< Numeri 29 >

1 “‘Pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiwiri muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse. Ili ndi tsiku limene muziliza malipenga.
“Celebren una reunión sagrada el primer día del séptimo mes. No hagas nada de tu trabajo normal. Este es el día en que tocarás las trompetas.
2 Muzipereka mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri a chaka chimodzi wopanda chilema monga nsembe zopsereza, fungo lokoma kwa Yehova.
Presenten un holocausto de un novillo, un carnero y siete corderos machos de un año, todos ellos sin defectos, como sacrificio aceptable al Señor,
3 Pa ngʼombe yayimuna iliyonse, muzipereka chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta. Pa nkhosa yayimuna iliyonse muzipereka makilogalamu awiri.
junto con sus ofrendas de grano de la mejor harina mezclada con aceite de oliva: tres décimos de un efa para el toro, dos décimos de un efa para el carnero,
4 Pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiri aja muzipereka kilogalamu imodzi.
y un décimo de un efa para cada uno de los siete corderos machos.
5 Muziperekanso mbuzi yayimuna kuti izikhala nsembe yopepesera machimo anu.
Presenten también una cabra macho como ofrenda por el pecado para hacerte justicia.
6 Izi ndi zowonjezera pa nsembe zopsereza za mwezi ndi mwezi komanso za tsiku ndi tsiku pamodzi ndi zopereka za chakudya ndi zopereka za chakumwa potsata malamulo ake. Izi ndi zopereka zotentha pa moto, zoperekedwa kwa Yehova, fungo lokoma.
Estas ofrendas se suman a los holocaustos mensuales y diarios junto con las ofrendas de grano y las ofrendas de bebida requeridas. Son ofrendas quemadas aceptables para el Señor.
7 “‘Pa tsiku lakhumi la mwezi wachisanu ndi chiwiriwu, muzichita msonkhano wopatulika. Muzisala zakudya ndipo musamagwire ntchito.
“Celebrarás una reunión sagrada el décimo día de este séptimo mes, y practiquen la abnegación. No hagas nada de tu trabajo normal.
8 Muzipereka kwa Yehova nsembe yopsereza, yotulutsa fungo lokoma lokondweretsa Yehovayo; ngʼombe yayimuna imodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri a chaka chimodzi. Zimenezi zizikhala zopanda chilema.
Presenta un holocausto de un novillo, un carnero y siete corderos machos de un año, todos ellos sin defectos, aceptables para el Señor.
9 Pa ngʼombe yayimuna iliyonse, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; pa nkhosa yayimuna iliyonse makilogalamu awiri;
Deben ir acompañados de sus ofrendas de grano de la mejor harina mezclada con aceite de oliva: tres décimas de efa para el toro, dos décimas de efa para el carnero,
10 kilogalamu imodzi pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiriwo.
y una décima de efa para cada uno de los siete corderos.
11 Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna kuti izikhala nsembe yopepesera machimo, kuwonjezera pa nsembe yopepesera machimo ya pa tsiku la mwambo ija, kuwonjezanso pa nsembe zopsereza za tsiku ndi tsiku zija, pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi cha chakumwa.
Presenta también un macho cabrío como ofrenda por el pecado, además de la ofrenda por el pecado para corregirte y el holocausto continuo con su ofrenda de grano y su libación.
12 “‘Pa tsiku la mwezi wachisanu ndi chiwiri, muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse. Muzichita madyerero a Yehova masiku asanu ndi awiri.
“Celebrea una reunión sagrada el día quince del séptimo mes. No hagas nada de tu trabajo normal. Debes celebrar un festival dedicado al Señor durante siete días.
13 Muzipereka nsembe yotentha pa moto, kuti izikhala fungo lokoma kwa Yehova, nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna khumi ndi atatu, nkhosa zazimuna ziwiri, ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
Presenta como holocausto aceptable al Señor: trece novillos, dos carneros y catorce corderos machos de un año, todos ellos sin defectos.
14 Pa mwana wangʼombe aliyense mwa ana angʼombe aamuna khumi ndi atatu aja, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta. Pa nkhosa iliyonse mwa nkhosa ziwiri zija, mukonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu awiri.
Se acompañarán con sus ofrendas de grano de la mejor harina mezclada con aceite de oliva: tres décimas de efa de la mejor harina mezclada con aceite de oliva por cada uno de los trece toros, dos décimas de efa por cada uno de los dos carneros,
15 Pa mwana wankhosa aliyense mwa ana ankhosa aamuna khumi ndi anayiwo, muzipereka chakudya cha kilogalamu imodzi.
y una décima de efa por cada uno de los catorce corderos.
16 Muziperekanso mbuzi yayimuna imodzi kuti izikhale nsembe yopepesera machimo, kuwonjezera pa nsembe zopsereza za tsiku ndi tsiku zija pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
También presentarás un macho cabrío como ofrenda por el pecado además del holocausto continuo con su ofrenda de grano y su libación.
17 “‘Pa tsiku lachiwiri muzipereka ana angʼombe aamuna khumi ndi awiri aja, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi aja, zonse zopanda chilema.
“El segundo día, presente doce novillos, dos carneros y catorce corderos machos de un año, todos ellos sin defectos.
18 Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka zopereka za chakudya ndi za chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
Deben ir acompañados por sus ofrendas de grano y bebidas para los toros, carneros y corderos, todo según el número requerido.
19 Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
Presenta también un macho cabrío como ofrenda por el pecado, además del continuo holocausto con su ofrenda de grano y su libación.
20 “‘Pa tsiku lachitatu muzipereka ngʼombe zazimuna khumi ndi imodzi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
“Al tercer día, presenta once novillos, dos carneros y catorce corderos machos de un año de edad, todos ellos sin defectos.
21 Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka zopereka za chakudya ndi za chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
Deben estar acompañados por sus ofrendas de grano y libaciones para los toros, carneros y corderos, todo de acuerdo al número requerido.
22 Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
Presenta también un macho cabrío como ofrenda por el pecado además del holocausto continuo con su ofrenda de grano y su libación.
23 “‘Pa tsiku lachinayi muzipereka ngʼombe zazimuna khumi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
“Al cuarto día presentarás diez novillos, dos carneros y catorce corderos machos de un año, todos ellos sin defectos.
24 Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
Deben ir acompañados por sus ofrendas de grano y libaciones para los toros, carneros y corderos, todo de acuerdo al número requerido.
25 Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
También presentarás un macho cabrío como ofrenda por el pecado, además del continuo holocausto con su ofrenda de grano y su libación.
26 “‘Pa tsiku lachisanu muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi zinayi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
“El quinto día presentarás nueve novillos, dos carneros y catorce corderos machos de un año, todos ellos sin defectos.
27 Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
Deben ir acompañados por sus ofrendas de grano y libaciones para los toros, carneros y corderos, todo de acuerdo con el número requerido.
28 Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
Presentarás también un macho cabrío como ofrenda por el pecado, además del continuo holocausto con su ofrenda de grano y su libación.
29 “‘Pa tsiku lachisanu ndi chimodzi muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi zitatu, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
“Al sexto día presentarás ocho novillos, dos carneros y catorce corderos machos de un año, todos ellos sin defectos.
30 Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
Deben estar acompañados por sus ofrendas de grano y libaciones para los toros, carneros y corderos, todo de acuerdo al número requerido.
31 Muziperekenso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
También se presentará un macho cabrío como ofrenda por el pecado, además del continuo holocausto con su ofrenda de grano y su libación.
32 “‘Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa amuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
“Al séptimo día presentar siete novillos, dos carneros y catorce corderos machos de un año de edad, todos ellos sin defectos.
33 Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
Deben estar acompañados por sus ofrendas de grano y libaciones para los toros, carneros y corderos, todo de acuerdo al número requerido.
34 Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
También se presentará un macho cabrío como ofrenda por el pecado, además del continuo holocausto con su ofrenda de grano y su libación.
35 “‘Pa tsiku lachisanu ndi chitatu muzichita msonkhano ndipo musamagwire ntchito iliyonse.
“En el octavo día todos ustedes se reunirán juntos. No hagan nada de su trabajo normal.
36 Muzipereka chopereka chotentha pa moto monga fungo lokoma kwa Yehova, nsembe yopsereza ya ngʼombe imodzi yayimuna, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa amuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
Presenta como holocausto aceptable al Señor: un toro, dos carneros y siete corderos machos de un año, todos ellos sin defectos.
37 Pamodzi ndi ngʼombe yayimunayo, nkhosa yayimunayo ndi ana ankhosawo, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
Deben ir acompañados de sus ofrendas de grano y de las libaciones para los toros, carneros y corderos, todo según el número requerido.
38 Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
También se presentará un macho cabrío como ofrenda por el pecado, además del continuo holocausto con su ofrenda de grano y su libación.
39 “‘Kuwonjezera pa zopereka zimene munalumbirira ndi pa zopereka zanu zaufulu, muzipereka zimenezi kwa Yehova pa masiku osankhika a chikondwerero chanu. Nsembe zanu zachakumwa ndi nsembe zanu zachiyanjano.’”
“Presenta estas ofrendas al Señor en los momentos en que se te requiera, además de tus ofrendas para cumplir una promesa y las ofrendas de libre albedrío, ya sean holocaustos, ofrendas de grano, libaciones o sacrificios de paz”.
40 Mose anawuza Aisraeli zonse zimene Yehova anamulamulira.
Moisés repitió todo esto a los israelitas como el Señor se lo ordenó.

< Numeri 29 >