< Numeri 3 >

1 Iyi ndi mbiri ya banja la Aaroni ndi Mose pa nthawi yomwe Yehova anayankhula ndi Mose pa phiri la Sinai.
Voici la postérité d’Aaron et de Moïse, au temps où l’Éternel parla à Moïse, sur la montagne de Sinaï.
2 Mayina a ana aamuna a Aaroni anali Nadabu, woyamba kubadwa, Abihu, Eliezara ndi Itamara.
Voici les noms des fils d’Aaron: Nadab, le premier-né, Abihu, Éléazar et Ithamar.
3 Amenewa ndi mayina a ana aamuna a Aaroni, ansembe odzozedwa omwe anapatulidwa kuti azitumikira ngati ansembe.
Ce sont là les noms des fils d’Aaron, qui reçurent l’onction comme sacrificateurs, et qui furent consacrés pour l’exercice du sacerdoce.
4 Koma Nadabu ndi Abihu, anagwa nafa pamaso pa Yehova pamene ankapereka nsembe ndi moto wachilendo pamaso pa Yehova mʼchipululu cha Sinai. Iwowo analibe ana aamuna. Choncho Eliezara ndi Itamara ndiwo amene ankatumikira ngati ansembe nthawi imene Aaroni abambo awo anali moyo.
Nadab et Abihu moururent devant l’Éternel, lorsqu’ils apportèrent devant l’Éternel du feu étranger, dans le désert de Sinaï; ils n’avaient point de fils. Éléazar et Ithamar exercèrent le sacerdoce, en présence d’Aaron, leur père.
5 Yehova anati kwa Mose,
L’Éternel parla à Moïse, et dit:
6 “Bweretsa fuko la Levi ndipo ulipereke kwa Aaroni wansembe kuti lizimutumikira.
Fais approcher la tribu de Lévi, et tu la placeras devant le sacrificateur Aaron, pour qu’elle soit à son service.
7 Azigwira ntchito yothandiza iyeyo ndi gulu lonse ku tenti ya msonkhano pogwira ntchito ya ku Chihema.
Ils auront le soin de ce qui est remis à sa garde et à la garde de toute l’assemblée, devant la tente d’assignation: ils feront le service du tabernacle.
8 Azisamalira zipangizo zonse za mu tenti ya msonkhano, ndipo azigwirira ntchito Aisraeli potumikira mu tenti.
Ils auront le soin de tous les ustensiles de la tente d’assignation, et de ce qui est remis à la garde des enfants d’Israël: ils feront le service du tabernacle.
9 Pereka Alevi kwa Aaroni ndi kwa ana ake aamuna. Amenewa ndiwo Aisraeli amene aperekedwa kwa iye kwathunthu.
Tu donneras les Lévites à Aaron et à ses fils; ils lui seront entièrement donnés, de la part des enfants d’Israël.
10 Usankhe Aaroni ndi ana ake aamuna kuti azitumikira pa ntchito ya unsembe. Koma wina aliyense woyandikira malo opatulika aphedwe.”
Tu établiras Aaron et ses fils pour qu’ils observent les fonctions de leur sacerdoce; et l’étranger qui approchera sera puni de mort.
11 Yehova anawuzanso Mose kuti,
L’Éternel parla à Moïse, et dit:
12 “Pakati pa Aisraeli onse ndatenga Alevi kulowa mʼmalo mwa mwana wamwamuna aliyense woyamba kubadwa kwa amayi a Chiisraeli. Alevi ndi anga,
Voici, j’ai pris les Lévites du milieu des enfants d’Israël, à la place de tous les premiers-nés, des premiers-nés des enfants d’Israël; et les Lévites m’appartiendront.
13 pakuti ana onse oyamba kubadwa ndi anga. Nditakantha ana onse oyamba kubadwa mu Igupto, ndinadzipatulira ndekha mwana aliyense woyamba kubadwa mu Israeli, wa munthu ndi nyama. Azikhala anga. Ine ndine Yehova.”
Car tout premier-né m’appartient; le jour où j’ai frappé tous les premiers-nés dans le pays d’Égypte, je me suis consacré tous les premiers-nés en Israël, tant des hommes que des animaux: ils m’appartiendront. Je suis l’Éternel.
14 Yehova anawuza Mose mʼchipululu cha Sinai kuti,
L’Éternel parla à Moïse, dans le désert de Sinaï, et dit:
15 “Werenga Alevi monga mwa mabanja awo ndi mafuko awo. Werenga mwamuna aliyense kuyambira wa mwezi umodzi kapena kupitirirapo.”
Fais le dénombrement des enfants de Lévi, selon les maisons de leurs pères, selon leurs familles; tu feras le dénombrement de tous les mâles, depuis l’âge d’un mois et au-dessus.
16 Choncho Mose anawawerenga potsatira zomwe Yehova anamulamulira.
Moïse en fit le dénombrement sur l’ordre de l’Éternel, en se conformant à l’ordre qui lui fut donné.
17 Mayina a ana aamuna a Levi ndi awa: Geresoni, Kohati ndi Merari.
Ce sont ici les fils de Lévi, d’après leurs noms: Guerschon, Kehath et Merari.
18 Mayina a ana a Geresoni potsata mabanja awo ndi awa: Libini ndi Simei.
Voici les noms des fils de Guerschon, selon leurs familles: Libni et Schimeï.
19 Ana a Kohati potsata mabanja awo ndi awa: Amramu, Izihari, Hebroni ndi Uzieli.
Voici les fils de Kehath, selon leurs familles: Amram, Jitsehar, Hébron et Uziel;
20 Ana a Merari potsata mabanja awo ndi awa: Mali ndi Musi. Amenewa ndiwo anali mabanja a Alevi monga mwa makolo awo.
et les fils de Merari, selon leurs familles: Machli et Muschi. Ce sont là les familles de Lévi, selon les maisons de leurs pères.
21 Kwa Geresoni kunali banja la Alibini, banja la Asimei. Amenewa ndiwo anali mabanja a Ageresoni.
De Guerschon descendent la famille de Libni et la famille de Schimeï, formant les familles des Guerschonites.
22 Chiwerengero cha amuna onse amene anawawerenga a mwezi umodzi kapena kupitirirapo chinali 7,500.
Ceux dont on fit le dénombrement, en comptant tous les mâles depuis l’âge d’un mois et au-dessus, furent sept mille cinq cents.
23 Mabanja a Ageresoni azimanga misasa yawo kumadzulo, kumbuyo kwa Chihema.
Les familles des Guerschonites campaient derrière le tabernacle à l’occident.
24 Mtsogoleri wa mabanja a Ageresoni anali Eliyasafu mwana wa Laeli.
Le chef de la maison paternelle des Guerschonites était Éliasaph, fils de Laël.
25 Ntchito imene Ageresoni anapatsidwa ku tenti ya msonkhano inali yosamalira Chihema ndi tenti, pamodzi ndi zophimbira zake, katani ya pa khomo la ku tenti ya msonkhano,
Pour ce qui concerne la tente d’assignation, on remit aux soins des fils de Guerschon le tabernacle et la tente, la couverture, le rideau qui est à l’entrée de la tente d’assignation;
26 ndi makatani wotchinga bwalo, katani ya pa chipata cholowera ku bwalo lozungulira Chihema ndi guwa lansembe, zingwe ndi zonse zokhudzana ndi ntchito yawo.
les toiles du parvis et le rideau de l’entrée du parvis, tout autour du tabernacle et de l’autel, et tous les cordages pour le service du tabernacle.
27 Kwa Kohati kunali mabanja a Amramu, Aizihara, Ahebroni ndi Auzieli. Awa ndiye anali mabanja a Akohati.
De Kehath descendent la famille des Amramites, la famille des Jitseharites, la famille des Hébronites et la famille des Uziélites, formant les familles des Kehathites.
28 Chiwerengero cha amuna onse a mwezi umodzi kapena kupitirirapo chinali 8,600. Akohati ankagwira ntchito yosamalira malo wopatulika.
En comptant tous les mâles depuis l’âge d’un mois et au-dessus, il y en eut huit mille six cents, qui furent chargés des soins du sanctuaire.
29 Mabanja a ana a Kohati ankamanga misasa yawo kummwera kwa Chihema.
Les familles des fils de Kehath campaient au côté méridional du tabernacle.
30 Mtsogoleri wa magulu a mabanja a Kohati anali Elizafani mwana wa Uzieli.
Le chef de la maison paternelle des familles des Kehathites était Élitsaphan, fils d’Uziel.
31 Iwo ankagwira ntchito yosamalira Bokosi la Chipangano, tebulo, choyikapo nyale, maguwa, zipangizo za kumalo wopatulika zimene ansembe ankagwiritsa ntchito, katani, ndi zonse zomwe ankagwiritsa ntchito.
On remit à leurs soins l’arche, la table, le chandelier, les autels, les ustensiles du sanctuaire, avec lesquels on fait le service, le voile et tout ce qui en dépend.
32 Mtsogoleri wamkulu wa Alevi anali Eliezara mwana wa Aaroni wansembe. Iye anasankhidwa kukhala woyangʼanira omwe ankasamalira malo wopatulika.
Le chef des chefs des Lévites était Éléazar, fils du sacrificateur Aaron; il avait la surveillance de ceux qui étaient chargés des soins du sanctuaire.
33 Kwa Merari kunali banja la Mali ndi banja la Musi. Amenewa ndiye anali mabanja a Amerari.
De Merari descendent la famille de Machli et la famille de Muschi, formant les familles des Merarites.
34 Chiwerengero cha amuna onse kuyambira a mwezi umodzi kapena kupitirirapo chinali 6,200.
Ceux dont on fit le dénombrement, en comptant tous les mâles depuis l’âge d’un mois et au-dessus, furent six mille deux cents.
35 Mtsogoleri wa magulu a mabanja a Amerari anali Zuriyeli mwana wa Abihaili. Iwo ankamanga misasa yawo kumpoto kwa Chihema.
Le chef de la maison paternelle des familles de Merari était Tsuriel, fils d’Abihaïl. Ils campaient du côté septentrional du tabernacle.
36 Amerari anapatsidwa ntchito yosamalira mitengo ya chihema, nsichi zake, mizati yake, matsinde ake, ndi zida zake zonse, ndi zonse zomwe ankagwiritsa ntchito,
On remit à la garde et aux soins des fils de Merari les planches du tabernacle, ses barres, ses colonnes et leurs bases, tous ses ustensiles et tout ce qui en dépend;
37 pamodzi ndi mizati yozungulira bwalo ndi matsinde ake, zikhomo za chihema ndi zingwe zake.
les colonnes du parvis tout autour, leurs bases, leurs pieux et leurs cordages.
38 Mose ndi Aaroni ndi ana ake aamuna ankamanga misasa yawo kummawa kwa chihema, kuyangʼana kotulukira dzuwa, kutsogolo kwa tenti ya msonkhano. Anali ndi ntchito yosamalira malo wopatulika mʼmalo mwa Aisraeli. Aliyense woyandikira malo wopatulika ankayenera kuphedwa.
Moïse, Aaron et ses fils campaient devant le tabernacle, à l’orient, devant la tente d’assignation, au levant; ils avaient la garde et le soin du sanctuaire, remis à la garde des enfants d’Israël; et l’étranger qui s’approchera sera puni de mort.
39 Alevi onse amene Mose ndi Aaroni anawawerenga potsatira lamulo la Yehova monga mwa magulu a mabanja awo, amuna onse kuyambira a mwezi umodzi kapena kupitirirapo anali 22,000.
Tous les Lévites dont Moïse et Aaron firent le dénombrement sur l’ordre de l’Éternel, selon leurs familles, tous les mâles depuis l’âge d’un mois et au-dessus, furent vingt-deux mille.
40 Yehova anawuza Mose kuti, “Werenga ana onse aamuna oyamba kubadwa mu Israeli, omwe ali ndi mwezi umodzi kapena kupitirirapo ndipo ulembe mndandanda wa mayina awo.
L’Éternel dit à Moïse: Fais le dénombrement de tous les premiers-nés mâles parmi les enfants d’Israël, depuis l’âge d’un mois et au-dessus, et compte-les d’après leurs noms.
41 Unditengere Alevi onse mʼmalo mwa ana oyamba kubadwa onse a Aisraeli, ndiponso ziweto zazimuna za Alevi mʼmalo mwa ziweto zonse zazimuna zoyamba kubadwa za Aisraeli. Ine ndine Yehova.”
Tu prendras les Lévites pour moi, l’Éternel, à la place de tous les premiers-nés des enfants d’Israël, et le bétail des Lévites à la place de tous les premiers-nés du bétail des enfants d’Israël.
42 Choncho Mose anawerenga ana aamuna onse oyamba kubadwa a Aisraeli monga momwe Yehova anamulamulira.
Moïse fit le dénombrement de tous les premiers-nés parmi les enfants d’Israël, selon l’ordre que l’Éternel lui avait donné.
43 Chiwerengero chonse cha ana aamuna oyamba kubadwa kuyambira a mwezi umodzi kapena kupitirirapo chinali 22, 273.
Tous les premiers-nés mâles, dont on fit le dénombrement, en comptant les noms, depuis l’âge d’un mois et au-dessus, furent vingt-deux mille deux cent soixante-treize.
44 Ndipo Yehova anawuzanso Mose kuti,
L’Éternel parla à Moïse, et dit:
45 “Tenga Alevi mʼmalo mwa ana aamuna oyamba kubadwa onse a Aisraeli, ndiponso zoweta zonse za Alevi mʼmalo mwa zoweta za Aisraeli. Alevi ndi anga. Ine ndine Yehova.
Prends les Lévites à la place de tous les premiers-nés des enfants d’Israël, et le bétail des Lévites à la place de leur bétail; et les Lévites m’appartiendront. Je suis l’Éternel.
46 Pofuna kuwombola ana aamuna 273 oyamba kubadwa a Aisraeli amene anaposa chiwerengero cha aamuna a fuko la Levi,
Pour le rachat des deux cent soixante-treize qui dépassent le nombre des Lévites, parmi les premiers-nés des enfants d’Israël,
47 utenge masekeli asanu pa munthu aliyense. Masekeliwo akhale ofanana ndi masekeli a ku malo wopatulika, kumene sekeli imodzi imakwanira magera makumi awiri.
tu prendras cinq sicles par tête; tu les prendras selon le sicle du sanctuaire, qui est de vingt guéras.
48 Ndalama zimenezi uzipereke kwa Aaroni ndi ana ake aamuna kuti ukhale mtengo woombolera Aisraeli woonjezerawo.”
Tu donneras l’argent à Aaron et à ses fils, pour le rachat de ceux qui dépassent le nombre des Lévites.
49 Choncho Mose anatenga ndalama zowombolera zija kuchokera kwa Aisraeli amene chiwerengero chawo chinaposa chiwerengero cha omwe anawomboledwa ndi Alevi.
Moïse prit l’argent pour le rachat de ceux qui dépassaient le nombre des rachetés par les Lévites;
50 Anatenga masekeli a siliva okwana 1,365 molingana ndi masekeli a ku malo opatulika, kuchokera kwa ana aamuna oyamba kubadwa a Aisraeli.
il prit l’argent des premiers-nés des enfants d’Israël: mille trois cent soixante-cinq sicles, selon le sicle du sanctuaire.
51 Mose anapereka ndalama zowombolera zija kwa Aaroni ndi ana ake aamuna monga mwa mawu amene Yehova analamulira.
Et Moïse donna l’argent du rachat à Aaron et à ses fils, sur l’ordre de l’Éternel, en se conformant à l’ordre que l’Éternel avait donné à Moïse.

< Numeri 3 >