< Numeri 29 >
1 “‘Pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiwiri muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse. Ili ndi tsiku limene muziliza malipenga.
Au septième mois, le premier jour du mois, vous aurez une sainte assemblée: vous ne ferez aucune œuvre servile. Ce sera pour vous le jour du son éclatant des trompettes.
2 Muzipereka mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri a chaka chimodzi wopanda chilema monga nsembe zopsereza, fungo lokoma kwa Yehova.
Vous offrirez comme holocauste d’agréable odeur à Yahweh un jeune taureau, un bélier et sept agneaux d’un an, sans défaut,
3 Pa ngʼombe yayimuna iliyonse, muzipereka chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta. Pa nkhosa yayimuna iliyonse muzipereka makilogalamu awiri.
et, comme leur oblation, de la fleur de farine pétrie à l’huile: trois dixièmes pour le taureau, deux dixièmes pour le bélier
4 Pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiri aja muzipereka kilogalamu imodzi.
et un dixième pour chacun des sept agneaux.
5 Muziperekanso mbuzi yayimuna kuti izikhala nsembe yopepesera machimo anu.
Vous offrirez aussi un bouc en sacrifice pour le péché, pour faire l’expiation pour vous.
6 Izi ndi zowonjezera pa nsembe zopsereza za mwezi ndi mwezi komanso za tsiku ndi tsiku pamodzi ndi zopereka za chakudya ndi zopereka za chakumwa potsata malamulo ake. Izi ndi zopereka zotentha pa moto, zoperekedwa kwa Yehova, fungo lokoma.
Vous ferez cela sans préjudice de l’holocauste du mois et de son oblation, de l’holocauste perpétuel et de son oblation, et de leurs libations d’après les règles prescrites. Ce sont des sacrifices par le feu, d’agréable odeur à Yahweh.
7 “‘Pa tsiku lakhumi la mwezi wachisanu ndi chiwiriwu, muzichita msonkhano wopatulika. Muzisala zakudya ndipo musamagwire ntchito.
Le dixième jour de ce septième mois, vous aurez une sainte assemblée et vous affligerez vos âmes: vous ne ferez aucune œuvre.
8 Muzipereka kwa Yehova nsembe yopsereza, yotulutsa fungo lokoma lokondweretsa Yehovayo; ngʼombe yayimuna imodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri a chaka chimodzi. Zimenezi zizikhala zopanda chilema.
Vous offrirez en holocauste d’agréable odeur à Yahweh un jeune taureau, un bélier et sept agneaux d’un an, sans défaut,
9 Pa ngʼombe yayimuna iliyonse, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; pa nkhosa yayimuna iliyonse makilogalamu awiri;
et, comme leur oblation, de la fleur de farine pétrie à l’huile: trois dixièmes pour le taureau, deux dixièmes pour le bélier
10 kilogalamu imodzi pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiriwo.
et un dixième pour chacun des sept agneaux.
11 Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna kuti izikhala nsembe yopepesera machimo, kuwonjezera pa nsembe yopepesera machimo ya pa tsiku la mwambo ija, kuwonjezanso pa nsembe zopsereza za tsiku ndi tsiku zija, pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi cha chakumwa.
Vous offrirez aussi un bouc en sacrifice pour le péché, sans préjudice du sacrifice expiatoire, de l’holocauste perpétuel, de son oblation, et de leurs libations.
12 “‘Pa tsiku la mwezi wachisanu ndi chiwiri, muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse. Muzichita madyerero a Yehova masiku asanu ndi awiri.
Le quinzième jour, du septième mois, vous aurez une sainte assemblée: vous ne ferez aucune œuvre servile. Et vous célébrerez une fête en l’honneur de Yahweh pendant sept jours.
13 Muzipereka nsembe yotentha pa moto, kuti izikhala fungo lokoma kwa Yehova, nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna khumi ndi atatu, nkhosa zazimuna ziwiri, ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
Vous offrirez un holocauste, sacrifice par le feu, d’agréable odeur à Yahweh: treize jeunes taureaux, deux béliers et quatorze agneaux d’un an, sans défaut,
14 Pa mwana wangʼombe aliyense mwa ana angʼombe aamuna khumi ndi atatu aja, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta. Pa nkhosa iliyonse mwa nkhosa ziwiri zija, mukonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu awiri.
et, comme leur oblation, de la fleur de farine pétrie à l’huile: trois dixièmes pour chacun des treize taureaux, deux dixièmes pour chacun des deux béliers,
15 Pa mwana wankhosa aliyense mwa ana ankhosa aamuna khumi ndi anayiwo, muzipereka chakudya cha kilogalamu imodzi.
et un dixième pour chacun des quatorze agneaux.
16 Muziperekanso mbuzi yayimuna imodzi kuti izikhale nsembe yopepesera machimo, kuwonjezera pa nsembe zopsereza za tsiku ndi tsiku zija pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
Vous offrirez aussi un bouc en sacrifice pour le péché, sans préjudice de l’holocauste perpétuel avec son oblation et sa libation.
17 “‘Pa tsiku lachiwiri muzipereka ana angʼombe aamuna khumi ndi awiri aja, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi aja, zonse zopanda chilema.
Le second jour, vous offrirez douze jeunes taureaux, deux béliers et quatorze agneaux d’un an, sans défaut,
18 Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka zopereka za chakudya ndi za chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
avec leur oblation et leurs libations, pour les taureaux, les béliers et les agneaux, selon leur nombre, d’après la règle.
19 Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
Vous offrirez aussi un bouc en sacrifice pour le péché, sans préjudice de l’holocauste perpétuel, de son oblation et de leurs libations.
20 “‘Pa tsiku lachitatu muzipereka ngʼombe zazimuna khumi ndi imodzi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
Le troisième jour, vous offrirez onze taureaux, deux béliers et quatorze agneaux d’un an, sans défaut,
21 Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka zopereka za chakudya ndi za chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
avec leur oblation et leurs libations, pour les taureaux, les béliers et les agneaux, selon leur nombre, d’après la règle.
22 Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
Vous offrirez aussi un bouc en sacrifice pour le péché, sans préjudice de l’holocauste perpétuel, de son oblation et de sa libation.
23 “‘Pa tsiku lachinayi muzipereka ngʼombe zazimuna khumi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
Le quatrième jour, vous offrirez dix taureaux, deux béliers et quatorze agneaux d’un an, sans défaut,
24 Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
avec leur oblation et leurs libations, pour les taureaux, les béliers et les agneaux, selon leur nombre d’après la règle.
25 Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
Vous offrirez aussi un bouc en sacrifice pour le péché, sans préjudice de l’holocauste perpétuel, de son oblation et de sa libation.
26 “‘Pa tsiku lachisanu muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi zinayi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
Le cinquième jour, vous offrirez neuf taureaux, deux béliers et quatorze agneaux d’un an, sans défaut,
27 Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
avec leur oblation et leurs libations, pour les taureaux, les béliers et les agneaux, selon leur nombre, d’après la règle.
28 Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
Vous offrirez aussi un bouc en sacrifice pour le péché, sans préjudice de l’holocauste perpétuel, de son oblation et de sa libation.
29 “‘Pa tsiku lachisanu ndi chimodzi muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi zitatu, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
Le sixième jour, vous offrirez huit taureaux, deux béliers et quatorze agneaux d’un an, sans défaut,
30 Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
avec leur oblation et leurs libations, pour les taureaux, les béliers et les agneaux, selon leur nombre, d’après la règle.
31 Muziperekenso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
Vous offrirez aussi un bouc en sacrifice pour le péché, sans préjudice de l’holocauste perpétuel, de son oblation et de sa libation.
32 “‘Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa amuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
Le septième jour, vous offrirez sept taureaux, deux béliers et quatorze agneaux d’un an, sans défaut,
33 Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
avec leur oblation et leurs libations, pour les taureaux, les béliers et les agneaux, selon leur nombre, d’après la règle.
34 Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
Vous offrirez aussi un bouc en sacrifice pour le péché, sans préjudice de l’holocauste perpétuel, de son oblation et de sa libation.
35 “‘Pa tsiku lachisanu ndi chitatu muzichita msonkhano ndipo musamagwire ntchito iliyonse.
Le huitième jour, vous aurez une assemblée solennelle: vous ne ferez aucune œuvre servile.
36 Muzipereka chopereka chotentha pa moto monga fungo lokoma kwa Yehova, nsembe yopsereza ya ngʼombe imodzi yayimuna, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa amuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
Vous offrirez un holocauste, un sacrifice par le feu d’agréable odeur à Yahweh: un taureau, un bélier et sept agneaux d’un an, sans défaut,
37 Pamodzi ndi ngʼombe yayimunayo, nkhosa yayimunayo ndi ana ankhosawo, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
avec leur oblation et leurs libations, pour le taureau, le bélier et les agneaux, selon leur nombre, d’après la règle.
38 Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
Vous offrirez aussi un bouc en sacrifice pour le péché, sans préjudice de l’holocauste perpétuel, de son oblation et de sa libation.
39 “‘Kuwonjezera pa zopereka zimene munalumbirira ndi pa zopereka zanu zaufulu, muzipereka zimenezi kwa Yehova pa masiku osankhika a chikondwerero chanu. Nsembe zanu zachakumwa ndi nsembe zanu zachiyanjano.’”
Tels sont les sacrifices que vous offrirez à Yahweh dans vos fêtes, sans préjudice de vos vœux et de vos offrandes volontaires: vos holocaustes, vos oblations, vos libations et vos sacrifices pacifiques. »
40 Mose anawuza Aisraeli zonse zimene Yehova anamulamulira.
Moïse parla aux enfants d’Israël selon tout ce que Yahweh lui avait ordonné: