< Numeri 28 >
1 Yehova anawuza Mose kuti,
L’Éternel parla à Moïse, et dit: Donne cet ordre aux enfants d’Israël, et dis-leur:
2 “Lamula Aisraeli kuti, ‘Onetsetsani kuti mukupereka kwa Ine pa nthawi yoyikika, chopereka cha chakudya chotentha pa moto monga fungo lokoma kwa Ine.’
Vous aurez soin de me présenter, au temps fixé, mon offrande, l’aliment de mes sacrifices consumés par le feu, et qui me sont d’une agréable odeur.
3 Awuze kuti, ‘Nsembe ya chakudya imene muzipereka pa moto kwa Yehova tsiku ndi tsiku ndi iyi: Ana ankhosa a chaka chimodzi awiri, wopanda chilema.
Tu leur diras: Voici le sacrifice consumé par le feu que vous offrirez à l’Éternel: chaque jour, deux agneaux d’un an sans défaut, comme holocauste perpétuel.
4 Mmawa muzipereka mwana wankhosa mmodzi ndipo winayo madzulo.
Tu offriras l’un des agneaux le matin, et l’autre agneau entre les deux soirs,
5 Muziperekanso kilogalamu imodzi ya ufa wosalala wosakaniza ndi lita imodzi ya mafuta a olivi.
et, pour l’offrande, un dixième d’épha de fleur de farine pétrie dans un quart de hin d’huile d’olives concassées.
6 Iyi ndi nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku imene analamula pa phiri la Sinai kuti ikhale fungo lokoma, nsembe yopsereza pa moto yopereka kwa Yehova.
C’est l’holocauste perpétuel, qui a été offert à la montagne de Sinaï; c’est un sacrifice consumé par le feu, d’une agréable odeur à l’Éternel.
7 Chopereka chachakumwa chikhale lita imodzi yachakumwa chaukali pa nkhosa iliyonse. Muzithira pamalo opatulika, kupereka kwa Yehova.
La libation sera d’un quart de hin pour chaque agneau: c’est dans le lieu saint que tu feras la libation de vin à l’Éternel.
8 Muzipereka mwana wankhosa winayo madzulo, pamodzi ndi chopereka chachakudya monga poyamba paja ndi chopereka chachakumwa monga mmawa. Ichi ndi chopereka chachakudya, fungo lokoma kwa Yehova.’”
Tu offriras le second agneau entre les deux soirs, avec une offrande et une libation semblables à celles du matin; c’est un sacrifice consumé par le feu, d’une agréable odeur à l’Éternel.
9 “‘Pa tsiku la Sabata, muzipereka nsembe ana ankhosa awiri a chaka chimodzi wopanda chilema, pamodzi ndi chopereka chachakumwa ndi chopereka chachakudya chokwana makilogalamu awiri a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta.
Le jour du sabbat, vous offrirez deux agneaux d’un an sans défaut, et, pour l’offrande, deux dixièmes de fleur de farine pétrie à l’huile, avec la libation.
10 Iyi ndi nsembe yopsereza ya pa Sabata iliyonse, kuwonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse ndi chopereka chake chachakumwa.’”
C’est l’holocauste du sabbat, pour chaque sabbat, outre l’holocauste perpétuel et la libation.
11 “Pa tsiku loyamba la mwezi uliwonse muzipereka kwa Yehova nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa yayimuna imodzi, ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi, onse wopanda chilema.
Au commencement de vos mois, vous offrirez en holocauste à l’Éternel deux jeunes taureaux, un bélier, et sept agneaux d’un an sans défaut;
12 Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pakhale chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; ndi nkhosa yayimuna, chopereka cha chakudya cha makilogalamu awiri a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta;
et, comme offrande pour chaque taureau, trois dixièmes de fleur de farine pétrie à l’huile; comme offrande pour le bélier, deux dixièmes de fleur de farine pétrie à l’huile;
13 ndipo pa mwana wankhosa aliyense, chopereka cha ufa wa kilogalamu imodzi ya ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, izi ndi za nsembe yopsereza, fungo lokoma, nsembe yotentha pa moto ya kwa Yehova.
comme offrande pour chaque agneau, un dixième de fleur de farine pétrie à l’huile. C’est un holocauste, un sacrifice consumé par le feu, d’une agréable odeur à l’Éternel.
14 Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pakhale chopereka cha chakumwa cha malita awiri a vinyo; ndipo pa nkhosa yayimuna, lita limodzi ndi theka, ndipo pa mwana wankhosa, lita limodzi. Iyi ndi nsembe yopsereza ya mwezi ndi mwezi yoperekedwa pa mwezi watsopano mʼkati mwa chaka.
Les libations seront d’un demi-hin de vin pour un taureau, d’un tiers de hin pour un bélier, et d’un quart de hin pour un agneau. C’est l’holocauste du commencement du mois, pour chaque mois, pour tous les mois de l’année.
15 Powonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse ndi chopereka chake cha chakumwa, mbuzi yayimuna imodzi iperekedwe kwa Yehova ngati nsembe yopepesera machimo.
On offrira à l’Éternel un bouc, en sacrifice d’expiation, outre l’holocauste perpétuel et la libation.
16 “‘Pa tsiku la 14 la mwezi woyamba muzichita Paska wa Yehova.
Le premier mois, le quatorzième jour du mois, ce sera la Pâque de l’Éternel.
17 Pa tsiku la 15 la mwezi womwewo pazikhala chikondwerero. Muzidya buledi wopanda yisiti kwa masiku asanu ndi awiri.
Le quinzième jour de ce mois sera un jour de fête. On mangera pendant sept jours des pains sans levain.
18 Pa tsiku loyamba muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse.
Le premier jour, il y aura une sainte convocation: vous ne ferez aucune œuvre servile.
19 Koma muzipereka kwa Yehova nsembe yotentha pa moto, nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri aamuna a chaka chimodzi, onsewo wopanda chilema.
Vous offrirez en holocauste à l’Éternel un sacrifice consumé par le feu: deux jeunes taureaux, un bélier, et sept agneaux d’un an sans défaut.
20 Pamodzi ndi ngʼombe yayimuna iliyonse, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; makilogalamu awiri pa nkhosa yayimuna iliyonse.
Vous y joindrez l’offrande de fleur de farine pétrie à l’huile, trois dixièmes pour un taureau, deux dixièmes pour un bélier,
21 Kilogalamu imodzi pa mwana wankhosa aliyense mwa ana ankhosa asanu ndi awiri aja.
et un dixième pour chacun des sept agneaux.
22 Muziphatikizapo mbuzi yayimuna monga nsembe yopepesera machimo anu.
Vous offrirez un bouc en sacrifice d’expiation, afin de faire pour vous l’expiation.
23 Muzikonza zimenezi nthawi zonse, powonjezera pa nsembe yopsereza ya mmawa.
Vous offrirez ces sacrifices, outre l’holocauste du matin, qui est un holocauste perpétuel.
24 Motere muzikonza chakudya cha nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pa masiku asanu ndi awiri ngati fungo lokomera Yehova. Zimenezi ziziperekedwa kuwonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse pamodzi ndi nsembe yachakumwa.
Vous les offrirez chaque jour, pendant sept jours, comme l’aliment d’un sacrifice consumé par le feu, d’une agréable odeur à l’Éternel. On les offrira, outre l’holocauste perpétuel et la libation.
25 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse.
Le septième jour, vous aurez une sainte convocation: vous ne ferez aucune œuvre servile.
26 “‘Pa tsiku la zipatso zoyambirira kucha, pamene mukupereka chopereka cha chakudya chatsopano kwa Yehova, pa nthawi ya chikondwerero cha Masabata, muzichita msonkhano wopatulika ndipo musagwire ntchito zolemetsa.
Le jour des prémices, où vous présenterez à l’Éternel une offrande, à votre fête des semaines, vous aurez une sainte convocation: vous ne ferez aucune œuvre servile.
27 Muzipereka nsembe zopsereza za ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa imodzi yayimuna ndi ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi monga fungo lokomera Yehova.
Vous offrirez en holocauste, d’une agréable odeur à l’Éternel, deux jeunes taureaux, un bélier, et sept agneaux d’un an.
28 Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pazikhala chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, pa nkhosa yayimuna iliyonse makilogalamu awiri.
Vous y joindrez l’offrande de fleur de farine pétrie à l’huile, trois dixièmes pour chaque taureau, deux dixièmes pour le bélier,
29 Ndipo pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiri aja, kilogalamu imodzi.
et un dixième pour chacun des sept agneaux.
30 Muziperekanso mbuzi yayimuna imodzi kuti izikhala nsembe yopepesera machimo anu.
Vous offrirez un bouc, afin de faire pour vous l’expiation.
31 Muzipereka zimenezi pamodzi ndi zopereka za zakumwa ndi nsembe yake ya chakudya. Onetsetsani kuti nyamazo zilibe chilema.
Vous offrirez ces sacrifices, outre l’holocauste perpétuel et l’offrande. Vous aurez des agneaux sans défaut, et vous joindrez les libations.