< Numeri 25 >

1 Aisraeli akukhala ku Sitimu, anayamba kuchita chigololo ndi akazi a ku Mowabu,
А докато Израил оставаше в Ситим, людете почнаха да блудствуват с моавките;
2 amene ankawayitana ku nsembe za milungu yawo. Anthuwo anadya chakudya chopereka kwa milungu ndi kupembedza milunguyo.
защото те канеха людете на жертвите на боговете си, и людете ядяха и се кланяха на боговете им.
3 Motero Aisraeli anapembedza nawo Baala-Peori ndipo Yehova anawapsera mtima kwambiri.
Израил се привърза за Ваалфегора; и Господният гняв пламна против Израиля.
4 Pamenepo Yehova anawuza Mose kuti, “Tenga atsogoleri onse a anthu awa, uwaphe poyera, pamaso pa Yehova kuti mkwiyo waukulu wa Yehova uchoke pa Israeli.”
Тогава Господ рече на Моисея: Хвани всичките първенци на людете и обеси ги за Господа пред слънцето, за да се отвърне от Израиля Господният яростен гняв.
5 Choncho Mose anawuza oweruza a Israeli kuti, “Aliyense wa inu ayenera kupha anthu ake amene anapembedza nawo Baala-Peori.”
И Моисей рече на Израилевите съдии: Убийте всеки подчинените си човеци, които се привързаха за Ваалфегора.
6 Kenaka mwamuna wina wa ku Israeli anabweretsa ku banja lake mkazi wa Chimidiyani pamaso pa Mose ndi anthu onse a Israeli pamene ankalira pa khomo la tenti ya msonkhano.
И, ето, един от израилтяните дойде и доведе на братята си една мадиамка пред очите на Моисея и пред цялото общество израилтяни, когато те плачеха пред входа на шатъра за срещане.
7 Finehasi mwana wa Eliezara, mwana wa wansembe Aaroni ataona izi, anachoka pa msonkhanowo, natenga mkondo mʼdzanja lake.
А Финеес, син на Елеазара син на свещеника Аарона, като видя стана изсред обществото, взе копие в ръката си,
8 Ndipo anatsatira Mwisraeliyu mpaka mʼtenti yake. Anasolola mkondowo ndi kubaya awiriwo kupyola Mwisraeliyo mpaka mʼthupi la mkaziyo. Pamenepo mliri unaleka pakati pa Aisraeli.
и влезе подир израилтянина в спалнята та прободе и двамата - израилтянина и жената в корема й. Така язвата престана от израилтяните.
9 Pa mliriwo, anthu okwana 24,000 anafa.
А умрелите от язвата бяха двадесет и четири хиляди души.
10 Yehova anawuza Mose kuti,
Тогава Господ говори на Моисея, казвайки:
11 “Finehasi mwana wa Eliezara, mwana wa wansembe Aaroni wabweza mkwiyo wanga pa Aisraeli chifukwa sanalole kuti wina aliyense apembedze mulungu wina koma Ine ndekha. Nʼchifukwa chake sindinawawononge mu mkwiyo wanga.
Финеес, син на Елеазара, син на свещеника Аарона, отвърна яростта Ми от израилтяните; понеже показа ревността всред тях подобна на Моята, така щото Аз не изтребих израилтяните в ревността си.
12 Tsono muwuze kuti ndikhazikitsa pangano langa la mtendere ndi iye.
За това кажи му: Ето, Аз му давам Моя завет на мир;
13 Ndikupangana naye pangano la unsembe wosatha, iyeyo pamodzi ndi zidzukulu zake zonse, chifukwa sanalole kuti anthu awukire Ine Mulungu, ndipo anachita ntchito yopepesera machimo Aisraeli.”
ще бъде нему и на потомството му подир него завет на вечно свещенство, защото беше ревностен за своя Бог и направи умилостивение за израилтяните.
14 Dzina la Mwisraeli yemwe anaphedwa ndi mkazi wa Chimidiyani anali Zimuri mwana wa Salu, mtsogoleri wa banja la Simeoni.
А името на убитият израилтянин, който беше убит с мадиамката, беше Зимрий син на Салу, първенец на един бащин дом от симеонците.
15 Ndipo dzina la mkazi wa Chimidiyani, yemwe anaphedwayo, linali Kozibi mwana wa Zuri, mtsogoleri wa fuko la ku Midiyaniko.
И името на убитата мадиамка беше Хазвия, дъщеря на Сура, началник на людете, от един бащин дом в Мадиам.
16 Yehova anawuza Mose kuti,
След това Господ говори на Моисея, казвайки:
17 “Amidiyani ndi adani anu ndipo uwaphe,
Измъчвайте мадиамците и поразете ги;
18 chifukwa ankakuonani inu ngati adani awo pamene anakupusitsani pa nkhani ya ku Peori, ndiponso za mlongo wawo Kozibi, mwana wamkazi wa mtsogoleri wa Amidiyani, mkazi yemwe anaphedwa pamene mliri unabwera chifukwa cha zimene zinachitika ku Peori.”
защото те ви измъчват с коварствата, с които ви примамиха чрез Фегора и чрез сестра си Хазвия, дъщеря на един мадиамски първенец, която беше убита в деня на язвата наложена поради Фегора.

< Numeri 25 >