< Numeri 27 >

1 Kenaka ana aakazi a Zelofehadi mwana wa Heferi, mwana wa Giliyadi, mwana wa Makiri, mwana wamwamuna wa Manase, a mʼmabanja a Manase, mwana wa Yosefe anabwera. Mayina a ana aakaziwo anali awa: Mala, Nowa, Hogila, Milika ndi Tiriza. Iwo anakayima
Joseph capa Manasseh imthung, Makhir, ahnie capa Gilead, ahnie capa Hepher, ahnie capa Zelophehad e canu naw doeh. A canunaw e minnaw teh, Mahlah, Noah, Hoglah, Milkah hoi Tirzah tinaw doeh.
2 pa chipata cha tenti ya msonkhano pamaso pa Mose, wansembe Eliezara, atsogoleri ndi anthu onse, ndipo anati,
Kamkhuengnae lukkareiim takhang koe Mosi hoi vaihma Eleazar hoi tamikalennaw kamkhuengnaw e hmalah a kangdue awh teh,
3 “Abambo athu anafera mʼchipululu koma sanali nawo mʼgulu la anthu otsatira Kora, omwe anasonkhana pamodzi kutsutsana ndi Yehova. Abambo athuwo anafa chifukwa cha tchimo lawo ndipo sanasiye ana aamuna.
Kahrawngum vah maimae na pa a due teh, BAWIPA taranlahoi cusin hane tamihu, Korah tamihu koe bawk van hoeh. Hatei, ama yon e lahoi a due teh a capa hai tawn hoeh
4 Nʼchifukwa chiyani dzina la abambo athu lasowa pakati pa fuko lawo, kodi popeza analibe mwana wamwamuna? Tipatseni cholowa chathu pakati pa abale a abambo athu.”
Capa a tawn hoeh kecu dawkvah, bangkongmaw apa min teh miphun thung hoi a kahma han, mintoenaw thung dawkvah, ka ham kawi na poe van leih ati awh.
5 Tsono Mose anabweretsa nkhani yawo pamaso pa Yehova
Hot patetlah Mosi ni hote lawk teh BAWIPA koe a pha sak.
6 ndipo Yehova anati kwa iye,
BAWIPA ni Mosi hah a pato teh,
7 “Zimene ana aakazi a Zelofehadi akunena ndi zoona. Uyenera kuwapatsadi cholowa chawo pakati pa abale a abambo awo ndipo uwapatse cholowa cha abambo awowo.
Zelophehad canunaw ni kathuem e a sak awh. A na pa hmaunawnghanaw rahak vah, a ham kawi na poe awh roeroe vaiteh, a na pa ham hah na poe awh han.
8 “Uza Aisraeli kuti, ‘Ngati munthu afa wosasiya mwana wamwamuna, muzipereka cholowa chake kwa mwana wake wamkazi.
Isarel catounnaw koevah, tami buet touh ca tongpa tawn laipalah dout pawiteh, a râw teh a canunaw na poe han.
9 Ngati alibe mwana wamkazi, muzipereka cholowa chakecho kwa abale ake.
Hahoi a canu tawn hoehpawiteh, a râw teh a hmaunawngha na poe han.
10 Ngati alibe abale muzipereka cholowa chake kwa abale a abambo ake.
Hmaunawngha tawn hoehpawiteh, a na pa e hmaunawngha na poe pouh han.
11 Ngati abambo ake analibe mʼbale, muzipereka cholowa chakecho kwa mnansi wake wa mʼbanja lake kuti chikhale chake. Ili likhale lamulo kwa Aisraeli, monga momwe Yehova analamulira Mose.’”
A na pa ni hmaunawngha tawn hoehpawiteh, a râw teh a huikonaw na poe vaiteh, ahnimouh ni a ham awh han. BAWIPA ni Mosi kâ a poe e patetlah Isarel canaw hanlah lawkcengnae phunglam lah ao han, telah dei pouh telah ati.
12 Kenaka Yehova anati kwa Mose, “Kwera phiri la Abarimu kuti ukaone dziko limene ndalipereka kwa Aisraeli.
BAWIPA ni Mosi koevah, Abarim mon dawkvah luen nateh, Isarel catounnaw ka poe hane ram hah radoung haw.
13 Ukakaliona udzamwalira ngati Aaroni mʼbale wako,
Hahoi na hmu toteh, na hmaunawngha Aron e a miphunnaw koevah, a ceikhai awh e patetlah nang hai na ceikhai awh han.
14 chifukwa pamene anthu anawukira ku madzi a Meriba mʼchipululu cha Zini, inu nonse simunamvere lamulo londilemekeza Ine ngati Woyera pamaso pawo.” (Awa anali madzi a ku Meriba ku Kadesi mʼchipululu cha Zini).
Bangkongtetpawiteh, Zin thingyei dawk taminaw pueng ni a phuenang awh navah, a mithmu vah tui dawk kai barilawa na poe nahanelah, kai ni kâ na poe e taranlahoi taran a thaw awh telah ati (hot teh Zin thingyei dawk Kadesh hoi Meribah tie lah a o).
15 Mose anati kwa Yehova,
Hahoi Mosi ni BAWIPA a pato teh,
16 “Ngati nʼkotheka Yehova, Mulungu wa mizimu ya anthu onse, sankhani munthu woti ayangʼanire gulu ili kuti
moithangnaw pueng e hringnae kaukkung Cathut BAWIPA e taminaw hah kakhoumkung tawn laipalah tu patetlah ao hoeh nahanlah tamihu,
17 alitsogolere potuluka ndi polowa, kuti anthu a Yehova asakhale ngati nkhosa zopanda mʼbusa.”
hmalah cei hoi ahnimouh tâcokhai hane hoi kâenkhai hane kahrawikung hah rawi seh, telah ati.
18 Pamenepo Yehova anawuza Mose kuti, “Tenga Yoswa mwana wa Nuni, munthu amene ali ndi mzimu wa utsogoleri, ndipo umusanjike dzanja lako.
BAWIPA ni Mosi koevah, Nun capa hnotithainae ka tawn e Joshua hrawi nateh, ahni van na kut toung pouh.
19 Umuyimiritse pamaso pa wansembe Eliezara ndi pamaso pa gulu lonse ndipo umupatse mphamvu zolamulira, anthuwo akuona.
Vaihma Eleazar hoi ka kamkhuengnaw hmalah kangdout sak nateh, ahnimae mithmu vah caksak.
20 Umupatse gawo lina la ulemerero wako kuti Aisraeli onse azimumvera.
Isarel catounnaw pueng ni a lawk a ngâi pouh thai nahan, na kâtawnnae a tangawn hah na poe han.
21 Ayime pamaso pa wansembe Eliezara, amene adzamudziwitse zimene Yehova akufuna pogwiritsa ntchito Urimu. Iye akalamula, Aisraeli onse azituluka ndipo akalamulanso, Aisraeliwo azibwereranso.”
Ahni teh vaihma Eleazar hmalah a kangdue vaiteh, ama ni BAWIPA hmalah, Urim hno lahoi lawkkamnae a la vaiteh, ama kâ lahoi Isarel catounnaw pueng teh a tâco a kâen awh han, telah ati.
22 Mose anachita monga Yehova anamulamulira. Anatenga Yoswa ndi kumuyimiritsa pamaso pa Eliezara wansembe ndi pamaso pa gulu lonse.
Mosi ni BAWIPA kâpoe e patetlah a sak, Joshua hah a hrawi teh, Eleazar hoi kamkhuengnaw hmalah a kangdue sak.
23 Ndipo anamusanjika manja ndi kumupatsa mphamvu, monga Yehova ananenera kudzera mwa Mose.
A lathueng vah kut a toung pouh teh, Mosi hno lahoi BAWIPA ni kâ a poe e patetlah kâtawnnae hah a poe.

< Numeri 27 >