< Numeri 26 >

1 Utatha mliri Yehova anati kwa Mose ndi Eliezara mwana wa Aaroni,
And it came to pass after the plague, That the Lord spoke unto Moses and unto Elazar the son of Aaron the priest, saying,
2 “Werengani Aisraeli onse mwa mabanja awo, onse a zaka makumi awiri kapena kuposera pamenepo omwe angathe kugwira ntchito ya usilikali mʼgulu lankhondo la Israeli.”
Take ye the sum of all the congregation of the children of Israel, from twenty years old and upward, by the descent from their fathers, all that are able to go forth to war in Israel.
3 Kotero mu zigwa za Mowabu pafupi ndi mtsinje wa Yorodani ku Yeriko, Mose ndi wansembe Eliezara anayankhula nawo kuti,
And Moses with El'azar the priest spoke with them in the plains of Moab by the Jordan opposite Jericho, saying,
4 “Werengani amuna a zaka makumi awiri kapena kuposera pamenepo, monga momwe Yehova walamulira Mose.” Aisraeli omwe anachokera ku Igupto ndi awa:
[Take the sum of the people, ] from twenty years old and upward; as the Lord commanded Moses and the children of Israel, who went forth out of the land of Egypt.
5 Zidzukulu za Rubeni, mwana woyamba wamwamuna wa Israeli, zinali izi: kuchokera mwa Hanoki, fuko la Ahanoki; kuchokera mwa Palu, fuko la Apalu;
Reuben, the eldest son of Israel: the children of Reuben, of Chanoch, the family of the Chanochites; of Pallu, the family of the Palluites;
6 kuchokera mwa Hezironi, fuko la Ahezironi; kuchokera mwa Karimi, fuko la Akarimi.
Of Chezron, the family of the Chezronites; of Carmi, the family of the Carmites.
7 Awa anali mafuko a Rubeni: onse amene anawerengedwa analipo 43,730.
These are the families of the Reubenites; and those that were numbered of them were forty and three thousand and seven hundred and thirty.
8 Mwana wa Palu anali Eliabu,
And the sons of Pallu: Eliab.
9 ndipo ana a Eliabu anali Nemueli, Datani ndi Abiramu. Datani ndi Abiramu anali gulu la akuluakulu aja amene anawukira Mose ndi Aaroni ndipo analinso mʼgulu la otsatira Kora pamene anawukira Yehova.
And the sons of Eliab: Nemuel, and Dathan, and Abiram. These are Dathan and Abiram, men called to the assembly, who quarreled against Moses and against Aaron in the company of Korach, at the time they quarreled against the Lord;
10 Nthaka inangʼambika ndi kuwameza pamodzi ndi Kora, kotero kuti gulu lawo linafa pamene moto unapsereza anthu 250 aja, nasanduka chenjezo.
When the earth opened her mouth, and swallowed them up together with Korach, while that company died, when the fire devoured the two hundred and fifty men; and they became a sign.
11 Koma ana a Kora sanafe nawo.
But the sons of Korach did not die.
12 Zidzukulu za Simeoni mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Nemueli, fuko la Anemuele; kuchokera mwa Yamini, fuko la Ayamini; kuchokera mwa Yakini fuko la Ayakini;
The sons of Simeon after their families: of Nemuel, the family of the Nemuelites; of Yamin, the family of the Yaminites; of Yachin, the family of the Yachinites;
13 kuchokera mwa Zera, mbumba ya Zera; kuchokera mwa Sauli, fuko la Asauli.
Of Zerach, the family of the Zarchites; of Shaul, the family of the Shaulites.
14 Awa anali mafuko a Simeoni. Iwowa analipo amuna 22,200.
These are the families of the Simeonites, twenty and two thousand and two hundred.
15 Zidzukulu za Gadi mwa mafuko awo ndi izi: kuchokera mwa Zefoni, fuko la Azefoni; kuchokera mwa Hagi, fuko la Ahagi; kuchokera mwa Suni, fuko la Asuni;
The children of Gad after their families: of Zephon, the family of the Zephonites; of Chaggi, the family of the Chaggites; of Shuni, the family of the Shunites;
16 kuchokera mwa Ozini, fuko la Aozini; kuchokera mwa Eri, fuko la Aeri;
Of Ozni, the family of the Oznites; of 'Eri, the family of the 'Erites;
17 kuchokera mwa Arodi, fuko la Aarodi; kuchokera mwa Arieli, fuko la a Areli.
Of Arod, the family of the Arodites; of Areli, the family of the Arelites;
18 Awa ndiwo anali mafuko a Gadi. Onse amene anawerengedwa analipo 40,500.
These are the families of the children of Gad according to those that were numbered of them, forty thousand and five hundred.
19 Eri ndi Onani anali ana aamuna a Yuda, koma anafera mu Kanaani.
The sons of Judah were 'Er and Onan; and 'Er with Onan died in the land of Canaan.
20 Zidzukulu za Yuda monga mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Sela, fuko la Asera; kuchokera mwa Perezi, fuko la Aperezi; kuchokera mwa Zera, mbumba ya Zera.
And the sons of Judah after their families were: of Shelah, the family of the Shelanites; of Perez, the family of the Parzites; of Zerach, the family of the Zarchites.
21 Zidzukulu za Perezi zinali izi: kuchokera mwa Hezironi, fuko la Ahezironi; kuchokera mwa Hamuli, fuko la Ahamuli.
And the sons of Perez were: of Chezron, the family of the Chezronites; of Chamul, the family of the Chamulites.
22 Awa ndiwo anali mafuko a Yuda. Amene anawerenga analipo 76,500.
These are the families of Judah, according to those that were numbered of them, seventy and six thousand and five hundred.
23 Zidzukulu za Isakara monga mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Tola, fuko la Atola; kuchokera mwa Puwa, fuko la Apuwa;
The sons of Issachar after their families: of Tola', the family of the Tola'ites; of Puva, the family of the Punites;
24 kuchokera mwa Yasubu, fuko la Ayasubu. Kuchokera mwa Simironi, fuko la Asimironi.
Of Yashub, the family of the Yashubites; of Shimron, the family of the Shimronites.
25 Awa ndi amene anali a fuko la Isakara. Amene anawerengedwa analipo 64,300.
These are the families of Issachar according to those that were numbered of them, sixty and four thousand and three hundred.
26 Zidzukulu za Zebuloni mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Seredi, fuko la Aseredi; kuchokera mwa Eloni, fuko la Aeloni; kuchokera mwa Yahaleeli, fuko la Ayahaleeli.
The sons of Zebulun after their families: of Sered, the family of the Sardites; of Elon, the family of the Elonites; of Yachleel, the family of the Yachleelites.
27 Awa ndiwo anali mafuko a Zebuloni. Amene anawerengedwa analipo 60,500.
These are the families of the Zebulonites according to those that were numbered of them, sixty thousand and five hundred.
28 Zidzukulu za Yosefe mwa mafuko awo kupyolera mwa Manase ndi Efereimu zinali izi:
The sons of Joseph after their families are Menasseh and Ephraim.
29 Zidzukulu za Manase: kuchokera mwa Makiri, fuko la Amakiri (Makiri anali abambo ake a Giliyadi); kuchokera mwa Giliyadi, fuko la Agiliyadi.
The sons of Menasseh: of Machir, the family of the Machirites; and Machir begat Gil'ad; of Gil'ad, the family of the Gil'adites.
30 Izi ndizo zinali zidzukulu za Giliyadi; kuchokera mwa Iyezeri, fuko la Aiyezeri; kuchokera mwa Heleki, fuko la Aheleki;
These are the sons of Gil'ad: of I'ezer, the family of the I'ezerites; of Chelek, the family of the Chelkites;
31 kuchokera mwa Asirieli, fuko la Aasirieli; kuchokera mwa Sekemu, fuko la Asekemu;
And of Assriel, the family of the Assrielites; and of Shechem, the family of the Shichmites;
32 kuchokera mwa Semida, fuko la Asemida; kuchokera mwa Heferi, fuko la Aheferi.
And of Shemida', the family of the Shemida'ites; and of Chepher, the family of the Chephrites.
33 (Zelofehadi mwana wa Heferi analibe ana aamuna koma ana aakazi okha, amene mayina awo anali: Mala, Nowa, Hogila, Milika ndi Tiriza.)
And Zelophehad the son of Chepher had no sons, but only daughters; and the names of the daughters of Zelophehad were Machlah, and No'ah, Choglah, Milcah, and Tirzah.
34 Awa ndiwo anali mafuko a Manase. Amene anawerengedwa analipo 52,700.
These are the families of Menasseh; and those that were numbered of them were fifty and two thousand and seven hundred.
35 Zidzukulu za Efereimu monga mwa mafuko awo zinali izi; kuchokera mwa Sutela, fuko la Asutela; kuchokera mwa Bekeri, fuko la Abekeri; kuchokera mwa Tahani, fuko la Atahani.
These are the sons of Ephraim after their families: of Shuthelach, the family of the Shuthalchites; of Becher, the family of the Bachrites; of Tachan, the family of the Tachanites.
36 Zidzukulu za Sutela zinali izi: kuchokera mwa Erani, fuko la Aerani.
And these are the sons of Shuthelach: of 'Eran, the family of the Eranites.
37 Awa ndiwo anali mafuko a Efereimu. Amene anawerengedwa analipo 32,500. Zimenezi zinali zidzukulu za Yosefe monga mwa mafuko awo.
These are the families of the sons of Ephraim according to those that were numbered of them, thirty and two thousand and five hundred: these are the sons of Joseph after their families.
38 Zidzukulu za Benjamini monga mwa mabanja awo zinali izi: kuchokera mwa Bela, fuko la Abela; kuchokera mwa Asibeli, fuko la Aasibeli; kuchokera mwa Ahiramu, fuko la Ahiramu;
The sons of Benjamin after their families: of Bela', the family of the Bal'ites; of Ashbel, the family of the Ashbelites; of Achiram, the family of the Achiramites;
39 kuchokera mwa Sufamu, fuko la Asufamu; kuchokera mwa Hufamu, fuko la Ahufamu;
Of Shephupham, the family of the Shuphamites; of Chupham, the family of the Chuphamites.
40 Zidzukulu za Bela kupyolera mwa Aridi ndi Naamani zinali izi: kuchokera mwa Aridi, fuko la Aaridi; kuchokera mwa Naamani, fuko la Anaamani;
And the sons of Bela' were Ard and Na'aman: of Ard, the family of the Ardites; and of Na'aman, the family of the Na'amites.
41 Awa ndiwo anali mabanja a Benjamini. Amene nawerengedwa analipo 45,600.
These are the sons of Benjamin after their families; and those that were numbered of them were forty and five thousand and six hundred.
42 Zidzukulu za Dani mwa mabanja awo zinali izi: kuchokera mwa Suhamu fuko la Asuhamu. Izi zinali zidzukulu za Dani.
These are the sons of Dan after their families: of Shucham, the family of the Shuchamites; these are the families of Dan after their families.
43 Onse a fuko la Asuhamu amene anawerengedwa analipo 64,400.
All the families of the Shuchamites, according to those that were numbered of them, were sixty and four thousand and four hundred.
44 Zidzukulu za Aseri monga mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Imina, fuko la Aimuna; kuchokera mwa Isivi, fuko la Ayisivi; kuchokera mwa Beriya, fuko la Aberiya;
The children of Asher after their families: of Yimnah, the family of the Yimnites; of Yishvi, the family of the Yishvites; of Beri'ah, the family of the Beri'ites.
45 ndipo kupyolera mwa zidzukulu za Beriya: kuchokera mwa Heberi, fuko la Aheberi; kuchokera mwa Malikieli, fuko la Amalikieli;
Of the sons of Beri'ah: of Cheber, the family of the Chebrites; of Malkiel, the family of the Makielites.
46 (Aseri anali ndi mwana wamkazi dzina lake Sera)
And the name of the daughter of Asher was Serach.
47 Awa ndiwo anali mafuko a Aseri. Onse amene anawerengedwa analipo 53,400.
These are the families of the sons of Asher according to those that were numbered of them, fifty and three thousand and four hundred.
48 Zidzukulu za Nafutali mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Yahazeeli, fuko la Ayahazeeli; kuchokera mwa Guni, fuko la Aguni;
The sons of Naphtali after their families: of Yachzeel, the family of the Yachzeelites; of Guni, the family of the Gunites;
49 kuchokera mwa Yezeri, fuko la Ayezeri; kuchokera mwa Silemu, fuko la Asilemu.
Of Yezer, the family of the Yizrites; of Shillem, the family of the Shillemites.
50 Awa ndiwo anali mafuko a Nafutali. Onse amene anawerengedwa analipo 45,400.
These are the families of Naphtali according to their families; and those that were numbered of them were forty and five thousand and four hundred.
51 Chiwerengero chonse cha amuna mu Israeli chinalipo 601,730.
These were the numbered of the children of Israel, six hundred thousand, and one thousand, seven hundred and thirty.
52 Yehova anawuza Mose kuti,
And the Lord spoke unto Moses, saying,
53 “Uwagawire dziko anthu awa kuti likhale cholowa chawo molingana ndi chiwerengero cha mayina awo.
Unto these shall the land be divided for an inheritance according to the number of the names.
54 Gulu lalikulu ulipatse cholowa chachikulu, ndipo lochepa cholowa chocheperapo. Gulu lililonse lilandire cholowa chake molingana ndi chiwerengero cha amene anawerengedwa.
To the large tribe shalt thou give the more inheritance, and to the small shalt thou give the less inheritance: to each according to those that were numbered thereof shall its inheritance be given.
55 Dzikolo uligawe pochita maere. Alandire cholowa chawocho potsata mayina a mafuko a makolo awo.
Nevertheless, through the lot shall the land be divided: according to the names of the tribes of their fathers shall they obtain their inheritance.
56 Cholowa chawo uchigawe pakati pa fuko lalikulu ndi lalingʼono mwa maere.”
By the decision of the lot shall the inheritance of each be divided, according as they are many or few.
57 Alevi omwe anawerengedwa monga mwa mafuko awo ndi awa: kuchokera mwa Geresoni, fuko la Ageresoni; kuchokera mwa Kohati, fuko la Akohati; kuchokera mwa Merari, fuko la Amerari.
And these are those that were numbered of the Levites after their families: of Gershon, the family of the Gershunites: of Kehath, the family of the Kehathites; of Merari, the family of the Merarites.
58 Awanso anali mabanja a Alevi: banja la Alibini, banja la Ahebroni, banja la Amali, banja la Amusi, fuko la Kora banja la Akohati, (Kohati anali abambo a Amramu.
These are the families of Levi: the family of the Libnites, the family of the Chebronites, the family of the Machlites, the family of the Mushites, the family of the Korchites; and Kehath begat 'Amran.
59 Dzina la mkazi wa Amramu linali Yokobedi, mdzukulu wa Levi, yemwe anabadwa mwa Alevi mu Igupto. Yokobedi anaberekera Amramu Aaroni, Mose ndi Miriamu mlongo wawo.
And the name of 'Amram's wife was Yochebed, the daughter of Levi, whom [her mother] bore to Levi in Egypt; and she bore unto Amram, Aaron and Moses, and Miriam their sister.
60 Aaroni anali abambo a Nadabu, Abihu, Eliezara ndi Itamara.
And there were born unto Aaron, Nadab, and Abihu, Elazar, and Ithamar.
61 Koma Nadabu ndi Abihu anafa pamene anapereka nsembe pamaso pa Yehova ndi moto wachilendo).
And Nadab and Abihu died, when they offered a strange fire before the Lord.
62 Alevi onse aamuna a mwezi umodzi kapena kuposera pamenepa analipo 23,000. Iwowo sanawerengedwe pamodzi ndi Aisraeli ena chifukwa sanalandire cholowa pakati pawo.
And those that were numbered of them were twenty and three thousand, all the males from a month old and upward; for they were not numbered among the children of Israel, because there was not given unto them any inheritance among the children of Israel.
63 Awa ndi amene anawerengedwa ndi Mose ndi Eliezara wansembe pamene ankawerenga Aisraeli pa zigwa za ku Mowabu mʼmbali mwa Yorodani ku Yeriko.
These are those that were numbered by Moses and Elazar the priest, who numbered the children of Israel in the plains of Moab by the Jordan, opposite Jericho.
64 Mwa anthu amenewa panalibe ndi mmodzi yemwe amene anali mʼgulu la Aisraeli omwe Mose ndi wansembe Aaroni anawawerenga mʼchipululu cha Sinai;
And among these there was not one man of those whom Moses and Aaron the priest had numbered, who numbered the children of Israel in the wilderness of Sinai.
65 Chifukwa Yehova anali atawuza Aisraeliwo kuti adzafera ndithu mʼchipululu, ndipo palibe ndi mmodzi yemwe amene anatsala kupatula Kalebe mwana wa Yefune ndi Yoswa mwana wa Nuni.
For the Lord had said of them, They shall surely die in the wilderness: and there was not left of them one man, save Caleb the son of Yephunneh, and Joshua the son of Nun.

< Numeri 26 >