< Numeri 28 >
1 Yehova anawuza Mose kuti,
Jehova Nyasaye nowacho ne Musa niya,
2 “Lamula Aisraeli kuti, ‘Onetsetsani kuti mukupereka kwa Ine pa nthawi yoyikika, chopereka cha chakudya chotentha pa moto monga fungo lokoma kwa Ine.’
“Mi jo-Israel chikni kiwachonegi kama: ‘Kelnauru chiwo mitimonago misengini miwangʼo pep mondo obed chiemba madum tik mangʼwe ngʼar e kinde mowinjore.’
3 Awuze kuti, ‘Nsembe ya chakudya imene muzipereka pa moto kwa Yehova tsiku ndi tsiku ndi iyi: Ana ankhosa a chaka chimodzi awiri, wopanda chilema.
Wachnegi niya, ‘Misengini miwangʼo ne Jehova Nyasaye e magi: nyirombe ariyo ma jo-higa achiel maonge songa, kaka chiwo mapile mowangʼ odiechiengʼ kodiechiengʼ.
4 Mmawa muzipereka mwana wankhosa mmodzi ndipo winayo madzulo.
Chiw nyarombo achiel gokinyi to machielo godhiambo,
5 Muziperekanso kilogalamu imodzi ya ufa wosalala wosakaniza ndi lita imodzi ya mafuta a olivi.
kaachiel gi chiwo mar cham moromo gorogoro achiel gi nus mar mogo mayom moruw gi mo mobi e olemb zeituni moromo lita achiel.
6 Iyi ndi nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku imene analamula pa phiri la Sinai kuti ikhale fungo lokoma, nsembe yopsereza pa moto yopereka kwa Yehova.
Ma e chiwo mapile mowangʼ mopwodhi e Got Sinai kaka gima dungʼ tik mangʼwe ngʼar mamoro Jehova Nyasaye, en misango miwangʼo pep mochiwne Jehova Nyasaye.
7 Chopereka chachakumwa chikhale lita imodzi yachakumwa chaukali pa nkhosa iliyonse. Muzithira pamalo opatulika, kupereka kwa Yehova.
Nyarombo ka nyarombo nokel gi misango miolo piny maromo divai lita achiel. Nyaka uol divaino ei kama ler mar lemo ne Jehova Nyasaye.
8 Muzipereka mwana wankhosa winayo madzulo, pamodzi ndi chopereka chachakudya monga poyamba paja ndi chopereka chachakumwa monga mmawa. Ichi ndi chopereka chachakudya, fungo lokoma kwa Yehova.’”
Chiw nyarombo mar ariyo godhiambo, kaachiel gi chiwo mar cham machalo kamano kod misango miolo piny ma iloso gokinyi. Ma en chiwo miwangʼo pep, misango madungʼ tik mangʼwe ngʼar mamoro Jehova Nyasaye.
9 “‘Pa tsiku la Sabata, muzipereka nsembe ana ankhosa awiri a chaka chimodzi wopanda chilema, pamodzi ndi chopereka chachakumwa ndi chopereka chachakudya chokwana makilogalamu awiri a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta.
“‘Chiengʼ Sabato, chiwuru misango mar nyiimbe ariyo maonge songa mahikgi achiel, kaachiel gi misango miolo piny kod chiwo mar cham maromo kilo abiriyo mar mogo mayom moru gi mo.
10 Iyi ndi nsembe yopsereza ya pa Sabata iliyonse, kuwonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse ndi chopereka chake chachakumwa.’”
Ma en misango miwangʼo pep Sabato ka Sabato, komedi ewi chiwo mapile mar misango miwangʼo pep kod misango miolo piny.
11 “Pa tsiku loyamba la mwezi uliwonse muzipereka kwa Yehova nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa yayimuna imodzi, ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi, onse wopanda chilema.
“‘Odiechiengʼ mokwongo mar dwe ka dwe, chiwne Jehova Nyasaye misango miwangʼo pep mar nyirwedhi ariyo, im achiel kod nyiimbe abiriyo moromo higa achiel, duto maonge songa.
12 Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pakhale chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; ndi nkhosa yayimuna, chopereka cha chakudya cha makilogalamu awiri a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta;
Rwath ka rwath nyaka chiw gi chiwo mar cham maromo kilo apar mar mogo mayom moru gi mo; im to chiw gi chiwo mar cham maromo kilo abiriyo mar mogo mayom moru gi mo;
13 ndipo pa mwana wankhosa aliyense, chopereka cha ufa wa kilogalamu imodzi ya ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, izi ndi za nsembe yopsereza, fungo lokoma, nsembe yotentha pa moto ya kwa Yehova.
to nyaim ka nyaim, to chiw gi cham maromo kilo adek mar mogo mayom moru gi mo. Ma en misango miwangʼo pep, gima dungʼ tik mangʼwe ngʼar mamoro Jehova Nyasaye.
14 Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pakhale chopereka cha chakumwa cha malita awiri a vinyo; ndipo pa nkhosa yayimuna, lita limodzi ndi theka, ndipo pa mwana wankhosa, lita limodzi. Iyi ndi nsembe yopsereza ya mwezi ndi mwezi yoperekedwa pa mwezi watsopano mʼkati mwa chaka.
Rwath ka rwath nyaka chiw gi misango miolo piny mar divai maromo lita angʼwen; im to chiw gi lita achiel mar divai; to nyaim ka nyaim, to chiw gi lita achiel mar divai. Ma en misango miwangʼo pep mar dwe ka dwe ma onego chiw e higa mangima sa moro amora ma dwe manyien opor.
15 Powonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse ndi chopereka chake cha chakumwa, mbuzi yayimuna imodzi iperekedwe kwa Yehova ngati nsembe yopepesera machimo.
Nywok achiel chiwne Jehova Nyasaye kaka misango mar pwodhruok kimedo gi misango miwangʼo pep mapile pile kod misango miolo piny michiwego.
16 “‘Pa tsiku la 14 la mwezi woyamba muzichita Paska wa Yehova.
“‘Nyaka utim Pasaka mar Jehova Nyasaye e odiechiengʼ mar apar gangʼwen mar dwe mokwongo.
17 Pa tsiku la 15 la mwezi womwewo pazikhala chikondwerero. Muzidya buledi wopanda yisiti kwa masiku asanu ndi awiri.
E odiechiengʼ mar apar gabich mar dweno nyaka ulos sawo; kuom ndalo abiriyo chamuru makati motedi ma ok oketie thowi.
18 Pa tsiku loyamba muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse.
Chiengʼ mokwongo mar jumano nyaka ubed gi chokruok mowal kendo kik uti tich moro amora mutiyo pile.
19 Koma muzipereka kwa Yehova nsembe yotentha pa moto, nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri aamuna a chaka chimodzi, onsewo wopanda chilema.
Chiwuru ne Jehova Nyasaye misango miwangʼo pep, misango mowangʼ mar nyirwedhi ariyo, im achiel kod nyiimbe abiriyo mahikgi achiel kendo maonge songa.
20 Pamodzi ndi ngʼombe yayimuna iliyonse, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; makilogalamu awiri pa nkhosa yayimuna iliyonse.
Rwath ka rwath nyaka chiw gi chiwo mar cham mar mogo mayom maromo kilo adek gi nus moru gi mo; im to ichiw gi mogo mayom maromo kilo ariyo moru gi mo;
21 Kilogalamu imodzi pa mwana wankhosa aliyense mwa ana ankhosa asanu ndi awiri aja.
to nyiimbe abiriyogo, to ichiw gi mogo mayom maromo kilo achiel moru gi mo.
22 Muziphatikizapo mbuzi yayimuna monga nsembe yopepesera machimo anu.
Umed nyanywok achiel mar chiwo mar pwodhruok e richo.
23 Muzikonza zimenezi nthawi zonse, powonjezera pa nsembe yopsereza ya mmawa.
Chiwuru magi kumedo ewi misango miwangʼo pep mapile pile gokinyi.
24 Motere muzikonza chakudya cha nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pa masiku asanu ndi awiri ngati fungo lokomera Yehova. Zimenezi ziziperekedwa kuwonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse pamodzi ndi nsembe yachakumwa.
Kamano bende kelnauru chiwo mitimogo misengini miwangʼo pile pile kuom ndalo abiriyo mondo chiemba odungʼ tik mangʼwe ngʼar ni Jehova Nyasaye; kendo nyaka ulose kumedo gi misango miwangʼo pep mapile pile kod misango miolo piny.
25 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse.
E odiechiengʼ mar abiriyo losuru chokruok mowal kendo kik uti tich moro amora mutiyo pile.
26 “‘Pa tsiku la zipatso zoyambirira kucha, pamene mukupereka chopereka cha chakudya chatsopano kwa Yehova, pa nthawi ya chikondwerero cha Masabata, muzichita msonkhano wopatulika ndipo musagwire ntchito zolemetsa.
“‘E odiechiengʼ mokwongo mar keyo mokwongo, kinde ma uchiwoe misango mar cham manyien ne Jehova Nyasaye e Sawo mar Jumbe, losuru chokruok maler kendo kik uti tijeu mapile.
27 Muzipereka nsembe zopsereza za ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa imodzi yayimuna ndi ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi monga fungo lokomera Yehova.
Chiwuru misango miwangʼo pep mag nyirwedhi ariyo, im achiel gi nyirombe abiriyo mahikgi en achiel kaka gima dungʼ tik mangʼwe ngʼar mamoro Jehova Nyasaye.
28 Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pazikhala chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, pa nkhosa yayimuna iliyonse makilogalamu awiri.
Rwath ka rwath nyaka chiw gi chiwo mar cham maromo kilo apar mar mogo mayom moru gi mo; im to uchiw gi kilo abiriyo;
29 Ndipo pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiri aja, kilogalamu imodzi.
to imbe abiriyogo moro ka moro to chiw gi kilo adek.
30 Muziperekanso mbuzi yayimuna imodzi kuti izikhala nsembe yopepesera machimo anu.
Ewi mago meduru nywok achiel kaka chiwo mar pwodhruok e richo.
31 Muzipereka zimenezi pamodzi ndi zopereka za zakumwa ndi nsembe yake ya chakudya. Onetsetsani kuti nyamazo zilibe chilema.
Chiwuru magi kaachiel gi misango miolo piny, kumedo gi misango miwangʼo pep mapile pile kod chiwo mar cham. Neuru ni jamnigo onge songa.