< Numeri 3 >
1 Iyi ndi mbiri ya banja la Aaroni ndi Mose pa nthawi yomwe Yehova anayankhula ndi Mose pa phiri la Sinai.
and these generation Aaron and Moses in/on/with day to speak: speak LORD with Moses in/on/with mountain: mount Sinai
2 Mayina a ana aamuna a Aaroni anali Nadabu, woyamba kubadwa, Abihu, Eliezara ndi Itamara.
and these name son: child Aaron [the] firstborn Nadab and Abihu Eleazar and Ithamar
3 Amenewa ndi mayina a ana aamuna a Aaroni, ansembe odzozedwa omwe anapatulidwa kuti azitumikira ngati ansembe.
these name son: child Aaron [the] priest [the] to anoint which to fill hand: donate their to/for to minister
4 Koma Nadabu ndi Abihu, anagwa nafa pamaso pa Yehova pamene ankapereka nsembe ndi moto wachilendo pamaso pa Yehova mʼchipululu cha Sinai. Iwowo analibe ana aamuna. Choncho Eliezara ndi Itamara ndiwo amene ankatumikira ngati ansembe nthawi imene Aaroni abambo awo anali moyo.
and to die Nadab and Abihu to/for face: before LORD in/on/with to present: bring they fire be a stranger to/for face: before LORD in/on/with wilderness (Wilderness of) Sinai and son: child not to be to/for them and to minister Eleazar and Ithamar upon face: before Aaron father their
and to speak: speak LORD to(wards) Moses to/for to say
6 “Bweretsa fuko la Levi ndipo ulipereke kwa Aaroni wansembe kuti lizimutumikira.
to present: bring [obj] tribe Levi and to stand: stand [obj] him to/for face: before Aaron [the] priest and to minister [obj] him
7 Azigwira ntchito yothandiza iyeyo ndi gulu lonse ku tenti ya msonkhano pogwira ntchito ya ku Chihema.
and to keep: guard [obj] charge his and [obj] charge all [the] congregation to/for face: before tent meeting to/for to serve: minister [obj] service: ministry [the] tabernacle
8 Azisamalira zipangizo zonse za mu tenti ya msonkhano, ndipo azigwirira ntchito Aisraeli potumikira mu tenti.
and to keep: guard [obj] all article/utensil tent meeting and [obj] charge son: descendant/people Israel to/for to serve: minister [obj] service: ministry [the] tabernacle
9 Pereka Alevi kwa Aaroni ndi kwa ana ake aamuna. Amenewa ndiwo Aisraeli amene aperekedwa kwa iye kwathunthu.
and to give: give [obj] [the] Levi to/for Aaron and to/for son: child his to give: give to give: give they(masc.) to/for him from with son: descendant/people Israel
10 Usankhe Aaroni ndi ana ake aamuna kuti azitumikira pa ntchito ya unsembe. Koma wina aliyense woyandikira malo opatulika aphedwe.”
and [obj] Aaron and [obj] son: child his to reckon: overseer and to keep: guard [obj] priesthood their and [the] be a stranger [the] approaching to die
11 Yehova anawuzanso Mose kuti,
and to speak: speak LORD to(wards) Moses to/for to say
12 “Pakati pa Aisraeli onse ndatenga Alevi kulowa mʼmalo mwa mwana wamwamuna aliyense woyamba kubadwa kwa amayi a Chiisraeli. Alevi ndi anga,
and I behold to take: take [obj] [the] Levi from midst son: descendant/people Israel underneath: instead all firstborn firstborn womb from son: descendant/people Israel and to be to/for me [the] Levi
13 pakuti ana onse oyamba kubadwa ndi anga. Nditakantha ana onse oyamba kubadwa mu Igupto, ndinadzipatulira ndekha mwana aliyense woyamba kubadwa mu Israeli, wa munthu ndi nyama. Azikhala anga. Ine ndine Yehova.”
for to/for me all firstborn in/on/with day to smite I all firstborn in/on/with land: country/planet Egypt to consecrate: consecate to/for me all firstborn in/on/with Israel from man till animal to/for me to be I LORD
14 Yehova anawuza Mose mʼchipululu cha Sinai kuti,
and to speak: speak LORD to(wards) Moses in/on/with wilderness (Wilderness of) Sinai to/for to say
15 “Werenga Alevi monga mwa mabanja awo ndi mafuko awo. Werenga mwamuna aliyense kuyambira wa mwezi umodzi kapena kupitirirapo.”
to reckon: list [obj] son: child Levi to/for house: household father their to/for family their all male from son: aged month and above [to] to reckon: list them
16 Choncho Mose anawawerenga potsatira zomwe Yehova anamulamulira.
and to reckon: list [obj] them Moses upon lip: word LORD like/as as which to command
17 Mayina a ana aamuna a Levi ndi awa: Geresoni, Kohati ndi Merari.
and to be these son: child Levi in/on/with name their Gershon and Kohath and Merari
18 Mayina a ana a Geresoni potsata mabanja awo ndi awa: Libini ndi Simei.
and these name son: child Gershon to/for family their Libni and Shimei
19 Ana a Kohati potsata mabanja awo ndi awa: Amramu, Izihari, Hebroni ndi Uzieli.
and son: child Kohath to/for family their Amram and Izhar Hebron and Uzziel
20 Ana a Merari potsata mabanja awo ndi awa: Mali ndi Musi. Amenewa ndiwo anali mabanja a Alevi monga mwa makolo awo.
and son: child Merari to/for family their Mahli and Mushi these they(masc.) family [the] Levi to/for house: household father their
21 Kwa Geresoni kunali banja la Alibini, banja la Asimei. Amenewa ndiwo anali mabanja a Ageresoni.
to/for Gershon family [the] Libnite and family [the] Shimeite these they(masc.) family [the] Gershonite
22 Chiwerengero cha amuna onse amene anawawerenga a mwezi umodzi kapena kupitirirapo chinali 7,500.
to reckon: list their in/on/with number all male from son: aged month and above [to] to reckon: list their seven thousand and five hundred
23 Mabanja a Ageresoni azimanga misasa yawo kumadzulo, kumbuyo kwa Chihema.
family [the] Gershonite after [the] tabernacle to camp sea: west [to]
24 Mtsogoleri wa mabanja a Ageresoni anali Eliyasafu mwana wa Laeli.
and leader house: household father to/for Gershonite Eliasaph son: child Lael
25 Ntchito imene Ageresoni anapatsidwa ku tenti ya msonkhano inali yosamalira Chihema ndi tenti, pamodzi ndi zophimbira zake, katani ya pa khomo la ku tenti ya msonkhano,
and charge son: child Gershon in/on/with tent meeting [the] tabernacle and [the] tent covering his and covering entrance tent meeting
26 ndi makatani wotchinga bwalo, katani ya pa chipata cholowera ku bwalo lozungulira Chihema ndi guwa lansembe, zingwe ndi zonse zokhudzana ndi ntchito yawo.
and curtain [the] court and [obj] covering entrance [the] court which upon [the] tabernacle and upon [the] altar around and [obj] cord his to/for all service: ministry his
27 Kwa Kohati kunali mabanja a Amramu, Aizihara, Ahebroni ndi Auzieli. Awa ndiye anali mabanja a Akohati.
and to/for Kohath family [the] Amramite and family [the] Izharite and family [the] Hebronite and family [the] Uzzielite these they(masc.) family [the] Kohathite
28 Chiwerengero cha amuna onse a mwezi umodzi kapena kupitirirapo chinali 8,600. Akohati ankagwira ntchito yosamalira malo wopatulika.
in/on/with number all male from son: aged month and above [to] eight thousand and six hundred to keep: guard charge [the] holiness
29 Mabanja a ana a Kohati ankamanga misasa yawo kummwera kwa Chihema.
family son: child Kohath to camp upon thigh [the] tabernacle south [to]
30 Mtsogoleri wa magulu a mabanja a Kohati anali Elizafani mwana wa Uzieli.
and leader house: household father to/for family [the] Kohathite Elizaphan son: child Uzziel
31 Iwo ankagwira ntchito yosamalira Bokosi la Chipangano, tebulo, choyikapo nyale, maguwa, zipangizo za kumalo wopatulika zimene ansembe ankagwiritsa ntchito, katani, ndi zonse zomwe ankagwiritsa ntchito.
and charge their [the] ark and [the] table and [the] lampstand and [the] altar and article/utensil [the] holiness which to minister in/on/with them and [the] covering and all service: ministry his
32 Mtsogoleri wamkulu wa Alevi anali Eliezara mwana wa Aaroni wansembe. Iye anasankhidwa kukhala woyangʼanira omwe ankasamalira malo wopatulika.
and leader leader [the] Levi Eleazar son: child Aaron [the] priest punishment to keep: guard charge [the] holiness
33 Kwa Merari kunali banja la Mali ndi banja la Musi. Amenewa ndiye anali mabanja a Amerari.
to/for Merari family [the] Mahlite and family [the] Mushite these they(masc.) family Merari
34 Chiwerengero cha amuna onse kuyambira a mwezi umodzi kapena kupitirirapo chinali 6,200.
and to reckon: list their in/on/with number all male from son: aged month and above [to] six thousand and hundred
35 Mtsogoleri wa magulu a mabanja a Amerari anali Zuriyeli mwana wa Abihaili. Iwo ankamanga misasa yawo kumpoto kwa Chihema.
and leader house: household father to/for family Merari Zuriel son: child Abihail upon thigh [the] tabernacle to camp north [to]
36 Amerari anapatsidwa ntchito yosamalira mitengo ya chihema, nsichi zake, mizati yake, matsinde ake, ndi zida zake zonse, ndi zonse zomwe ankagwiritsa ntchito,
and punishment charge son: child Merari board [the] tabernacle and bar his and pillar his and socket his and all article/utensil his and all service: ministry his
37 pamodzi ndi mizati yozungulira bwalo ndi matsinde ake, zikhomo za chihema ndi zingwe zake.
and pillar [the] court around and socket their and peg their and cord their
38 Mose ndi Aaroni ndi ana ake aamuna ankamanga misasa yawo kummawa kwa chihema, kuyangʼana kotulukira dzuwa, kutsogolo kwa tenti ya msonkhano. Anali ndi ntchito yosamalira malo wopatulika mʼmalo mwa Aisraeli. Aliyense woyandikira malo wopatulika ankayenera kuphedwa.
and [the] to camp to/for face: before [the] tabernacle east [to] to/for face: before tent meeting east [to] Moses and Aaron and son: child his to keep: guard charge [the] sanctuary to/for charge son: descendant/people Israel and [the] be a stranger [the] approaching to die
39 Alevi onse amene Mose ndi Aaroni anawawerenga potsatira lamulo la Yehova monga mwa magulu a mabanja awo, amuna onse kuyambira a mwezi umodzi kapena kupitirirapo anali 22,000.
all to reckon: list [the] Levi which to reckon: list Moses and Aaron upon lip: word LORD to/for family their all male from son: aged month and above [to] two and twenty thousand
40 Yehova anawuza Mose kuti, “Werenga ana onse aamuna oyamba kubadwa mu Israeli, omwe ali ndi mwezi umodzi kapena kupitirirapo ndipo ulembe mndandanda wa mayina awo.
and to say LORD to(wards) Moses to reckon: list all firstborn male to/for son: descendant/people Israel from son: aged month and above [to] and to lift: count [obj] number name their
41 Unditengere Alevi onse mʼmalo mwa ana oyamba kubadwa onse a Aisraeli, ndiponso ziweto zazimuna za Alevi mʼmalo mwa ziweto zonse zazimuna zoyamba kubadwa za Aisraeli. Ine ndine Yehova.”
and to take: take [obj] [the] Levi to/for me I LORD underneath: instead all firstborn in/on/with son: descendant/people Israel and [obj] animal [the] Levi underneath: instead all firstborn in/on/with animal son: descendant/people Israel
42 Choncho Mose anawerenga ana aamuna onse oyamba kubadwa a Aisraeli monga momwe Yehova anamulamulira.
and to reckon: list Moses like/as as which to command LORD [obj] him [obj] all firstborn in/on/with son: descendant/people Israel
43 Chiwerengero chonse cha ana aamuna oyamba kubadwa kuyambira a mwezi umodzi kapena kupitirirapo chinali 22, 273.
and to be all firstborn male in/on/with number name from son: aged month and above [to] to/for to reckon: list their two and twenty thousand three and seventy and hundred
44 Ndipo Yehova anawuzanso Mose kuti,
and to speak: speak LORD to(wards) Moses to/for to say
45 “Tenga Alevi mʼmalo mwa ana aamuna oyamba kubadwa onse a Aisraeli, ndiponso zoweta zonse za Alevi mʼmalo mwa zoweta za Aisraeli. Alevi ndi anga. Ine ndine Yehova.
to take: take [obj] [the] Levi underneath: instead all firstborn in/on/with son: descendant/people Israel and [obj] animal [the] Levi underneath: instead animal their and to be to/for me [the] Levi I LORD
46 Pofuna kuwombola ana aamuna 273 oyamba kubadwa a Aisraeli amene anaposa chiwerengero cha aamuna a fuko la Levi,
and [obj] ransomed [the] three and [the] seventy and [the] hundred [the] to remain upon [the] Levi from firstborn son: descendant/people Israel
47 utenge masekeli asanu pa munthu aliyense. Masekeliwo akhale ofanana ndi masekeli a ku malo wopatulika, kumene sekeli imodzi imakwanira magera makumi awiri.
and to take: take five five shekel to/for head in/on/with shekel [the] holiness to take: take twenty gerah [the] shekel
48 Ndalama zimenezi uzipereke kwa Aaroni ndi ana ake aamuna kuti ukhale mtengo woombolera Aisraeli woonjezerawo.”
and to give: give [the] silver: money to/for Aaron and to/for son: child his ransomed [the] to remain in/on/with them
49 Choncho Mose anatenga ndalama zowombolera zija kuchokera kwa Aisraeli amene chiwerengero chawo chinaposa chiwerengero cha omwe anawomboledwa ndi Alevi.
and to take: take Moses [obj] silver: money [the] redemption from with [the] to remain upon ransomed [the] Levi
50 Anatenga masekeli a siliva okwana 1,365 molingana ndi masekeli a ku malo opatulika, kuchokera kwa ana aamuna oyamba kubadwa a Aisraeli.
from with firstborn son: descendant/people Israel to take: take [obj] [the] silver: money five and sixty and three hundred and thousand in/on/with shekel [the] holiness
51 Mose anapereka ndalama zowombolera zija kwa Aaroni ndi ana ake aamuna monga mwa mawu amene Yehova analamulira.
and to give: give Moses [obj] silver: money ([the] ransomed *Q(k)*) to/for Aaron and to/for son: child his upon lip: word LORD like/as as which to command LORD [obj] Moses