< Numeri 29 >

1 “‘Pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiwiri muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse. Ili ndi tsiku limene muziliza malipenga.
"'Au septième mois, le premier jour du mois, vous aurez une sainte convocation; vous ne ferez aucun travail régulier. C'est un jour où l'on fait sonner les trompettes pour vous.
2 Muzipereka mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri a chaka chimodzi wopanda chilema monga nsembe zopsereza, fungo lokoma kwa Yehova.
Vous offrirez un holocauste d'agréable odeur à Yahvé: un jeune taureau, un bélier, sept agneaux mâles d'un an sans défaut;
3 Pa ngʼombe yayimuna iliyonse, muzipereka chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta. Pa nkhosa yayimuna iliyonse muzipereka makilogalamu awiri.
et leur offrande de farine, de la fleur de farine mélangée à de l'huile: 3 et leur offrande de farine fine mélangée à de l'huile: trois dixièmes pour le taureau, deux dixièmes pour le bélier,
4 Pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiri aja muzipereka kilogalamu imodzi.
et un dixième pour chacun des sept agneaux;
5 Muziperekanso mbuzi yayimuna kuti izikhala nsembe yopepesera machimo anu.
et un bouc en sacrifice pour le péché, afin de faire l'expiation pour toi;
6 Izi ndi zowonjezera pa nsembe zopsereza za mwezi ndi mwezi komanso za tsiku ndi tsiku pamodzi ndi zopereka za chakudya ndi zopereka za chakumwa potsata malamulo ake. Izi ndi zopereka zotentha pa moto, zoperekedwa kwa Yehova, fungo lokoma.
en plus de l'holocauste de la nouvelle lune et de son offrande de farine, de l'holocauste perpétuel et de son offrande de farine, et de leurs libations, selon les règles établies, en sacrifice consumé par le feu devant l'Éternel, d'une agréable odeur.
7 “‘Pa tsiku lakhumi la mwezi wachisanu ndi chiwiriwu, muzichita msonkhano wopatulika. Muzisala zakudya ndipo musamagwire ntchito.
"'Le dixième jour de ce septième mois, vous aurez une convocation sainte. Vous affligerez vos âmes. Vous ne ferez aucun travail,
8 Muzipereka kwa Yehova nsembe yopsereza, yotulutsa fungo lokoma lokondweretsa Yehovayo; ngʼombe yayimuna imodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri a chaka chimodzi. Zimenezi zizikhala zopanda chilema.
mais vous offrirez à Yahvé un holocauste d'agréable odeur: un jeune taureau, un bélier, sept agneaux mâles d'un an, tous sans défaut,
9 Pa ngʼombe yayimuna iliyonse, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; pa nkhosa yayimuna iliyonse makilogalamu awiri;
et leur offrande de farine fine mélangée à de l'huile: trois dixièmes pour le taureau, deux dixièmes pour le bélier,
10 kilogalamu imodzi pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiriwo.
un dixième pour chacun des sept agneaux,
11 Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna kuti izikhala nsembe yopepesera machimo, kuwonjezera pa nsembe yopepesera machimo ya pa tsiku la mwambo ija, kuwonjezanso pa nsembe zopsereza za tsiku ndi tsiku zija, pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi cha chakumwa.
un bouc en sacrifice pour le péché, en plus du sacrifice d'expiation pour le péché, de l'holocauste perpétuel, de l'offrande de farine et des libations.
12 “‘Pa tsiku la mwezi wachisanu ndi chiwiri, muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse. Muzichita madyerero a Yehova masiku asanu ndi awiri.
"'Le quinzième jour du septième mois, vous aurez une sainte convocation. Vous ne ferez aucun travail régulier. Vous célébrerez une fête en l'honneur de Yahvé pendant sept jours.
13 Muzipereka nsembe yotentha pa moto, kuti izikhala fungo lokoma kwa Yehova, nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna khumi ndi atatu, nkhosa zazimuna ziwiri, ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
Vous offrirez un holocauste, un sacrifice consumé par le feu, d'une odeur agréable à l'Éternel: treize jeunes taureaux, deux béliers, quatorze agneaux mâles d'un an, tous sans défaut;
14 Pa mwana wangʼombe aliyense mwa ana angʼombe aamuna khumi ndi atatu aja, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta. Pa nkhosa iliyonse mwa nkhosa ziwiri zija, mukonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu awiri.
et leur offrande de farine, de la fleur de farine mélangée à de l'huile: trois dixièmes pour chaque taureau des treize taureaux, deux dixièmes pour chaque bélier des deux béliers,
15 Pa mwana wankhosa aliyense mwa ana ankhosa aamuna khumi ndi anayiwo, muzipereka chakudya cha kilogalamu imodzi.
et un dixième pour chaque agneau des quatorze agneaux;
16 Muziperekanso mbuzi yayimuna imodzi kuti izikhale nsembe yopepesera machimo, kuwonjezera pa nsembe zopsereza za tsiku ndi tsiku zija pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
et un bouc pour le sacrifice pour le péché, en plus de l'holocauste perpétuel, de l'offrande et de la libation.
17 “‘Pa tsiku lachiwiri muzipereka ana angʼombe aamuna khumi ndi awiri aja, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi aja, zonse zopanda chilema.
"'Le second jour, tu offriras douze jeunes taureaux, deux béliers et quatorze agneaux mâles d'un an sans défaut,
18 Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka zopereka za chakudya ndi za chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
avec leurs offrandes et leurs libations pour les taureaux, les béliers et les agneaux, selon leur nombre, d'après l'ordonnance;
19 Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
et un bouc pour le sacrifice pour le péché, en plus de l'holocauste perpétuel, avec ses offrandes et ses libations.
20 “‘Pa tsiku lachitatu muzipereka ngʼombe zazimuna khumi ndi imodzi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
"'Le troisième jour, onze taureaux, deux béliers, quatorze agneaux mâles d'un an sans défaut,
21 Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka zopereka za chakudya ndi za chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
avec leurs offrandes et leurs libations pour les taureaux, les béliers et les agneaux, selon leur nombre, d'après les règles établies;
22 Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
et un bouc pour le sacrifice pour le péché, en plus de l'holocauste perpétuel, de l'offrande et de la libation.
23 “‘Pa tsiku lachinayi muzipereka ngʼombe zazimuna khumi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
"'Le quatrième jour, dix taureaux, deux béliers, quatorze agneaux mâles d'un an sans défaut;
24 Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
leurs offrandes et leurs libations pour les taureaux, pour les béliers et pour les agneaux, selon leur nombre, d'après les règles établies;
25 Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
et un bouc pour le sacrifice pour le péché, en plus de l'holocauste perpétuel, de son offrande et de sa libation.
26 “‘Pa tsiku lachisanu muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi zinayi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
"'Le cinquième jour, neuf taureaux, deux béliers, quatorze agneaux mâles d'un an sans défaut,
27 Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
avec leurs offrandes et leurs libations pour les taureaux, les béliers et les agneaux, selon leur nombre, d'après les règles établies,
28 Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
et un bouc pour le sacrifice pour le péché, en plus de l'holocauste perpétuel, de l'offrande et de la libation.
29 “‘Pa tsiku lachisanu ndi chimodzi muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi zitatu, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
"'Le sixième jour, huit taureaux, deux béliers, quatorze agneaux mâles d'un an sans défaut,
30 Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
avec leurs offrandes et leurs libations pour les taureaux, pour les béliers et pour les agneaux, selon leur nombre, d'après les règles établies,
31 Muziperekenso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
et un bouc pour le sacrifice pour le péché, en plus de l'holocauste perpétuel, de son offrande et de ses libations.
32 “‘Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa amuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
"'Le septième jour, sept taureaux, deux béliers, quatorze agneaux mâles d'un an sans défaut,
33 Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
avec leurs offrandes et leurs libations pour les taureaux, les béliers et les agneaux, selon leur nombre, d'après les règles établies,
34 Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
et un bouc pour le sacrifice pour le péché, en plus de l'holocauste perpétuel, de son offrande et de sa libation.
35 “‘Pa tsiku lachisanu ndi chitatu muzichita msonkhano ndipo musamagwire ntchito iliyonse.
"'Le huitième jour, vous aurez une assemblée solennelle. Vous ne ferez aucun travail régulier;
36 Muzipereka chopereka chotentha pa moto monga fungo lokoma kwa Yehova, nsembe yopsereza ya ngʼombe imodzi yayimuna, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa amuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
mais vous offrirez un holocauste, un sacrifice consumé par le feu, d'une agréable odeur à Yahvé: un taureau, un bélier, sept agneaux mâles d'un an sans défaut;
37 Pamodzi ndi ngʼombe yayimunayo, nkhosa yayimunayo ndi ana ankhosawo, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
l'offrande et la libation du taureau, du bélier et des agneaux seront déterminées d'après leur nombre, selon les règles établies;
38 Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
et un bouc en sacrifice pour le péché, en plus de l'holocauste perpétuel, de l'offrande et de la libation.
39 “‘Kuwonjezera pa zopereka zimene munalumbirira ndi pa zopereka zanu zaufulu, muzipereka zimenezi kwa Yehova pa masiku osankhika a chikondwerero chanu. Nsembe zanu zachakumwa ndi nsembe zanu zachiyanjano.’”
"'Tu les offriras à Yahvé lors de tes fêtes, en plus de tes vœux et de tes offrandes volontaires, pour tes holocaustes, tes offrandes de repas, tes libations et tes sacrifices de paix'".
40 Mose anawuza Aisraeli zonse zimene Yehova anamulamulira.
Moïse dit aux enfants d'Israël tout ce que l'Éternel lui avait ordonné.

< Numeri 29 >