< Numeri 28 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
Yavé habló a Moisés:
2 “Lamula Aisraeli kuti, ‘Onetsetsani kuti mukupereka kwa Ine pa nthawi yoyikika, chopereka cha chakudya chotentha pa moto monga fungo lokoma kwa Ine.’
Manda a los hijos de Israel: Tendrán cuidado de presentar mi ofrenda, mi alimento por medio de mis sacrificios quemados de olor que me apacigua, en su tiempo señalado.
3 Awuze kuti, ‘Nsembe ya chakudya imene muzipereka pa moto kwa Yehova tsiku ndi tsiku ndi iyi: Ana ankhosa a chaka chimodzi awiri, wopanda chilema.
Y les dirás: El sacrificio quemado que presentarán a Yavé cada día será dos corderos añales sin defecto para el holocausto continuo.
4 Mmawa muzipereka mwana wankhosa mmodzi ndipo winayo madzulo.
Ofrecerán el primer cordero en la mañana, y el segundo, al llegar la noche.
5 Muziperekanso kilogalamu imodzi ya ufa wosalala wosakaniza ndi lita imodzi ya mafuta a olivi.
La ofrenda vegetal será 2,2 litros de flor de harina, amasada con 0,9 litros de aceite de olivas machacadas.
6 Iyi ndi nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku imene analamula pa phiri la Sinai kuti ikhale fungo lokoma, nsembe yopsereza pa moto yopereka kwa Yehova.
Es un holocausto continuo, un sacrificio quemado a Yavé que fue ordenado en la Montaña Sinaí como olor que apacigua, una ofrenda ofrecida por fuego a Yavé.
7 Chopereka chachakumwa chikhale lita imodzi yachakumwa chaukali pa nkhosa iliyonse. Muzithira pamalo opatulika, kupereka kwa Yehova.
Su libación de vino será 0,9 litros con cada cordero. En el Santuario derramarás la libación de licor fuerte a Yavé.
8 Muzipereka mwana wankhosa winayo madzulo, pamodzi ndi chopereka chachakudya monga poyamba paja ndi chopereka chachakumwa monga mmawa. Ichi ndi chopereka chachakudya, fungo lokoma kwa Yehova.’”
El segundo cordero lo ofrecerán al llegar la noche. Lo harán como el sacrificio de la mañana con su libación. Es un sacrificio quemado de olor que apacigua a Yavé.
9 “‘Pa tsiku la Sabata, muzipereka nsembe ana ankhosa awiri a chaka chimodzi wopanda chilema, pamodzi ndi chopereka chachakumwa ndi chopereka chachakudya chokwana makilogalamu awiri a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta.
Pero el día sábado ofrecerán dos corderos añales sin defecto, y 4,4 litros de flor de harina amasada con aceite, como ofrenda vegetal con su libación.
10 Iyi ndi nsembe yopsereza ya pa Sabata iliyonse, kuwonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse ndi chopereka chake chachakumwa.’”
Este es el holocausto de cada sábado, además del holocausto continuo y su libación.
11 “Pa tsiku loyamba la mwezi uliwonse muzipereka kwa Yehova nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa yayimuna imodzi, ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi, onse wopanda chilema.
Al principio de cada mes ofrecerán en holocausto a Yavé dos becerros de la manada vacuna, un carnero y siete corderos añales sin defecto,
12 Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pakhale chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; ndi nkhosa yayimuna, chopereka cha chakudya cha makilogalamu awiri a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta;
6,6 litros de flor de harina amasada con aceite, como ofrenda vegetal con cada becerro, y 4,4 litros de flor de harina amasada con aceite, como ofrenda vegetal con el carnero,
13 ndipo pa mwana wankhosa aliyense, chopereka cha ufa wa kilogalamu imodzi ya ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, izi ndi za nsembe yopsereza, fungo lokoma, nsembe yotentha pa moto ya kwa Yehova.
y 2,2 litros de flor de harina amasada con aceite, como ofrenda vegetal con cada cordero. Es holocausto de olor que apacigua, sacrificio quemado a Yavé.
14 Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pakhale chopereka cha chakumwa cha malita awiri a vinyo; ndipo pa nkhosa yayimuna, lita limodzi ndi theka, ndipo pa mwana wankhosa, lita limodzi. Iyi ndi nsembe yopsereza ya mwezi ndi mwezi yoperekedwa pa mwezi watsopano mʼkati mwa chaka.
Sus libaciones de vino son: 1,8 litros por cada becerro, 1,2 litros por el carnero y 0,9 litros por cada cordero. Este es el holocausto de cada mes para todos los meses del año.
15 Powonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse ndi chopereka chake cha chakumwa, mbuzi yayimuna imodzi iperekedwe kwa Yehova ngati nsembe yopepesera machimo.
También se ofrecerá a Yavé un macho cabrío como sacrificio por el pecado, además del holocausto continuo con su libación.
16 “‘Pa tsiku la 14 la mwezi woyamba muzichita Paska wa Yehova.
En el mes primero, el día 14 del mes, es Pascua de Yavé.
17 Pa tsiku la 15 la mwezi womwewo pazikhala chikondwerero. Muzidya buledi wopanda yisiti kwa masiku asanu ndi awiri.
El día 15 de ese mes será la fiesta solemne. Durante siete días se comerán panes sin levadura.
18 Pa tsiku loyamba muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse.
El primer día habrá una santa convocación. No harán obra servil.
19 Koma muzipereka kwa Yehova nsembe yotentha pa moto, nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri aamuna a chaka chimodzi, onsewo wopanda chilema.
Ofrecerán un sacrificio quemado en holocausto a Yavé de dos becerros de la manada vacuna, un carnero y siete corderos añales, y serán perfectos.
20 Pamodzi ndi ngʼombe yayimuna iliyonse, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; makilogalamu awiri pa nkhosa yayimuna iliyonse.
Su ofrenda vegetal será de harina amasada con aceite, 6,6 litros por cada becerro y 4,4 litros por el carnero.
21 Kilogalamu imodzi pa mwana wankhosa aliyense mwa ana ankhosa asanu ndi awiri aja.
Ofrecerás 2,2 litros por cada uno de los siete corderos
22 Muziphatikizapo mbuzi yayimuna monga nsembe yopepesera machimo anu.
y un macho cabrío como sacrificio por el pecado para hacer sacrificio que apacigua a favor de ustedes.
23 Muzikonza zimenezi nthawi zonse, powonjezera pa nsembe yopsereza ya mmawa.
Ofrecerán éstos, además del holocausto de la mañana, que es el holocausto continuo.
24 Motere muzikonza chakudya cha nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pa masiku asanu ndi awiri ngati fungo lokomera Yehova. Zimenezi ziziperekedwa kuwonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse pamodzi ndi nsembe yachakumwa.
Harán estas cosas cada uno de los siete días. Es alimento y sacrificio quemado de olor que apacigua a Yavé. Se ofrecerán además del holocausto continuo con su libación.
25 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse.
El séptimo día tendrán una santa convocación. No harán obra servil.
26 “‘Pa tsiku la zipatso zoyambirira kucha, pamene mukupereka chopereka cha chakudya chatsopano kwa Yehova, pa nthawi ya chikondwerero cha Masabata, muzichita msonkhano wopatulika ndipo musagwire ntchito zolemetsa.
En el día de las primicias, cuando ofrezcan una ofrenda vegetal nueva a Yavé en su fiesta solemne de las semanas, tendrán una santa convocación. No harán obra servil.
27 Muzipereka nsembe zopsereza za ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa imodzi yayimuna ndi ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi monga fungo lokomera Yehova.
Ofrecerán en holocausto, en olor que apacigua a Yavé, dos becerros de la manada vacuna, un carnero, siete corderos añales,
28 Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pazikhala chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, pa nkhosa yayimuna iliyonse makilogalamu awiri.
y la ofrenda vegetal de ellos, flor de harina amasada con aceite, 6,6 litros por cada becerro, 4,4 litros por el carnero
29 Ndipo pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiri aja, kilogalamu imodzi.
y 2,2 litros por cada uno de los siete corderos,
30 Muziperekanso mbuzi yayimuna imodzi kuti izikhala nsembe yopepesera machimo anu.
además de un macho cabrío para hacer sacrificio de olor que apacigua por ustedes.
31 Muzipereka zimenezi pamodzi ndi zopereka za zakumwa ndi nsembe yake ya chakudya. Onetsetsani kuti nyamazo zilibe chilema.
Esto ofrecerán, además del holocausto continuo y de su ofrenda vegetal. Los ofrecerán sin defecto con su libación.

< Numeri 28 >