< Numeri 28 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
The Lord also said to Moses:
2 “Lamula Aisraeli kuti, ‘Onetsetsani kuti mukupereka kwa Ine pa nthawi yoyikika, chopereka cha chakudya chotentha pa moto monga fungo lokoma kwa Ine.’
Command the children of Israel, and thou shalt say to them: Offer ye my oblation and my bread, and burnt sacrifice of most sweet odour, in their due seasons.
3 Awuze kuti, ‘Nsembe ya chakudya imene muzipereka pa moto kwa Yehova tsiku ndi tsiku ndi iyi: Ana ankhosa a chaka chimodzi awiri, wopanda chilema.
These are the sacrifices which you shall offer: Two lambs of a year old without blemish every day for the perpetual holocaust:
4 Mmawa muzipereka mwana wankhosa mmodzi ndipo winayo madzulo.
One you shall offer in the morning, and the other in the evening:
5 Muziperekanso kilogalamu imodzi ya ufa wosalala wosakaniza ndi lita imodzi ya mafuta a olivi.
And the tenth part of an ephi of flour, which shall be tempered with the purest oil, of the measure of the fourth part of a hin.
6 Iyi ndi nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku imene analamula pa phiri la Sinai kuti ikhale fungo lokoma, nsembe yopsereza pa moto yopereka kwa Yehova.
It is the continual holocaust which you offered in mount Sinai for a most sweet. odour of a sacrifice by fire to the Lord.
7 Chopereka chachakumwa chikhale lita imodzi yachakumwa chaukali pa nkhosa iliyonse. Muzithira pamalo opatulika, kupereka kwa Yehova.
And for a libation you shall offer of wine the fourth part of a hin for every lamb in the sanctuary of the Lord.
8 Muzipereka mwana wankhosa winayo madzulo, pamodzi ndi chopereka chachakudya monga poyamba paja ndi chopereka chachakumwa monga mmawa. Ichi ndi chopereka chachakudya, fungo lokoma kwa Yehova.’”
And you shall offer the other lamb in like manner ill the evening according to all the rites of the morning sacrifice, and of the libations thereof, an oblation of most sweet odour to the Lord.
9 “‘Pa tsiku la Sabata, muzipereka nsembe ana ankhosa awiri a chaka chimodzi wopanda chilema, pamodzi ndi chopereka chachakumwa ndi chopereka chachakudya chokwana makilogalamu awiri a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta.
And on the sabbath day you shall offer two lambs of a year old without blemish, and two tenths of flour tempered with oil in sacrifice, and the libations,
10 Iyi ndi nsembe yopsereza ya pa Sabata iliyonse, kuwonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse ndi chopereka chake chachakumwa.’”
Which regularly are poured out every sabbath for the perpetual holocaust.
11 “Pa tsiku loyamba la mwezi uliwonse muzipereka kwa Yehova nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa yayimuna imodzi, ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi, onse wopanda chilema.
And on the first day of the month you shall offer a holocaust to the Lord, two calves of the herd, one ram, and seven lambs of a year old, without blemish,
12 Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pakhale chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; ndi nkhosa yayimuna, chopereka cha chakudya cha makilogalamu awiri a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta;
And three tenths of flour tempered with oil in sacrifice for every calf: and two tenths of flour tempered with oil for every ram:
13 ndipo pa mwana wankhosa aliyense, chopereka cha ufa wa kilogalamu imodzi ya ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, izi ndi za nsembe yopsereza, fungo lokoma, nsembe yotentha pa moto ya kwa Yehova.
And the tenth of a tenth of flour tempered with oil in sacrifice for every lamb. It is a holocaust of most sweet odour and an offering by fire to the Lord.
14 Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pakhale chopereka cha chakumwa cha malita awiri a vinyo; ndipo pa nkhosa yayimuna, lita limodzi ndi theka, ndipo pa mwana wankhosa, lita limodzi. Iyi ndi nsembe yopsereza ya mwezi ndi mwezi yoperekedwa pa mwezi watsopano mʼkati mwa chaka.
And these shall be the libations of wine that are to be poured out for every victim: Half a hin for every calf, a third for a ram, and a fourth for a lamb. This shall be the holocaust for every month, as they succeed one another in the course of the year.
15 Powonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse ndi chopereka chake cha chakumwa, mbuzi yayimuna imodzi iperekedwe kwa Yehova ngati nsembe yopepesera machimo.
A buck goat also shall be offered to the Lord for a sin offering over and above the perpetual holocaust with its libations.
16 “‘Pa tsiku la 14 la mwezi woyamba muzichita Paska wa Yehova.
And in the first month, on the fourteenth day of the month, shall be the phase of the Lord,
17 Pa tsiku la 15 la mwezi womwewo pazikhala chikondwerero. Muzidya buledi wopanda yisiti kwa masiku asanu ndi awiri.
And on the fifteenth day the solemn feast: seven days shall they eat unleavened bread.
18 Pa tsiku loyamba muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse.
And the first day of them shall be venerable and holy: you shall not do any servile work therein.
19 Koma muzipereka kwa Yehova nsembe yotentha pa moto, nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri aamuna a chaka chimodzi, onsewo wopanda chilema.
And you shall offer a burnt sacrifice a holocaust to the Lord, two calves of the herd, one ram, seven lambs of a year old, without blemish:
20 Pamodzi ndi ngʼombe yayimuna iliyonse, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; makilogalamu awiri pa nkhosa yayimuna iliyonse.
And for the sacrifices of every one three tenths of flour which shall be tempered with oil to every calf, and two tenths to every ram,
21 Kilogalamu imodzi pa mwana wankhosa aliyense mwa ana ankhosa asanu ndi awiri aja.
And the tenth of a tenth, to every lamb, that is to say, to all the seven lambs:
22 Muziphatikizapo mbuzi yayimuna monga nsembe yopepesera machimo anu.
And one buck goat for sin, to make atonement for you,
23 Muzikonza zimenezi nthawi zonse, powonjezera pa nsembe yopsereza ya mmawa.
Besides the morning holocaust which you shall always offer.
24 Motere muzikonza chakudya cha nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pa masiku asanu ndi awiri ngati fungo lokomera Yehova. Zimenezi ziziperekedwa kuwonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse pamodzi ndi nsembe yachakumwa.
So shall you do every day of the seven days for the food of the fire, and for a most sweet odour to the Lord, which shall rise from the holocaust, and from the libations of each.
25 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse.
The seventh day also shall be most solemn and holy unto you: you shall do no servile work therein.
26 “‘Pa tsiku la zipatso zoyambirira kucha, pamene mukupereka chopereka cha chakudya chatsopano kwa Yehova, pa nthawi ya chikondwerero cha Masabata, muzichita msonkhano wopatulika ndipo musagwire ntchito zolemetsa.
The day also of firstfruits, when after the weeks are accomplished, you shall offer new fruits to the Lord, shall be venerable and holy: you shall do no servile work therein.
27 Muzipereka nsembe zopsereza za ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa imodzi yayimuna ndi ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi monga fungo lokomera Yehova.
And you shall offer a holocaust for a most sweet odour to the Lord, two calves of the herd, one ram, and seven lambs of a year old, without blemish:
28 Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pazikhala chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, pa nkhosa yayimuna iliyonse makilogalamu awiri.
And in the sacrifices of them three tenths of flour tempered with oil to every calf, two to every ram,
29 Ndipo pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiri aja, kilogalamu imodzi.
The tenth of a tenth to every lamb, which in all are seven lambs: a buck goat also,
30 Muziperekanso mbuzi yayimuna imodzi kuti izikhala nsembe yopepesera machimo anu.
Which is slain for expiation: besides the perpetual holocaust and the libations thereof.
31 Muzipereka zimenezi pamodzi ndi zopereka za zakumwa ndi nsembe yake ya chakudya. Onetsetsani kuti nyamazo zilibe chilema.
You shall offer them all without blemish with their libations.

< Numeri 28 >