< Numeri 24 >

1 Tsopano Balaamu ataona kuti kunakomera Yehova kudalitsa Israeli, sanapitenso ku mawula monga ankachitira kale, koma kuyangʼana ku chipululu.
Vida pak Balám, že by se líbilo Hospodinu, aby dobrořečil Izraelovi, již více nešel jako prvé, jednou i po druhé, k čárům svým, ale obrátil tvář svou proti poušti.
2 Balaamu atayangʼana, anaona Aisraeli atamanga misasa yawo fuko ndi fuko. Pamenepo mzimu wa Mulungu unabwera pa iye
A pozdvih očí svých, viděl Izraele bydlícího v staních po svých pokoleních, a byl nad ním duch Boží.
3 ndipo ananena uthenga wake: “Uthenga wa Balaamu mwana wa Beori, uthenga wa amene diso lake ndi lotsekuka,
I vzav podobenství své, dí: Řekl Balám, syn Beorův, řekl muž mající otevřené oči,
4 uthenga wa amene amamva mawu a Mulungu, yemwe amaona masomphenya wochokera kwa Wamphamvuzonse, yemwe amagwa chafufumimba, koma maso ake ali chipenyere:
Řekl slyšící výmluvnosti Boha silného, kterýž vidění všemohoucího vidí, kterýž když padne, otevřené má oči:
5 “Matenti ako ndi okongola kwambiri iwe Yakobo, misasa yako, iwe Israeli!
Jak velmi krásní jsou stánkové tvoji, Jákobe, příbytkové tvoji, Izraeli!
6 “Monga zigwa zotambalala, monga minda mʼmbali mwa mtsinje, monga aloe wodzalidwa ndi Yehova, monga mikungudza mʼmbali mwa madzi.
Tak jako se potokové rozšiřují, jako zahrady vedlé řeky, jako stromoví aloes, kteréž štípil Hospodin, jako cedrové podlé vod.
7 Madzi adzayenderera mʼmitsuko yake; mbewu zake zidzakhala ndi madzi ambiri. “Mfumu yake idzakhala yamphamvu kuposa Agagi; ufumu wake udzakwezedwa.
Poteče voda z okovu jeho, a símě jeho u vodách mnohých. A král jeho vyvýšen bude více než Agag, a vyzdvihne se království jeho.
8 “Mulungu womutulutsa mʼdziko la Igupto ali ndi mphamvu ngati za njati. Amawononga mitundu yomuwukira ndi kuphwanya mafupa awo, amalasa ndi mivi yake.
Bůh silný vyvedl jej z Egypta, jako udatnost jednorožcova jest jemu; sžereť národy protivné sobě, a kosti jich potře a střelami svými prostřílí.
9 Monga mkango waumuna, amabisala nagona pansi, monga mkango waukazi, adzamuputa ndani? “Amene adalitsa iwe, adalitsike ndipo amene atemberera iwe, atembereredwe!”
Složil se a ležel jako lvíče, a jako lev zůřivý; kdo jej zbudí? Kdo by požehnání dával tobě, požehnaný bude, a kdožť by zlořečil, bude zlořečený.
10 Kenaka Balaki anakwiyira Balaamu. Anawomba mʼmanja ndi kunena naye kuti, “Ndinakuyitana kuti utemberere adani anga, koma taona, wawadalitsa katatu konseka.
Tedy zapáliv se hněvem Balák proti Balámovi, tleskl rukama svýma a řekl Balámovi: Abys zlořečil nepřátelům mým, povolal jsem tebe, a aj, ustavičně dobrořečil jsi jim již po třikrát.
11 Tsopano choka msanga uzipita kwanu! Ndinanena kuti ndidzakulipira bwino kwambiri, koma Yehova sanafune kuti ulandire malipirowo.”
Protož nyní navrať se raději k místu svému. Bylť jsem řekl: Velikou ctí tě ctíti chci, a hle, Hospodin zbavil tě cti.
12 Balaamu anayankha Balaki kuti, “Kodi sindinawawuze amithenga amene munawatumiza kwa ine,
Jemuž odpověděl Balám: Však hned poslům tvým, kteréž jsi poslal ke mně, mluvil jsem, řka:
13 kuti ngakhale Balaki atandipatsa nyumba yake yaufumu yodzaza ndi siliva ndi golide sindingathe kuchita zinthu mwa ine ndekha, zabwino kapena zoyipa, kuposa lamulo la Yehova ndi kuti ndiyenera kunena zokhazo zimene Yehova akunena?
Byť mi dal Balák plný dům svůj stříbra a zlata, nebudu moci přestoupiti řeči Hospodinovy, abych činil dobré neb zlé sám od sebe; což mi Hospodin oznámí, to mluviti budu,
14 Tsopano ndikupita kwa anthu anga, koma tabwerani ndikuchenjezeni zimene anthu awa adzachitira anthu anu masiku akubwerawa.”
(Ale však ještě já, již odcházeje k lidu svému, počkej, poradím tobě, ) co učiní lid ten lidu tvému v posledních dnech.
15 Ndipo iye ananena uthenga wake nati, “Uthenga wa Balaamu mwana wa Beori, uthenga wa amene diso lake ndi lotsekuka.
Tedy vzav podobenství své, dí: Řekl Balám, syn Beorův, řekl muž mající oči otevřené,
16 Uthenga wa amene amamva mawu a Mulungu, amene ali ndi nzeru zochokera kwa Wammwambamwamba, amene amaona masomphenya wochokera kwa Wamphamvuzonse, amene amagwa chafufumimba koma diso lake lili lotsekuka:
Řekl slyšící výmluvnosti Boha silného, kterýž zná naučení nejvyššího, a vidění všemohoucího vidí, kterýž když padne, otevřené má oči:
17 “Ndikumuona iye koma osati tsopano; ndikumupenya iye koma osati pafupi. Nyenyezi idzatuluka mwa Yakobo; ndodo yaufumu idzatuluka mwa Israeli. Iye adzagonjetsa Mowabu ndi kugonjetsa ana onse a Seti.
Uzřímť jej, ale ne nyní, pohledím na něj, ale ne z blízka. Vyjdeť hvězda z Jákoba, a povstane berla z Izraele, kteráž poláme knížata Moábská, a zkazí všecky syny Set.
18 Edomu adzagonjetsedwa; Seiri, mdani wake, adzawonongedwa koma mphamvu za Israeli zidzachuluka.
I bude Edom podmaněn, a Seir v vládařstí přijde nepřátelům svým; nebo Izrael zmužile sobě počínati bude.
19 Wolamulira adzachokera mwa Yakobo ndipo adzawononga otsala a mu mzindamo.”
Panovati bude pošlý z Jákoba, a zahladí ostatky z každého města.
20 Kenaka Balaamu anaona Aamaleki ndipo ananena uthenga wake uwu: “Aamaleki anali oyamba mwa mitundu ya anthu koma potsiriza pake adzawonongeka.”
A když uzřel Amalecha, vzav podobenství své, řekl: Jakož počátek národů Amalech, tak konec jeho do gruntu zahyne.
21 Kenaka anaonanso Akeni ndipo ananena uthenga wake, “Malo amene mukukhalamo ndi otetezedwa, chisa chanu chinayikidwa pa thanthwe;
Uzřev pak Cinea, vzav podobenství své, řekl: Pevný jest příbytek tvůj, a na skále založils hnízdo své;
22 komabe inu Akeni mudzawonongedwa, pamene Asuri adzakutengeni ukapolo.”
Ale však vyhnán bude Cineus, Assur zajatého jej povede.
23 Ndipo ananenanso uthenga wina kuti, “Aa, ndani adzakhala ndi moyo Mulungu akachita zimenezi?
Opět vzav podobenství své, řekl: Ach, kdo bude živ, když toto učiní Bůh silný?
24 Sitima zapamadzi zidzabwera kuchokera ku madooko a Kitimu; kupondereza Asuri ndi Eberi, koma iwonso adzawonongeka.”
A bárky z země Citim připlynou a ssouží Assyrské, ssouží také Židy, ale i ten lid do konce zahyne.
25 Pamenepo Balaamu ananyamuka ndi kubwerera kwawo ndipo Balaki anapitanso njira yake.
Potom vstav Balám, odšel a navrátil se na místo své; Balák také odšel cestou svou.

< Numeri 24 >