< Numeri 28 >

1 Yehova anawuza Mose kuti,
And the Lord said to Moses,
2 “Lamula Aisraeli kuti, ‘Onetsetsani kuti mukupereka kwa Ine pa nthawi yoyikika, chopereka cha chakudya chotentha pa moto monga fungo lokoma kwa Ine.’
Give orders to the children of Israel and say to them, Let it be your care to give me my offerings at their regular times, the food of the offerings made by fire to me for a sweet smell.
3 Awuze kuti, ‘Nsembe ya chakudya imene muzipereka pa moto kwa Yehova tsiku ndi tsiku ndi iyi: Ana ankhosa a chaka chimodzi awiri, wopanda chilema.
Say to them, This is the offering made by fire which you are to give to the Lord; he-lambs of the first year without any mark, two every day as a regular burned offering.
4 Mmawa muzipereka mwana wankhosa mmodzi ndipo winayo madzulo.
Let one be offered in the morning, and the other at evening;
5 Muziperekanso kilogalamu imodzi ya ufa wosalala wosakaniza ndi lita imodzi ya mafuta a olivi.
And the tenth part of an ephah of the best meal for a meal offering mixed with the fourth part of a hin of clear oil.
6 Iyi ndi nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku imene analamula pa phiri la Sinai kuti ikhale fungo lokoma, nsembe yopsereza pa moto yopereka kwa Yehova.
It is a regular burned offering, as it was ordered in Mount Sinai, for a sweet smell, an offering made by fire to the Lord.
7 Chopereka chachakumwa chikhale lita imodzi yachakumwa chaukali pa nkhosa iliyonse. Muzithira pamalo opatulika, kupereka kwa Yehova.
And for its drink offering take the fourth part of a hin for one lamb: in the holy place let the wine be drained out for a drink offering for the Lord.
8 Muzipereka mwana wankhosa winayo madzulo, pamodzi ndi chopereka chachakudya monga poyamba paja ndi chopereka chachakumwa monga mmawa. Ichi ndi chopereka chachakudya, fungo lokoma kwa Yehova.’”
Let the other lamb be offered at evening; like the meal offering of the morning and its drink offering, let it be offered as an offering made by fire for a sweet smell to the Lord.
9 “‘Pa tsiku la Sabata, muzipereka nsembe ana ankhosa awiri a chaka chimodzi wopanda chilema, pamodzi ndi chopereka chachakumwa ndi chopereka chachakudya chokwana makilogalamu awiri a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta.
And on the Sabbath day, two he-lambs of the first year, without any mark, and two tenth parts of the best meal for a meal offering mixed with oil, and its drink offering:
10 Iyi ndi nsembe yopsereza ya pa Sabata iliyonse, kuwonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse ndi chopereka chake chachakumwa.’”
This is the burned offering for every Sabbath day, in addition to the regular burned offering, and its drink offering.
11 “Pa tsiku loyamba la mwezi uliwonse muzipereka kwa Yehova nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa yayimuna imodzi, ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi, onse wopanda chilema.
And on the first day of every month you are to give a burned offering to the Lord; two oxen, one male sheep, and seven he-lambs of the first year, without any mark;
12 Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pakhale chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; ndi nkhosa yayimuna, chopereka cha chakudya cha makilogalamu awiri a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta;
And three tenth parts of the best meal for a meal offering mixed with oil, for every ox; and two tenth parts of the best meal for a meal offering mixed with oil, for the one sheep;
13 ndipo pa mwana wankhosa aliyense, chopereka cha ufa wa kilogalamu imodzi ya ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, izi ndi za nsembe yopsereza, fungo lokoma, nsembe yotentha pa moto ya kwa Yehova.
And a separate tenth part of the best meal mixed with oil for a meal offering for every lamb; for a burned offering of a sweet smell, an offering made by fire to the Lord.
14 Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pakhale chopereka cha chakumwa cha malita awiri a vinyo; ndipo pa nkhosa yayimuna, lita limodzi ndi theka, ndipo pa mwana wankhosa, lita limodzi. Iyi ndi nsembe yopsereza ya mwezi ndi mwezi yoperekedwa pa mwezi watsopano mʼkati mwa chaka.
And their drink offerings are to be half a hin of wine for an ox, and the third part of a hin for a male sheep, and the fourth part of a hin for a lamb: this is the burned offering for every month through all the months of the year.
15 Powonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse ndi chopereka chake cha chakumwa, mbuzi yayimuna imodzi iperekedwe kwa Yehova ngati nsembe yopepesera machimo.
And one he-goat for a sin-offering to the Lord; it is to be offered in addition to the regular burned offering and its drink offering.
16 “‘Pa tsiku la 14 la mwezi woyamba muzichita Paska wa Yehova.
And in the first month, on the fourteenth day of the month, is the Lord's Passover.
17 Pa tsiku la 15 la mwezi womwewo pazikhala chikondwerero. Muzidya buledi wopanda yisiti kwa masiku asanu ndi awiri.
On the fifteenth day of this month there is to be a feast; for seven days let your food be unleavened cakes.
18 Pa tsiku loyamba muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse.
On the first day there is to be a holy meeting: you may do no sort of field-work:
19 Koma muzipereka kwa Yehova nsembe yotentha pa moto, nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri aamuna a chaka chimodzi, onsewo wopanda chilema.
And you are to give an offering made by fire, a burned offering to the Lord; two oxen, one male sheep, and seven he-lambs of the first year, without any mark:
20 Pamodzi ndi ngʼombe yayimuna iliyonse, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; makilogalamu awiri pa nkhosa yayimuna iliyonse.
And their meal offering, the best meal mixed with oil: let three tenth parts of an ephah be offered for an ox and two tenth parts for a male sheep;
21 Kilogalamu imodzi pa mwana wankhosa aliyense mwa ana ankhosa asanu ndi awiri aja.
And a separate tenth part for every one of the seven lambs;
22 Muziphatikizapo mbuzi yayimuna monga nsembe yopepesera machimo anu.
And one he-goat for a sin-offering to take away your sin.
23 Muzikonza zimenezi nthawi zonse, powonjezera pa nsembe yopsereza ya mmawa.
These are to be offered in addition to the morning burned offering, which is a regular burned offering at all times.
24 Motere muzikonza chakudya cha nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pa masiku asanu ndi awiri ngati fungo lokomera Yehova. Zimenezi ziziperekedwa kuwonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse pamodzi ndi nsembe yachakumwa.
In this way, every day for seven days, give the food of the offering made by fire, a sweet smell to the Lord: it is to be offered in addition to the regular burned offering, and its drink offering.
25 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse.
Then on the seventh day there will be a holy meeting; you may do no field-work.
26 “‘Pa tsiku la zipatso zoyambirira kucha, pamene mukupereka chopereka cha chakudya chatsopano kwa Yehova, pa nthawi ya chikondwerero cha Masabata, muzichita msonkhano wopatulika ndipo musagwire ntchito zolemetsa.
And at the time of the first-fruits, when you give an offering of new meal to the Lord at your feast of weeks, there is to be a holy meeting: you may do no field-work:
27 Muzipereka nsembe zopsereza za ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa imodzi yayimuna ndi ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi monga fungo lokomera Yehova.
And give a burned offering for a sweet smell to the Lord; two oxen, one male sheep, and seven he-lambs of the first year;
28 Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pazikhala chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, pa nkhosa yayimuna iliyonse makilogalamu awiri.
And their meal offering, the best meal mixed with oil, three tenth parts for an ox, two tenth parts for a male sheep,
29 Ndipo pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiri aja, kilogalamu imodzi.
And a separate tenth part for every one of the seven lambs;
30 Muziperekanso mbuzi yayimuna imodzi kuti izikhala nsembe yopepesera machimo anu.
And one he-goat to take away your sin.
31 Muzipereka zimenezi pamodzi ndi zopereka za zakumwa ndi nsembe yake ya chakudya. Onetsetsani kuti nyamazo zilibe chilema.
These are in addition to the regular burned offering and its meal offering; take care that they are without any mark, and let them be offered with their drink offerings.

< Numeri 28 >