< Numeri 27 >

1 Kenaka ana aakazi a Zelofehadi mwana wa Heferi, mwana wa Giliyadi, mwana wa Makiri, mwana wamwamuna wa Manase, a mʼmabanja a Manase, mwana wa Yosefe anabwera. Mayina a ana aakaziwo anali awa: Mala, Nowa, Hogila, Milika ndi Tiriza. Iwo anakayima
Tada doðoše kæeri Salpada sina Ofera sina Galada sina Mahira sina Manasijina, od plemena Manasije sina Josifova, a imena im bjehu Mala, Nuja, Egla, Melha i Tersa.
2 pa chipata cha tenti ya msonkhano pamaso pa Mose, wansembe Eliezara, atsogoleri ndi anthu onse, ndipo anati,
I stadoše pred Mojsija i pred Eleazara sveštenika i pred knezove i sav zbor na vratima šatora od sastanka, i rekoše:
3 “Abambo athu anafera mʼchipululu koma sanali nawo mʼgulu la anthu otsatira Kora, omwe anasonkhana pamodzi kutsutsana ndi Yehova. Abambo athuwo anafa chifukwa cha tchimo lawo ndipo sanasiye ana aamuna.
Otac naš umrije u pustinji, ali ne bješe u društvu s onima koji se pobuniše na Gospoda u buni Korejevoj, nego umrije od grijeha svojega, a ne ostavi sinova.
4 Nʼchifukwa chiyani dzina la abambo athu lasowa pakati pa fuko lawo, kodi popeza analibe mwana wamwamuna? Tipatseni cholowa chathu pakati pa abale a abambo athu.”
Zašto da se istrijebi ime oca našega iz porodice njegove zato što nije imao sina? Daj nam našljedstvo meðu braæom oca našega.
5 Tsono Mose anabweretsa nkhani yawo pamaso pa Yehova
I iznese Mojsije stvar njihovu pred Gospoda.
6 ndipo Yehova anati kwa iye,
A Gospod reèe Mojsiju govoreæi:
7 “Zimene ana aakazi a Zelofehadi akunena ndi zoona. Uyenera kuwapatsadi cholowa chawo pakati pa abale a abambo awo ndipo uwapatse cholowa cha abambo awowo.
Pravo govore kæeri Salpadove; podaj im pravo da imaju našljedstvo meðu braæom oca svojega, i prenesi našljedstvo oca njihova na njih.
8 “Uza Aisraeli kuti, ‘Ngati munthu afa wosasiya mwana wamwamuna, muzipereka cholowa chake kwa mwana wake wamkazi.
A sinovima Izrailjevijem kaži i reci: kad ko umre a nema sina, onda prenesite našljedstvo njegovo na kæer njegovu;
9 Ngati alibe mwana wamkazi, muzipereka cholowa chakecho kwa abale ake.
Ako li ni kæeri nema, onda podajte našljedstvo njegovo braæi njegovoj;
10 Ngati alibe abale muzipereka cholowa chake kwa abale a abambo ake.
Ako li ni braæe nema, onda podajte našljedstvo njegovo braæi oca njegova;
11 Ngati abambo ake analibe mʼbale, muzipereka cholowa chakecho kwa mnansi wake wa mʼbanja lake kuti chikhale chake. Ili likhale lamulo kwa Aisraeli, monga momwe Yehova analamulira Mose.’”
Ako li nema ni braæe oèine, onda podajte našljedstvo njegovo onomu ko mu je najbliži u rodu njegovu, i neka je njegovo. I to neka bude sinovima Izrailjevijem zakon za suðenje, kako zapovjedi Gospod Mojsiju.
12 Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Kwera phiri la Abarimu kuti ukaone dziko limene ndalipereka kwa Aisraeli.
Još reèe Gospod Mojsiju: izidi na goru ovu Avarimsku, i vidi zemlju koju sam dao sinovima Izrailjevijem.
13 Ukakaliona udzamwalira ngati Aaroni mʼbale wako,
I kad je vidiš, pribraæeš se k rodu svojemu i ti, kao što se pribrao Aron brat tvoj.
14 chifukwa pamene anthu anawukira ku madzi a Meriba mʼchipululu cha Zini, inu nonse simunamvere lamulo londilemekeza Ine ngati Woyera pamaso pawo.” (Awa anali madzi a ku Meriba ku Kadesi mʼchipululu cha Zini).
Jer ne poslušaste rijeèi moje u pustinji Sinu u svaði narodnoj, kad je trebalo da me proslavite na vodi pred oèima njihovijem. To je voda od svaðe u Kadisu u pustinji Sinu.
15 Mose anati kwa Yehova,
I reèe Mojsije Gospodu govoreæi:
16 “Ngati nʼkotheka Yehova, Mulungu wa mizimu ya anthu onse, sankhani munthu woti ayangʼanire gulu ili kuti
Gospode Bože duhovima i svakom tijelu, postavi èovjeka nad ovijem zborom,
17 alitsogolere potuluka ndi polowa, kuti anthu a Yehova asakhale ngati nkhosa zopanda mʼbusa.”
Koji æe izlaziti pred njima i koji æe dolaziti pred njima, koji æe ih izvoditi i opet dovoditi, da ne bi bio zbor Gospodnji kao ovce koje nemaju pastira.
18 Pamenepo Yehova anawuza Mose kuti, “Tenga Yoswa mwana wa Nuni, munthu amene ali ndi mzimu wa utsogoleri, ndipo umusanjike dzanja lako.
A Gospod reèe Mojsiju: uzmi k sebi Isusa sina Navina, èovjeka u kom je duh moj, i metni ruku svoju na nj,
19 Umuyimiritse pamaso pa wansembe Eliezara ndi pamaso pa gulu lonse ndipo umupatse mphamvu zolamulira, anthuwo akuona.
I izvedi ga pred Eleazara sveštenika i pred sav zbor, i podaj mu zapovijesti pred njima.
20 Umupatse gawo lina la ulemerero wako kuti Aisraeli onse azimumvera.
I podaj mu od slave svoje, da ga sluša sav zbor sinova Izrailjevijeh.
21 Ayime pamaso pa wansembe Eliezara, amene adzamudziwitse zimene Yehova akufuna pogwiritsa ntchito Urimu. Iye akalamula, Aisraeli onse azituluka ndipo akalamulanso, Aisraeliwo azibwereranso.”
I neka staje pred Eleazara sveštenika da ga pita za sud Urim pred Gospodom; po zapovijesti njegovoj neka polaze i po zapovijesti njegovoj neka dolaze on i svi sinovi Izrailjevi s njim i sav zbor.
22 Mose anachita monga Yehova anamulamulira. Anatenga Yoswa ndi kumuyimiritsa pamaso pa Eliezara wansembe ndi pamaso pa gulu lonse.
I uèini Mojsije kako mu zapovjedi Gospod; i uzev Isusa postavi ga pred Eleazara sveštenika i pred sav zbor.
23 Ndipo anamusanjika manja ndi kumupatsa mphamvu, monga Yehova ananenera kudzera mwa Mose.
I metnu ruke svoje na nj, i dade mu zapovijesti, kako bješe zapovjedio Gospod preko Mojsija.

< Numeri 27 >