< Numeri 27 >
1 Kenaka ana aakazi a Zelofehadi mwana wa Heferi, mwana wa Giliyadi, mwana wa Makiri, mwana wamwamuna wa Manase, a mʼmabanja a Manase, mwana wa Yosefe anabwera. Mayina a ana aakaziwo anali awa: Mala, Nowa, Hogila, Milika ndi Tiriza. Iwo anakayima
Et les filles de Zelophehad, fils de Hépher, fils de Galaad, fils de Makir, fils de Manassé, des familles de Manassé, fils de Joseph, s'approchèrent. Voici les noms de ses filles: Mahla, Noé, Hogla, Milca et Tirza.
2 pa chipata cha tenti ya msonkhano pamaso pa Mose, wansembe Eliezara, atsogoleri ndi anthu onse, ndipo anati,
Elles se présentèrent devant Moïse, devant le sacrificateur Éléazar, devant les princes et toute l'assemblée, à l'entrée de la tente de la Rencontre, et dirent:
3 “Abambo athu anafera mʼchipululu koma sanali nawo mʼgulu la anthu otsatira Kora, omwe anasonkhana pamodzi kutsutsana ndi Yehova. Abambo athuwo anafa chifukwa cha tchimo lawo ndipo sanasiye ana aamuna.
« Notre père est mort dans le désert. Il n'était pas du nombre de ceux qui se sont ligués contre Yahvé, à la suite de Koré, mais il est mort dans son propre péché. Il n'a pas eu de fils.
4 Nʼchifukwa chiyani dzina la abambo athu lasowa pakati pa fuko lawo, kodi popeza analibe mwana wamwamuna? Tipatseni cholowa chathu pakati pa abale a abambo athu.”
Pourquoi le nom de notre père serait-il retranché du milieu de sa famille, parce qu'il n'a pas eu de fils? Donne-nous une possession parmi les frères de notre père ».
5 Tsono Mose anabweretsa nkhani yawo pamaso pa Yehova
Moïse porta leur cause devant Yahvé.
6 ndipo Yehova anati kwa iye,
L'Éternel parla à Moïse, et dit:
7 “Zimene ana aakazi a Zelofehadi akunena ndi zoona. Uyenera kuwapatsadi cholowa chawo pakati pa abale a abambo awo ndipo uwapatse cholowa cha abambo awowo.
« Les filles de Tselophehad ont raison. Tu leur donneras une possession en héritage parmi les frères de leur père. Tu leur feras passer l'héritage de leur père.
8 “Uza Aisraeli kuti, ‘Ngati munthu afa wosasiya mwana wamwamuna, muzipereka cholowa chake kwa mwana wake wamkazi.
Tu parleras aux enfants d'Israël en disant: « Si un homme meurt et n'a pas de fils, tu feras passer son héritage à sa fille.
9 Ngati alibe mwana wamkazi, muzipereka cholowa chakecho kwa abale ake.
S'il n'a pas de fille, tu donneras son héritage à ses frères.
10 Ngati alibe abale muzipereka cholowa chake kwa abale a abambo ake.
S'il n'a pas de frères, tu donneras son héritage aux frères de son père.
11 Ngati abambo ake analibe mʼbale, muzipereka cholowa chakecho kwa mnansi wake wa mʼbanja lake kuti chikhale chake. Ili likhale lamulo kwa Aisraeli, monga momwe Yehova analamulira Mose.’”
Si son père n'a pas de frères, vous donnerez son héritage à son parent le plus proche de sa famille, et il le possédera. Ceci sera une loi et une ordonnance pour les enfants d'Israël, comme Yahvé l'a ordonné à Moïse.'"
12 Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Kwera phiri la Abarimu kuti ukaone dziko limene ndalipereka kwa Aisraeli.
Yahvé dit à Moïse: « Monte sur cette montagne d'Abarim, et regarde le pays que j'ai donné aux enfants d'Israël.
13 Ukakaliona udzamwalira ngati Aaroni mʼbale wako,
Quand tu l'auras vu, toi aussi, tu seras recueilli auprès de ton peuple, comme Aaron, ton frère, a été recueilli;
14 chifukwa pamene anthu anawukira ku madzi a Meriba mʼchipululu cha Zini, inu nonse simunamvere lamulo londilemekeza Ine ngati Woyera pamaso pawo.” (Awa anali madzi a ku Meriba ku Kadesi mʼchipululu cha Zini).
car, dans les querelles de l'assemblée, vous vous êtes rebellés contre ma parole, dans le désert de Tsin, pour m'honorer comme saint aux eaux, sous leurs yeux. » (Ce sont les eaux de Meribah de Kadesh dans le désert de Zin).
15 Mose anati kwa Yehova,
Moïse parla à l'Éternel, et dit:
16 “Ngati nʼkotheka Yehova, Mulungu wa mizimu ya anthu onse, sankhani munthu woti ayangʼanire gulu ili kuti
« Que l'Éternel, le Dieu des esprits de toute chair, établisse un homme sur l'assemblée,
17 alitsogolere potuluka ndi polowa, kuti anthu a Yehova asakhale ngati nkhosa zopanda mʼbusa.”
qui sorte devant eux et qui entre devant eux, qui les conduise dehors et qui les fasse entrer, afin que l'assemblée de l'Éternel ne soit pas comme des brebis qui n'ont pas de berger. »
18 Pamenepo Yehova anawuza Mose kuti, “Tenga Yoswa mwana wa Nuni, munthu amene ali ndi mzimu wa utsogoleri, ndipo umusanjike dzanja lako.
Yahvé dit à Moïse: « Prends Josué, fils de Nun, un homme en qui réside l'Esprit, et pose ta main sur lui.
19 Umuyimiritse pamaso pa wansembe Eliezara ndi pamaso pa gulu lonse ndipo umupatse mphamvu zolamulira, anthuwo akuona.
Tu le placeras devant le sacrificateur Éléazar et devant toute l'assemblée, et tu le recommanderas à leurs yeux.
20 Umupatse gawo lina la ulemerero wako kuti Aisraeli onse azimumvera.
Tu lui donneras l'autorité, afin que toute l'assemblée des enfants d'Israël lui obéisse.
21 Ayime pamaso pa wansembe Eliezara, amene adzamudziwitse zimene Yehova akufuna pogwiritsa ntchito Urimu. Iye akalamula, Aisraeli onse azituluka ndipo akalamulanso, Aisraeliwo azibwereranso.”
Il se présentera devant le prêtre Éléazar, qui examinera pour lui le jugement de l'urim devant l'Éternel. A sa parole, ils sortiront, et à sa parole, ils entreront, lui et tous les enfants d'Israël avec lui, toute l'assemblée. »
22 Mose anachita monga Yehova anamulamulira. Anatenga Yoswa ndi kumuyimiritsa pamaso pa Eliezara wansembe ndi pamaso pa gulu lonse.
Moïse fit ce que l'Éternel lui avait ordonné. Il prit Josué et le plaça devant le prêtre Éléazar et devant toute l'assemblée.
23 Ndipo anamusanjika manja ndi kumupatsa mphamvu, monga Yehova ananenera kudzera mwa Mose.
Il lui imposa les mains et lui donna des ordres, comme Yahvé l'avait dit par Moïse.