< Numeri 23 >
1 Balaamu anati kwa Balaki, “Mundimangire maguwa ansembe asanu ndi awiri pano, ndipo mukonzenso ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri ndi nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri.”
Och Bileam sade till Balak: Bygg mig här sju altare, och låt mig få hit sju stutar och sju vädrar.
2 Balaki anachita monga Balaamu ananenera ndipo awiriwo anapereka ngʼombe imodzi ndi nkhosa yayimuna imodzi pa guwa lansembe lililonse.
Balak gjorde som Bileam honom sade. Och både Balak och Bileam offrade, ju på hvart altare en stut och en vädur.
3 Kenaka Balaamu anati kwa Balaki, “Khalani pano pafupi ndi nsembe yanu ineyo ndipite pambali. Mwina Yehova adzabwera kuti akumane nane. Chilichonse chimene akandionetse ndidzakuwuzani” Choncho anapita ku malo okwera a chipululu.
Och Bileam sade till Balak: Gack till ditt bränneoffer; och jag vill gå bort; om tilläfventyrs Herren kan komma emot mig, och undervisa mig hvad jag skall säga dig. Och gick åstad hasteliga.
4 Mulungu anakumana naye ndipo Balaamu anati, “Ndakonza maguwa asanu ndi awiri ndipo pa guwa lililonse ndaperekapo nsembe ya ngʼombe yayimuna imodzi ndi nkhosa yayimuna imodzinso.”
Och Gud kom emot Bileam. Men han sade till honom: Sju altare hafver jag tillredt, och ju på hvart altaret en stut och en vädur offrat.
5 Yehova anawuza Balaamu kuti, “Bwerera kwa Balaki ndipo ukamuwuze uthenga uwu.”
Och Herren gaf Bileam ordet i munnen, och sade: Gack till Balak igen, och säg alltså.
6 Ndipo anabwerera kwa iye namupeza atayima pafupi ndi nsembe yake pamodzi ndi akuluakulu onse a Mowabu.
Och då han kom igen till honom, si då stod han när sitt bränneoffer, med alla de Moabiters Förstar.
7 Ndipo Balaamu ananena uthenga wake: “Balaki ananditenga kuchoka ku Aramu, mfumu ya ku Mowabu kuchokera ku mapiri a kummawa. Iye anati, ‘Bwera, temberera Yakobo mʼmalo mwanga, pita nyoza Israeli.’
Då hof han sitt tal upp, och sade: Utaf Syrien hafver Balak, de Moabiters Konung, låtit hemta mig, ifrå bergen österut: Kom och förbanna mig Jacob; kom, tala ondt emot Israel.
8 Ndingatemberere bwanji amene Mulungu sanawatemberere? Ndinganyoze bwanji amene Yehova sanawanyoze?
Huru skall jag förbanna den Gud icke förbannar? Huru skall jag tala ondt emot den Herren intet ondt emot talar?
9 Kuchokera pamwamba pa mapiri ndikuona anthu, ndikuwaona kuchokera pa zitunda. Ndikuona anthu okhala pawokha, osakhala mʼgulu limodzi ndi mitundu ina.
Ty af bergshöjden ser jag honom väl, och af högarna skådar jag honom. Si, det folket varder allena boendes, och icke skall räknadt varda ibland Hedningar.
10 Ndani angawerenge zidzukulu za Yakobo zochuluka ngati fumbi, kapena chimodzi mwa zigawo zinayi za Israeli? Lekeni ndife imfa ya oyera mtima, ndi chimaliziro changa chikhale ngati chawo!”
Ho kan räkna Jacobs stoft, och talet på fjerdedelen af Israel? Min själ dö med de rättfärdigas död, och min ände varde såsom dessas ände.
11 Balaki anati kwa Balaamu, “Wandichitira chiyani? Ndinakuyitana kuti utemberere adani anga, ndipo taona, sunachite chilichonse koma kuwadalitsa!”
Då sade Balak till Bileam: Hvad gör du mig? Jag hafver låtit hemta dig till att förbanna mina fiendar, och si, du välsignar dem.
12 Iye anayankha kuti, “Kodi sindinayenera kuyankhula zimene Yehova anandiwuza?”
Han svarade, och sade: Skulle jag icke det hålla och tala, som Herren gifver mig i munnen?
13 Kenaka Balaki anawuza Balaamu kuti, “Tiye tipite limodzi ku malo ena komwe ungawaone. Udzangoona gulu limodzi osati onsewo. Ndipo pamenepo, ukawatemberere mʼmalo mwanga.”
Balak sade till honom: Kom då med mig på en annan plats, dädan du hans ända ser, och dock icke allansamman ser; och förbanna mig honom der.
14 Tsono anamutengera ku munda wa Zofimu pamwamba pa phiri la Pisiga ndipo kumeneko anamanga maguwa ansembe asanu ndi awiri ndipo anapereka nsembe ngʼombe yayimuna imodzi ndi nkhosa yayimuna imodzi pa guwa lansembe lililonse.
Och tog han honom på en fri plan, uppå kullen af berget Pisga, och byggde sju altare, och offrade ju på hvart altaret en stut och en vädur;
15 Balaamu anawuza Balaki kuti, “Khalani pano pafupi ndi nsembe yanu pamene ine ndikukakumana ndi Mulungu cha uko.”
Och sade till Balak: Gack till ditt bränneoffer; jag vill vänta derborta.
16 Yehova anakumana ndi Balaamu ndipo anamuyankhula kuti, “Bwerera kwa Balaki ndipo ukamuwuze uthenga uwu.”
Och Herren kom emot Bileam, och gaf honom ordet i hans mun, och sade: Gack till Balak igen, och säg alltså.
17 Ndipo anapita kwa iye ndipo anamupeza atayimirira pafupi ndi nsembe yake pamodzi ndi akuluakulu a ku Mowabu. Balaki anafunsa Balaamu kuti, “Yehova wayankhula chiyani?”
Och då han kom igen till honom, si, då stod han när sitt bränneoffer, med de Moabiters Förstar. Och Balak sade till honom: Hvad hafver Herren sagt?
18 Pamenepo Balaamu ananena uthenga wake: “Nyamuka Balaki ndipo tamvera; Undimvere iwe mwana wa Zipori.
Och han hof upp sitt tal, och sade: Statt upp, Balak, och hör; fatta i öronen hvad jag säger, du Zipors son:
19 Mulungu si munthu kuti aname, kapena mwana wa munthu kuti asinthe maganizo ake. Kodi amayankhula koma osachita? Kodi amalonjeza koma osakwaniritsa?
Gud är icke en menniska, att han kan ljuga; eller menniskobarn, att honom något kan ångra. Skulle han säga något, och icke görat? Skulle han något tala, och icke hållat?
20 Wandilamula kuti ndidalitse, Iyeyo wadalitsa ndipo sindingasinthe.
Si, till att välsigna är jag hit hafd; jag välsignar, och kan icke omvändat.
21 “Palibe kuwukira kulikonse kumene wakuona mwa Yakobo, sanaone chovuta mu Israeli. Yehova Mulungu wawo ali nawo: mfuwu wa mfumu uli pakati pawo.
Man ser ingen mödo i Jacob, och intet arbete i Israel; Herren hans Gud är när honom, och Konungens trummetning ibland honom.
22 Mulungu wowatulutsa mʼdziko la Igupto, ali ndi mphamvu ngati za njati.
Gud hafver fört honom utur Egypten; hans frimodighet är såsom ens enhörnings.
23 Palibe matsenga amene angalimbane ndi Yakobo, palibe mawula amene angalimbane ndi Israeli. Tsopano za Yakobo ndi Israeli adzanena kuti, ‘Onani zimene Mulungu wachita!’
Ty ingen trollkarl är i Jacob, och ingen spåman i Israel. I sin tid varder man sägandes om Jacob och om Israel, hvilka under Gud gör.
24 Taonani, anthu anyamuka ngati mkango waukazi; adzuka okha ngati mkango waumuna umene supuma mpaka utadya nyama imene wagwira ndi kumwa magazi a nyama yogwidwayo.”
Si, det folket varder uppståndandes såsom ett ungt lejon, och varder sig uppresandes såsom ett lejon; det skall icke lägga sig, tilldess det äter rof, och dricker deras blod, som slagne äro.
25 Ndipo Balaki anati kwa Balaamu, “Usawatemberere ndi pangʼono pomwe kapena kuwadalitsa!
Då sade Balak till Bileam: Du skall hvarken förbanna dem, eller välsigna dem.
26 “Balaamu anayankha Balaki kuti, ‘Kodi sindinakuwuzeni kuti ndiyenera kuchita zimene Yehova wanena?’”
Bileam svarade, och sade till Balak: Hafver jag icke sagt dig, att allt det Herren talandes vorde, det måste jag göra?
27 Kenaka Balaki anati kwa Balaamu, “Bwera ndikutengere ku malo ena. Mwina chidzamukondweretsa Mulungu kuti uwatemberere kumeneko mʼmalo mwanga.”
Balak sade till honom: Kom, jag vill hafva dig på en annan plats; om tilläfventyrs Gudi må täckas, att du förbannar dem der.
28 Ndipo Balaki anamutengera Balaamu pamwamba pa Peori, poyangʼanana ndi chipululu.
Och han tog honom upp på kullen af det berget Peor, hvilket vet åt öknena.
29 Balaamu anati kwa Balaki, “Mundimangire maguwa ansembe asanu ndi awiri pano ndipo mundikonzere ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri.”
Och Bileam sade till Balak: Bygg mig här sju altare, och låt mig få sju stutar och sju vädrar.
30 Balaki anachita monga Balaamu ananenera ndipo anapereka nsembe ngʼombe imodzi yayimuna ndi nkhosa imodzi yayimuna pa guwa lililonse.
Balak gjorde såsom Bileam sade, och offrade ju uppå hvart altaret en stut och en vädur.