< Numeri 28 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
És szólt az Örökkévaló Mózeshez, mondván:
2 “Lamula Aisraeli kuti, ‘Onetsetsani kuti mukupereka kwa Ine pa nthawi yoyikika, chopereka cha chakudya chotentha pa moto monga fungo lokoma kwa Ine.’
Parancsold meg Izrael fiainak és mondd nekik: Áldozatomat, kenyeremet, tűzáldozataim szerint, kellemes illatul számomra, őrizzétek meg, hogy bemutassátok nekem a maga idejében.
3 Awuze kuti, ‘Nsembe ya chakudya imene muzipereka pa moto kwa Yehova tsiku ndi tsiku ndi iyi: Ana ankhosa a chaka chimodzi awiri, wopanda chilema.
Mondd meg nekik: Ez a tűzáldozat, melyet az Örökkévalónak bemutassatok: egyéves juhokat, épeket, kettőt napjában égőáldozatul, állandóan.
4 Mmawa muzipereka mwana wankhosa mmodzi ndipo winayo madzulo.
Az egyik juhot készítsd el reggel, a másik, juhot készítsd el estefelé.
5 Muziperekanso kilogalamu imodzi ya ufa wosalala wosakaniza ndi lita imodzi ya mafuta a olivi.
És egy tized éfo lánglisztet ételáldozatul, elegyítve egy negyed hin törött olajjal.
6 Iyi ndi nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku imene analamula pa phiri la Sinai kuti ikhale fungo lokoma, nsembe yopsereza pa moto yopereka kwa Yehova.
Állandó égőáldozat, melyet elkészítettek a Szináj hegyén kellemes illatul, tűzáldozat az Örökkévalónak.
7 Chopereka chachakumwa chikhale lita imodzi yachakumwa chaukali pa nkhosa iliyonse. Muzithira pamalo opatulika, kupereka kwa Yehova.
És italáldozata egy negyed hin egy juhhoz, a szentélyben öntsd ki a részegítő italt italáldozatul az Örökkévalónak.
8 Muzipereka mwana wankhosa winayo madzulo, pamodzi ndi chopereka chachakudya monga poyamba paja ndi chopereka chachakumwa monga mmawa. Ichi ndi chopereka chachakudya, fungo lokoma kwa Yehova.’”
A második juhot pedig készítsd el estefelé; mint a reggelinek ételáldozatát és italáldozatát készítsd el kellemes illatú tűzáldozat gyanánt az Örökkévalónak.
9 “‘Pa tsiku la Sabata, muzipereka nsembe ana ankhosa awiri a chaka chimodzi wopanda chilema, pamodzi ndi chopereka chachakumwa ndi chopereka chachakudya chokwana makilogalamu awiri a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta.
A szombat napján pedig két juhot, egyéveset, épeket, meg két tized lánglisztet ételáldozatul, elegyítve olajjal, és italáldozatát.
10 Iyi ndi nsembe yopsereza ya pa Sabata iliyonse, kuwonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse ndi chopereka chake chachakumwa.’”
A szombat égőáldozata ez szombatonként, az állandó égőáldozat és annak italáldozata mellett.
11 “Pa tsiku loyamba la mwezi uliwonse muzipereka kwa Yehova nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa yayimuna imodzi, ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi, onse wopanda chilema.
Hónapjaitok elején pedig mutassatok be égőáldozatot az Örökkévalónak, két fiatal tulkot és egy kost, hét egyéves juhot, épeket.
12 Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pakhale chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; ndi nkhosa yayimuna, chopereka cha chakudya cha makilogalamu awiri a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta;
És három tized lánglisztet ételáldozatul, elegyítve olajjal, egy tulokhoz és két tized lánglisztet ételáldozatul, elegyítve olajjal, egy koshoz.
13 ndipo pa mwana wankhosa aliyense, chopereka cha ufa wa kilogalamu imodzi ya ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, izi ndi za nsembe yopsereza, fungo lokoma, nsembe yotentha pa moto ya kwa Yehova.
És egy-egy tized lánglisztet ételáldozatul, elegyítve olajjal, egy juhhoz; égőáldozat az, kellemes illatul, tűzáldozat az Örökkévalónak.
14 Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pakhale chopereka cha chakumwa cha malita awiri a vinyo; ndipo pa nkhosa yayimuna, lita limodzi ndi theka, ndipo pa mwana wankhosa, lita limodzi. Iyi ndi nsembe yopsereza ya mwezi ndi mwezi yoperekedwa pa mwezi watsopano mʼkati mwa chaka.
Italáldozataik pedig egy fél hin legyen a tulokhoz, egyharmad hin a koshoz és egynegyed hin bor a juhhoz; ez az újhold égőáldozata újholdanként, az év hónapjai szerint.
15 Powonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse ndi chopereka chake cha chakumwa, mbuzi yayimuna imodzi iperekedwe kwa Yehova ngati nsembe yopepesera machimo.
Meg egy kecskebak vétekáldozat gyanánt az Örökkévalónak; az állandó égőáldozaton kívül készíttessék el és italáldozata.
16 “‘Pa tsiku la 14 la mwezi woyamba muzichita Paska wa Yehova.
Az első hónapban, a hónap tizennegyedik napján, peszách van az Örökkévalónak.
17 Pa tsiku la 15 la mwezi womwewo pazikhala chikondwerero. Muzidya buledi wopanda yisiti kwa masiku asanu ndi awiri.
És tizenötödik napján ennek a hónapnak ünnep; hét napon át kovásztalant egyenek.
18 Pa tsiku loyamba muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse.
Az első napon szent gyülekezés legyen, semmi szolgai munkát ne végezzetek.
19 Koma muzipereka kwa Yehova nsembe yotentha pa moto, nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri aamuna a chaka chimodzi, onsewo wopanda chilema.
És mutassatok be tűzáldozatul égőáldozatot az Örökkévalónak: két fiatal tulkot, meg egy kost és hét egyéves juhot, épek legyenek nálatok.
20 Pamodzi ndi ngʼombe yayimuna iliyonse, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; makilogalamu awiri pa nkhosa yayimuna iliyonse.
Ételáldozatuk pedig lángliszt, elegyítve olajjal; három tizedet a tulokhoz és két tizedet készítsetek a koshoz;
21 Kilogalamu imodzi pa mwana wankhosa aliyense mwa ana ankhosa asanu ndi awiri aja.
egy-egy tizedet készíts egy juhhoz, a hét juhhoz.
22 Muziphatikizapo mbuzi yayimuna monga nsembe yopepesera machimo anu.
És egy bakot vétekáldozatnak, hogy engesztelést szerezzen értetek.
23 Muzikonza zimenezi nthawi zonse, powonjezera pa nsembe yopsereza ya mmawa.
A reggeli égőáldozaton kívül, mely az állandó égőáldozatra való, készítsétek el ezeket.
24 Motere muzikonza chakudya cha nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pa masiku asanu ndi awiri ngati fungo lokomera Yehova. Zimenezi ziziperekedwa kuwonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse pamodzi ndi nsembe yachakumwa.
Ezek szerint készítsétek el naponta, hét napon át a kellemes illatú tűzáldozat kenyerét az Örökkévalónak; az állandó égőáldozat mellett készítsétek el, meg italáldozatát.
25 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse.
És a hetedik napon szent gyülekezés legyen nálatok, semmi szolgai munkát ne végezzetek.
26 “‘Pa tsiku la zipatso zoyambirira kucha, pamene mukupereka chopereka cha chakudya chatsopano kwa Yehova, pa nthawi ya chikondwerero cha Masabata, muzichita msonkhano wopatulika ndipo musagwire ntchito zolemetsa.
A zsengék napján, midőn bemutattok új ételáldozatot az Örökkévalónak, heteitek ünnepén szent gyülekezés legyen nálatok, semmi szolgai munkát ne végezzetek.
27 Muzipereka nsembe zopsereza za ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa imodzi yayimuna ndi ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi monga fungo lokomera Yehova.
Mutassatok be égőáldozatot kellemes illatul az Örökkévalónak: két fiatal tulkot, egy kost, hét juhot, egyéveset.
28 Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pazikhala chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, pa nkhosa yayimuna iliyonse makilogalamu awiri.
És ételáldozatuk gyanánt lánglisztet, elegyítve olajjal, három tizedet egy tulokhoz, két tizedet egy koshoz;
29 Ndipo pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiri aja, kilogalamu imodzi.
egy-egy tizedet egy juhhoz, a hét juhhoz.
30 Muziperekanso mbuzi yayimuna imodzi kuti izikhala nsembe yopepesera machimo anu.
Egy kecskebakot, hogy engesztelést szerezzen értetek.
31 Muzipereka zimenezi pamodzi ndi zopereka za zakumwa ndi nsembe yake ya chakudya. Onetsetsani kuti nyamazo zilibe chilema.
Az állandó égőáldozaton és annak ételáldozatán kívül készítsétek el, épek legyenek nálatok, és azok ételáldozatát.

< Numeri 28 >