< Numeri 27 >
1 Kenaka ana aakazi a Zelofehadi mwana wa Heferi, mwana wa Giliyadi, mwana wa Makiri, mwana wamwamuna wa Manase, a mʼmabanja a Manase, mwana wa Yosefe anabwera. Mayina a ana aakaziwo anali awa: Mala, Nowa, Hogila, Milika ndi Tiriza. Iwo anakayima
Then came near the daughters of Zelophehad, son of Hepher, son of Gilead son of Machir son of Manasseh pertaining to the families of Manasseh, son of Joseph, —these being the names of his daughters, Mahlah Noah and Hoglah and Milcah, and Tirzah.
2 pa chipata cha tenti ya msonkhano pamaso pa Mose, wansembe Eliezara, atsogoleri ndi anthu onse, ndipo anati,
So they stood before Moses and before Eleazar the priest, and before the princes, and all the assembly, —at the entrance of the tent of meeting, saying:
3 “Abambo athu anafera mʼchipululu koma sanali nawo mʼgulu la anthu otsatira Kora, omwe anasonkhana pamodzi kutsutsana ndi Yehova. Abambo athuwo anafa chifukwa cha tchimo lawo ndipo sanasiye ana aamuna.
Our father, died in the desert, although, he, was not among the assembly that conspired against Yahweh, in the assembly of Korah, —but, in his own sin, died he; and sons, had he none.
4 Nʼchifukwa chiyani dzina la abambo athu lasowa pakati pa fuko lawo, kodi popeza analibe mwana wamwamuna? Tipatseni cholowa chathu pakati pa abale a abambo athu.”
Wherefore should the name of our father be withdrawn out of the midst of his family, because he had no son? Give ye unto us a possession, in the midst of the brethren of our father.
5 Tsono Mose anabweretsa nkhani yawo pamaso pa Yehova
And Moses brought near their cause before Yahweh.
6 ndipo Yehova anati kwa iye,
Then spake Yahweh unto Moses, saying:
7 “Zimene ana aakazi a Zelofehadi akunena ndi zoona. Uyenera kuwapatsadi cholowa chawo pakati pa abale a abambo awo ndipo uwapatse cholowa cha abambo awowo.
A right thing, are the daughters of Zelophehad speaking: Thou shalt, surely give, them a possession for an inheritance, in the midst of the brethren of their father, —and shalt cause the inheritance of their father to pass over unto them.
8 “Uza Aisraeli kuti, ‘Ngati munthu afa wosasiya mwana wamwamuna, muzipereka cholowa chake kwa mwana wake wamkazi.
And unto the sons of Israel, shalt thou speak, saying, —When, any man, shall die, having no son, then shall ye cause his inheritance to pass over to his daughter.
9 Ngati alibe mwana wamkazi, muzipereka cholowa chakecho kwa abale ake.
And, if he hath no daughter, then shall ye give his inheritance unto his, brethren.
10 Ngati alibe abale muzipereka cholowa chake kwa abale a abambo ake.
And if he hath no brethren, then shall ye give his inheritance unto the brethren of his father.
11 Ngati abambo ake analibe mʼbale, muzipereka cholowa chakecho kwa mnansi wake wa mʼbanja lake kuti chikhale chake. Ili likhale lamulo kwa Aisraeli, monga momwe Yehova analamulira Mose.’”
And, if his father hath no brethren, then shall ye give his inheritance unto his blood-relation that is near unto him of his family, and he shall possess it, —So shall it serve the sons of Israel as a regulative statute, As Yahweh commanded Moses.
12 Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Kwera phiri la Abarimu kuti ukaone dziko limene ndalipereka kwa Aisraeli.
And Yahweh said unto Moses, Go up into this mount of Abarim, —and see, the land which I have given unto the sons of Israel;
13 Ukakaliona udzamwalira ngati Aaroni mʼbale wako,
And, when thou hast seen it, then shalt thou also be withdrawn unto thy kinsfolk, —as Aaron thy brother was withdrawn;
14 chifukwa pamene anthu anawukira ku madzi a Meriba mʼchipululu cha Zini, inu nonse simunamvere lamulo londilemekeza Ine ngati Woyera pamaso pawo.” (Awa anali madzi a ku Meriba ku Kadesi mʼchipululu cha Zini).
because ye resisted my bidding—in the desert of Zin when the assembly contended, —that ye should hallow me regarding the waters, before their eyes, —the same, were the waters of Meribah, of Kadesh in the desert of Zin.
15 Mose anati kwa Yehova,
Then spake Moses unto Yahweh saying:
16 “Ngati nʼkotheka Yehova, Mulungu wa mizimu ya anthu onse, sankhani munthu woti ayangʼanire gulu ili kuti
Let Yahweh, God of the spirits of all flesh, appoint a man over the assembly;
17 alitsogolere potuluka ndi polowa, kuti anthu a Yehova asakhale ngati nkhosa zopanda mʼbusa.”
who may go out before them and who may come in before them, and who may take them out and who may bring them in, —that the assembly of Yahweh become not as sheep that have no shepherd.
18 Pamenepo Yehova anawuza Mose kuti, “Tenga Yoswa mwana wa Nuni, munthu amene ali ndi mzimu wa utsogoleri, ndipo umusanjike dzanja lako.
And Yahweh said unto Moses: Take thee Joshua son of Nun, a man in whom is spirit, —then shalt thou lean thy hand upon him;
19 Umuyimiritse pamaso pa wansembe Eliezara ndi pamaso pa gulu lonse ndipo umupatse mphamvu zolamulira, anthuwo akuona.
and shalt cause him to stand before Eleazar the priest, and before all the assembly, —and shalt charge him before their eyes;
20 Umupatse gawo lina la ulemerero wako kuti Aisraeli onse azimumvera.
and shalt put some of thine honour upon him, —that all the assembly of the sons of Israel may hearken.
21 Ayime pamaso pa wansembe Eliezara, amene adzamudziwitse zimene Yehova akufuna pogwiritsa ntchito Urimu. Iye akalamula, Aisraeli onse azituluka ndipo akalamulanso, Aisraeliwo azibwereranso.”
And, before Eleazar the priest, shall he stand, and shall ask by him for the decision of the Lights, before Yahweh, —at the bidding thereof, shall they go out, and at the bidding thereof, shall they come in—he, and all the sons of Israel with him, even all the assembly.
22 Mose anachita monga Yehova anamulamulira. Anatenga Yoswa ndi kumuyimiritsa pamaso pa Eliezara wansembe ndi pamaso pa gulu lonse.
And Moses did as Yahweh commanded him, —and took Joshua, and caused him to stand before Eleazar the priest, and before all the assembly;
23 Ndipo anamusanjika manja ndi kumupatsa mphamvu, monga Yehova ananenera kudzera mwa Mose.
and leaned his hands upon him and charged him, —As Yahweh spake by the hand of Moses.