< Numeri 28 >
1 Yehova anawuza Mose kuti,
Господ говори още на Моисея, казвайки:
2 “Lamula Aisraeli kuti, ‘Onetsetsani kuti mukupereka kwa Ine pa nthawi yoyikika, chopereka cha chakudya chotentha pa moto monga fungo lokoma kwa Ine.’
Заповядай на израилтяните, като им кажеш: Внимавайте да Ми принасяте на определеното им време Моите приноси, хляба Ми за благоуханна чрез огън жертва на Мене.
3 Awuze kuti, ‘Nsembe ya chakudya imene muzipereka pa moto kwa Yehova tsiku ndi tsiku ndi iyi: Ana ankhosa a chaka chimodzi awiri, wopanda chilema.
И кажи им: Ето приносът чрез огън, който ще принасяте Господу: две едногодишни агнета на ден, без недостатък, за всегдашно всеизгаряне.
4 Mmawa muzipereka mwana wankhosa mmodzi ndipo winayo madzulo.
Едно агне да принасяш заран, а другото агне да принасяш вечер;
5 Muziperekanso kilogalamu imodzi ya ufa wosalala wosakaniza ndi lita imodzi ya mafuta a olivi.
а за хлебен принос една десета от ефа чисто брашно, смесено с четвърт ин първоток дървено масло.
6 Iyi ndi nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku imene analamula pa phiri la Sinai kuti ikhale fungo lokoma, nsembe yopsereza pa moto yopereka kwa Yehova.
Това е всегдашно всеизгаряне, определено на Синайската планина, за благоуханна жертва чрез огън Господу.
7 Chopereka chachakumwa chikhale lita imodzi yachakumwa chaukali pa nkhosa iliyonse. Muzithira pamalo opatulika, kupereka kwa Yehova.
И възлиянието му да бъде четвърт ин за едното агне; в светилището да възливаш силно питие за възлияние Господу.
8 Muzipereka mwana wankhosa winayo madzulo, pamodzi ndi chopereka chachakudya monga poyamba paja ndi chopereka chachakumwa monga mmawa. Ichi ndi chopereka chachakudya, fungo lokoma kwa Yehova.’”
А другото агне да принасяш привечер: както утринния хлебен принос, и както възлиянието му, така да го принасяш за благоуханна жертва чрез огън Господу.
9 “‘Pa tsiku la Sabata, muzipereka nsembe ana ankhosa awiri a chaka chimodzi wopanda chilema, pamodzi ndi chopereka chachakumwa ndi chopereka chachakudya chokwana makilogalamu awiri a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta.
А в съботен ден да принасяте две две едногодишни агнета, без недостатък, и две десети от ефа чисто брашно, смесено с дървено масло за хлебен принос с възлиянието му.
10 Iyi ndi nsembe yopsereza ya pa Sabata iliyonse, kuwonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse ndi chopereka chake chachakumwa.’”
Това е всеизгарянето за всяка събота, освен всегдашното всеизгаряне с възлиянието му.
11 “Pa tsiku loyamba la mwezi uliwonse muzipereka kwa Yehova nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa yayimuna imodzi, ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi, onse wopanda chilema.
В новолунията си да принасяте за всеизгаряне Господу два юнеца, един овен, седем едногодишни агнета без недостатък;
12 Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pakhale chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; ndi nkhosa yayimuna, chopereka cha chakudya cha makilogalamu awiri a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta;
и за всеки юнец три десети от ефа чисто брашно, смесено с дървено масло за хлебен принос; и за единия овен две десети от ефа чисто брашно, смесено с дървено масло за хлебен принос;
13 ndipo pa mwana wankhosa aliyense, chopereka cha ufa wa kilogalamu imodzi ya ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, izi ndi za nsembe yopsereza, fungo lokoma, nsembe yotentha pa moto ya kwa Yehova.
и за всяко агне по една десета от ефа чисто брашно, смесено с дървено масло за хлебен принос. Това е всеизгаряне, за благоуханна жертва чрез огън Господу.
14 Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pakhale chopereka cha chakumwa cha malita awiri a vinyo; ndipo pa nkhosa yayimuna, lita limodzi ndi theka, ndipo pa mwana wankhosa, lita limodzi. Iyi ndi nsembe yopsereza ya mwezi ndi mwezi yoperekedwa pa mwezi watsopano mʼkati mwa chaka.
И възлиянието им да бъде вино, половин ин за юнеца, една трета от ин за овена и четвърт ин за агнето. Това е всеизгарянето за един месец през месеците на годината.
15 Powonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse ndi chopereka chake cha chakumwa, mbuzi yayimuna imodzi iperekedwe kwa Yehova ngati nsembe yopepesera machimo.
И освен всегдашното всеизгаряне да се принася Господу един козел в принос за грях, с възлиянието му.
16 “‘Pa tsiku la 14 la mwezi woyamba muzichita Paska wa Yehova.
На четиринадесетия ден от първия месец е Господната пасха.
17 Pa tsiku la 15 la mwezi womwewo pazikhala chikondwerero. Muzidya buledi wopanda yisiti kwa masiku asanu ndi awiri.
А на петнадесетия ден от тоя месец е празник; седем дена да се яде безквасен хляб.
18 Pa tsiku loyamba muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse.
На първия ден да има свето събрание, и да не работите никаква слугинска работа;
19 Koma muzipereka kwa Yehova nsembe yotentha pa moto, nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri aamuna a chaka chimodzi, onsewo wopanda chilema.
а да принесете жертва чрез огън, за всеизгаряне Господу: два юнеца, един овен и седем едногодишни агнета, които да бъдат без недостатък.
20 Pamodzi ndi ngʼombe yayimuna iliyonse, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; makilogalamu awiri pa nkhosa yayimuna iliyonse.
А хлебният им принос да бъде от чисто брашно, смесено с дървено масло; три десети от ефа да принесете за юнеца; две десети за овена;
21 Kilogalamu imodzi pa mwana wankhosa aliyense mwa ana ankhosa asanu ndi awiri aja.
и по една десета от ефа да принесеш за всяко от седемте агнета;
22 Muziphatikizapo mbuzi yayimuna monga nsembe yopepesera machimo anu.
и един козел в принос за грях, за да се извърши умилостивение за вас.
23 Muzikonza zimenezi nthawi zonse, powonjezera pa nsembe yopsereza ya mmawa.
Тия да принесете в прибавка на утринното всеизгаряне, което е всегдашно всеизгаряне.
24 Motere muzikonza chakudya cha nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pa masiku asanu ndi awiri ngati fungo lokomera Yehova. Zimenezi ziziperekedwa kuwonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse pamodzi ndi nsembe yachakumwa.
Така да принасяте храната всеки ден през седемте дена за благоуханна жертва чрез огън Господу: това да се принася с възлиянието му, в прибавка на всегдашното всеизгаряне.
25 Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse.
А на седмия ден да имате свето събрание и да не работите никаква слугинска работа.
26 “‘Pa tsiku la zipatso zoyambirira kucha, pamene mukupereka chopereka cha chakudya chatsopano kwa Yehova, pa nthawi ya chikondwerero cha Masabata, muzichita msonkhano wopatulika ndipo musagwire ntchito zolemetsa.
Също и в деня на първите плодове, когато принасяте нов хлебен принос Господу през празника ви на седмиците, да имате своето събрание, и да не работите никаква слугинска работа.
27 Muzipereka nsembe zopsereza za ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa imodzi yayimuna ndi ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi monga fungo lokomera Yehova.
И за благоухание Господу да принесете във всеизгаряне два юнеца, един овен и седем едногодишни агнета.
28 Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pazikhala chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, pa nkhosa yayimuna iliyonse makilogalamu awiri.
А хлебният им принос да бъде от чисто брашно, смесено с дървено масло, - три десети от ефа за всеки юнец, две десети за единия овен,
29 Ndipo pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiri aja, kilogalamu imodzi.
и по една десета за всяко от седемте агнета;
30 Muziperekanso mbuzi yayimuna imodzi kuti izikhala nsembe yopepesera machimo anu.
и един козел, за да се извърши умилостивение за вас.
31 Muzipereka zimenezi pamodzi ndi zopereka za zakumwa ndi nsembe yake ya chakudya. Onetsetsani kuti nyamazo zilibe chilema.
Тия да принесете (без недостатък да бъдат) с възлиянието им, в прибавка на всегдашното всеизгаряне с хлебния му принос.