< Numeri 27 >
1 Kenaka ana aakazi a Zelofehadi mwana wa Heferi, mwana wa Giliyadi, mwana wa Makiri, mwana wamwamuna wa Manase, a mʼmabanja a Manase, mwana wa Yosefe anabwera. Mayina a ana aakaziwo anali awa: Mala, Nowa, Hogila, Milika ndi Tiriza. Iwo anakayima
Then the daughters of Zelophehad, the son of Hepher, the son of Gilead, the son of Machir, the son of Manasseh, of the families of Manasseh, the son of Joseph, came forward: their names are Mahlah, Noah, and Hoglah, and Milcah, and Tirzah.
2 pa chipata cha tenti ya msonkhano pamaso pa Mose, wansembe Eliezara, atsogoleri ndi anthu onse, ndipo anati,
They came before Moses and Eleazar the priest and the chiefs and all the people at the door of the Tent of meeting, and said,
3 “Abambo athu anafera mʼchipululu koma sanali nawo mʼgulu la anthu otsatira Kora, omwe anasonkhana pamodzi kutsutsana ndi Yehova. Abambo athuwo anafa chifukwa cha tchimo lawo ndipo sanasiye ana aamuna.
Death overtook our father in the waste land; he was not among those who were banded together with Korah against the Lord; but death came to him in his sin; and he had no sons.
4 Nʼchifukwa chiyani dzina la abambo athu lasowa pakati pa fuko lawo, kodi popeza analibe mwana wamwamuna? Tipatseni cholowa chathu pakati pa abale a abambo athu.”
Why is the name of our father to be taken away from among his family, because he had no son? Give us a heritage among our father's brothers.
5 Tsono Mose anabweretsa nkhani yawo pamaso pa Yehova
So Moses put their cause before the Lord.
6 ndipo Yehova anati kwa iye,
And the Lord said to Moses,
7 “Zimene ana aakazi a Zelofehadi akunena ndi zoona. Uyenera kuwapatsadi cholowa chawo pakati pa abale a abambo awo ndipo uwapatse cholowa cha abambo awowo.
What the daughters of Zelophehad say is right: certainly you are to give them a heritage among their father's brothers: and let the property which would have been their father's go to them.
8 “Uza Aisraeli kuti, ‘Ngati munthu afa wosasiya mwana wamwamuna, muzipereka cholowa chake kwa mwana wake wamkazi.
And say to the children of Israel, If a man has no son at the time of his death, let his heritage go to his daughter.
9 Ngati alibe mwana wamkazi, muzipereka cholowa chakecho kwa abale ake.
And if he has no daughter, then give his heritage to his brothers.
10 Ngati alibe abale muzipereka cholowa chake kwa abale a abambo ake.
And if he has no brothers, then give his heritage to his father's brothers.
11 Ngati abambo ake analibe mʼbale, muzipereka cholowa chakecho kwa mnansi wake wa mʼbanja lake kuti chikhale chake. Ili likhale lamulo kwa Aisraeli, monga momwe Yehova analamulira Mose.’”
And if his father has no brothers, then give it to his nearest relation in the family, as his heritage: this is to be a decision made by law for the children of Israel, as the Lord gave orders to Moses.
12 Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Kwera phiri la Abarimu kuti ukaone dziko limene ndalipereka kwa Aisraeli.
And the Lord said to Moses, Go up into this mountain of Abarim so that you may see the land which I have given to the children of Israel.
13 Ukakaliona udzamwalira ngati Aaroni mʼbale wako,
And when you have seen it, you will be put to rest with your people, as your brother Aaron was:
14 chifukwa pamene anthu anawukira ku madzi a Meriba mʼchipululu cha Zini, inu nonse simunamvere lamulo londilemekeza Ine ngati Woyera pamaso pawo.” (Awa anali madzi a ku Meriba ku Kadesi mʼchipululu cha Zini).
Because in the waste land of Zin, when the people were angry, you and he went against my word and did not keep my name holy before their eyes, at the waters. (These are the waters of Meribah in Kadesh in the waste land of Zin.)
15 Mose anati kwa Yehova,
Then Moses said to the Lord,
16 “Ngati nʼkotheka Yehova, Mulungu wa mizimu ya anthu onse, sankhani munthu woti ayangʼanire gulu ili kuti
Let the Lord, the God of the spirits of all flesh, put a man at the head of this people,
17 alitsogolere potuluka ndi polowa, kuti anthu a Yehova asakhale ngati nkhosa zopanda mʼbusa.”
To go out and come in before them and be their guide; so that the people of the Lord may not be like sheep without a keeper.
18 Pamenepo Yehova anawuza Mose kuti, “Tenga Yoswa mwana wa Nuni, munthu amene ali ndi mzimu wa utsogoleri, ndipo umusanjike dzanja lako.
And the Lord said to Moses, Take Joshua, the son of Nun, a man in whom is the spirit, and put your hand on him;
19 Umuyimiritse pamaso pa wansembe Eliezara ndi pamaso pa gulu lonse ndipo umupatse mphamvu zolamulira, anthuwo akuona.
And take him before Eleazar the priest and all the meeting of the people, and give him his orders before their eyes.
20 Umupatse gawo lina la ulemerero wako kuti Aisraeli onse azimumvera.
And put your honour on him, so that all the children of Israel may be under his authority.
21 Ayime pamaso pa wansembe Eliezara, amene adzamudziwitse zimene Yehova akufuna pogwiritsa ntchito Urimu. Iye akalamula, Aisraeli onse azituluka ndipo akalamulanso, Aisraeliwo azibwereranso.”
He will take his place before Eleazar the priest, so that he may get directions from the Lord for him, with the Urim: at his word they will go out, and at his word they will come in, he and all the children of Israel.
22 Mose anachita monga Yehova anamulamulira. Anatenga Yoswa ndi kumuyimiritsa pamaso pa Eliezara wansembe ndi pamaso pa gulu lonse.
So Moses did as the Lord said: he took Joshua and put him before Eleazar the priest and the meeting of the people:
23 Ndipo anamusanjika manja ndi kumupatsa mphamvu, monga Yehova ananenera kudzera mwa Mose.
And he put his hands on him and gave him his orders, as the Lord had said by Moses.