< Numeri 29 >

1 “‘Pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiwiri muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse. Ili ndi tsiku limene muziliza malipenga.
Og i den syvende Maaned, paa den første Dag i Maaneden, skal der være eder en hellig Sammenkaldelse, I skulle ingen Arbejdsgerning gøre, det skal være eder en Basunklangs Dag.
2 Muzipereka mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri a chaka chimodzi wopanda chilema monga nsembe zopsereza, fungo lokoma kwa Yehova.
Og I skulle gøre Brændoffer til en behagelig Lugt for Herren: Een ung Tyr, een Væder, syv Lam, aargamle, uden Lyde;
3 Pa ngʼombe yayimuna iliyonse, muzipereka chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta. Pa nkhosa yayimuna iliyonse muzipereka makilogalamu awiri.
og deres Madoffer, Mel, blandet med Olie, tre Tiendeparter til Tyren og to Tiendeparter til Væderen
4 Pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiri aja muzipereka kilogalamu imodzi.
og en Tiendepart til hvert Lam af de syv Lam;
5 Muziperekanso mbuzi yayimuna kuti izikhala nsembe yopepesera machimo anu.
og een Gedebuk til Syndoffer, til at gøre Forligelse for eder;
6 Izi ndi zowonjezera pa nsembe zopsereza za mwezi ndi mwezi komanso za tsiku ndi tsiku pamodzi ndi zopereka za chakudya ndi zopereka za chakumwa potsata malamulo ake. Izi ndi zopereka zotentha pa moto, zoperekedwa kwa Yehova, fungo lokoma.
foruden Maaneds Brændofret og dets Madoffer, og det bestandige Brændoffer og dets Madoffer og deres Drikofre, efter deres Vis; til en behagelig Lugt, et Ildoffer for Herren.
7 “‘Pa tsiku lakhumi la mwezi wachisanu ndi chiwiriwu, muzichita msonkhano wopatulika. Muzisala zakudya ndipo musamagwire ntchito.
Og paa den tiende Dag i denne syvende Maaned skal der være eder en hellig Sammenkaldelse, og I skulle ydmyge eders Sjæle, I skulle intet Arbejde gøre.
8 Muzipereka kwa Yehova nsembe yopsereza, yotulutsa fungo lokoma lokondweretsa Yehovayo; ngʼombe yayimuna imodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri a chaka chimodzi. Zimenezi zizikhala zopanda chilema.
Men I skulle ofre Brændoffer for Herren til en behagelig Lugt: Een ung Tyr, een Væder, syv Lam, aargamle; uden Lyde skulle de være eder;
9 Pa ngʼombe yayimuna iliyonse, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; pa nkhosa yayimuna iliyonse makilogalamu awiri;
og deres Madoffer, Mel, blandet med Olie, tre Tiendeparter til Tyren, to Tiendeparter til den ene Væder,
10 kilogalamu imodzi pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiriwo.
een Tiendepart til hvert Lam af de syv Lam;
11 Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna kuti izikhala nsembe yopepesera machimo, kuwonjezera pa nsembe yopepesera machimo ya pa tsiku la mwambo ija, kuwonjezanso pa nsembe zopsereza za tsiku ndi tsiku zija, pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi cha chakumwa.
een Gedebuk til Syndoffer, foruden Forligelsens Syndoffer og det bestandige Brændoffer og dets Madoffer og deres Drikofre.
12 “‘Pa tsiku la mwezi wachisanu ndi chiwiri, muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse. Muzichita madyerero a Yehova masiku asanu ndi awiri.
Og paa den femtende Dag i den syvende Maaned skal der være eder en hellig Sammenkaldelse; I skulle ingen Arbejdsgerning gøre, og I skulle højtideligholde Højtid for Herren i syv Dage.
13 Muzipereka nsembe yotentha pa moto, kuti izikhala fungo lokoma kwa Yehova, nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna khumi ndi atatu, nkhosa zazimuna ziwiri, ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
Og I skulle ofre Brændoffer, et Ildoffer til en behagelig Lugt for Herren: Tretten unge Tyre, to Vædre, fjorten Lam, aargamle; de skulle være uden Lyde;
14 Pa mwana wangʼombe aliyense mwa ana angʼombe aamuna khumi ndi atatu aja, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta. Pa nkhosa iliyonse mwa nkhosa ziwiri zija, mukonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu awiri.
og deres Madoffer, Mel, blandet med Olie, tre Tiendeparter til hver Tyr af de tretten Tyre, to Tiendeparter til hver Væder af de to Vædre
15 Pa mwana wankhosa aliyense mwa ana ankhosa aamuna khumi ndi anayiwo, muzipereka chakudya cha kilogalamu imodzi.
og een Tiendepart til hvert Lam af de fjorten Lam;
16 Muziperekanso mbuzi yayimuna imodzi kuti izikhale nsembe yopepesera machimo, kuwonjezera pa nsembe zopsereza za tsiku ndi tsiku zija pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
dertil een Gedebuk til Syndoffer, foruden det bestandige Brændoffer, dets Madoffer og dets Drikoffer.
17 “‘Pa tsiku lachiwiri muzipereka ana angʼombe aamuna khumi ndi awiri aja, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi aja, zonse zopanda chilema.
Og paa den anden Dag tolv unge Tyre, to Vædre, fjorten Lam, aargamle, uden Lyde,
18 Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka zopereka za chakudya ndi za chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
og deres Madofrer og deres Drikofre til Tyrene, til Vædrene og til Lammene efter deres Tal, paa sædvanlig Vis;
19 Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
dertil een Gedebuk til Syndoffer, foruden det bestandige Brændoffer og dets Madoffer og deres Drikofre.
20 “‘Pa tsiku lachitatu muzipereka ngʼombe zazimuna khumi ndi imodzi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
Og paa den tredje Dag elleve Tyre, to Vædre, fjorten Lam, aargamle, uden Lyde,
21 Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka zopereka za chakudya ndi za chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
og deres Madoffer og deres Drikofre til Tyrene, til Vædrene og til Lammene efter deres Tal, paa sædvanlig Vis;
22 Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
dertil een Gedebuk til Syndoffer, foruden det bestandige Brændoffer og dets Madoffer og dets Drikoffer.
23 “‘Pa tsiku lachinayi muzipereka ngʼombe zazimuna khumi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
Og paa den fjerde Dag ti Tyre, to Vædre, fjorten Lam, aargamle, uden Lyde,
24 Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
deres Madoffer og deres Drikofre til Tyrene, til Vædrene og til Lammene efter deres Tal, paa sædvanlig Vis;
25 Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
dertil een Gedebuk til Syndoffer, foruden det bestandige Brændoffer og dets Madoffer og dets Drikoffer.
26 “‘Pa tsiku lachisanu muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi zinayi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
Og paa den femte Dag ni Tyre, to Vædre, fjorten Lam, aargamle, uden Lyde,
27 Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
og deres Madoffer og deres Drikofre til Tyrene, til Vædrene og til Lammene efter deres Tal, paa sædvanlig Vis;
28 Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
dertil een Gedebuk til Syndoffer, foruden det bestandige Brændoffer og dets Madoffer og dets Drikoffer.
29 “‘Pa tsiku lachisanu ndi chimodzi muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi zitatu, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
Og paa den sjette Dag otte Tyre, to Vædre, fjorten Lam, aargamle, uden Lyde,
30 Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
og deres Madoffer og deres Drikofre til Tyrene, til Vædrene og til Lammene efter deres Tal, paa sædvanlig Vis;
31 Muziperekenso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
dertil een Gedebuk til Syndoffer, foruden det bestandige Brændoffer, dets Madoffer og dets Drikoffer.
32 “‘Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa amuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
Og paa den syvende Dag syv Tyre, to Vædre, fjorten Lam, aargamle, uden Lyde,
33 Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
og deres Madoffer og deres Drikofre til Tyrene, til Vædrene og til Lammene efter deres Tal, paa deres sædvanlige Vis;
34 Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
dertil een Gedebuk til Syndoffer, foruden det bestandige Brændoffer, dets Madoffer og dets Drikofre.
35 “‘Pa tsiku lachisanu ndi chitatu muzichita msonkhano ndipo musamagwire ntchito iliyonse.
Paa den ottende Dag skal der være eder en Slutningshøjtid, da skulle I ingen Arbejdsgerning gøre.
36 Muzipereka chopereka chotentha pa moto monga fungo lokoma kwa Yehova, nsembe yopsereza ya ngʼombe imodzi yayimuna, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa amuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema.
Og I skulle ofre Brændoffer, et Ildoffer til en behagelig Lugt for Herren, een Tyr, een Væder, syv Lam, aargamle, uden Lyde,
37 Pamodzi ndi ngʼombe yayimunayo, nkhosa yayimunayo ndi ana ankhosawo, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo.
deres Madoffer og deres Drikoffer til Tyren, til Vædrene og til Lammene efter deres Tal, paa sædvanlig Vis,
38 Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.
dertil een Gedebuk til Syndoffer, foruden det bestandige Brændoffer og dets Madoffer og dets Drikoffer.
39 “‘Kuwonjezera pa zopereka zimene munalumbirira ndi pa zopereka zanu zaufulu, muzipereka zimenezi kwa Yehova pa masiku osankhika a chikondwerero chanu. Nsembe zanu zachakumwa ndi nsembe zanu zachiyanjano.’”
Disse Ting skulle I gøre for Herren paa eders bestemte Tider, foruden eders Løfter og eders frivillige Gaver, hvad enten det er eders Brændofre eller eders Madofre eller eders Drikofre eller eders Takofre.
40 Mose anawuza Aisraeli zonse zimene Yehova anamulamulira.
Og Mose sagde til Israels Børn alt dette, ligesom Herren havde befalet Mose.

< Numeri 29 >