< Numeri 24 >

1 Tsopano Balaamu ataona kuti kunakomera Yehova kudalitsa Israeli, sanapitenso ku mawula monga ankachitira kale, koma kuyangʼana ku chipululu.
UBalami esebonile ukuthi kuhle emehlweni eNkosi ukubusisa uIsrayeli, kahambanga njengezinye izikhathi ukuyadinga imilingo; kodwa wakhangelisa ubuso bakhe enkangala.
2 Balaamu atayangʼana, anaona Aisraeli atamanga misasa yawo fuko ndi fuko. Pamenepo mzimu wa Mulungu unabwera pa iye
Kwathi uBalami ephakamisa amehlo akhe, wabona uIsrayeli ehlezi ngokwezizwe zakhe, loMoya kaNkulunkulu waba phezu kwakhe.
3 ndipo ananena uthenga wake: “Uthenga wa Balaamu mwana wa Beori, uthenga wa amene diso lake ndi lotsekuka,
Wasephakamisa umfanekiso wakhe wathi: UBalami indodana kaBeyori uthi, lendoda olihlo layo livulekile ithi,
4 uthenga wa amene amamva mawu a Mulungu, yemwe amaona masomphenya wochokera kwa Wamphamvuzonse, yemwe amagwa chafufumimba, koma maso ake ali chipenyere:
uthi ozwayo amazwi kaNkulunkulu, obonayo umbono kaSomandla, esiwa, njalo kwembulwe amehlo.
5 “Matenti ako ndi okongola kwambiri iwe Yakobo, misasa yako, iwe Israeli!
Mahle kangakanani amathente akho, Jakobe, amakhaya akho, Israyeli!
6 “Monga zigwa zotambalala, monga minda mʼmbali mwa mtsinje, monga aloe wodzalidwa ndi Yehova, monga mikungudza mʼmbali mwa madzi.
Njengezigodi zisabalele, njengezivande ngasemfuleni, njengezinhlaba iNkosi ezihlanyeleyo, njengezihlahla zemisedari ngasemanzini!
7 Madzi adzayenderera mʼmitsuko yake; mbewu zake zidzakhala ndi madzi ambiri. “Mfumu yake idzakhala yamphamvu kuposa Agagi; ufumu wake udzakwezedwa.
Amanzi azageleza evela embizeni zakhe, lenhlanyelo yakhe izakuba semanzini amanengi, lenkosi yakhe izakuba nkulu kuloAgagi, lombuso wakhe uzaphakama.
8 “Mulungu womutulutsa mʼdziko la Igupto ali ndi mphamvu ngati za njati. Amawononga mitundu yomuwukira ndi kuphwanya mafupa awo, amalasa ndi mivi yake.
UNkulunkulu wamkhupha eGibhithe, ulokunjengamandla enyathi, uzakudla izizwe, izitha zakhe, njalo uzakwephula amathambo azo, njalo azitshoke ngemitshoko yakhe.
9 Monga mkango waumuna, amabisala nagona pansi, monga mkango waukazi, adzamuputa ndani? “Amene adalitsa iwe, adalitsike ndipo amene atemberera iwe, atembereredwe!”
Waqutha, walala phansi njengesilwane, lanjengesilwane esisikazi; ngubani ozamvusa? Okubusisayo abusiswe, lokuqalekisayo aqalekiswe!
10 Kenaka Balaki anakwiyira Balaamu. Anawomba mʼmanja ndi kunena naye kuti, “Ndinakuyitana kuti utemberere adani anga, koma taona, wawadalitsa katatu konseka.
Njalo ulaka lukaBalaki lwavuthela uBalami, watshaya izandla zakhe, uBalaki wasesithi kuBalami: Ngikubize ukuze uqalekise izitha zami, kodwa khangela, uzibusisile lokuzibusisa okwalezizikhathi ezintathu.
11 Tsopano choka msanga uzipita kwanu! Ndinanena kuti ndidzakulipira bwino kwambiri, koma Yehova sanafune kuti ulandire malipirowo.”
Khathesi-ke zibalekele uye endaweni yakho. Bengithe ngizakuhlonipha ngodumo, kodwa khangela, iNkosi ikuvimbile kudumo.
12 Balaamu anayankha Balaki kuti, “Kodi sindinawawuze amithenga amene munawatumiza kwa ine,
UBalami wasesithi kuBalaki: Kangikhulumanga yini lakuzithunywa obuzithume kimi ngisithi:
13 kuti ngakhale Balaki atandipatsa nyumba yake yaufumu yodzaza ndi siliva ndi golide sindingathe kuchita zinthu mwa ine ndekha, zabwino kapena zoyipa, kuposa lamulo la Yehova ndi kuti ndiyenera kunena zokhazo zimene Yehova akunena?
Uba uBalaki ebezangipha indlu yakhe igcwele isiliva legolide, bengingayikweqa umlayo weNkosi, ukwenza okuhle kumbe okubi okwenhliziyo yami; lokho iNkosi ekutshoyo yilokho engizakukhuluma?
14 Tsopano ndikupita kwa anthu anga, koma tabwerani ndikuchenjezeni zimene anthu awa adzachitira anthu anu masiku akubwerawa.”
Khathesi-ke, khangela, ngiya ebantwini bakithi; woza ngikucebise ukuthi lababantu bazakwenzani ebantwini bakini ensukwini zokucina.
15 Ndipo iye ananena uthenga wake nati, “Uthenga wa Balaamu mwana wa Beori, uthenga wa amene diso lake ndi lotsekuka.
Wasephakamisa umfanekiso wakhe wathi: UBalami indodana kaBeyori uthi, lendoda elamehlo avulekileyo ithi,
16 Uthenga wa amene amamva mawu a Mulungu, amene ali ndi nzeru zochokera kwa Wammwambamwamba, amene amaona masomphenya wochokera kwa Wamphamvuzonse, amene amagwa chafufumimba koma diso lake lili lotsekuka:
uthi ozwayo amazwi kaNkulunkulu, lowazi ulwazi loPhezukonke, obonayo umbono kaSomandla, esiwa, njalo kuvuleke amehlo.
17 “Ndikumuona iye koma osati tsopano; ndikumupenya iye koma osati pafupi. Nyenyezi idzatuluka mwa Yakobo; ndodo yaufumu idzatuluka mwa Israeli. Iye adzagonjetsa Mowabu ndi kugonjetsa ana onse a Seti.
Ngizambona, kodwa hatshi khathesi, ngizamkhangela, kodwa kungeseduze; kuzavela inkanyezi kuJakobe, lentonga yobukhosi izavuka koIsrayeli, itshaye amagumbi akoMowabi, njalo ichithe bonke abantwana bakaShethi.
18 Edomu adzagonjetsedwa; Seiri, mdani wake, adzawonongedwa koma mphamvu za Israeli zidzachuluka.
Njalo uEdoma uzakuba yimfuyo, loSeyiri abe yimfuyo yezitha zakhe, kodwa uIsrayeli uzakwenza ngobuqhawe,
19 Wolamulira adzachokera mwa Yakobo ndipo adzawononga otsala a mu mzindamo.”
kuzavela-ke koJakobe umbusi, njalo uzabhubhisa oseleyo emzini.
20 Kenaka Balaamu anaona Aamaleki ndipo ananena uthenga wake uwu: “Aamaleki anali oyamba mwa mitundu ya anthu koma potsiriza pake adzawonongeka.”
Esebone uAmaleki, waphakamisa umfanekiso wakhe wathi: UAmaleki wayengowokuqala wezizwe, kodwa ukucina kwakhe kuyikubhubha okupheleleyo.
21 Kenaka anaonanso Akeni ndipo ananena uthenga wake, “Malo amene mukukhalamo ndi otetezedwa, chisa chanu chinayikidwa pa thanthwe;
Esebone amaKeni, waphakamisa umfanekiso wakhe wathi: Iqinile indlu yakho, isidleke sakho usimise edwaleni.
22 komabe inu Akeni mudzawonongedwa, pamene Asuri adzakutengeni ukapolo.”
Kanti-ke uKhayini uzachithwa, aze akuthumbe uAshuri.
23 Ndipo ananenanso uthenga wina kuti, “Aa, ndani adzakhala ndi moyo Mulungu akachita zimenezi?
Wasephakamisa umfanekiso wakhe wathi: Maye, ngubani ozaphila nxa uNkulunkulu esenza lokhu?
24 Sitima zapamadzi zidzabwera kuchokera ku madooko a Kitimu; kupondereza Asuri ndi Eberi, koma iwonso adzawonongeka.”
Imikhumbi izavela ekhunjini lweKitimi, ihluphe uAshuri, ihluphe uEberi; njalo laye uzabhubha okwesikhathi sonke.
25 Pamenepo Balaamu ananyamuka ndi kubwerera kwawo ndipo Balaki anapitanso njira yake.
UBalami wasesukuma wahamba wabuyela endaweni yakhe; loBalaki laye wahamba ngendlela yakhe.

< Numeri 24 >