< Numeri 24 >

1 Tsopano Balaamu ataona kuti kunakomera Yehova kudalitsa Israeli, sanapitenso ku mawula monga ankachitira kale, koma kuyangʼana ku chipululu.
Balaam now realized that Yahweh wanted to bless the Israeli people, [not curse them]. So he did not use magic/divination [like a shaman would do] to find out what Yahweh wanted, as he often did. Instead, he turned toward the desert.
2 Balaamu atayangʼana, anaona Aisraeli atamanga misasa yawo fuko ndi fuko. Pamenepo mzimu wa Mulungu unabwera pa iye
He saw the Israeli people camped there [in their tents], with each tribe gathered in its own group. Then the Spirit of God took control of him,
3 ndipo ananena uthenga wake: “Uthenga wa Balaamu mwana wa Beori, uthenga wa amene diso lake ndi lotsekuka,
and enabled him to give this prophetic message to Balak: “I, Balaam, the son of Beor, am giving this prophecy; I am speaking as a man who sees [what will happen in the future] clearly speaks.
4 uthenga wa amene amamva mawu a Mulungu, yemwe amaona masomphenya wochokera kwa Wamphamvuzonse, yemwe amagwa chafufumimba, koma maso ake ali chipenyere:
I hear this message from God; I see a vision from him who is all-powerful. My eyes are open as I prostrate myself in front of him.
5 “Matenti ako ndi okongola kwambiri iwe Yakobo, misasa yako, iwe Israeli!
You descendants of Jacob, your tents are very beautiful; they are truly lovely!
6 “Monga zigwa zotambalala, monga minda mʼmbali mwa mtsinje, monga aloe wodzalidwa ndi Yehova, monga mikungudza mʼmbali mwa madzi.
Your tents are spread out [in front of me like groves of palm trees in] valleys, like gardens alongside a river. They are like strong aloe trees/plants that Yahweh has planted, like [strong] cedar trees [that grow] along the rivers.
7 Madzi adzayenderera mʼmitsuko yake; mbewu zake zidzakhala ndi madzi ambiri. “Mfumu yake idzakhala yamphamvu kuposa Agagi; ufumu wake udzakwezedwa.
Your water buckets will always be full; the seeds [that you plant] will always have plenty of water [to make them grow]. The Israelis’ king will be greater than [King] Agag; the kingdom that he rules will be honored.
8 “Mulungu womutulutsa mʼdziko la Igupto ali ndi mphamvu ngati za njati. Amawononga mitundu yomuwukira ndi kuphwanya mafupa awo, amalasa ndi mivi yake.
God brought the Israelis out of Egypt, [leading them along] with his great power [MTY] like a wild ox has. He devastates all the nations that oppose him; he breaks all those people’s bones into pieces, and shoots them with his arrows.
9 Monga mkango waumuna, amabisala nagona pansi, monga mkango waukazi, adzamuputa ndani? “Amene adalitsa iwe, adalitsike ndipo amene atemberera iwe, atembereredwe!”
The Israelis are like lions that crouch and lie down, [ready to pounce on their prey] [SIM]. They are like lionesses [that are resting, but ready to attack]; no one [RHQ] would dare to arouse them! [God] will bless everyone who blesses you Israelis, and he will curse everyone who curses you.”
10 Kenaka Balaki anakwiyira Balaamu. Anawomba mʼmanja ndi kunena naye kuti, “Ndinakuyitana kuti utemberere adani anga, koma taona, wawadalitsa katatu konseka.
Then King Balak was extremely angry with Balaam. He showed with his hands that he was very angry, and he [shouted at Balaam], “I summoned you here to curse my enemies! Instead, you have (blessed/asked God to bless) them three times!
11 Tsopano choka msanga uzipita kwanu! Ndinanena kuti ndidzakulipira bwino kwambiri, koma Yehova sanafune kuti ulandire malipirowo.”
So now, get out of here! Go back home! I said that I would pay you a lot of money [if you cursed them], but Yahweh has prevented you from getting any pay!”
12 Balaamu anayankha Balaki kuti, “Kodi sindinawawuze amithenga amene munawatumiza kwa ine,
Balaam said to Balak, “[Do you not remember what] [RHQ] I told the messengers that you sent to me? I said,
13 kuti ngakhale Balaki atandipatsa nyumba yake yaufumu yodzaza ndi siliva ndi golide sindingathe kuchita zinthu mwa ine ndekha, zabwino kapena zoyipa, kuposa lamulo la Yehova ndi kuti ndiyenera kunena zokhazo zimene Yehova akunena?
‘Even if Balak would give me a palace filled with silver and gold, I would not disobey Yahweh. I cannot do anything bad or anything that is good [that he does not approve of].’ And I told you that I could say only what Yahweh says to me.
14 Tsopano ndikupita kwa anthu anga, koma tabwerani ndikuchenjezeni zimene anthu awa adzachitira anthu anu masiku akubwerawa.”
So yes, I will return to my people, but first, allow me to tell you what will happen to you Moab people in the future.”
15 Ndipo iye ananena uthenga wake nati, “Uthenga wa Balaamu mwana wa Beori, uthenga wa amene diso lake ndi lotsekuka.
So Balaam said this [to Balak]: “I, Balaam, son of Beor, am again giving a prophecy, speaking as a man who sees [what will happen in the future] clearly speaks.
16 Uthenga wa amene amamva mawu a Mulungu, amene ali ndi nzeru zochokera kwa Wammwambamwamba, amene amaona masomphenya wochokera kwa Wamphamvuzonse, amene amagwa chafufumimba koma diso lake lili lotsekuka:
I hear a message from God; I know things that God, who lives in heaven, has [revealed to me]. I see a vision from him who is all-powerful. My eyes are open as I prostrate myself in front of him.
17 “Ndikumuona iye koma osati tsopano; ndikumupenya iye koma osati pafupi. Nyenyezi idzatuluka mwa Yakobo; ndodo yaufumu idzatuluka mwa Israeli. Iye adzagonjetsa Mowabu ndi kugonjetsa ana onse a Seti.
The things that I see [in the vision] are not [going to happen] now; I see things [that God will cause to happen] in the future. A man who is [a descendant of] Jacob will appear like a star [MET]; a king who holds a scepter will be one of the Israeli people. He will crush the heads of you people of Moab; he will wipe out the descendants of Seth.
18 Edomu adzagonjetsedwa; Seiri, mdani wake, adzawonongedwa koma mphamvu za Israeli zidzachuluka.
The Israelis will occupy Edom, and they will conquer their enemies [who live near] Seir [Mountain]. The Israeli people will be victorious/strong.
19 Wolamulira adzachokera mwa Yakobo ndipo adzawononga otsala a mu mzindamo.”
A ruler who is a descendant of Jacob will come; he will get rid of the people who still live in the city [where Balaam first met Balak].”
20 Kenaka Balaamu anaona Aamaleki ndipo ananena uthenga wake uwu: “Aamaleki anali oyamba mwa mitundu ya anthu koma potsiriza pake adzawonongeka.”
Then Balaam looked out over where the Amalek people-group [lived], and he prophesied this: “The Amalek people-group were the greatest nation, but they will be wiped out.”
21 Kenaka anaonanso Akeni ndipo ananena uthenga wake, “Malo amene mukukhalamo ndi otetezedwa, chisa chanu chinayikidwa pa thanthwe;
Then he looked out over the area where the Ken people-group [lived], and he prophesied this: “You [think that] the place where you live is secure/safe like a nest that is made in the cliffs [MET],
22 komabe inu Akeni mudzawonongedwa, pamene Asuri adzakutengeni ukapolo.”
but you will be wiped out when the army of Assyria conquers you.”
23 Ndipo ananenanso uthenga wina kuti, “Aa, ndani adzakhala ndi moyo Mulungu akachita zimenezi?
Balaam ended his prophecies by saying, “Also, (who can (survive/escape) when God does all these things?/no one will be able to (survive/escape) when God does all these things!) [RHQ]
24 Sitima zapamadzi zidzabwera kuchokera ku madooko a Kitimu; kupondereza Asuri ndi Eberi, koma iwonso adzawonongeka.”
Ships will come from Cyprus [Island], and [the men in those ships] will defeat [the armies of] Assyria and Eber. But God will get rid of those men, too.”
25 Pamenepo Balaamu ananyamuka ndi kubwerera kwawo ndipo Balaki anapitanso njira yake.
Then Balaam and Balak returned to their homes.

< Numeri 24 >