< Numeri 26 >

1 Utatha mliri Yehova anati kwa Mose ndi Eliezara mwana wa Aaroni,
After the plague, Yahweh spoke to Moses and to Eleazar the son of Aaron the priest, saying,
2 “Werengani Aisraeli onse mwa mabanja awo, onse a zaka makumi awiri kapena kuposera pamenepo omwe angathe kugwira ntchito ya usilikali mʼgulu lankhondo la Israeli.”
“Take a census of all the congregation of the children of Israel, from twenty years old and upward, by their fathers’ houses, all who are able to go out to war in Israel.”
3 Kotero mu zigwa za Mowabu pafupi ndi mtsinje wa Yorodani ku Yeriko, Mose ndi wansembe Eliezara anayankhula nawo kuti,
Moses and Eleazar the priest spoke with them in the plains of Moab by the Jordan at Jericho, saying,
4 “Werengani amuna a zaka makumi awiri kapena kuposera pamenepo, monga momwe Yehova walamulira Mose.” Aisraeli omwe anachokera ku Igupto ndi awa:
“Take a census, from twenty years old and upward, as Yahweh commanded Moses and the children of Israel.” These are those who came out of the land of Egypt.
5 Zidzukulu za Rubeni, mwana woyamba wamwamuna wa Israeli, zinali izi: kuchokera mwa Hanoki, fuko la Ahanoki; kuchokera mwa Palu, fuko la Apalu;
Reuben, the firstborn of Israel; the sons of Reuben: of Hanoch, the family of the Hanochites; of Pallu, the family of the Palluites;
6 kuchokera mwa Hezironi, fuko la Ahezironi; kuchokera mwa Karimi, fuko la Akarimi.
of Hezron, the family of the Hezronites; of Carmi, the family of the Carmites.
7 Awa anali mafuko a Rubeni: onse amene anawerengedwa analipo 43,730.
These are the families of the Reubenites; and those who were counted of them were forty-three thousand seven hundred thirty.
8 Mwana wa Palu anali Eliabu,
The son of Pallu: Eliab.
9 ndipo ana a Eliabu anali Nemueli, Datani ndi Abiramu. Datani ndi Abiramu anali gulu la akuluakulu aja amene anawukira Mose ndi Aaroni ndipo analinso mʼgulu la otsatira Kora pamene anawukira Yehova.
The sons of Eliab: Nemuel, Dathan, and Abiram. These are that Dathan and Abiram who were called by the congregation, who rebelled against Moses and against Aaron in the company of Korah when they rebelled against Yahweh;
10 Nthaka inangʼambika ndi kuwameza pamodzi ndi Kora, kotero kuti gulu lawo linafa pamene moto unapsereza anthu 250 aja, nasanduka chenjezo.
and the earth opened its mouth, and swallowed them up together with Korah when that company died; at the time the fire devoured two hundred fifty men, and they became a sign.
11 Koma ana a Kora sanafe nawo.
Notwithstanding, the sons of Korah didn’t die.
12 Zidzukulu za Simeoni mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Nemueli, fuko la Anemuele; kuchokera mwa Yamini, fuko la Ayamini; kuchokera mwa Yakini fuko la Ayakini;
The sons of Simeon after their families: of Nemuel, the family of the Nemuelites; of Jamin, the family of the Jaminites; of Jachin, the family of the Jachinites;
13 kuchokera mwa Zera, mbumba ya Zera; kuchokera mwa Sauli, fuko la Asauli.
of Zerah, the family of the Zerahites; of Shaul, the family of the Shaulites.
14 Awa anali mafuko a Simeoni. Iwowa analipo amuna 22,200.
These are the families of the Simeonites, twenty-two thousand two hundred.
15 Zidzukulu za Gadi mwa mafuko awo ndi izi: kuchokera mwa Zefoni, fuko la Azefoni; kuchokera mwa Hagi, fuko la Ahagi; kuchokera mwa Suni, fuko la Asuni;
The sons of Gad after their families: of Zephon, the family of the Zephonites; of Haggi, the family of the Haggites; of Shuni, the family of the Shunites;
16 kuchokera mwa Ozini, fuko la Aozini; kuchokera mwa Eri, fuko la Aeri;
of Ozni, the family of the Oznites; of Eri, the family of the Erites;
17 kuchokera mwa Arodi, fuko la Aarodi; kuchokera mwa Arieli, fuko la a Areli.
of Arod, the family of the Arodites; of Areli, the family of the Arelites.
18 Awa ndiwo anali mafuko a Gadi. Onse amene anawerengedwa analipo 40,500.
These are the families of the sons of Gad according to those who were counted of them, forty thousand and five hundred.
19 Eri ndi Onani anali ana aamuna a Yuda, koma anafera mu Kanaani.
The sons of Judah: Er and Onan. Er and Onan died in the land of Canaan.
20 Zidzukulu za Yuda monga mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Sela, fuko la Asera; kuchokera mwa Perezi, fuko la Aperezi; kuchokera mwa Zera, mbumba ya Zera.
The sons of Judah after their families were: of Shelah, the family of the Shelanites; of Perez, the family of the Perezites; of Zerah, the family of the Zerahites.
21 Zidzukulu za Perezi zinali izi: kuchokera mwa Hezironi, fuko la Ahezironi; kuchokera mwa Hamuli, fuko la Ahamuli.
The sons of Perez were: of Hezron, the family of the Hezronites; of Hamul, the family of the Hamulites.
22 Awa ndiwo anali mafuko a Yuda. Amene anawerenga analipo 76,500.
These are the families of Judah according to those who were counted of them, seventy-six thousand five hundred.
23 Zidzukulu za Isakara monga mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Tola, fuko la Atola; kuchokera mwa Puwa, fuko la Apuwa;
The sons of Issachar after their families: of Tola, the family of the Tolaites; of Puvah, the family of the Punites;
24 kuchokera mwa Yasubu, fuko la Ayasubu. Kuchokera mwa Simironi, fuko la Asimironi.
of Jashub, the family of the Jashubites; of Shimron, the family of the Shimronites.
25 Awa ndi amene anali a fuko la Isakara. Amene anawerengedwa analipo 64,300.
These are the families of Issachar according to those who were counted of them, sixty-four thousand three hundred.
26 Zidzukulu za Zebuloni mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Seredi, fuko la Aseredi; kuchokera mwa Eloni, fuko la Aeloni; kuchokera mwa Yahaleeli, fuko la Ayahaleeli.
The sons of Zebulun after their families: of Sered, the family of the Seredites; of Elon, the family of the Elonites; of Jahleel, the family of the Jahleelites.
27 Awa ndiwo anali mafuko a Zebuloni. Amene anawerengedwa analipo 60,500.
These are the families of the Zebulunites according to those who were counted of them, sixty thousand five hundred.
28 Zidzukulu za Yosefe mwa mafuko awo kupyolera mwa Manase ndi Efereimu zinali izi:
The sons of Joseph after their families: Manasseh and Ephraim.
29 Zidzukulu za Manase: kuchokera mwa Makiri, fuko la Amakiri (Makiri anali abambo ake a Giliyadi); kuchokera mwa Giliyadi, fuko la Agiliyadi.
The sons of Manasseh: of Machir, the family of the Machirites; and Machir became the father of Gilead; of Gilead, the family of the Gileadites.
30 Izi ndizo zinali zidzukulu za Giliyadi; kuchokera mwa Iyezeri, fuko la Aiyezeri; kuchokera mwa Heleki, fuko la Aheleki;
These are the sons of Gilead: of Iezer, the family of the Iezerites; of Helek, the family of the Helekites;
31 kuchokera mwa Asirieli, fuko la Aasirieli; kuchokera mwa Sekemu, fuko la Asekemu;
and Asriel, the family of the Asrielites; and Shechem, the family of the Shechemites;
32 kuchokera mwa Semida, fuko la Asemida; kuchokera mwa Heferi, fuko la Aheferi.
and Shemida, the family of the Shemidaites; and Hepher, the family of the Hepherites.
33 (Zelofehadi mwana wa Heferi analibe ana aamuna koma ana aakazi okha, amene mayina awo anali: Mala, Nowa, Hogila, Milika ndi Tiriza.)
Zelophehad the son of Hepher had no sons, but daughters: and the names of the daughters of Zelophehad were Mahlah, Noah, Hoglah, Milcah, and Tirzah.
34 Awa ndiwo anali mafuko a Manase. Amene anawerengedwa analipo 52,700.
These are the families of Manasseh. Those who were counted of them were fifty-two thousand seven hundred.
35 Zidzukulu za Efereimu monga mwa mafuko awo zinali izi; kuchokera mwa Sutela, fuko la Asutela; kuchokera mwa Bekeri, fuko la Abekeri; kuchokera mwa Tahani, fuko la Atahani.
These are the sons of Ephraim after their families: of Shuthelah, the family of the Shuthelahites; of Becher, the family of the Becherites; of Tahan, the family of the Tahanites.
36 Zidzukulu za Sutela zinali izi: kuchokera mwa Erani, fuko la Aerani.
These are the sons of Shuthelah: of Eran, the family of the Eranites.
37 Awa ndiwo anali mafuko a Efereimu. Amene anawerengedwa analipo 32,500. Zimenezi zinali zidzukulu za Yosefe monga mwa mafuko awo.
These are the families of the sons of Ephraim according to those who were counted of them, thirty-two thousand five hundred. These are the sons of Joseph after their families.
38 Zidzukulu za Benjamini monga mwa mabanja awo zinali izi: kuchokera mwa Bela, fuko la Abela; kuchokera mwa Asibeli, fuko la Aasibeli; kuchokera mwa Ahiramu, fuko la Ahiramu;
The sons of Benjamin after their families: of Bela, the family of the Belaites; of Ashbel, the family of the Ashbelites; of Ahiram, the family of the Ahiramites;
39 kuchokera mwa Sufamu, fuko la Asufamu; kuchokera mwa Hufamu, fuko la Ahufamu;
of Shephupham, the family of the Shuphamites; of Hupham, the family of the Huphamites.
40 Zidzukulu za Bela kupyolera mwa Aridi ndi Naamani zinali izi: kuchokera mwa Aridi, fuko la Aaridi; kuchokera mwa Naamani, fuko la Anaamani;
The sons of Bela were Ard and Naaman: the family of the Ardites; and of Naaman, the family of the Naamites.
41 Awa ndiwo anali mabanja a Benjamini. Amene nawerengedwa analipo 45,600.
These are the sons of Benjamin after their families; and those who were counted of them were forty-five thousand six hundred.
42 Zidzukulu za Dani mwa mabanja awo zinali izi: kuchokera mwa Suhamu fuko la Asuhamu. Izi zinali zidzukulu za Dani.
These are the sons of Dan after their families: of Shuham, the family of the Shuhamites. These are the families of Dan after their families.
43 Onse a fuko la Asuhamu amene anawerengedwa analipo 64,400.
All the families of the Shuhamites, according to those who were counted of them, were sixty-four thousand four hundred.
44 Zidzukulu za Aseri monga mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Imina, fuko la Aimuna; kuchokera mwa Isivi, fuko la Ayisivi; kuchokera mwa Beriya, fuko la Aberiya;
The sons of Asher after their families: of Imnah, the family of the Imnites; of Ishvi, the family of the Ishvites; of Beriah, the family of the Berites.
45 ndipo kupyolera mwa zidzukulu za Beriya: kuchokera mwa Heberi, fuko la Aheberi; kuchokera mwa Malikieli, fuko la Amalikieli;
Of the sons of Beriah: of Heber, the family of the Heberites; of Malchiel, the family of the Malchielites.
46 (Aseri anali ndi mwana wamkazi dzina lake Sera)
The name of the daughter of Asher was Serah.
47 Awa ndiwo anali mafuko a Aseri. Onse amene anawerengedwa analipo 53,400.
These are the families of the sons of Asher according to those who were counted of them, fifty-three thousand four hundred.
48 Zidzukulu za Nafutali mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Yahazeeli, fuko la Ayahazeeli; kuchokera mwa Guni, fuko la Aguni;
The sons of Naphtali after their families: of Jahzeel, the family of the Jahzeelites; of Guni, the family of the Gunites;
49 kuchokera mwa Yezeri, fuko la Ayezeri; kuchokera mwa Silemu, fuko la Asilemu.
of Jezer, the family of the Jezerites; of Shillem, the family of the Shillemites.
50 Awa ndiwo anali mafuko a Nafutali. Onse amene anawerengedwa analipo 45,400.
These are the families of Naphtali according to their families; and those who were counted of them were forty-five thousand four hundred.
51 Chiwerengero chonse cha amuna mu Israeli chinalipo 601,730.
These are those who were counted of the children of Israel, six hundred one thousand seven hundred thirty.
52 Yehova anawuza Mose kuti,
Yahweh spoke to Moses, saying,
53 “Uwagawire dziko anthu awa kuti likhale cholowa chawo molingana ndi chiwerengero cha mayina awo.
“To these the land shall be divided for an inheritance according to the number of names.
54 Gulu lalikulu ulipatse cholowa chachikulu, ndipo lochepa cholowa chocheperapo. Gulu lililonse lilandire cholowa chake molingana ndi chiwerengero cha amene anawerengedwa.
To the more you shall give the more inheritance, and to the fewer you shall give the less inheritance. To everyone according to those who were counted of him shall his inheritance be given.
55 Dzikolo uligawe pochita maere. Alandire cholowa chawocho potsata mayina a mafuko a makolo awo.
Notwithstanding, the land shall be divided by lot. According to the names of the tribes of their fathers they shall inherit.
56 Cholowa chawo uchigawe pakati pa fuko lalikulu ndi lalingʼono mwa maere.”
According to the lot shall their inheritance be divided between the more and the fewer.”
57 Alevi omwe anawerengedwa monga mwa mafuko awo ndi awa: kuchokera mwa Geresoni, fuko la Ageresoni; kuchokera mwa Kohati, fuko la Akohati; kuchokera mwa Merari, fuko la Amerari.
These are those who were counted of the Levites after their families: of Gershon, the family of the Gershonites; of Kohath, the family of the Kohathites; of Merari, the family of the Merarites.
58 Awanso anali mabanja a Alevi: banja la Alibini, banja la Ahebroni, banja la Amali, banja la Amusi, fuko la Kora banja la Akohati, (Kohati anali abambo a Amramu.
These are the families of Levi: the family of the Libnites, the family of the Hebronites, the family of the Mahlites, the family of the Mushites, and the family of the Korahites. Kohath became the father of Amram.
59 Dzina la mkazi wa Amramu linali Yokobedi, mdzukulu wa Levi, yemwe anabadwa mwa Alevi mu Igupto. Yokobedi anaberekera Amramu Aaroni, Mose ndi Miriamu mlongo wawo.
The name of Amram’s wife was Jochebed, the daughter of Levi, who was born to Levi in Egypt. She bore to Amram Aaron and Moses, and Miriam their sister.
60 Aaroni anali abambo a Nadabu, Abihu, Eliezara ndi Itamara.
To Aaron were born Nadab and Abihu, Eleazar and Ithamar.
61 Koma Nadabu ndi Abihu anafa pamene anapereka nsembe pamaso pa Yehova ndi moto wachilendo).
Nadab and Abihu died when they offered strange fire before Yahweh.
62 Alevi onse aamuna a mwezi umodzi kapena kuposera pamenepa analipo 23,000. Iwowo sanawerengedwe pamodzi ndi Aisraeli ena chifukwa sanalandire cholowa pakati pawo.
Those who were counted of them were twenty-three thousand, every male from a month old and upward; for they were not counted among the children of Israel, because there was no inheritance given them among the children of Israel.
63 Awa ndi amene anawerengedwa ndi Mose ndi Eliezara wansembe pamene ankawerenga Aisraeli pa zigwa za ku Mowabu mʼmbali mwa Yorodani ku Yeriko.
These are those who were counted by Moses and Eleazar the priest, who counted the children of Israel in the plains of Moab by the Jordan at Jericho.
64 Mwa anthu amenewa panalibe ndi mmodzi yemwe amene anali mʼgulu la Aisraeli omwe Mose ndi wansembe Aaroni anawawerenga mʼchipululu cha Sinai;
But among these there was not a man of them who were counted by Moses and Aaron the priest, who counted the children of Israel in the wilderness of Sinai.
65 Chifukwa Yehova anali atawuza Aisraeliwo kuti adzafera ndithu mʼchipululu, ndipo palibe ndi mmodzi yemwe amene anatsala kupatula Kalebe mwana wa Yefune ndi Yoswa mwana wa Nuni.
For Yahweh had said of them, “They shall surely die in the wilderness.” There was not a man left of them, except Caleb the son of Jephunneh, and Joshua the son of Nun.

< Numeri 26 >