< Numeri 29 >

1 “‘Pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiwiri muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse. Ili ndi tsiku limene muziliza malipenga.
“And in the seventh month, on the first of the month, you have a holy convocation; you do no servile work; it is a day of shouting to you;
2 Muzipereka mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri a chaka chimodzi wopanda chilema monga nsembe zopsereza, fungo lokoma kwa Yehova.
and you have prepared a burnt-offering for refreshing fragrance to YHWH: one bullock, a son of the herd, one ram, seven lambs, sons of a year, perfect ones;
3 Pa ngʼombe yayimuna iliyonse, muzipereka chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta. Pa nkhosa yayimuna iliyonse muzipereka makilogalamu awiri.
and their present of flour mixed with oil: three-tenth parts for the bullock, two-tenth parts for the ram,
4 Pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiri aja muzipereka kilogalamu imodzi.
and one-tenth part for one lamb, for the seven lambs;
5 Muziperekanso mbuzi yayimuna kuti izikhala nsembe yopepesera machimo anu.
and one kid of the goats [for] a sin-offering, to make atonement for you;
6 Izi ndi zowonjezera pa nsembe zopsereza za mwezi ndi mwezi komanso za tsiku ndi tsiku pamodzi ndi zopereka za chakudya ndi zopereka za chakumwa potsata malamulo ake. Izi ndi zopereka zotentha pa moto, zoperekedwa kwa Yehova, fungo lokoma.
apart from the burnt-offering of the month and its present, and the continual burnt-offering and its present, and their drink-offerings, according to their ordinance, for refreshing fragrance, a fire-offering to YHWH.
7 “‘Pa tsiku lakhumi la mwezi wachisanu ndi chiwiriwu, muzichita msonkhano wopatulika. Muzisala zakudya ndipo musamagwire ntchito.
And on the tenth of this seventh month you have a holy convocation, and you have humbled your souls; you do no work;
8 Muzipereka kwa Yehova nsembe yopsereza, yotulutsa fungo lokoma lokondweretsa Yehovayo; ngʼombe yayimuna imodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri a chaka chimodzi. Zimenezi zizikhala zopanda chilema.
and you have brought a burnt-offering near to YHWH, a refreshing fragrance: one bullock, a son of the herd, one ram, seven lambs, sons of a year; they are perfect ones for you;
9 Pa ngʼombe yayimuna iliyonse, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; pa nkhosa yayimuna iliyonse makilogalamu awiri;
and their present of flour mixed with oil: three-tenth parts for the bullock, two-tenth parts for one ram,
10 kilogalamu imodzi pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiriwo.
a tenth—a tenth part for one lamb, for the seven lambs,
11 Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna kuti izikhala nsembe yopepesera machimo, kuwonjezera pa nsembe yopepesera machimo ya pa tsiku la mwambo ija, kuwonjezanso pa nsembe zopsereza za tsiku ndi tsiku zija, pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi cha chakumwa.
one kid of the goats [for] a sin-offering, apart from the sin-offering of the atonements, and the continual burnt-offering and its present, and their drink-offerings.
12 “‘Pa tsiku la mwezi wachisanu ndi chiwiri, muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse. Muzichita madyerero a Yehova masiku asanu ndi awiri.
And on the fifteenth day of the seventh month you have a holy convocation; you do no servile work; and you have celebrated a festival to YHWH [for] seven days,
13 Muzipereka nsembe yotentha pa moto, kuti izikhala fungo lokoma kwa Yehova, nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna khumi ndi atatu, nkhosa zazimuna ziwiri, ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
and have brought a burnt-offering near, a fire-offering of refreshing fragrance, to YHWH: thirteen bullocks, sons of the herd, two rams, fourteen lambs, sons of a year; they are perfect ones;
14 Pa mwana wangʼombe aliyense mwa ana angʼombe aamuna khumi ndi atatu aja, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta. Pa nkhosa iliyonse mwa nkhosa ziwiri zija, mukonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu awiri.
and their present of flour mixed with oil: three-tenth parts for one bullock, for the thirteen bullocks, two-tenth parts for one ram, for the two rams,
15 Pa mwana wankhosa aliyense mwa ana ankhosa aamuna khumi ndi anayiwo, muzipereka chakudya cha kilogalamu imodzi.
and a tenth—a tenth part for one lamb, for the fourteen lambs;
16 Muziperekanso mbuzi yayimuna imodzi kuti izikhale nsembe yopepesera machimo, kuwonjezera pa nsembe zopsereza za tsiku ndi tsiku zija pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
and one kid of the goats [for] a sin-offering, apart from the continual burnt-offering, its present, and its drink-offering.
17 “‘Pa tsiku lachiwiri muzipereka ana angʼombe aamuna khumi ndi awiri aja, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi aja, zonse zopanda chilema.
And on the second day: twelve bullocks, sons of the herd, two rams, fourteen lambs, sons of a year, perfect ones;
18 Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka zopereka za chakudya ndi za chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
and their present and their drink-offerings for the bullocks, for the rams, and for the sheep, in their number, according to the ordinance;
19 Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
and one kid of the goats [for] a sin-offering, apart from the continual burnt-offering, and its present, and their drink-offerings.
20 “‘Pa tsiku lachitatu muzipereka ngʼombe zazimuna khumi ndi imodzi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
And on the third day: eleven bullocks, two rams, fourteen lambs, sons of a year, perfect ones;
21 Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka zopereka za chakudya ndi za chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
and their present and their drink-offerings for the bullocks, for the rams, and for the lambs, in their number, according to the ordinance;
22 Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
and one goat [for] a sin-offering, apart from the continual burnt-offering, and its present, and its drink-offering.
23 “‘Pa tsiku lachinayi muzipereka ngʼombe zazimuna khumi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
And on the fourth day: ten bullocks, two rams, fourteen lambs, sons of a year, perfect ones;
24 Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
their present and their drink-offerings for the bullocks, for the rams, and for the lambs, in their number, according to the ordinance;
25 Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
and one kid of the goats [for] a sin-offering, apart from the continual burnt-offering, its present, and its drink-offering.
26 “‘Pa tsiku lachisanu muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi zinayi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
And on the fifth day: nine bullocks, two rams, fourteen lambs, sons of a year, perfect ones;
27 Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
and their present and their drink-offerings for the bullocks, for the rams, and for the lambs, in their number, according to the ordinance;
28 Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
and one goat [for] a sin-offering, apart from the continual burnt-offering, and its present, and its drink-offering.
29 “‘Pa tsiku lachisanu ndi chimodzi muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi zitatu, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
And on the sixth day: eight bullocks, two rams, fourteen lambs, sons of a year, perfect ones;
30 Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
and their present and their drink-offerings for the bullocks, for the rams, and for the lambs, in their number, according to the ordinance;
31 Muziperekenso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
and one goat [for] a sin-offering, apart from the continual burnt-offering, its present, and its drink-offering.
32 “‘Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa amuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
And on the seventh day: seven bullocks, two rams, fourteen lambs, sons of a year, perfect ones;
33 Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
and their present and their drink-offerings for the bullocks, for the rams, and for the lambs, in their number, according to the ordinance;
34 Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
and one goat [for] a sin-offering, apart from the continual burnt-offering, its present, and its drink-offering.
35 “‘Pa tsiku lachisanu ndi chitatu muzichita msonkhano ndipo musamagwire ntchito iliyonse.
On the eighth day you have a restraint; you do no servile work;
36 Muzipereka chopereka chotentha pa moto monga fungo lokoma kwa Yehova, nsembe yopsereza ya ngʼombe imodzi yayimuna, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa amuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
and you have brought a burnt-offering near, a fire-offering of refreshing fragrance, to YHWH: one bullock, one ram, seven lambs, sons of a year, perfect ones;
37 Pamodzi ndi ngʼombe yayimunayo, nkhosa yayimunayo ndi ana ankhosawo, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
their present and their drink-offerings for the bullock, for the ram, and for the lambs, in their number, according to the ordinance;
38 Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
and one goat [for] a sin-offering, apart from the continual burnt-offering, and its present, and its drink-offering.
39 “‘Kuwonjezera pa zopereka zimene munalumbirira ndi pa zopereka zanu zaufulu, muzipereka zimenezi kwa Yehova pa masiku osankhika a chikondwerero chanu. Nsembe zanu zachakumwa ndi nsembe zanu zachiyanjano.’”
You prepare these to YHWH in your appointed times—apart from your vows and your free-will offerings—for your burnt-offerings, and for your presents, and for your drink-offerings, and for your peace-offerings.”
40 Mose anawuza Aisraeli zonse zimene Yehova anamulamulira.
And Moses speaks to the sons of Israel according to all that YHWH has commanded Moses.

< Numeri 29 >