< Numeri 26 >

1 Utatha mliri Yehova anati kwa Mose ndi Eliezara mwana wa Aaroni,
Or, à la suite de cette mortalité, l’Éternel dit à Moïse et à Eléazar, fils d’Aaron le pontife, ce qui suit:
2 “Werengani Aisraeli onse mwa mabanja awo, onse a zaka makumi awiri kapena kuposera pamenepo omwe angathe kugwira ntchito ya usilikali mʼgulu lankhondo la Israeli.”
"Faites le relevé de la communauté entière des enfants d’Israël, depuis l’âge de vingt ans et au-delà, par familles paternelles; de tous ceux qui sont aptes au service en Israël."
3 Kotero mu zigwa za Mowabu pafupi ndi mtsinje wa Yorodani ku Yeriko, Mose ndi wansembe Eliezara anayankhula nawo kuti,
Moïse et Eléazar le pontife leur en firent part, dans les plaines de Moab, au bord du Jourdain faisant face à Jéricho, en disant:
4 “Werengani amuna a zaka makumi awiri kapena kuposera pamenepo, monga momwe Yehova walamulira Mose.” Aisraeli omwe anachokera ku Igupto ndi awa:
"…Depuis l’âge de vingt ans et au-delà; ainsi que l’Éternel l’avait prescrit à Moïse et aux enfants d’Israël, lorsqu’ils furent sortis du pays d’Egypte."
5 Zidzukulu za Rubeni, mwana woyamba wamwamuna wa Israeli, zinali izi: kuchokera mwa Hanoki, fuko la Ahanoki; kuchokera mwa Palu, fuko la Apalu;
Ruben, premier-né d’Israël. Les fils de Ruben: Hénok, d’où la famille des Hénokites; de Pallou, la famille des Pallouïtes;
6 kuchokera mwa Hezironi, fuko la Ahezironi; kuchokera mwa Karimi, fuko la Akarimi.
de Heçrôn, la famille des Heçronites; de Karmi, la famille des Karmites.
7 Awa anali mafuko a Rubeni: onse amene anawerengedwa analipo 43,730.
Telles sont les familles issues de Ruben; on y compta quarante-trois mille sept cent trente hommes.
8 Mwana wa Palu anali Eliabu,
Fils de Pallou: Eliab.
9 ndipo ana a Eliabu anali Nemueli, Datani ndi Abiramu. Datani ndi Abiramu anali gulu la akuluakulu aja amene anawukira Mose ndi Aaroni ndipo analinso mʼgulu la otsatira Kora pamene anawukira Yehova.
Fils d’Eliab: Nemouêl, Dathan et Abiram. C’Est ce Dathan et cet Abiram, dignitaires de la communauté, qui s’attaquèrent à Moïse et à Aaron avec la faction de Coré, lorsque celle-ci s’attaqua à l’Éternel.
10 Nthaka inangʼambika ndi kuwameza pamodzi ndi Kora, kotero kuti gulu lawo linafa pamene moto unapsereza anthu 250 aja, nasanduka chenjezo.
Mais la terre ouvrit son sein et les engloutit avec Coré, pendant que périssait le reste du parti, que le feu consumait les deux cent cinquante hommes, frappés pour l’exemple.
11 Koma ana a Kora sanafe nawo.
Quant aux fils de Coré, ils ne périrent point.
12 Zidzukulu za Simeoni mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Nemueli, fuko la Anemuele; kuchokera mwa Yamini, fuko la Ayamini; kuchokera mwa Yakini fuko la Ayakini;
Fils de Siméon, selon leurs familles: de Nemouêl, la famille des Nemouêlites; de Yamîn, la famille des Yaminites; de Yakhîn, la famille des Yakhinites;
13 kuchokera mwa Zera, mbumba ya Zera; kuchokera mwa Sauli, fuko la Asauli.
de Zérah, la famille des Zarhites; de Chaoul, la famille des Chaoulites.
14 Awa anali mafuko a Simeoni. Iwowa analipo amuna 22,200.
Telles sont les familles issues de Siméon: vingt-deux mille deux cents hommes.
15 Zidzukulu za Gadi mwa mafuko awo ndi izi: kuchokera mwa Zefoni, fuko la Azefoni; kuchokera mwa Hagi, fuko la Ahagi; kuchokera mwa Suni, fuko la Asuni;
Fils de Gad, selon leurs familles: de Cefôn, la famille des Cefonites; de Hagghi, la famille des Hagghites; de Chouni, la famille des Chounites;
16 kuchokera mwa Ozini, fuko la Aozini; kuchokera mwa Eri, fuko la Aeri;
d’Ozni, la famille des Oznites; de Eri, la famille des Erites;
17 kuchokera mwa Arodi, fuko la Aarodi; kuchokera mwa Arieli, fuko la a Areli.
d’Arod, la famille des Arodites; d’Arêli, la famille des Arêlites.
18 Awa ndiwo anali mafuko a Gadi. Onse amene anawerengedwa analipo 40,500.
Telles sont les familles des fils de Gad, selon leur dénombrement: quarante mille cinq cents hommes.
19 Eri ndi Onani anali ana aamuna a Yuda, koma anafera mu Kanaani.
Fils de Juda: Er et Onân; mais Er et Onân moururent dans le pays de Canaan.
20 Zidzukulu za Yuda monga mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Sela, fuko la Asera; kuchokera mwa Perezi, fuko la Aperezi; kuchokera mwa Zera, mbumba ya Zera.
Les autres fils de Juda furent, selon leurs familles: Chêla, d’où la famille des Chêlanites; de Péreç, la famille des Parcites; de Zérah, la famille des Zarhites.
21 Zidzukulu za Perezi zinali izi: kuchokera mwa Hezironi, fuko la Ahezironi; kuchokera mwa Hamuli, fuko la Ahamuli.
Les fils de Péreç furent: Heçrôn, d’où la famille des Heçronites; Hamoul, d’où la famille des Hamoulites.
22 Awa ndiwo anali mafuko a Yuda. Amene anawerenga analipo 76,500.
Telles sont les familles de Juda, selon leur dénombrement: soixante-seize mille cinq cents hommes.
23 Zidzukulu za Isakara monga mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Tola, fuko la Atola; kuchokera mwa Puwa, fuko la Apuwa;
Fils d’Issachar, selon leurs familles: Tola, d’où la famille des Tolaïtes; Pouvva, d’où la famille des Pounites;
24 kuchokera mwa Yasubu, fuko la Ayasubu. Kuchokera mwa Simironi, fuko la Asimironi.
de Yachoub, la famille des Yachoubites; de Chimrôn, la famille des Chimronites.
25 Awa ndi amene anali a fuko la Isakara. Amene anawerengedwa analipo 64,300.
Telles sont les familles d’Issachar, selon leur dénombrement: soixante-quatre mille trois cents hommes.
26 Zidzukulu za Zebuloni mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Seredi, fuko la Aseredi; kuchokera mwa Eloni, fuko la Aeloni; kuchokera mwa Yahaleeli, fuko la Ayahaleeli.
Fils de Zabulon, selon leurs familles: de Séred, la famille des Sardites; d’Elôn, la famille des Elonites; de Yahleêl, la famille des Yahleêlites.
27 Awa ndiwo anali mafuko a Zebuloni. Amene anawerengedwa analipo 60,500.
Telles sont les familles issues de Zabulon, selon leur dénombrement: soixante mille cinq cents hommes.
28 Zidzukulu za Yosefe mwa mafuko awo kupyolera mwa Manase ndi Efereimu zinali izi:
Fils de Joseph, selon leurs familles: Manassé et Ephraïm.
29 Zidzukulu za Manase: kuchokera mwa Makiri, fuko la Amakiri (Makiri anali abambo ake a Giliyadi); kuchokera mwa Giliyadi, fuko la Agiliyadi.
Fils de Manassé: Makhir, d’où la famille des Makhirites. Makhir engendra Ghilad: de Ghilad, la famille des Ghiladites.
30 Izi ndizo zinali zidzukulu za Giliyadi; kuchokera mwa Iyezeri, fuko la Aiyezeri; kuchokera mwa Heleki, fuko la Aheleki;
Suivent les fils de Ghllad: lézer, d’où la famille des lézrites; de Hêlek, la famille des Hélkites;
31 kuchokera mwa Asirieli, fuko la Aasirieli; kuchokera mwa Sekemu, fuko la Asekemu;
puis Asriêl, d’où la famille des Asriêlites; Chékem, d’où la famille des Chikmites;
32 kuchokera mwa Semida, fuko la Asemida; kuchokera mwa Heferi, fuko la Aheferi.
Chemida, d’où la famille des Chemidaïtes; de Héfer, la famille des Héfrites.
33 (Zelofehadi mwana wa Heferi analibe ana aamuna koma ana aakazi okha, amene mayina awo anali: Mala, Nowa, Hogila, Milika ndi Tiriza.)
Celofhad, fils de Héfer, n’eut point de fils, mais seulement des filles. Les filles de Celofhad se nommaient: Mahla, Nos, Hogla, Milca et Tirça.
34 Awa ndiwo anali mafuko a Manase. Amene anawerengedwa analipo 52,700.
Ce sont là les familles de Manassé: on y comptait cinquante-deux mille sept cents hommes.
35 Zidzukulu za Efereimu monga mwa mafuko awo zinali izi; kuchokera mwa Sutela, fuko la Asutela; kuchokera mwa Bekeri, fuko la Abekeri; kuchokera mwa Tahani, fuko la Atahani.
Ceux-ci sont les fils d’Ephraïm, selon leurs familles: de Choutélah, la famille des Choutalhites; de Béker, la famille des Bakrites; de Tahân, la famille des Tahanites.
36 Zidzukulu za Sutela zinali izi: kuchokera mwa Erani, fuko la Aerani.
Et ceux-ci sont les descendants de Choutélah: Erân, d’où la famille des Eranites.
37 Awa ndiwo anali mafuko a Efereimu. Amene anawerengedwa analipo 32,500. Zimenezi zinali zidzukulu za Yosefe monga mwa mafuko awo.
Telles sont les familles des fils d’Ephraïm, selon leur dénombrement: trente-deux mille cinq cents hommes. Tels sont les descendants de Joseph, selon leurs familles.
38 Zidzukulu za Benjamini monga mwa mabanja awo zinali izi: kuchokera mwa Bela, fuko la Abela; kuchokera mwa Asibeli, fuko la Aasibeli; kuchokera mwa Ahiramu, fuko la Ahiramu;
Fils de Benjamin, selon leurs familles: de Béla, la famille des Balites; d’Achbêl, la famille des Achbélites; d’Ahiram, la famille des Ahiramites;
39 kuchokera mwa Sufamu, fuko la Asufamu; kuchokera mwa Hufamu, fuko la Ahufamu;
de Chefoufam, la famille des Chefoufamites; de Houfam, la famille des Houfamites.
40 Zidzukulu za Bela kupyolera mwa Aridi ndi Naamani zinali izi: kuchokera mwa Aridi, fuko la Aaridi; kuchokera mwa Naamani, fuko la Anaamani;
Béla eut pour fils Ard' et Naamân: d’où la famille des Ardites, et de Naamân, la famille des Naamites.
41 Awa ndiwo anali mabanja a Benjamini. Amene nawerengedwa analipo 45,600.
Tels sont les descendants de Benjamin, selon leurs familles: on y compta quarante-cinq mille six cents hommes.
42 Zidzukulu za Dani mwa mabanja awo zinali izi: kuchokera mwa Suhamu fuko la Asuhamu. Izi zinali zidzukulu za Dani.
Voici les descendants de Dan, selon leurs familles: de Chouham, la famille des Chouhamites. Ce sont là les familles de Dan, compté selon ses familles.
43 Onse a fuko la Asuhamu amene anawerengedwa analipo 64,400.
Total des familles issues de Chouham, d’après leur dénombrement: soixante-quatre mille quatre cents hommes.
44 Zidzukulu za Aseri monga mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Imina, fuko la Aimuna; kuchokera mwa Isivi, fuko la Ayisivi; kuchokera mwa Beriya, fuko la Aberiya;
Fils d’Asher, selon leurs familles: de Yimna, la famille des Yimna; de Yichvi, la famille des Yichvites; de Berïa, la famille des Beriites.
45 ndipo kupyolera mwa zidzukulu za Beriya: kuchokera mwa Heberi, fuko la Aheberi; kuchokera mwa Malikieli, fuko la Amalikieli;
Pour les fils de Berïa: de Héber, la famille des Hébrites; de Malkiêl, la famille des Malkiélites.
46 (Aseri anali ndi mwana wamkazi dzina lake Sera)
Puis la fille d’Asher, nommée Sérah.
47 Awa ndiwo anali mafuko a Aseri. Onse amene anawerengedwa analipo 53,400.
Telles sont les familles des fils d’Asher, selon leur dénombrement: cinquante-trois mille quatre cents hommes.
48 Zidzukulu za Nafutali mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Yahazeeli, fuko la Ayahazeeli; kuchokera mwa Guni, fuko la Aguni;
Fils de Nephtali, selon leurs familles: de Yahceêl, la famille des Yahceélites; de Gouni, la famille des Gounites;
49 kuchokera mwa Yezeri, fuko la Ayezeri; kuchokera mwa Silemu, fuko la Asilemu.
de Yêcer, la famille des Yiçrites; de Chillem, la famille des Chillémites.
50 Awa ndiwo anali mafuko a Nafutali. Onse amene anawerengedwa analipo 45,400.
Telles sont les familles de Nephtali, compté selon ses familles; leur dénombrement donna quarante-cinq mille quatre cents hommes.
51 Chiwerengero chonse cha amuna mu Israeli chinalipo 601,730.
Résultat du dénombrement des enfants d’Israël: six cent un mille sept cent trente hommes.
52 Yehova anawuza Mose kuti,
L’Éternel parla à Moïse en ces termes:
53 “Uwagawire dziko anthu awa kuti likhale cholowa chawo molingana ndi chiwerengero cha mayina awo.
"C’Est entre ceux-là que le pays sera partagé comme héritage, selon le relevé des noms.
54 Gulu lalikulu ulipatse cholowa chachikulu, ndipo lochepa cholowa chocheperapo. Gulu lililonse lilandire cholowa chake molingana ndi chiwerengero cha amene anawerengedwa.
Aux plus nombreux tu donneras une plus grande part, aux moins nombreux une part inférieure: chaque tribu recevra sa part selon le chiffre de sa population.
55 Dzikolo uligawe pochita maere. Alandire cholowa chawocho potsata mayina a mafuko a makolo awo.
Toutefois, c’est au sort qu’on distribuera le pays; chacun aura son lot selon la désignation de sa tribu paternelle.
56 Cholowa chawo uchigawe pakati pa fuko lalikulu ndi lalingʼono mwa maere.”
Ce lot sera attribué par la voie du sort, que la famille soit considérable ou non."
57 Alevi omwe anawerengedwa monga mwa mafuko awo ndi awa: kuchokera mwa Geresoni, fuko la Ageresoni; kuchokera mwa Kohati, fuko la Akohati; kuchokera mwa Merari, fuko la Amerari.
Voici maintenant le relevé des Lévites, selon leurs familles: pour Gerson, la famille des Gersonites; pour Kehath, la famille des Kehathites; pour Merari, la famille des Merarites.
58 Awanso anali mabanja a Alevi: banja la Alibini, banja la Ahebroni, banja la Amali, banja la Amusi, fuko la Kora banja la Akohati, (Kohati anali abambo a Amramu.
Voici les familles Issues de Lévi: la famille des Libnites, la famille des Hébronites, celle des Mahlites, celle des Mouchites, celle des Coréites. Kehath engendra Amram.
59 Dzina la mkazi wa Amramu linali Yokobedi, mdzukulu wa Levi, yemwe anabadwa mwa Alevi mu Igupto. Yokobedi anaberekera Amramu Aaroni, Mose ndi Miriamu mlongo wawo.
Et le nom de l’épouse d’Amram était Jocabed, fille de Lévi, laquelle naquit à Lévi en Egypte. Elle enfanta à Amram Aaron, Moïse et Miryam, leur sœur.
60 Aaroni anali abambo a Nadabu, Abihu, Eliezara ndi Itamara.
Aaron eut pour fils Nadab et Abihou, Eléazar et Ithamar;
61 Koma Nadabu ndi Abihu anafa pamene anapereka nsembe pamaso pa Yehova ndi moto wachilendo).
mais Nadab et Abihou moururent, pour avoir apporté un feu profane devant le Seigneur.
62 Alevi onse aamuna a mwezi umodzi kapena kuposera pamenepa analipo 23,000. Iwowo sanawerengedwe pamodzi ndi Aisraeli ena chifukwa sanalandire cholowa pakati pawo.
Or, leur population dénombrée se monta à vingt-trois mille mâles âgés d’un mois et au-dessus; car ils n’avaient point figuré dans le recensement des enfants d’Israël, n’ayant point reçu de patrimoine comme ceux-ci.
63 Awa ndi amene anawerengedwa ndi Mose ndi Eliezara wansembe pamene ankawerenga Aisraeli pa zigwa za ku Mowabu mʼmbali mwa Yorodani ku Yeriko.
Tel fut le résultat du recensement opéré par Moïse, et le pontife Eléazar à l’égard des enfants d’Israël, dans les plaines de Moab, près du Jourdain, vers Jéricho.
64 Mwa anthu amenewa panalibe ndi mmodzi yemwe amene anali mʼgulu la Aisraeli omwe Mose ndi wansembe Aaroni anawawerenga mʼchipululu cha Sinai;
Parmi eux ne se trouvait pas un seul homme de ceux qu’avait recensés Moïse et le pontife Aaron, lorsqu’ils avaient dénombré les Israélites dans le désert de Sinaï.
65 Chifukwa Yehova anali atawuza Aisraeliwo kuti adzafera ndithu mʼchipululu, ndipo palibe ndi mmodzi yemwe amene anatsala kupatula Kalebe mwana wa Yefune ndi Yoswa mwana wa Nuni.
Car l’Éternel avait déclaré, quant à ceux-là, qu’ils devaient mourir dans le désert; et aucun d’eux n’avait survécu, excepté Caleb, fils de Yefounné, et Josué, fils de Noun.

< Numeri 26 >