< Numeri 26 >

1 Utatha mliri Yehova anati kwa Mose ndi Eliezara mwana wa Aaroni,
Now after the disease was over, the Lord said to Moses and Eleazar, the son of Aaron the priest,
2 “Werengani Aisraeli onse mwa mabanja awo, onse a zaka makumi awiri kapena kuposera pamenepo omwe angathe kugwira ntchito ya usilikali mʼgulu lankhondo la Israeli.”
Let all the children of Israel be numbered, by the names of their fathers' families, all those of twenty years old and over who are able to go to war in Israel.
3 Kotero mu zigwa za Mowabu pafupi ndi mtsinje wa Yorodani ku Yeriko, Mose ndi wansembe Eliezara anayankhula nawo kuti,
So Moses and Eleazar the priest gave them the order in the lowlands of Moab by Jordan at Jericho, saying,
4 “Werengani amuna a zaka makumi awiri kapena kuposera pamenepo, monga momwe Yehova walamulira Mose.” Aisraeli omwe anachokera ku Igupto ndi awa:
Let all the people of twenty years old and over be numbered, as the Lord has given orders to Moses and the children of Israel who have come out of Egypt.
5 Zidzukulu za Rubeni, mwana woyamba wamwamuna wa Israeli, zinali izi: kuchokera mwa Hanoki, fuko la Ahanoki; kuchokera mwa Palu, fuko la Apalu;
Reuben, the first son of Israel: the sons of Reuben by their families: of Hanoch, the family of the Hanochites: of Pallu, the family of the Palluites:
6 kuchokera mwa Hezironi, fuko la Ahezironi; kuchokera mwa Karimi, fuko la Akarimi.
Of Hezron, the family of the Hezronites: of Carmi, the family of the Carmites.
7 Awa anali mafuko a Rubeni: onse amene anawerengedwa analipo 43,730.
These are the families of the Reubenites: their number was forty-three thousand, seven hundred and thirty.
8 Mwana wa Palu anali Eliabu,
And the sons of Pallu, Eliab
9 ndipo ana a Eliabu anali Nemueli, Datani ndi Abiramu. Datani ndi Abiramu anali gulu la akuluakulu aja amene anawukira Mose ndi Aaroni ndipo analinso mʼgulu la otsatira Kora pamene anawukira Yehova.
And the sons of Eliab: Nemuel and Dathan and Abiram. These are the same Dathan and Abiram who had a place in the meeting of the people, who together with Korah made an outcry against Moses and Aaron and against the Lord:
10 Nthaka inangʼambika ndi kuwameza pamodzi ndi Kora, kotero kuti gulu lawo linafa pamene moto unapsereza anthu 250 aja, nasanduka chenjezo.
And they went down into the open mouth of the earth, together with Korah, when death overtook him and all his band; at the time when two hundred and fifty men were burned in the fire, and they became a sign.
11 Koma ana a Kora sanafe nawo.
But death did not overtake the sons of Korah.
12 Zidzukulu za Simeoni mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Nemueli, fuko la Anemuele; kuchokera mwa Yamini, fuko la Ayamini; kuchokera mwa Yakini fuko la Ayakini;
The sons of Simeon by their families: of Nemuel, the family of the Nemuelites: of Jamin, the family of the Jaminites: of Jachin, the family of the Jachinites:
13 kuchokera mwa Zera, mbumba ya Zera; kuchokera mwa Sauli, fuko la Asauli.
Of Zerah, the family of the Zerahites: of Shaul, the family of the Shaulites.
14 Awa anali mafuko a Simeoni. Iwowa analipo amuna 22,200.
These are the families of the Simeonites, twenty-two thousand, two hundred.
15 Zidzukulu za Gadi mwa mafuko awo ndi izi: kuchokera mwa Zefoni, fuko la Azefoni; kuchokera mwa Hagi, fuko la Ahagi; kuchokera mwa Suni, fuko la Asuni;
The sons of Gad by their families: of Zephon, the family of the Zephonites: of Haggi, the family of the Haggites: of Shuni, the family of the Shunites:
16 kuchokera mwa Ozini, fuko la Aozini; kuchokera mwa Eri, fuko la Aeri;
Of Ozni, the family of the Oznites: of Eri, the family of the Erites:
17 kuchokera mwa Arodi, fuko la Aarodi; kuchokera mwa Arieli, fuko la a Areli.
Of Arod, the family of the Arodites: of Areli, the family of the Arelites.
18 Awa ndiwo anali mafuko a Gadi. Onse amene anawerengedwa analipo 40,500.
These are the families of the sons of Gad as they were numbered, forty thousand, five hundred.
19 Eri ndi Onani anali ana aamuna a Yuda, koma anafera mu Kanaani.
The sons of Judah, Er and Onan: and Er and Onan had come to their death in the land of Canaan.
20 Zidzukulu za Yuda monga mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Sela, fuko la Asera; kuchokera mwa Perezi, fuko la Aperezi; kuchokera mwa Zera, mbumba ya Zera.
And the sons of Judah by their families were: of Shelah, the family of the Shelahites: of Perez, the family of the Perezites: of Zerah, the family of the Zerahites.
21 Zidzukulu za Perezi zinali izi: kuchokera mwa Hezironi, fuko la Ahezironi; kuchokera mwa Hamuli, fuko la Ahamuli.
And the sons of Perez were: of Hezron, the family of the Hezronites: of Hamul, the family of the Hamulites.
22 Awa ndiwo anali mafuko a Yuda. Amene anawerenga analipo 76,500.
These are the families of Judah as they were numbered, seventy-six thousand, five hundred.
23 Zidzukulu za Isakara monga mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Tola, fuko la Atola; kuchokera mwa Puwa, fuko la Apuwa;
The sons of Issachar by their families: of Tola, the family of the Tolaites: of Puvah, the family of the Punites:
24 kuchokera mwa Yasubu, fuko la Ayasubu. Kuchokera mwa Simironi, fuko la Asimironi.
Of Jashub, the family of the Jashubites: of Shimron, the family of the Shimronites.
25 Awa ndi amene anali a fuko la Isakara. Amene anawerengedwa analipo 64,300.
These are the families of Issachar, as they were numbered, sixty-four thousand, three hundred.
26 Zidzukulu za Zebuloni mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Seredi, fuko la Aseredi; kuchokera mwa Eloni, fuko la Aeloni; kuchokera mwa Yahaleeli, fuko la Ayahaleeli.
The sons of Zebulun by their families: of Sered, the family of the Seredites: of Elon, the family of the Elonites: of Jahleel, the family of the Jahleelites.
27 Awa ndiwo anali mafuko a Zebuloni. Amene anawerengedwa analipo 60,500.
These are the families of the Zebulunites as they were numbered, sixty thousand, five hundred.
28 Zidzukulu za Yosefe mwa mafuko awo kupyolera mwa Manase ndi Efereimu zinali izi:
The sons of Joseph by their families: Manasseh and Ephraim.
29 Zidzukulu za Manase: kuchokera mwa Makiri, fuko la Amakiri (Makiri anali abambo ake a Giliyadi); kuchokera mwa Giliyadi, fuko la Agiliyadi.
The sons of Manasseh: of Machir, the family of the Machirites: and Machir was the father of Gilead: of Gilead, the family of the Gileadites.
30 Izi ndizo zinali zidzukulu za Giliyadi; kuchokera mwa Iyezeri, fuko la Aiyezeri; kuchokera mwa Heleki, fuko la Aheleki;
These are the sons of Gilead: of Iezer, the family of the Iezerites: of Helek, the family of the Helekites:
31 kuchokera mwa Asirieli, fuko la Aasirieli; kuchokera mwa Sekemu, fuko la Asekemu;
And of Asriel, the family of the Asrielites: and of Shechem, the family of the Shechemites:
32 kuchokera mwa Semida, fuko la Asemida; kuchokera mwa Heferi, fuko la Aheferi.
And of Shemida, the family of the Shemidaites: and of Hepher, the family of the Hepherites.
33 (Zelofehadi mwana wa Heferi analibe ana aamuna koma ana aakazi okha, amene mayina awo anali: Mala, Nowa, Hogila, Milika ndi Tiriza.)
And Zelophehad, the son of Hepher, had no sons, but only daughters, and the names of the daughters of Zelophehad were Mahlah, and Noah, Hoglah, Milcah, and Tirzah.
34 Awa ndiwo anali mafuko a Manase. Amene anawerengedwa analipo 52,700.
These are the families of Manasseh; and those who were numbered of them were fifty-two thousand, seven hundred.
35 Zidzukulu za Efereimu monga mwa mafuko awo zinali izi; kuchokera mwa Sutela, fuko la Asutela; kuchokera mwa Bekeri, fuko la Abekeri; kuchokera mwa Tahani, fuko la Atahani.
These are the sons of Ephraim by their families: of Shuthelah, the family of the Shuthelahites: of Becher, the family of the Becherites: of Tahan, the family of the Tahanites.
36 Zidzukulu za Sutela zinali izi: kuchokera mwa Erani, fuko la Aerani.
And these are the sons of Shuthelah: of Eran, the family of the Eranites:
37 Awa ndiwo anali mafuko a Efereimu. Amene anawerengedwa analipo 32,500. Zimenezi zinali zidzukulu za Yosefe monga mwa mafuko awo.
These are the families of Ephraim as they were numbered, thirty-two thousand, five hundred. These are the sons of Joseph by their families.
38 Zidzukulu za Benjamini monga mwa mabanja awo zinali izi: kuchokera mwa Bela, fuko la Abela; kuchokera mwa Asibeli, fuko la Aasibeli; kuchokera mwa Ahiramu, fuko la Ahiramu;
The sons of Benjamin by their families: of Bela, the family of the Belaites: of Ashbel, the family of the Ashbelites: of Ahiram, the family of the Ahiramites:
39 kuchokera mwa Sufamu, fuko la Asufamu; kuchokera mwa Hufamu, fuko la Ahufamu;
Of Shephupham, the family of the Shuphamites: and of Hupham, the family of the Huphamites.
40 Zidzukulu za Bela kupyolera mwa Aridi ndi Naamani zinali izi: kuchokera mwa Aridi, fuko la Aaridi; kuchokera mwa Naamani, fuko la Anaamani;
And the sons of Bela were Ard and Naaman: of Ard, the family of the Ardites: of Naaman, the family of the Naamites.
41 Awa ndiwo anali mabanja a Benjamini. Amene nawerengedwa analipo 45,600.
These are the sons of Benjamin by their families: and those who were numbered of them were forty-five thousand, six hundred.
42 Zidzukulu za Dani mwa mabanja awo zinali izi: kuchokera mwa Suhamu fuko la Asuhamu. Izi zinali zidzukulu za Dani.
These are the sons of Dan by their families: of Shuham, the family of the Shuhamites. These are the families of Dan by their families.
43 Onse a fuko la Asuhamu amene anawerengedwa analipo 64,400.
All the families of the Shuhamites, as they were numbered, were sixty-four thousand, four hundred.
44 Zidzukulu za Aseri monga mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Imina, fuko la Aimuna; kuchokera mwa Isivi, fuko la Ayisivi; kuchokera mwa Beriya, fuko la Aberiya;
The sons of Asher by their families: of Imnah, the family of the Imnites: of Ishvi, the family of the Ishvites: of Beriah, the family of the Beriites.
45 ndipo kupyolera mwa zidzukulu za Beriya: kuchokera mwa Heberi, fuko la Aheberi; kuchokera mwa Malikieli, fuko la Amalikieli;
Of the sons of Beriah: of Heber, the family of the Heberites: of Malchiel, the family of the Malchielites:
46 (Aseri anali ndi mwana wamkazi dzina lake Sera)
And the name of the daughter of Asher was Serah.
47 Awa ndiwo anali mafuko a Aseri. Onse amene anawerengedwa analipo 53,400.
These are the families of the sons of Asher as they were numbered, fifty-three thousand, four hundred.
48 Zidzukulu za Nafutali mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Yahazeeli, fuko la Ayahazeeli; kuchokera mwa Guni, fuko la Aguni;
The sons of Naphtali by their families: of Jahzeel, the family of the Jahzeelites: of Guni, the family of the Gunites:
49 kuchokera mwa Yezeri, fuko la Ayezeri; kuchokera mwa Silemu, fuko la Asilemu.
Of Jezer, the family of the Jezerites: of Shillem, the family of the Shillemites.
50 Awa ndiwo anali mafuko a Nafutali. Onse amene anawerengedwa analipo 45,400.
These are the families of Naphtali by their families: and those who were numbered of them were forty-five thousand, four hundred.
51 Chiwerengero chonse cha amuna mu Israeli chinalipo 601,730.
Those who were numbered of the children of Israel were six hundred and one thousand, seven hundred and thirty.
52 Yehova anawuza Mose kuti,
And the Lord said to Moses,
53 “Uwagawire dziko anthu awa kuti likhale cholowa chawo molingana ndi chiwerengero cha mayina awo.
Let there be a division of the land among these, for their heritage, in relation to the number of names.
54 Gulu lalikulu ulipatse cholowa chachikulu, ndipo lochepa cholowa chocheperapo. Gulu lililonse lilandire cholowa chake molingana ndi chiwerengero cha amene anawerengedwa.
To those families who are more in number, give a greater heritage; to those who are less in number, a smaller part: to every one let the heritage be given in relation to the number in his family.
55 Dzikolo uligawe pochita maere. Alandire cholowa chawocho potsata mayina a mafuko a makolo awo.
But let the distribution of the land be made by the decision of the Lord: by the names of the tribes of their fathers let their heritage be given them.
56 Cholowa chawo uchigawe pakati pa fuko lalikulu ndi lalingʼono mwa maere.”
As it is ordered by the decision of the Lord, let distribution be made between those who are more in number and those who are less.
57 Alevi omwe anawerengedwa monga mwa mafuko awo ndi awa: kuchokera mwa Geresoni, fuko la Ageresoni; kuchokera mwa Kohati, fuko la Akohati; kuchokera mwa Merari, fuko la Amerari.
These were those of the Levites who were numbered by their families: of Gershon, the family of the Gershonites: of Kohath, the family of the Kohathites: of Merari, the family of the Merarites.
58 Awanso anali mabanja a Alevi: banja la Alibini, banja la Ahebroni, banja la Amali, banja la Amusi, fuko la Kora banja la Akohati, (Kohati anali abambo a Amramu.
These are the families of Levi: the family of the Libnites, the family of the Hebronites, the family of the Mahlites, the family of the Mushites, the family of the Korahites. And Kohath was the father of Amram.
59 Dzina la mkazi wa Amramu linali Yokobedi, mdzukulu wa Levi, yemwe anabadwa mwa Alevi mu Igupto. Yokobedi anaberekera Amramu Aaroni, Mose ndi Miriamu mlongo wawo.
Amram's wife was Jochebed, the daughter of Levi, whom he had in Egypt: by Amram she had Moses and Aaron and their sister Miriam.
60 Aaroni anali abambo a Nadabu, Abihu, Eliezara ndi Itamara.
Aaron's sons were Nadab and Abihu, Eleazar and Ithamar.
61 Koma Nadabu ndi Abihu anafa pamene anapereka nsembe pamaso pa Yehova ndi moto wachilendo).
Death overtook Nadab and Abihu when they made an offering of strange fire before the Lord.
62 Alevi onse aamuna a mwezi umodzi kapena kuposera pamenepa analipo 23,000. Iwowo sanawerengedwe pamodzi ndi Aisraeli ena chifukwa sanalandire cholowa pakati pawo.
Of these, twenty-three thousand males, from one month old and over, were numbered: they were not numbered with the rest of the children of Israel, for they had no heritage among the children of Israel.
63 Awa ndi amene anawerengedwa ndi Mose ndi Eliezara wansembe pamene ankawerenga Aisraeli pa zigwa za ku Mowabu mʼmbali mwa Yorodani ku Yeriko.
All these were numbered by Moses and Eleazar the priest when the children of Israel were numbered in the lowlands of Moab by the Jordan at Jericho.
64 Mwa anthu amenewa panalibe ndi mmodzi yemwe amene anali mʼgulu la Aisraeli omwe Mose ndi wansembe Aaroni anawawerenga mʼchipululu cha Sinai;
But among all these was not one of those numbered by Moses and Aaron the priest when the children of Israel were numbered in the waste land of Sinai.
65 Chifukwa Yehova anali atawuza Aisraeliwo kuti adzafera ndithu mʼchipululu, ndipo palibe ndi mmodzi yemwe amene anatsala kupatula Kalebe mwana wa Yefune ndi Yoswa mwana wa Nuni.
For the Lord had said of them, Death will certainly overtake them in the waste land. And of them all, only Caleb, the son of Jephunneh, and Joshua, the son of Nun, were still living.

< Numeri 26 >