< Numeri 23 >

1 Balaamu anati kwa Balaki, “Mundimangire maguwa ansembe asanu ndi awiri pano, ndipo mukonzenso ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri ndi nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri.”
Balaam disse a Balak, “Construa aqui sete altares para mim, e prepare aqui sete touros e sete carneiros para mim”.
2 Balaki anachita monga Balaamu ananenera ndipo awiriwo anapereka ngʼombe imodzi ndi nkhosa yayimuna imodzi pa guwa lansembe lililonse.
Balak fez como Balaam tinha falado; e Balak e Balaam ofereceram em cada altar um touro e um carneiro.
3 Kenaka Balaamu anati kwa Balaki, “Khalani pano pafupi ndi nsembe yanu ineyo ndipite pambali. Mwina Yehova adzabwera kuti akumane nane. Chilichonse chimene akandionetse ndidzakuwuzani” Choncho anapita ku malo okwera a chipululu.
Balaam disse a Balak: “Fique de pé com sua oferta queimada, e eu irei”. Talvez Yahweh venha ao meu encontro”. O que quer que ele me mostre, eu lhe direi”. Ele foi a uma altura nua.
4 Mulungu anakumana naye ndipo Balaamu anati, “Ndakonza maguwa asanu ndi awiri ndipo pa guwa lililonse ndaperekapo nsembe ya ngʼombe yayimuna imodzi ndi nkhosa yayimuna imodzinso.”
Deus encontrou Balaão e lhe disse: “Preparei os sete altares e ofereci um touro e um carneiro em cada altar”.
5 Yehova anawuza Balaamu kuti, “Bwerera kwa Balaki ndipo ukamuwuze uthenga uwu.”
Yahweh pôs uma palavra na boca de Balaam, e disse: “Volte para Balak, e assim você falará”.
6 Ndipo anabwerera kwa iye namupeza atayima pafupi ndi nsembe yake pamodzi ndi akuluakulu onse a Mowabu.
Ele voltou para ele, e eis que estava junto a seu holocausto, ele e todos os príncipes dos moabitas.
7 Ndipo Balaamu ananena uthenga wake: “Balaki ananditenga kuchoka ku Aramu, mfumu ya ku Mowabu kuchokera ku mapiri a kummawa. Iye anati, ‘Bwera, temberera Yakobo mʼmalo mwanga, pita nyoza Israeli.’
Ele retomou sua parábola, e disse, “De Aram, Balak me trouxe”, o rei dos Moab das montanhas do Leste. Venha, amaldiçoe Jacob por mim. Venha, desafie Israel.
8 Ndingatemberere bwanji amene Mulungu sanawatemberere? Ndinganyoze bwanji amene Yehova sanawanyoze?
Como devo amaldiçoar quem Deus não amaldiçoou? Como devo desafiar quem Javé não desafiou?
9 Kuchokera pamwamba pa mapiri ndikuona anthu, ndikuwaona kuchokera pa zitunda. Ndikuona anthu okhala pawokha, osakhala mʼgulu limodzi ndi mitundu ina.
Pois do alto das rochas eu o vejo. Das colinas, eu o vejo. Eis que é um povo que mora sozinho, e não devem ser listadas entre as nações.
10 Ndani angawerenge zidzukulu za Yakobo zochuluka ngati fumbi, kapena chimodzi mwa zigawo zinayi za Israeli? Lekeni ndife imfa ya oyera mtima, ndi chimaliziro changa chikhale ngati chawo!”
Quem pode contar o pó de Jacob, ou contar a quarta parte de Israel? Deixe-me morrer a morte dos justos! Que meu último fim seja como o dele”!
11 Balaki anati kwa Balaamu, “Wandichitira chiyani? Ndinakuyitana kuti utemberere adani anga, ndipo taona, sunachite chilichonse koma kuwadalitsa!”
Balak disse a Balaam: “O que você fez comigo? Eu o levei para amaldiçoar meus inimigos, e eis que você os abençoou completamente”.
12 Iye anayankha kuti, “Kodi sindinayenera kuyankhula zimene Yehova anandiwuza?”
Ele respondeu e disse: “Não devo ter cuidado para falar aquilo que Iavé põe na minha boca?”.
13 Kenaka Balaki anawuza Balaamu kuti, “Tiye tipite limodzi ku malo ena komwe ungawaone. Udzangoona gulu limodzi osati onsewo. Ndipo pamenepo, ukawatemberere mʼmalo mwanga.”
Balak disse-lhe: “Por favor, venha comigo para outro lugar, onde você possa vê-los”. Você verá apenas uma parte deles e não os verá todos”. Amaldiçoe-os de lá por mim”.
14 Tsono anamutengera ku munda wa Zofimu pamwamba pa phiri la Pisiga ndipo kumeneko anamanga maguwa ansembe asanu ndi awiri ndipo anapereka nsembe ngʼombe yayimuna imodzi ndi nkhosa yayimuna imodzi pa guwa lansembe lililonse.
Ele o levou para o campo de Zophim, ao topo de Pisgah, e construiu sete altares, e ofereceu um touro e um carneiro em cada altar.
15 Balaamu anawuza Balaki kuti, “Khalani pano pafupi ndi nsembe yanu pamene ine ndikukakumana ndi Mulungu cha uko.”
Ele disse a Balak: “Fique aqui ao lado de sua oferta queimada, enquanto eu encontro Deus ali”.
16 Yehova anakumana ndi Balaamu ndipo anamuyankhula kuti, “Bwerera kwa Balaki ndipo ukamuwuze uthenga uwu.”
Yahweh encontrou Balaam, e colocou uma palavra em sua boca, e disse: “Volte para Balak, e diga isto”.
17 Ndipo anapita kwa iye ndipo anamupeza atayimirira pafupi ndi nsembe yake pamodzi ndi akuluakulu a ku Mowabu. Balaki anafunsa Balaamu kuti, “Yehova wayankhula chiyani?”
Ele veio até ele, e eis que ele estava junto a seu holocausto, e os príncipes dos Moab com ele. Balak lhe disse: “O que Javé falou?”.
18 Pamenepo Balaamu ananena uthenga wake: “Nyamuka Balaki ndipo tamvera; Undimvere iwe mwana wa Zipori.
Ele retomou sua parábola, e disse, “Levanta-te, Balak, e ouve! Ouça-me, seu filho de Zippor.
19 Mulungu si munthu kuti aname, kapena mwana wa munthu kuti asinthe maganizo ake. Kodi amayankhula koma osachita? Kodi amalonjeza koma osakwaniritsa?
Deus não é um homem, que ele deve mentir, nem um filho do homem, que deveria se arrepender. Ele já disse, e não o fará? Ou ele já falou e não vai fazer com que seja bom?
20 Wandilamula kuti ndidalitse, Iyeyo wadalitsa ndipo sindingasinthe.
Eis que recebi uma ordem para abençoar. Ele abençoou, e eu não posso reverter isso.
21 “Palibe kuwukira kulikonse kumene wakuona mwa Yakobo, sanaone chovuta mu Israeli. Yehova Mulungu wawo ali nawo: mfuwu wa mfumu uli pakati pawo.
Ele não viu iniqüidade em Jacob. Nem ele viu perversidade em Israel. Yahweh, seu Deus, está com ele. O grito de um rei está entre eles.
22 Mulungu wowatulutsa mʼdziko la Igupto, ali ndi mphamvu ngati za njati.
Deus os traz para fora do Egito. Ele tem como que a força do boi selvagem.
23 Palibe matsenga amene angalimbane ndi Yakobo, palibe mawula amene angalimbane ndi Israeli. Tsopano za Yakobo ndi Israeli adzanena kuti, ‘Onani zimene Mulungu wachita!’
Certamente não há nenhum encantamento com Jacob; também não há nenhuma adivinhação com Israel. Agora se falará de Jacó e de Israel, O que Deus tem feito!
24 Taonani, anthu anyamuka ngati mkango waukazi; adzuka okha ngati mkango waumuna umene supuma mpaka utadya nyama imene wagwira ndi kumwa magazi a nyama yogwidwayo.”
Eis que um povo se levanta como uma leoa. Como um leão, ele se levanta. Ele não deve deitar-se até que coma a presa, e bebe o sangue dos mortos”.
25 Ndipo Balaki anati kwa Balaamu, “Usawatemberere ndi pangʼono pomwe kapena kuwadalitsa!
Balak disse a Balaam: “Nem os amaldiçoe, nem os abençoe”.
26 “Balaamu anayankha Balaki kuti, ‘Kodi sindinakuwuzeni kuti ndiyenera kuchita zimene Yehova wanena?’”
Mas Balaam respondeu a Balak: “Eu não te disse, dizendo: 'Tudo o que Yahweh fala, que eu devo fazer?
27 Kenaka Balaki anati kwa Balaamu, “Bwera ndikutengere ku malo ena. Mwina chidzamukondweretsa Mulungu kuti uwatemberere kumeneko mʼmalo mwanga.”
Balak disse a Balaam: “Venha agora, eu o levarei a outro lugar; talvez agrade a Deus que você possa amaldiçoá-los por mim de lá”.
28 Ndipo Balaki anamutengera Balaamu pamwamba pa Peori, poyangʼanana ndi chipululu.
Balak levou Balaam para o topo de Peor, que olha para baixo no deserto.
29 Balaamu anati kwa Balaki, “Mundimangire maguwa ansembe asanu ndi awiri pano ndipo mundikonzere ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri.”
Balaam disse a Balak: “Construa sete altares para mim aqui, e prepare sete touros e sete carneiros para mim aqui”.
30 Balaki anachita monga Balaamu ananenera ndipo anapereka nsembe ngʼombe imodzi yayimuna ndi nkhosa imodzi yayimuna pa guwa lililonse.
Balak fez como Balaam havia dito, e ofereceu um touro e um carneiro em cada altar.

< Numeri 23 >