< Numeri 28 >
1 Yehova anawuza Mose kuti,
Och Herren talade med Mose, och sade:
2 “Lamula Aisraeli kuti, ‘Onetsetsani kuti mukupereka kwa Ine pa nthawi yoyikika, chopereka cha chakudya chotentha pa moto monga fungo lokoma kwa Ine.’
Bjud Israels barnom, och säg till dem: Mitt bröds offer, hvilket mitt offer är till en söt lukt, skolen I hålla i sinom tid, så att I mig det offren.
3 Awuze kuti, ‘Nsembe ya chakudya imene muzipereka pa moto kwa Yehova tsiku ndi tsiku ndi iyi: Ana ankhosa a chaka chimodzi awiri, wopanda chilema.
Och säg till dem: Dessa äro de offer, som I offra skolen Herranom: årsgamla lamb, de som utan vank äro, dagliga tu till dagligit bränneoffer;
4 Mmawa muzipereka mwana wankhosa mmodzi ndipo winayo madzulo.
Ett lamb om morgonen, det andra om aftonen.
5 Muziperekanso kilogalamu imodzi ya ufa wosalala wosakaniza ndi lita imodzi ya mafuta a olivi.
Dertill tiondeparten af ett epha semlomjöl till spisoffer, blandadt med oljo, den stött är, en fjerdepart af ett hin.
6 Iyi ndi nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku imene analamula pa phiri la Sinai kuti ikhale fungo lokoma, nsembe yopsereza pa moto yopereka kwa Yehova.
Det är ett dagligit bränneoffer, det I uppå Sinai berg offraden, till en söt lukt af ett offer Herranom.
7 Chopereka chachakumwa chikhale lita imodzi yachakumwa chaukali pa nkhosa iliyonse. Muzithira pamalo opatulika, kupereka kwa Yehova.
Dertill dess drickoffer, ju till hvart lambet en fjerdedel af ett hin; och det skall offradt varda i helgedomenom, obemängdt Herranom.
8 Muzipereka mwana wankhosa winayo madzulo, pamodzi ndi chopereka chachakudya monga poyamba paja ndi chopereka chachakumwa monga mmawa. Ichi ndi chopereka chachakudya, fungo lokoma kwa Yehova.’”
Det andra lambet skall du göra om aftonen, såsom spisoffret om morgonen, och dess drickoffer till en söt lukts offer Herranom.
9 “‘Pa tsiku la Sabata, muzipereka nsembe ana ankhosa awiri a chaka chimodzi wopanda chilema, pamodzi ndi chopereka chachakumwa ndi chopereka chachakudya chokwana makilogalamu awiri a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta.
Men om Sabbathsdagen tu årsgamla lamb utan vank, och två tiungar af semlomjöl till spisoffer, blandadt med oljo, och dess drickoffer.
10 Iyi ndi nsembe yopsereza ya pa Sabata iliyonse, kuwonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse ndi chopereka chake chachakumwa.’”
Det är hvars Sabbathens bränneoffer, utöfver det dagliga bränneoffret, med sitt drickoffer.
11 “Pa tsiku loyamba la mwezi uliwonse muzipereka kwa Yehova nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa yayimuna imodzi, ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi, onse wopanda chilema.
Men på första dagen i edra månader skolen I offra Herranom ett bränneoffer, två unga stutar, en vädur, sju årsgamla lamb utan vank;
12 Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pakhale chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; ndi nkhosa yayimuna, chopereka cha chakudya cha makilogalamu awiri a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta;
Och ju tre tiungar semlomjöl till spisoffer, blandadt med oljo, till en stut, och två tiungar semlomjöl till spisoffer, blandadt med oljo, till en vädur;
13 ndipo pa mwana wankhosa aliyense, chopereka cha ufa wa kilogalamu imodzi ya ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, izi ndi za nsembe yopsereza, fungo lokoma, nsembe yotentha pa moto ya kwa Yehova.
Och ju en tiung semlomjöl till spisoffer, med oljo blandadt, till ett lamb; det är bränneoffret till en söt lukt, ett offer Herranom.
14 Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pakhale chopereka cha chakumwa cha malita awiri a vinyo; ndipo pa nkhosa yayimuna, lita limodzi ndi theka, ndipo pa mwana wankhosa, lita limodzi. Iyi ndi nsembe yopsereza ya mwezi ndi mwezi yoperekedwa pa mwezi watsopano mʼkati mwa chaka.
Och deras drickoffer skall vara, ett halft hin vin till stuten, en tredjedel af ett hin till väduren, en fjerdedel af ett hin till lambet; det är bränneoffret till hvar månad om året.
15 Powonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse ndi chopereka chake cha chakumwa, mbuzi yayimuna imodzi iperekedwe kwa Yehova ngati nsembe yopepesera machimo.
Dertill skall man göra en getabock till ett syndoffer Herranom, öfver det dagliga bränneoffret, och dess drickoffer.
16 “‘Pa tsiku la 14 la mwezi woyamba muzichita Paska wa Yehova.
Men på fjortonde dagenom i första månaden är Passah Herranom.
17 Pa tsiku la 15 la mwezi womwewo pazikhala chikondwerero. Muzidya buledi wopanda yisiti kwa masiku asanu ndi awiri.
Och uppå femtonde dagenom i samma månaden är högtid; i sju dagar skall man äta osyradt bröd.
18 Pa tsiku loyamba muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse.
Den förste dagen skall kallas helig, att I sammankommen; intet tjenstearbete skolen I göra deruppå.
19 Koma muzipereka kwa Yehova nsembe yotentha pa moto, nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri aamuna a chaka chimodzi, onsewo wopanda chilema.
Och skolen I göra Herranom bränneoffer, två unga stutar, en vädur, sju årsgamla lamb utan vank;
20 Pamodzi ndi ngʼombe yayimuna iliyonse, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; makilogalamu awiri pa nkhosa yayimuna iliyonse.
Med deras spisoffer, tre tiungar semlomjöl, blandadt med oljo, till hvar stuten, och två tiungar till väduren;
21 Kilogalamu imodzi pa mwana wankhosa aliyense mwa ana ankhosa asanu ndi awiri aja.
Och ju en tiung till hvart af de sju lamben.
22 Muziphatikizapo mbuzi yayimuna monga nsembe yopepesera machimo anu.
Dertill en bock till syndoffer, på det I skolen försonade varda.
23 Muzikonza zimenezi nthawi zonse, powonjezera pa nsembe yopsereza ya mmawa.
Och det skolen I göra om morgonen, förutan det bränneoffret, som ett dagligit bränneoffer är.
24 Motere muzikonza chakudya cha nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pa masiku asanu ndi awiri ngati fungo lokomera Yehova. Zimenezi ziziperekedwa kuwonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse pamodzi ndi nsembe yachakumwa.
Efter detta sättet skolen I hvar dag i de sju dagar offra bröd till en söt lukts offer Herranom, till det dagliga bränneoffret, dertill dess drickoffer.
25 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse.
Och den sjunde dagen skall kallas helig ibland eder, att I sammankommen; intet tjenstearbete skolen I göra deruppå.
26 “‘Pa tsiku la zipatso zoyambirira kucha, pamene mukupereka chopereka cha chakudya chatsopano kwa Yehova, pa nthawi ya chikondwerero cha Masabata, muzichita msonkhano wopatulika ndipo musagwire ntchito zolemetsa.
Och förstlingens dag, då I offren det nya spisoffret Herranom, när edra veckor äro framledna, skall helig kallas, att I sammankommen; intet tjenstearbete skolen I göra deruppå.
27 Muzipereka nsembe zopsereza za ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa imodzi yayimuna ndi ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi monga fungo lokomera Yehova.
Och skolen I göra Herranom bränneoffer till en söt lukt, två unga stutar, en vädur, sju årsgamla lamb;
28 Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pazikhala chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, pa nkhosa yayimuna iliyonse makilogalamu awiri.
Med deras spisoffer, tre tiungar semlomjöl, blandadt med oljo, till hvar stuten, två tiungar till väduren;
29 Ndipo pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiri aja, kilogalamu imodzi.
Och ju en tiung till hvart och ett af de sju lamben;
30 Muziperekanso mbuzi yayimuna imodzi kuti izikhala nsembe yopepesera machimo anu.
Och en getabock till att försona eder.
31 Muzipereka zimenezi pamodzi ndi zopereka za zakumwa ndi nsembe yake ya chakudya. Onetsetsani kuti nyamazo zilibe chilema.
Detta skolen I göra, förutan det dagliga bränneoffret med sitt spisoffer; utan vank skall det vara; dertill deras drickoffer.