< Numeri 28 >
1 Yehova anawuza Mose kuti,
Yahvé parla à Moïse, et dit:
2 “Lamula Aisraeli kuti, ‘Onetsetsani kuti mukupereka kwa Ine pa nthawi yoyikika, chopereka cha chakudya chotentha pa moto monga fungo lokoma kwa Ine.’
Donne des ordres aux enfants d'Israël, et dis-leur: Veillez à ce que vous présentiez mon offrande, mon aliment pour mes sacrifices consumés par le feu, comme une odeur agréable pour moi, en son temps.
3 Awuze kuti, ‘Nsembe ya chakudya imene muzipereka pa moto kwa Yehova tsiku ndi tsiku ndi iyi: Ana ankhosa a chaka chimodzi awiri, wopanda chilema.
Tu leur diras: « Voici le sacrifice consumé par le feu que vous offrirez à l'Éternel: des agneaux mâles d'un an sans défaut, deux par jour, pour l'holocauste perpétuel.
4 Mmawa muzipereka mwana wankhosa mmodzi ndipo winayo madzulo.
Tu offriras l'un des agneaux le matin, et tu offriras l'autre agneau le soir,
5 Muziperekanso kilogalamu imodzi ya ufa wosalala wosakaniza ndi lita imodzi ya mafuta a olivi.
avec un dixième d'épha de fleur de farine pour l'offrande, mélangé à un quart de hin d'huile battue.
6 Iyi ndi nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku imene analamula pa phiri la Sinai kuti ikhale fungo lokoma, nsembe yopsereza pa moto yopereka kwa Yehova.
C'est l'holocauste perpétuel qui a été ordonné sur la montagne de Sinaï, comme un parfum agréable, un sacrifice consumé par le feu à l'Éternel.
7 Chopereka chachakumwa chikhale lita imodzi yachakumwa chaukali pa nkhosa iliyonse. Muzithira pamalo opatulika, kupereka kwa Yehova.
Sa libation sera de la quatrième partie d'un hin pour chaque agneau. Tu verseras une libation de boisson forte à l'Éternel dans le lieu saint.
8 Muzipereka mwana wankhosa winayo madzulo, pamodzi ndi chopereka chachakudya monga poyamba paja ndi chopereka chachakumwa monga mmawa. Ichi ndi chopereka chachakudya, fungo lokoma kwa Yehova.’”
Tu offriras l'autre agneau le soir. Tu l'offriras, comme l'offrande du matin et comme sa libation, en sacrifice consumé par le feu, comme une odeur agréable à Yahvé.
9 “‘Pa tsiku la Sabata, muzipereka nsembe ana ankhosa awiri a chaka chimodzi wopanda chilema, pamodzi ndi chopereka chachakumwa ndi chopereka chachakudya chokwana makilogalamu awiri a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta.
"'Le jour du sabbat, tu offriras deux agneaux mâles d'un an, sans défaut, et deux dixièmes d'un épha de fleur de farine, en offrande de farine mélangée à de l'huile, avec sa libation:
10 Iyi ndi nsembe yopsereza ya pa Sabata iliyonse, kuwonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse ndi chopereka chake chachakumwa.’”
C'est l'holocauste de chaque sabbat, en plus de l'holocauste perpétuel et de sa libation.
11 “Pa tsiku loyamba la mwezi uliwonse muzipereka kwa Yehova nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa yayimuna imodzi, ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi, onse wopanda chilema.
"'Au commencement de vos mois, vous offrirez un holocauste à Yahvé: deux jeunes taureaux, un bélier, sept agneaux mâles d'un an sans défaut,
12 Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pakhale chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; ndi nkhosa yayimuna, chopereka cha chakudya cha makilogalamu awiri a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta;
et trois dixièmes d'un épha de fleur de farine pour une offrande de farine mélangée à de l'huile, pour chaque taureau; deux dixièmes de fleur de farine pour une offrande de farine mélangée à de l'huile, pour le bélier;
13 ndipo pa mwana wankhosa aliyense, chopereka cha ufa wa kilogalamu imodzi ya ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, izi ndi za nsembe yopsereza, fungo lokoma, nsembe yotentha pa moto ya kwa Yehova.
et un dixième de fleur de farine mélangée à de l'huile pour une offrande de farine, pour chaque agneau, comme holocauste d'odeur agréable, un sacrifice par le feu à l'Éternel.
14 Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pakhale chopereka cha chakumwa cha malita awiri a vinyo; ndipo pa nkhosa yayimuna, lita limodzi ndi theka, ndipo pa mwana wankhosa, lita limodzi. Iyi ndi nsembe yopsereza ya mwezi ndi mwezi yoperekedwa pa mwezi watsopano mʼkati mwa chaka.
Leurs libations seront d'un demi-hin de vin pour le taureau, d'un tiers de hin pour le bélier et d'un quart de hin pour l'agneau. C'est l'holocauste de chaque mois, pendant tous les mois de l'année.
15 Powonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse ndi chopereka chake cha chakumwa, mbuzi yayimuna imodzi iperekedwe kwa Yehova ngati nsembe yopepesera machimo.
On offrira aussi un bouc en sacrifice pour le péché à Yahvé, en plus de l'holocauste perpétuel et de la libation.
16 “‘Pa tsiku la 14 la mwezi woyamba muzichita Paska wa Yehova.
"'Le premier mois, le quatorzième jour du mois, c'est la Pâque de Yahvé.
17 Pa tsiku la 15 la mwezi womwewo pazikhala chikondwerero. Muzidya buledi wopanda yisiti kwa masiku asanu ndi awiri.
Le quinzième jour de ce mois, il y aura une fête. On mangera des pains sans levain pendant sept jours.
18 Pa tsiku loyamba muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse.
Le premier jour, il y aura une convocation sainte. Tu ne feras aucun travail régulier,
19 Koma muzipereka kwa Yehova nsembe yotentha pa moto, nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri aamuna a chaka chimodzi, onsewo wopanda chilema.
mais tu offriras un sacrifice consumé par le feu, un holocauste à l'Éternel: deux jeunes taureaux, un bélier et sept agneaux mâles d'un an. Ils seront sans défaut,
20 Pamodzi ndi ngʼombe yayimuna iliyonse, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; makilogalamu awiri pa nkhosa yayimuna iliyonse.
avec leur offrande de farine, de la fleur de farine mélangée à de l'huile. Tu offriras trois dixièmes pour le taureau, et deux dixièmes pour le bélier.
21 Kilogalamu imodzi pa mwana wankhosa aliyense mwa ana ankhosa asanu ndi awiri aja.
Tu offriras un dixième pour chacun des sept agneaux;
22 Muziphatikizapo mbuzi yayimuna monga nsembe yopepesera machimo anu.
et un bouc en sacrifice pour le péché, afin de faire l'expiation pour toi.
23 Muzikonza zimenezi nthawi zonse, powonjezera pa nsembe yopsereza ya mmawa.
Tu les offriras en plus de l'holocauste du matin, qui est un holocauste perpétuel.
24 Motere muzikonza chakudya cha nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pa masiku asanu ndi awiri ngati fungo lokomera Yehova. Zimenezi ziziperekedwa kuwonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse pamodzi ndi nsembe yachakumwa.
C'est ainsi que tu offriras chaque jour, pendant sept jours, l'aliment du sacrifice consumé par le feu, d'une odeur agréable à Yahvé. Elle sera offerte en plus de l'holocauste perpétuel et de sa libation.
25 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse.
Le septième jour, vous aurez une sainte convocation. Vous ne ferez aucun travail régulier.
26 “‘Pa tsiku la zipatso zoyambirira kucha, pamene mukupereka chopereka cha chakudya chatsopano kwa Yehova, pa nthawi ya chikondwerero cha Masabata, muzichita msonkhano wopatulika ndipo musagwire ntchito zolemetsa.
"'Le jour des prémices, lorsque vous offrirez une nouvelle offrande à Yahvé à l'occasion de votre fête des semaines, vous aurez une sainte convocation. Tu ne feras aucun travail régulier,
27 Muzipereka nsembe zopsereza za ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa imodzi yayimuna ndi ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi monga fungo lokomera Yehova.
mais tu offriras un holocauste d'agréable odeur à Yahvé: deux jeunes taureaux, un bélier, sept agneaux mâles d'un an,
28 Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pazikhala chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, pa nkhosa yayimuna iliyonse makilogalamu awiri.
et leur offrande de farine fine mélangée à de l'huile, trois dixièmes pour chaque taureau, deux dixièmes pour le bélier,
29 Ndipo pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiri aja, kilogalamu imodzi.
un dixième pour chacun des sept agneaux,
30 Muziperekanso mbuzi yayimuna imodzi kuti izikhala nsembe yopepesera machimo anu.
et un bouc, afin de faire l'expiation pour toi.
31 Muzipereka zimenezi pamodzi ndi zopereka za zakumwa ndi nsembe yake ya chakudya. Onetsetsani kuti nyamazo zilibe chilema.
En plus de l'holocauste perpétuel et de l'offrande, tu les offriras avec leurs libations. Veille à ce qu'ils soient sans défaut.