoni, Kohati ndi Merari.
La ngamabizo amadodana kaLevi: uGeshoni, uKhohathi kanye loMerari.
18 Mayina a ana a Geresoni potsata mabanja awo ndi awa: Libini ndi Simei.
La ngamabizo abosendo lukaGeshoni: uLibhini loShimeyi.
19 Ana a Kohati potsata mabanja awo ndi awa: Amramu, Izihari, Hebroni ndi Uzieli.
Abosendo lukaKhohathi babeyilaba: u-Amramu, u-Izihari, uHebhroni kanye lo-Uziyeli.
20 Ana a Merari potsata mabanja awo ndi awa: Mali ndi Musi. Amenewa ndiwo anali mabanja a Alevi monga mwa makolo awo.
Abosendo lukaMerari babeyilaba: uMahili loMushi. Laba kwakungabosendo lwabaLevi, kusiya ngezindlu zabo.
21 Kwa Geresoni kunali banja la Alibini, banja la Asimei. Amenewa ndiwo anali mabanja a Ageresoni.
KuGeshoni kwavela usendo lwamaLibhini lolwamaShimeyi; laba yibo abosendo lwamaGeshoni.
22 Chiwerengero cha amuna onse amene anawawerenga a mwezi umodzi kapena kupitirirapo chinali 7,500.
Inani lamadoda wonke kusukela kwabalenyanga eyodwa bezelwe kusiya phezulu ababalwayo babezinkulungwane eziyisikhombisa lamakhulu amahlanu.
23 Mabanja a Ageresoni azimanga misasa yawo kumadzulo, kumbuyo kwa Chihema.
Abosendo lwamaGeshoni babezahlala ezihonqweni zabo entshonalanga, ngemuva kwethabanikeli.
24 Mtsogoleri wa mabanja a Ageresoni anali Eliyasafu mwana wa Laeli.
Umkhokheli wabezindlu zabakoGeshoni kwakungu-Eliyasafi indodana kaLayeli.
25 Ntchito imene Ageresoni anapatsidwa ku tenti ya msonkhano inali yosamalira Chihema ndi tenti, pamodzi ndi zophimbira zake, katani ya pa khomo la ku tenti ya msonkhano,
Umsebenzi wamadodana kaGeshoni ethenteni lokuhlangana wawungowokulondoloza ithabanikeli, ithente, isembeso salo, ikhetheni lesango lethente lokuhlangana,
26 ndi makatani wotchinga bwalo, katani ya pa chipata cholowera ku bwalo lozungulira Chihema ndi guwa lansembe, zingwe ndi zonse zokhudzana ndi ntchito yawo.
amakhetheni eguma, ikhetheni lesango leguma elihonqolozele ithabanikeli kanye le-alithari, lamagoda, lakho konke okuphathelane lalowo msebenzi.
27 Kwa Kohati kunali mabanja a Amramu, Aizihara, Ahebroni ndi Auzieli. Awa ndiye anali mabanja a Akohati.
Abosendo lukaKhohathi kwakungama-Amramu, ama-Izihari, amaHebhroni kanye lama-Uziyeli. Laba yibo abosendo lwamaKhohathi.
28 Chiwerengero cha amuna onse a mwezi umodzi kapena kupitirirapo chinali 8,600. Akohati ankagwira ntchito yosamalira malo wopatulika.
Inani lamadoda wonke kusukela kwabalenyanga eyodwa bezelwe kusiya phezulu babezinkulungwane eziyisificaminwembili lamakhulu ayisithupha. AmaKhohathi yiwo ayelomlandu wokugcina indawo engcwele.
29 Mabanja a ana a Kohati ankamanga misasa yawo kummwera kwa Chihema.
Abosendo lwamaKhohathi bahlala ezihonqweni zabo eningizimu yethabanikeli.
30 Mtsogoleri wa magulu a mabanja a Kohati anali Elizafani mwana wa Uzieli.
Umkhokheli wabezindlu zabosendo lwamaKhohathi kwakungu-Elizafani indodana ka-Uziyeli.
31 Iwo ankagwira ntchito yosamalira Bokosi la Chipangano, tebulo, choyikapo nyale, maguwa, zipangizo za kumalo wopatulika zimene ansembe ankagwiritsa ntchito, katani, ndi zonse zomwe ankagwiritsa ntchito.
Babelomlandu wokugcina umtshokotsho wesivumelwano, itafula, uluthi lwezibane, ama-alithare, impahla zendawo engcwele ezazisetshenziswa emsebenzini wokukhonza.
32 Mtsogoleri wamkulu wa Alevi anali Eliezara mwana wa Aaroni wansembe. Iye anasankhidwa kukhala woyangʼanira omwe ankasamalira malo wopatulika.
U-Eliyazari indodana ka-Aroni, umphristi, wayengumkhokheli omkhulu wabaLevi. Wabekwa phezu kwalabo ababelomlandu wokugcina indawo engcwele.
33 Kwa Merari kunali banja la Mali ndi banja la Musi. Amenewa ndiye anali mabanja a Amerari.
Abosendo lukaMerari kwakungamaMahili lamaMushi; laba babengabosendo lwamaMerari.
34 Chiwerengero cha amuna onse kuyambira a mwezi umodzi kapena kupitirirapo chinali 6,200.
Inani lamadoda asukela kwabalenyanga eyodwa bezelwe kusiya phezulu ababalwayo babezinkulungwane eziyisithupha lamakhulu amabili.
35 Mtsogoleri wa magulu a mabanja a Amerari anali Zuriyeli mwana wa Abihaili. Iwo ankamanga misasa yawo kumpoto kwa Chihema.
Umkhokheli wezindlu zosendo lwamaMerari kwakunguZuriyeli indodana ka-Abhihayili; babezahlala ezihonqweni zabo enyakatho yethabanikeli.
36 Amerari anapatsidwa ntchito yosamalira mitengo ya chihema, nsichi zake, mizati yake, matsinde ake, ndi zida zake zonse, ndi zonse zomwe ankagwiritsa ntchito,
Abosendo lwamaMerari babelomlandu wokugcina amathala ethabanikeli, imithando, izinsika, izisekelo, izitsha zalo zonke lakho konke okuphathelane lemisebenzi yakho,
37 pamodzi ndi mizati yozungulira bwalo ndi matsinde ake, zikhomo za chihema ndi zingwe zake.
kanye lezinsika lezisekelo zazo ezihonqolozele iguma, izikhonkwane zethente kanye lamagoda.
38 Mose ndi Aaroni ndi ana ake aamuna ankamanga misasa yawo kummawa kwa chihema, kuyangʼana kotulukira dzuwa, kutsogolo kwa tenti ya msonkhano. Anali ndi ntchito yosamalira malo wopatulika mʼmalo mwa Aisraeli. Aliyense woyandikira malo wopatulika ankayenera kuphedwa.
UMosi kanye lo-Aroni lamadodana akhe babezahlala ezihonqweni zabo empumalanga yethabanikeli, phambi kwethente lokuhlangana. Babelomlandu wokugcinela abako-Israyeli indawo engcwele. Loba ngubani omunye owayezasondela endaweni engcwele kwakumele abulawe.
39 Alevi onse amene Mose ndi Aaroni anawawerenga potsatira lamulo la Yehova monga mwa magulu a mabanja awo, amuna onse kuyambira a mwezi umodzi kapena kupitirirapo anali 22,000.
Inani labaLevi bonke ababalwayo njengokulaywa kukaMosi lo-Aroni nguThixo kulandelwa insendo zawo, kusukela kwabesilisa ababelenyanga eyodwa yokuzalwa kusiya phezulu, babezinkulungwane ezingamatshumi amabili lambili.
40 Yehova anawuza Mose kuti, “Werenga ana onse aamuna oyamba kubadwa mu Israeli, omwe ali ndi mwezi umodzi kapena kupitirirapo ndipo ulembe mndandanda wa mayina awo.
UThixo wathi kuMosi, “Bala wonke amazibulo esilisa ako-Israyeli kusukela kwabalenyanga eyodwa bezelwe kusiya phezulu wenze uluhlu lwamabizo abo.
41 Unditengere Alevi onse mʼmalo mwa ana oyamba kubadwa onse a Aisraeli, ndiponso ziweto zazimuna za Alevi mʼmalo mwa ziweto zonse zazimuna zoyamba kubadwa za Aisraeli. Ine ndine Yehova.”
Esikhundleni samabizo ako-Israyeli nginika abaLevi, njalo lezifuyo zabaLevi esikhundleni samazibulo ezifuyo zabako-Israyeli. Mina nginguThixo.”
42 Choncho Mose anawerenga ana aamuna onse oyamba kubadwa a Aisraeli monga momwe Yehova anamulamulira.
Ngalokho-ke uMosi wabala wonke amazibulo abako-Israyeli, njengokulaywa kwakhe nguThixo.
43 Chiwerengero chonse cha ana aamuna oyamba kubadwa kuyambira a mwezi umodzi kapena kupitirirapo chinali 22, 273.
Inani lawo wonke amazibulo esilisa kusukela kwalenyanga eyodwa yokuzalwa kusiya phezulu, ebhalwe ngoluhlu lwamabizo, ayezinkulungwane ezingamatshumi amabili lambili, lamakhulu amabili alamatshumi ayisikhombisa lantathu.
44 Ndipo Yehova anawuzanso Mose kuti,
UThixo wabuya wathi kuMosi,
45 “Tenga Alevi mʼmalo mwa ana aamuna oyamba kubadwa onse a Aisraeli, ndiponso zoweta zonse za Alevi mʼmalo mwa zoweta za Aisraeli. Alevi ndi anga. Ine ndine Yehova.
“Esikhundleni samazibulo ako-Israyeli thatha abaLevi, lezifuyo zabaLevi esikhundleni sezifuyo zabo. AbaLevi kumele babengabami. Mina nginguThixo.
46 Pofuna kuwombola ana aamuna 273 oyamba kubadwa a Aisraeli amene anaposa chiwerengero cha aamuna a fuko la Levi,
Ukuhlenga amazibulo ako-Israyeli angamakhulu amabili alamatshumi ayisikhombisa lantathu abangaphezu kwenani labaLevi,
47 utenge masekeli asanu pa munthu aliyense. Masekeliwo akhale ofanana ndi masekeli a ku malo wopatulika, kumene sekeli imodzi imakwanira magera makumi awiri.
thatha amashekeli amahlanu omunye ngamunye wabo, kusiya ngeshekeli lendawo engcwele, elilesisindo samagera angamatshumi amabili.
48 Ndalama zimenezi uzipereke kwa Aaroni ndi ana ake aamuna kuti ukhale mtengo woombolera Aisraeli woonjezerawo.”
Imali yokuhlenga abako-Israyeli abangaphezu kwenani uyiphe u-Aroni lamadodana akhe.”
49 Choncho Mose anatenga ndalama zowombolera zija kuchokera kwa Aisraeli amene chiwerengero chawo chinaposa chiwerengero cha omwe anawomboledwa ndi Alevi.
Lakanye uMosi wayibutha imali yokuhlenga labo ababelinani eledlula kwabahlengwa ngabaLevi.
50 Anatenga masekeli a siliva okwana 1,365 molingana ndi masekeli a ku malo opatulika, kuchokera kwa ana aamuna oyamba kubadwa a Aisraeli.
Wamukela kuvela emazibulweni abako-Israyeli isiliva esingamashekeli ayinkulungwane elamakhulu amathathu lamatshumi ayisithupha lanhlanu ngesilinganiso seshekeli lendawo engcwele.
51 Mose anapereka ndalama zowombolera zija kwa Aaroni ndi ana ake aamuna monga mwa mawu amene Yehova analamulira.
UMosi waqhubela u-Aroni lamadodana akhe imali yokuhlenga, njengokulaywa kwakhe nguThixo.