< Numeri 28 >
1 Yehova anawuza Mose kuti,
And he spoke Yahweh to Moses saying.
2 “Lamula Aisraeli kuti, ‘Onetsetsani kuti mukupereka kwa Ine pa nthawi yoyikika, chopereka cha chakudya chotentha pa moto monga fungo lokoma kwa Ine.’
Command [the] people of Israel and you will say to them offering my food my for fire offerings my [the] odor of soothing my you will take care to bring near to me at appointed time its.
3 Awuze kuti, ‘Nsembe ya chakudya imene muzipereka pa moto kwa Yehova tsiku ndi tsiku ndi iyi: Ana ankhosa a chaka chimodzi awiri, wopanda chilema.
And you will say to them this [is] the fire offering which you will bring near to Yahweh lambs sons of a year unblemished two for the day a burnt offering continually.
4 Mmawa muzipereka mwana wankhosa mmodzi ndipo winayo madzulo.
The lamb one you will offer in the morning and the lamb second you will offer between the evenings.
5 Muziperekanso kilogalamu imodzi ya ufa wosalala wosakaniza ndi lita imodzi ya mafuta a olivi.
And [the] tenth of ephah fine flour to a grain offering mixed with oil pressed fourth of hin.
6 Iyi ndi nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku imene analamula pa phiri la Sinai kuti ikhale fungo lokoma, nsembe yopsereza pa moto yopereka kwa Yehova.
A burnt offering of continuity which was instituted at [the] mountain of Sinai to an odor of soothing a fire offering to Yahweh.
7 Chopereka chachakumwa chikhale lita imodzi yachakumwa chaukali pa nkhosa iliyonse. Muzithira pamalo opatulika, kupereka kwa Yehova.
And drink offering its [will be] [the] fourth of hin for the lamb one in the holy place pour out a drink offering of strong drink to Yahweh.
8 Muzipereka mwana wankhosa winayo madzulo, pamodzi ndi chopereka chachakudya monga poyamba paja ndi chopereka chachakumwa monga mmawa. Ichi ndi chopereka chachakudya, fungo lokoma kwa Yehova.’”
And the lamb second you will offer between the evenings like [the] grain offering of the morning and like drink offering its you will offer [it] a fire offering of an odor of soothing to Yahweh.
9 “‘Pa tsiku la Sabata, muzipereka nsembe ana ankhosa awiri a chaka chimodzi wopanda chilema, pamodzi ndi chopereka chachakumwa ndi chopereka chachakudya chokwana makilogalamu awiri a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta.
And on [the] day of the sabbath two lambs sons of a year unblemished and two tenths [of an ephah] fine flour a grain offering mixed with oil and drink offering its.
10 Iyi ndi nsembe yopsereza ya pa Sabata iliyonse, kuwonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse ndi chopereka chake chachakumwa.’”
[the] burnt offering of [the] sabbath On sabbath its [is] to [the] burnt offering of continuity and drink offering its.
11 “Pa tsiku loyamba la mwezi uliwonse muzipereka kwa Yehova nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa yayimuna imodzi, ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi, onse wopanda chilema.
And at [the] beginnings of months your you will bring near a burnt offering to Yahweh young bulls young ones of cattle two and a ram one lambs sons of a year seven unblemished.
12 Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pakhale chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; ndi nkhosa yayimuna, chopereka cha chakudya cha makilogalamu awiri a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta;
And three tenths [of an ephah] fine flour a grain offering mixed with oil for the young bull one and two tenths [of an ephah] fine flour a grain offering mixed with oil for the ram one.
13 ndipo pa mwana wankhosa aliyense, chopereka cha ufa wa kilogalamu imodzi ya ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, izi ndi za nsembe yopsereza, fungo lokoma, nsembe yotentha pa moto ya kwa Yehova.
And a tenth [of an ephah] a tenth [of an ephah] fine flour a grain offering mixed with oil for the lamb one a burnt offering an odor of soothing a fire offering to Yahweh.
14 Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pakhale chopereka cha chakumwa cha malita awiri a vinyo; ndipo pa nkhosa yayimuna, lita limodzi ndi theka, ndipo pa mwana wankhosa, lita limodzi. Iyi ndi nsembe yopsereza ya mwezi ndi mwezi yoperekedwa pa mwezi watsopano mʼkati mwa chaka.
And drink offerings their half of hin it will belong for the young bull and [the] third of hin for the ram and [the] fourth of hin for the lamb wine this [is the] burnt offering of a month in month its for [the] months of the year.
15 Powonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse ndi chopereka chake cha chakumwa, mbuzi yayimuna imodzi iperekedwe kwa Yehova ngati nsembe yopepesera machimo.
And a male goat of goats one to a sin offering to Yahweh to [the] burnt offering of continuity it will be offered and drink offering its.
16 “‘Pa tsiku la 14 la mwezi woyamba muzichita Paska wa Yehova.
And [will be] in the month first on [the] four-teen day of the month a passover to Yahweh.
17 Pa tsiku la 15 la mwezi womwewo pazikhala chikondwerero. Muzidya buledi wopanda yisiti kwa masiku asanu ndi awiri.
And [will be] on [the] fif-teen day of the month this a festival seven days unleavened bread it will be eaten.
18 Pa tsiku loyamba muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse.
[will be] on the Day first a convocation of holiness any work of servitude not you will do.
19 Koma muzipereka kwa Yehova nsembe yotentha pa moto, nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri aamuna a chaka chimodzi, onsewo wopanda chilema.
And you will bring near a fire offering a burnt offering to Yahweh young bulls young ones of cattle two and a ram one and seven lambs sons of a year unblemished they will be to you.
20 Pamodzi ndi ngʼombe yayimuna iliyonse, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; makilogalamu awiri pa nkhosa yayimuna iliyonse.
And grain offering their fine flour mixed with oil three tenths [of an ephah] for the young bull and two tenths [of an ephah] for the ram you will offer.
21 Kilogalamu imodzi pa mwana wankhosa aliyense mwa ana ankhosa asanu ndi awiri aja.
A tenth a tenth you will offer for the lamb one for [the] seven the lambs.
22 Muziphatikizapo mbuzi yayimuna monga nsembe yopepesera machimo anu.
And a male goat of a sin offering one to make atonement on you.
23 Muzikonza zimenezi nthawi zonse, powonjezera pa nsembe yopsereza ya mmawa.
Besides [the] burnt offering of the morning which [is] for [the] burnt offering of continuity you will offer these [things].
24 Motere muzikonza chakudya cha nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pa masiku asanu ndi awiri ngati fungo lokomera Yehova. Zimenezi ziziperekedwa kuwonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse pamodzi ndi nsembe yachakumwa.
Like these [things] you will offer for the day seven days food of a fire offering of an odor of soothing to Yahweh to [the] burnt offering of continuity it will be offered and drink offering its.
25 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse.
And on the day seventh a convocation of holiness it will be to you any work of servitude not you will do.
26 “‘Pa tsiku la zipatso zoyambirira kucha, pamene mukupereka chopereka cha chakudya chatsopano kwa Yehova, pa nthawi ya chikondwerero cha Masabata, muzichita msonkhano wopatulika ndipo musagwire ntchito zolemetsa.
And on [the] day of the first-fruits when bring near you a grain offering new to Yahweh at weeks your a convocation of holiness it will be to you any work of servitude not you will do.
27 Muzipereka nsembe zopsereza za ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa imodzi yayimuna ndi ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi monga fungo lokomera Yehova.
And you will bring near a burnt offering to an odor of soothing to Yahweh young bulls young ones of cattle two a ram one seven lambs sons of a year.
28 Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pazikhala chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, pa nkhosa yayimuna iliyonse makilogalamu awiri.
And grain offering their fine flour mixed with oil three tenths [of an ephah] for the young bull one two tenths [of an ephah] for the ram one.
29 Ndipo pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiri aja, kilogalamu imodzi.
A tenth a tenth for the lamb one for [the] seven the lambs.
30 Muziperekanso mbuzi yayimuna imodzi kuti izikhala nsembe yopepesera machimo anu.
A male goat of goats one to make atonement on you.
31 Muzipereka zimenezi pamodzi ndi zopereka za zakumwa ndi nsembe yake ya chakudya. Onetsetsani kuti nyamazo zilibe chilema.
Besides [the] burnt offering of continuity and grain offering its you will offer [them] unblemished they will be to you and drink offerings their.