< Numeri 25 >

1 Aisraeli akukhala ku Sitimu, anayamba kuchita chigololo ndi akazi a ku Mowabu,
Forsothe in that tyme Israel dwellide in Sechym; and the puple dide fornycacioun with the douytris of Moab;
2 amene ankawayitana ku nsembe za milungu yawo. Anthuwo anadya chakudya chopereka kwa milungu ndi kupembedza milunguyo.
whiche douytris clepiden hem to her sacrifices, and thei eten, and worschipiden the goddis of tho douytris;
3 Motero Aisraeli anapembedza nawo Baala-Peori ndipo Yehova anawapsera mtima kwambiri.
and Israel made sacrifice to Belphegor. And the Lord was wrooth,
4 Pamenepo Yehova anawuza Mose kuti, “Tenga atsogoleri onse a anthu awa, uwaphe poyera, pamaso pa Yehova kuti mkwiyo waukulu wa Yehova uchoke pa Israeli.”
and seide to Moises, Take thou alle the princes of the puple, and hange hem ayens the sunne in iebatis, that my wodnesse, `that is stronge veniaunce, be turned awai fro Israel.
5 Choncho Mose anawuza oweruza a Israeli kuti, “Aliyense wa inu ayenera kupha anthu ake amene anapembedza nawo Baala-Peori.”
And Moises seide to the iugis of Israel, Ech man sle his neiyboris, that maden sacrifice to Belphagor.
6 Kenaka mwamuna wina wa ku Israeli anabweretsa ku banja lake mkazi wa Chimidiyani pamaso pa Mose ndi anthu onse a Israeli pamene ankalira pa khomo la tenti ya msonkhano.
And, lo! oon of the sones of Israel entride bifor his britheren to `an hoore of Madian, in the siyt of Moises, and al the cumpeny of the sones of Israel, whiche wepten bifor the yatis of the tabernacle.
7 Finehasi mwana wa Eliezara, mwana wa wansembe Aaroni ataona izi, anachoka pa msonkhanowo, natenga mkondo mʼdzanja lake.
And whanne Phynees, the sone of Eleazar, sone of Aaron, preest, hadde seyn this, he roos fro the myddis of the multitude; and whanne he hadde take a swerd,
8 Ndipo anatsatira Mwisraeliyu mpaka mʼtenti yake. Anasolola mkondowo ndi kubaya awiriwo kupyola Mwisraeliyo mpaka mʼthupi la mkaziyo. Pamenepo mliri unaleka pakati pa Aisraeli.
he entride aftir the man of Israel in to the `hoore hows, and stikide thorou both togidere, that is, the man and the womman, in the places of gendryng. And the veniaunce ceesside fro the sones of Israel,
9 Pa mliriwo, anthu okwana 24,000 anafa.
and foure and twenti thousand of men weren slayn.
10 Yehova anawuza Mose kuti,
And the Lord seide to Moises,
11 “Finehasi mwana wa Eliezara, mwana wa wansembe Aaroni wabweza mkwiyo wanga pa Aisraeli chifukwa sanalole kuti wina aliyense apembedze mulungu wina koma Ine ndekha. Nʼchifukwa chake sindinawawononge mu mkwiyo wanga.
Fynees, the sone of Eleazar, sone of Aaron, preest, turnede away myn yre fro the sones of Israel; for he was stirid ayens hem bi my feruent loue, that Y my silf schulde not do awai the sones of Israel in my greet hete, `ether strong veniaunce.
12 Tsono muwuze kuti ndikhazikitsa pangano langa la mtendere ndi iye.
Therfor speke thou to hym, Lo! Y yyue to hym the pees of my couenaunt,
13 Ndikupangana naye pangano la unsembe wosatha, iyeyo pamodzi ndi zidzukulu zake zonse, chifukwa sanalole kuti anthu awukire Ine Mulungu, ndipo anachita ntchito yopepesera machimo Aisraeli.”
and it schal be an euerlastynge couenaunt of preesthod, as wel to hym silf as to his seed; for he louyde feruentli for his God, and he clenside the greet trespas of the sones of Israel.
14 Dzina la Mwisraeli yemwe anaphedwa ndi mkazi wa Chimidiyani anali Zimuri mwana wa Salu, mtsogoleri wa banja la Simeoni.
Forsothe the name of the man of Israel, that was slayn with the womman of Madian, was Zambri, the sone of Salu, duyk of the kynrede and lynage of Symeon.
15 Ndipo dzina la mkazi wa Chimidiyani, yemwe anaphedwayo, linali Kozibi mwana wa Zuri, mtsogoleri wa fuko la ku Midiyaniko.
Forsothe the womman of Madian that was slayn togidere, was clepid Cobri, the douyter of Sur, the nobleste prince of Madianytis.
16 Yehova anawuza Mose kuti,
And the Lord spak to Moises and seide,
17 “Amidiyani ndi adani anu ndipo uwaphe,
`Madianytis feele you enemyes, and smyte ye hem;
18 chifukwa ankakuonani inu ngati adani awo pamene anakupusitsani pa nkhani ya ku Peori, ndiponso za mlongo wawo Kozibi, mwana wamkazi wa mtsogoleri wa Amidiyani, mkazi yemwe anaphedwa pamene mliri unabwera chifukwa cha zimene zinachitika ku Peori.”
for also thei diden enemyliche ayens you, and disseyueden thorow tresouns, bi the idol of Phegor, and bi `the douyter of Corbri, duyk of Madian, her sister, which douyter was sleyn in the dai of veniaunce, for the sacrilege of Phegor.

< Numeri 25 >