< Numeri 26 >

1 Utatha mliri Yehova anati kwa Mose ndi Eliezara mwana wa Aaroni,
И бысть но язве, и рече Господь к Моисею и Елеазару жерцу, глаголя:
2 “Werengani Aisraeli onse mwa mabanja awo, onse a zaka makumi awiri kapena kuposera pamenepo omwe angathe kugwira ntchito ya usilikali mʼgulu lankhondo la Israeli.”
возми начало всего сонма сынов Израилевых от двадесяти лет и вышше, но домом отечеств их, всяк исходяй вооружитися во Израили.
3 Kotero mu zigwa za Mowabu pafupi ndi mtsinje wa Yorodani ku Yeriko, Mose ndi wansembe Eliezara anayankhula nawo kuti,
И глагола Моисей и Елеазар жрец к ним во Аравофе Моавли при Иордане у Иерихона, глаголя:
4 “Werengani amuna a zaka makumi awiri kapena kuposera pamenepo, monga momwe Yehova walamulira Mose.” Aisraeli omwe anachokera ku Igupto ndi awa:
от двадесяти лет и вышше, якоже заповеда Господь Моисею: и сынове Израилтестии изшедшии из Египта:
5 Zidzukulu za Rubeni, mwana woyamba wamwamuna wa Israeli, zinali izi: kuchokera mwa Hanoki, fuko la Ahanoki; kuchokera mwa Palu, fuko la Apalu;
Рувим первенец Израилев. Сынове же Рувимли: Енох и сонм Енохов, Фаллу сонм Фаллов,
6 kuchokera mwa Hezironi, fuko la Ahezironi; kuchokera mwa Karimi, fuko la Akarimi.
Асрону сонм Асронов, Харму сонм Хармиин.
7 Awa anali mafuko a Rubeni: onse amene anawerengedwa analipo 43,730.
Сии сонми Рувимли: и бысть соглядание их четыредесять три тысящы и шесть сот и тридесять.
8 Mwana wa Palu anali Eliabu,
И сынове Фалловы Елиав.
9 ndipo ana a Eliabu anali Nemueli, Datani ndi Abiramu. Datani ndi Abiramu anali gulu la akuluakulu aja amene anawukira Mose ndi Aaroni ndipo analinso mʼgulu la otsatira Kora pamene anawukira Yehova.
И сынове Елиавли Намуил и Дафан и Авирон: сии нарочитии сонму: сии суть воставше на Моисеа и Аарона в сонме Кореове в крамоле на Господа:
10 Nthaka inangʼambika ndi kuwameza pamodzi ndi Kora, kotero kuti gulu lawo linafa pamene moto unapsereza anthu 250 aja, nasanduka chenjezo.
и отверзши земля уста своя пожре их и Кореа в смерти сонма его, егда пояде огнь двести и пятьдесят, и быша в знамение.
11 Koma ana a Kora sanafe nawo.
Сынове же Кореовы не измроша.
12 Zidzukulu za Simeoni mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Nemueli, fuko la Anemuele; kuchokera mwa Yamini, fuko la Ayamini; kuchokera mwa Yakini fuko la Ayakini;
И сынове Симеони, сонм сынов Симеоних: Намуилу сонм Намуилов, Иамину сонм Иаминов, Иахину сонм Иахинов,
13 kuchokera mwa Zera, mbumba ya Zera; kuchokera mwa Sauli, fuko la Asauli.
Заре сонм Зарин, Саулу сонм Саулов.
14 Awa anali mafuko a Simeoni. Iwowa analipo amuna 22,200.
Сии сонми Симеони от соглядания их двадесять две тысящы и двести.
15 Zidzukulu za Gadi mwa mafuko awo ndi izi: kuchokera mwa Zefoni, fuko la Azefoni; kuchokera mwa Hagi, fuko la Ahagi; kuchokera mwa Suni, fuko la Asuni;
Сынове же Иудины Ир и Авнан и Силом, и Фарес и Зара: и умре Ир и Авнан в земли Ханаани.
16 kuchokera mwa Ozini, fuko la Aozini; kuchokera mwa Eri, fuko la Aeri;
И быша сынове Иудины по сонмом своим: Силому сонм Силомль, Фаресу сонм Фаресов, Заре сонм Зарин.
17 kuchokera mwa Arodi, fuko la Aarodi; kuchokera mwa Arieli, fuko la a Areli.
И быша сынове Фаресовы: Асрону сонм Асронов, Иамуилу сонм Иамуилов.
18 Awa ndiwo anali mafuko a Gadi. Onse amene anawerengedwa analipo 40,500.
Сии сонми Иудины по согляданию их седмьдесят шесть тысящ и пять сот.
19 Eri ndi Onani anali ana aamuna a Yuda, koma anafera mu Kanaani.
И сынове Иссахаровы по сонмом своим: Фоле сонм Фолин Фуеви сонм Фуин,
20 Zidzukulu za Yuda monga mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Sela, fuko la Asera; kuchokera mwa Perezi, fuko la Aperezi; kuchokera mwa Zera, mbumba ya Zera.
Иасуву сонм Иасувин, Амвраму сонм Амврамль.
21 Zidzukulu za Perezi zinali izi: kuchokera mwa Hezironi, fuko la Ahezironi; kuchokera mwa Hamuli, fuko la Ahamuli.
Сии сонми Иссахаровы но согляданию их шестьдесят и четыри тысящы и четыреста.
22 Awa ndiwo anali mafuko a Yuda. Amene anawerenga analipo 76,500.
Сынове Завулони по сонмом своим: Сареду сонм Саредин, Аллону сонм Аллонин, Аллилу сонм Аллилин.
23 Zidzukulu za Isakara monga mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Tola, fuko la Atola; kuchokera mwa Puwa, fuko la Apuwa;
Сии сонми Завулони по согляданию их шестьдесят тысящ и пять сот.
24 kuchokera mwa Yasubu, fuko la Ayasubu. Kuchokera mwa Simironi, fuko la Asimironi.
Сынове Гадовы по сонмом их: Сафону сонм Сафонин, Аггину сонм Аггинов, Сунину сонм Сунинов,
25 Awa ndi amene anali a fuko la Isakara. Amene anawerengedwa analipo 64,300.
Азену сонм Азенин, Адду сонм Аддин,
26 Zidzukulu za Zebuloni mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Seredi, fuko la Aseredi; kuchokera mwa Eloni, fuko la Aeloni; kuchokera mwa Yahaleeli, fuko la Ayahaleeli.
Ароаду сонм Ароадин, Ариилу сонм Арииль.
27 Awa ndiwo anali mafuko a Zebuloni. Amene anawerengedwa analipo 60,500.
Сии сонми сынов Гадовых но согляданию их четыредесять и четыри тысящы и пять сот.
28 Zidzukulu za Yosefe mwa mafuko awo kupyolera mwa Manase ndi Efereimu zinali izi:
Сынове Асировы по сонмом их: Иамину сонм Иаминов, Иесую сонм Иесуинь,
29 Zidzukulu za Manase: kuchokera mwa Makiri, fuko la Amakiri (Makiri anali abambo ake a Giliyadi); kuchokera mwa Giliyadi, fuko la Agiliyadi.
Вариаю сонм Вариаинь, Ховеру сонм Ховерин, Мелхиилу сонм Мелхиилин,
30 Izi ndizo zinali zidzukulu za Giliyadi; kuchokera mwa Iyezeri, fuko la Aiyezeri; kuchokera mwa Heleki, fuko la Aheleki;
имя же дщери Асирове Сара,
31 kuchokera mwa Asirieli, fuko la Aasirieli; kuchokera mwa Sekemu, fuko la Asekemu;
сии сонми Асировы но согляданию их четыредесять три тысящи и четыреста.
32 kuchokera mwa Semida, fuko la Asemida; kuchokera mwa Heferi, fuko la Aheferi.
Сынове Иосифли по сонмом их: Манассиа и Ефрем.
33 (Zelofehadi mwana wa Heferi analibe ana aamuna koma ana aakazi okha, amene mayina awo anali: Mala, Nowa, Hogila, Milika ndi Tiriza.)
Сынове Манассиины: Махиру сонм Махирин: и Махир роди Галаада, Галааду сонм Галаадин.
34 Awa ndiwo anali mafuko a Manase. Amene anawerengedwa analipo 52,700.
И сии сынове Галаадины: Ахиезеру сонм Ахиезеров, Хелеку сонм Хелеков,
35 Zidzukulu za Efereimu monga mwa mafuko awo zinali izi; kuchokera mwa Sutela, fuko la Asutela; kuchokera mwa Bekeri, fuko la Abekeri; kuchokera mwa Tahani, fuko la Atahani.
Есриилу сонм Есриилов, Сихему сонм Сихемль,
36 Zidzukulu za Sutela zinali izi: kuchokera mwa Erani, fuko la Aerani.
Симаеру сонм Симаерин, и Оферу сонм Оферов.
37 Awa ndiwo anali mafuko a Efereimu. Amene anawerengedwa analipo 32,500. Zimenezi zinali zidzukulu za Yosefe monga mwa mafuko awo.
И Салпааду сыну Оферову не быша ему сынове, но токмо дщери. И сия имена дщерем Салпаадовым: Маала и Нуа, и Егла и Мелха и Ферса.
38 Zidzukulu za Benjamini monga mwa mabanja awo zinali izi: kuchokera mwa Bela, fuko la Abela; kuchokera mwa Asibeli, fuko la Aasibeli; kuchokera mwa Ahiramu, fuko la Ahiramu;
Сии сонми Манассиины по согляданию их пятьдесят и две тысящы и седмь сот.
39 kuchokera mwa Sufamu, fuko la Asufamu; kuchokera mwa Hufamu, fuko la Ahufamu;
И сии сынове Ефремли: Суфалу сонм Суфалин, Танаху сонм Танахин.
40 Zidzukulu za Bela kupyolera mwa Aridi ndi Naamani zinali izi: kuchokera mwa Aridi, fuko la Aaridi; kuchokera mwa Naamani, fuko la Anaamani;
Сии сынове Суфаловы: Едену сонм Еденин.
41 Awa ndiwo anali mabanja a Benjamini. Amene nawerengedwa analipo 45,600.
Сии сонми Ефремли по согляданию их тридесять две тысящы и пять сот. Сии сонми сынов Иосифовых по сонмом их.
42 Zidzukulu za Dani mwa mabanja awo zinali izi: kuchokera mwa Suhamu fuko la Asuhamu. Izi zinali zidzukulu za Dani.
Сынове Вениамини по сонмом их: Валу сонм Валин, Асивиру сонм Асивиров, Иахирану сонм Иахиранин, Софану сонм Софанин.
43 Onse a fuko la Asuhamu amene anawerengedwa analipo 64,400.
И быша сынове Валу Адерь и Ноеман:
44 Zidzukulu za Aseri monga mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Imina, fuko la Aimuna; kuchokera mwa Isivi, fuko la Ayisivi; kuchokera mwa Beriya, fuko la Aberiya;
Адеру сонм Адерин, и Ноеману сонм Ноеманин.
45 ndipo kupyolera mwa zidzukulu za Beriya: kuchokera mwa Heberi, fuko la Aheberi; kuchokera mwa Malikieli, fuko la Amalikieli;
Сии сынове Вениамини по сонмом их по согляданию их четыредесять и пять тысящ и шесть сот.
46 (Aseri anali ndi mwana wamkazi dzina lake Sera)
И сынове Дановы по сонмом их: Самею сонм Самеин: сии сонми Дановы но сонмом их.
47 Awa ndiwo anali mafuko a Aseri. Onse amene anawerengedwa analipo 53,400.
Вси сонми Самеини по согляданию их шестьдесят четыри тысящы и четыреста.
48 Zidzukulu za Nafutali mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Yahazeeli, fuko la Ayahazeeli; kuchokera mwa Guni, fuko la Aguni;
Сынове Неффалимли по сонмом их: Асиилу сонм Асиилев, Гоину сонм Гоинин,
49 kuchokera mwa Yezeri, fuko la Ayezeri; kuchokera mwa Silemu, fuko la Asilemu.
Иесрию сонм Иесриев, Селлиму сонм Селлимов.
50 Awa ndiwo anali mafuko a Nafutali. Onse amene anawerengedwa analipo 45,400.
Сии сонми Неффалимли по согляданию их четыредесять пять тысящ и четыреста.
51 Chiwerengero chonse cha amuna mu Israeli chinalipo 601,730.
Сие соглядание сынов Израилевых шесть сот едина тысяща и седмь сот тридесять.
52 Yehova anawuza Mose kuti,
И рече Господь к Моисею, глаголя:
53 “Uwagawire dziko anthu awa kuti likhale cholowa chawo molingana ndi chiwerengero cha mayina awo.
сим разделится земля в наследие по числу имен:
54 Gulu lalikulu ulipatse cholowa chachikulu, ndipo lochepa cholowa chocheperapo. Gulu lililonse lilandire cholowa chake molingana ndi chiwerengero cha amene anawerengedwa.
множайшым да умножиши наследие, и малейшым да умалиши наследие их: коемуждо, якоже суть соглядани, да дастся наследие их:
55 Dzikolo uligawe pochita maere. Alandire cholowa chawocho potsata mayina a mafuko a makolo awo.
по жребием да разделится земля именам, по племенем отечеств своих да наследят:
56 Cholowa chawo uchigawe pakati pa fuko lalikulu ndi lalingʼono mwa maere.”
от жребия да разделиши наследие их между многими и малыми.
57 Alevi omwe anawerengedwa monga mwa mafuko awo ndi awa: kuchokera mwa Geresoni, fuko la Ageresoni; kuchokera mwa Kohati, fuko la Akohati; kuchokera mwa Merari, fuko la Amerari.
И сынове Левиини но сонмом их: Гирсону сонм Гирсонов, Каафу сонм Каафов, Мераре сонм Мерарин.
58 Awanso anali mabanja a Alevi: banja la Alibini, banja la Ahebroni, banja la Amali, banja la Amusi, fuko la Kora banja la Akohati, (Kohati anali abambo a Amramu.
Сии сонми сынов Левииных: сонм Ловенин, сонм Хевронин, и сонм Мусин, и сонм Кореов. И Кааф роди Амрама.
59 Dzina la mkazi wa Amramu linali Yokobedi, mdzukulu wa Levi, yemwe anabadwa mwa Alevi mu Igupto. Yokobedi anaberekera Amramu Aaroni, Mose ndi Miriamu mlongo wawo.
Имя же жене Амрамли Иохавеф, дщи Левиина, яже роди сих Левии во Египте, и роди Амраму Аарона и Моисеа и Мариам сестру их.
60 Aaroni anali abambo a Nadabu, Abihu, Eliezara ndi Itamara.
И родишася Аарону Надав и Авиуд, и Елеазар и Ифамар.
61 Koma Nadabu ndi Abihu anafa pamene anapereka nsembe pamaso pa Yehova ndi moto wachilendo).
И умре Надав и Авиуд, егда принесоста огнь чуждий пред Господем в пустыни Синайстей.
62 Alevi onse aamuna a mwezi umodzi kapena kuposera pamenepa analipo 23,000. Iwowo sanawerengedwe pamodzi ndi Aisraeli ena chifukwa sanalandire cholowa pakati pawo.
И быша от соглядания их двадесять три тысящы, всяк мужеск пол от единаго месяца и вышше: не быша бо соглядани посреде сынов Израилевых, яко не дадеся им жребий посреде сынов Израилевых.
63 Awa ndi amene anawerengedwa ndi Mose ndi Eliezara wansembe pamene ankawerenga Aisraeli pa zigwa za ku Mowabu mʼmbali mwa Yorodani ku Yeriko.
И сие соглядание Моисеа и Елеазара жерца, иже соглядаша сынов Израилевых во Аравофе Моавли, у Иордана при Иерихоне.
64 Mwa anthu amenewa panalibe ndi mmodzi yemwe amene anali mʼgulu la Aisraeli omwe Mose ndi wansembe Aaroni anawawerenga mʼchipululu cha Sinai;
И в сих не бяше человек от согляданых Моисеом и Аароном, ихже соглядаша сынов Израилевых в пустыни Синайстей.
65 Chifukwa Yehova anali atawuza Aisraeliwo kuti adzafera ndithu mʼchipululu, ndipo palibe ndi mmodzi yemwe amene anatsala kupatula Kalebe mwana wa Yefune ndi Yoswa mwana wa Nuni.
Понеже рече Господь им: смертию измрут в пустыни. И не остася от них ни един, кроме Халева сына Иефонниина и Иисуса сына Навина.

< Numeri 26 >