< Numeri 28 >
1 Yehova anawuza Mose kuti,
UThixo wathi kuMosi,
2 “Lamula Aisraeli kuti, ‘Onetsetsani kuti mukupereka kwa Ine pa nthawi yoyikika, chopereka cha chakudya chotentha pa moto monga fungo lokoma kwa Ine.’
“Phana abako-Israyeli umlayo lo uthi kubo, ‘Nanzelelani ukuthi lingilethele ngesikhathi esimisiweyo imihlatshelo yokudla, njengephunga elimnandi kimi.’
3 Awuze kuti, ‘Nsembe ya chakudya imene muzipereka pa moto kwa Yehova tsiku ndi tsiku ndi iyi: Ana ankhosa a chaka chimodzi awiri, wopanda chilema.
Tshono uthi kubo: ‘Lo ngumnikelo owenziwe ngomlilo okumele liwuse kuThixo: amazinyane emvu amabili angelasici njalo alomnyaka owodwa ezelwe, kube ngumnikelo wokutshiswa wansuku zonke.
4 Mmawa muzipereka mwana wankhosa mmodzi ndipo winayo madzulo.
Linikele izinyane lemvu elilodwa ekuseni beselinikela elinye kusihlwa,
5 Muziperekanso kilogalamu imodzi ya ufa wosalala wosakaniza ndi lita imodzi ya mafuta a olivi.
ndawonye lomnikelo wamabele ayisilinganiso sokwetshumi kwehefa yefulawa ecolekileyo exutshaniswe lengxenye yesine yehini yamafutha ahluzwe ema-oliveni.
6 Iyi ndi nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku imene analamula pa phiri la Sinai kuti ikhale fungo lokoma, nsembe yopsereza pa moto yopereka kwa Yehova.
Lo ngumnikelo wokutshiswa wezikhathi zonke owamiswa entabeni yaseSinayi njengephunga elimnandi, umnikelo owenzelwa uThixo ngomlilo.
7 Chopereka chachakumwa chikhale lita imodzi yachakumwa chaukali pa nkhosa iliyonse. Muzithira pamalo opatulika, kupereka kwa Yehova.
Umnikelo wokunathwayo ozakwenziwa ndawonye lengxenye yesine yehini yokunathwayo okulemvubelo ndawonye lezinyane lemvu. Thela umnikelo wokunathwayo phambi kukaThixo endlini engcwele.
8 Muzipereka mwana wankhosa winayo madzulo, pamodzi ndi chopereka chachakudya monga poyamba paja ndi chopereka chachakumwa monga mmawa. Ichi ndi chopereka chachakudya, fungo lokoma kwa Yehova.’”
Unikele izinyane lesibili kusihlwa ndawonye lomnikelo wamabele ofanayo lomnikelo wokunathwayo ofana lalowo owunikele ekuseni. Lo ngumhlatshelo wokudla, iphunga elimnandi kuThixo.’”
9 “‘Pa tsiku la Sabata, muzipereka nsembe ana ankhosa awiri a chaka chimodzi wopanda chilema, pamodzi ndi chopereka chachakumwa ndi chopereka chachakudya chokwana makilogalamu awiri a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta.
“‘Ngosuku lweSabatha, ulungise umnikelo wamazinyane emvu amabili alomnyaka owodwa ezelwe engelasici, ndawonye lomnikelo wokunathwayo kanye lomnikelo wamabele ozingxenye ezimbili zehefa etshumini zefulawa ecolekileyo exutshaniswe lamafutha.
10 Iyi ndi nsembe yopsereza ya pa Sabata iliyonse, kuwonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse ndi chopereka chake chachakumwa.’”
Lo ngumnikelo wokutshiswa kuwo wonke amasabatha, phezu komnikelo wokutshiswa lowokunathwayo ojayelekileyo.’”
11 “Pa tsiku loyamba la mwezi uliwonse muzipereka kwa Yehova nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa yayimuna imodzi, ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi, onse wopanda chilema.
“‘Ngosuku lwakuqala inyanga zonke, letha kuThixo umnikelo wokutshiswa wenkunzi ezingamaguqa ezimbili, inqama eyodwa lamazinyane ezimvu amaduna alomnyaka ezelwe, angelasici.
12 Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pakhale chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; ndi nkhosa yayimuna, chopereka cha chakudya cha makilogalamu awiri a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta;
Inkunzi eyodwa izahamba lomnikelo wamabele ozingxenye ezintathu etshumini zehefa yefulawa ecolekileyo exutshaniswe lamafutha; inqama izahamba lomnikelo wamabele ayingxenye ezimbili etshumini zehefa yefulawa ecolekileyo exutshaniswe lamafutha;
13 ndipo pa mwana wankhosa aliyense, chopereka cha ufa wa kilogalamu imodzi ya ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, izi ndi za nsembe yopsereza, fungo lokoma, nsembe yotentha pa moto ya kwa Yehova.
izinyane lemvu ngalinye lizahamba lomnikelo wamabele oyingxenye eyodwa etshumini lehefa yefulawa ecolekileyo exutshaniswe lamafutha. Lokhu ngokomnikelo wokutshiswa, iphunga elimnandi, umnikelo owenzelwa uThixo ngomlilo.
14 Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pakhale chopereka cha chakumwa cha malita awiri a vinyo; ndipo pa nkhosa yayimuna, lita limodzi ndi theka, ndipo pa mwana wankhosa, lita limodzi. Iyi ndi nsembe yopsereza ya mwezi ndi mwezi yoperekedwa pa mwezi watsopano mʼkati mwa chaka.
Inkunzi nganye izahamba lomnikelo wokunathwayo okuyingxenye yehini yewayini; lenqama, ingxenye yesithathu yehini; kuthi izinyane lemvu ngalinye lihambe lengxenye yesine yehini. Lo ngumnikelo wokutshiswa owenyanga zonke okumele wenziwe ekuthwaseni kwezinyanga zonke ngomnyaka.
15 Powonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse ndi chopereka chake cha chakumwa, mbuzi yayimuna imodzi iperekedwe kwa Yehova ngati nsembe yopepesera machimo.
Ngaphandle komnikelo wokutshiswa ojayelekileyo kanye lomnikelo wakhona wokunathwayo, impongo eyodwa kumele iphiwe uThixo njengomnikelo wesono.’”
16 “‘Pa tsiku la 14 la mwezi woyamba muzichita Paska wa Yehova.
“‘Ngosuku lwetshumi lane ngenyanga yakuqala kuzakuba lePhasika likaThixo.
17 Pa tsiku la 15 la mwezi womwewo pazikhala chikondwerero. Muzidya buledi wopanda yisiti kwa masiku asanu ndi awiri.
Ngosuku lwetshumi lanhlanu lwaleyonyanga kuzakuba lomkhosi; okwensuku eziyisikhombisa lizakudla isinkwa esingelamvubelo.
18 Pa tsiku loyamba muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse.
Ngosuku lwakuqala lenze umbuthano ongcwele njalo lingenzi imisebenzi yenu yansuku zonke.
19 Koma muzipereka kwa Yehova nsembe yotentha pa moto, nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri aamuna a chaka chimodzi, onsewo wopanda chilema.
Kodwa linikele kuThixo umnikelo owenziwe ngomlilo, umnikelo wokutshiswa owenkunzi ezingamaguqa ezimbili, inqama eyodwa kanye lamazinyane ezimvu amaduna ayisikhombisa alomnyaka owodwa ezelwe, konke kungelasici.
20 Pamodzi ndi ngʼombe yayimuna iliyonse, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; makilogalamu awiri pa nkhosa yayimuna iliyonse.
Kuzakuthi inkunzi nganye liyinikele kanye lomnikelo wamabele ayingxenye yokuthathu etshumini lehefa yefulawa ecolekileyo exutshaniswe lamafutha; kuthi inqama ihambe lokubili etshumini;
21 Kilogalamu imodzi pa mwana wankhosa aliyense mwa ana ankhosa asanu ndi awiri aja.
kuthi-ke linye ngalinye izinyane lemvu kwayisikhombisa, lihambe lokukodwa etshumini.
22 Muziphatikizapo mbuzi yayimuna monga nsembe yopepesera machimo anu.
Akubekhona lempongo eyodwa ukuba ibe ngumnikelo wesono ukuzenzela indlela yokubuyisana.
23 Muzikonza zimenezi nthawi zonse, powonjezera pa nsembe yopsereza ya mmawa.
Phezu kwalokho lungisani umnikelo wokutshiswa wekuseni ojayelekileyo.
24 Motere muzikonza chakudya cha nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pa masiku asanu ndi awiri ngati fungo lokomera Yehova. Zimenezi ziziperekedwa kuwonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse pamodzi ndi nsembe yachakumwa.
Ngaleyondlela nikelani umhlatshelo wokudla okwensuku eziyisikhombisa kube liphunga elimnandi kuThixo; lokhu kumele kulungiswe kusengezelela umnikelo ojayelekileyo wokutshiswa kanye lomnikelo wakho wokunathwayo.
25 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse.
Ngosuku lwesikhombisa lizakuba lombuthano ongcwele njalo lingenzi imisebenzi yenu yansuku zonke.’”
26 “‘Pa tsiku la zipatso zoyambirira kucha, pamene mukupereka chopereka cha chakudya chatsopano kwa Yehova, pa nthawi ya chikondwerero cha Masabata, muzichita msonkhano wopatulika ndipo musagwire ntchito zolemetsa.
“‘Ngosuku lwezithelo zakuqala, nxa lisethula kuThixo umnikelo wamabele amatsha ngesikhathi soMkhosi wamaViki, wobani lombuthano ongcwele njalo lingenzi imisebenzi yensukwini.
27 Muzipereka nsembe zopsereza za ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa imodzi yayimuna ndi ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi monga fungo lokomera Yehova.
Nikelani umnikelo wokutshiswa ngenkunzi ezingamaguqa ezimbili, inqama eyodwa kanye lamazinyane amaduna ayisikhombisa awezimvu alomnyaka owodwa ezelwe kube liphunga elimnandi kuThixo.
28 Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pazikhala chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, pa nkhosa yayimuna iliyonse makilogalamu awiri.
Kuzakuthi inkunzi nganye liyilungise kanye lomnikelo wamabele ayingxenye yokuthathu etshumini lehefa yefulawa ecolekileyo exutshaniswe lamafutha; kuthi inqama ihambe lokubili etshumini;
29 Ndipo pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiri aja, kilogalamu imodzi.
kuthi-ke linye ngalinye izinyane lemvu ngalinye kwayisikhombisa, lihambe lokukodwa etshumini.
30 Muziperekanso mbuzi yayimuna imodzi kuti izikhala nsembe yopepesera machimo anu.
Akubekhona lempongo eyodwa ukuba ibe ngumnikelo wesono ukuzenzela indlela yokubuyisana.
31 Muzipereka zimenezi pamodzi ndi zopereka za zakumwa ndi nsembe yake ya chakudya. Onetsetsani kuti nyamazo zilibe chilema.
Lungisani lokho ndawonye leminikelo yokunathwayo, ukwengezelela eminikelweni ejayelekileyo yokutshiswa kanye lomnikelo wawo wamabele. Nanzelelani ukuthi lezozifuyo azilasici.’”