< Numeri 23 >

1 Balaamu anati kwa Balaki, “Mundimangire maguwa ansembe asanu ndi awiri pano, ndipo mukonzenso ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri ndi nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri.”
Then said Balaam unto Balak: Build me here seven altars, —and prepare me here, seven bullocks and seven rams.
2 Balaki anachita monga Balaamu ananenera ndipo awiriwo anapereka ngʼombe imodzi ndi nkhosa yayimuna imodzi pa guwa lansembe lililonse.
And Balak did as Balaam had spoken, —and Balak and Balaam caused to ascend a bullock and a ram on each altar.
3 Kenaka Balaamu anati kwa Balaki, “Khalani pano pafupi ndi nsembe yanu ineyo ndipite pambali. Mwina Yehova adzabwera kuti akumane nane. Chilichonse chimene akandionetse ndidzakuwuzani” Choncho anapita ku malo okwera a chipululu.
Then said Balaam unto Balak: Station thyself by thine ascending-sacrifice, and let me go my way—peradventure Yahweh may come and meet me, and what thing soever he may show me, I will tell thee. So he went his way to a bare height.
4 Mulungu anakumana naye ndipo Balaamu anati, “Ndakonza maguwa asanu ndi awiri ndipo pa guwa lililonse ndaperekapo nsembe ya ngʼombe yayimuna imodzi ndi nkhosa yayimuna imodzinso.”
And God came unto Balaam, —so he said unto him The seven altars, have I built in a row, and have caused to ascend, bullock and a ram on each altar.
5 Yehova anawuza Balaamu kuti, “Bwerera kwa Balaki ndipo ukamuwuze uthenga uwu.”
And Yahweh put a word into the mouth of Balaam, —and said—Return unto Balak, and, thus, shalt thou speak.
6 Ndipo anabwerera kwa iye namupeza atayima pafupi ndi nsembe yake pamodzi ndi akuluakulu onse a Mowabu.
So he returned unto him, and lo! he was stationed by his ascending-sacrifice, —he, and all the princes of Moab.
7 Ndipo Balaamu ananena uthenga wake: “Balaki ananditenga kuchoka ku Aramu, mfumu ya ku Mowabu kuchokera ku mapiri a kummawa. Iye anati, ‘Bwera, temberera Yakobo mʼmalo mwanga, pita nyoza Israeli.’
So he took up his parable and said, —From Aram, doth Balak conduct me, The king of Moab, from the mountains of the East, Come thou! curse me Jacob, Yea, come thou! rage on Israel.
8 Ndingatemberere bwanji amene Mulungu sanawatemberere? Ndinganyoze bwanji amene Yehova sanawanyoze?
How can I revile one whom GOD hath not reviled? Yea, how can I rage on one on whom Yahweh hath not raged?
9 Kuchokera pamwamba pa mapiri ndikuona anthu, ndikuwaona kuchokera pa zitunda. Ndikuona anthu okhala pawokha, osakhala mʼgulu limodzi ndi mitundu ina.
Surely from the head of the rocks, do I see him, Yea, from the hills, do I observe him, —Lo! a people, who alone doth dwell, And among the nations, he doth not reckon himself.
10 Ndani angawerenge zidzukulu za Yakobo zochuluka ngati fumbi, kapena chimodzi mwa zigawo zinayi za Israeli? Lekeni ndife imfa ya oyera mtima, ndi chimaliziro changa chikhale ngati chawo!”
Who hath counted the dust of Jacob? Or who hath numbered the fourth part of Israel? Let me die the death of the upright, And let my hereafter be like his!
11 Balaki anati kwa Balaamu, “Wandichitira chiyani? Ndinakuyitana kuti utemberere adani anga, ndipo taona, sunachite chilichonse koma kuwadalitsa!”
Then said Balak unto Balaam, What hast thou done for me? To revile mine enemies, I summoned thee, and lo! thou hast kept on blessing.
12 Iye anayankha kuti, “Kodi sindinayenera kuyankhula zimene Yehova anandiwuza?”
And he answered and said, —Was it not to be so that whatsoever Yahweh should put into my mouth, the same, should I take heed to speak?
13 Kenaka Balaki anawuza Balaamu kuti, “Tiye tipite limodzi ku malo ena komwe ungawaone. Udzangoona gulu limodzi osati onsewo. Ndipo pamenepo, ukawatemberere mʼmalo mwanga.”
Then said Balak unto him—Come, I pray thee, with me unto another place, from whence thou mayest see him, nothing but his utmost part, shalt thou see, but all of him, shalt thou not see, —and so revile me him from thence.
14 Tsono anamutengera ku munda wa Zofimu pamwamba pa phiri la Pisiga ndipo kumeneko anamanga maguwa ansembe asanu ndi awiri ndipo anapereka nsembe ngʼombe yayimuna imodzi ndi nkhosa yayimuna imodzi pa guwa lansembe lililonse.
And he took him to the field of Zophim, unto the head of Pisgah, —and built seven altars, and caused to ascend a bullock and a ram on each altar.
15 Balaamu anawuza Balaki kuti, “Khalani pano pafupi ndi nsembe yanu pamene ine ndikukakumana ndi Mulungu cha uko.”
Then said he to Balak, Station thyself here by thine ascending-sacrifice, —while, I, meet him yonder.
16 Yehova anakumana ndi Balaamu ndipo anamuyankhula kuti, “Bwerera kwa Balaki ndipo ukamuwuze uthenga uwu.”
And Yahweh met Balaam, and put a word into his mouth, —and said—Return unto Balak and thus shalt thou speak.
17 Ndipo anapita kwa iye ndipo anamupeza atayimirira pafupi ndi nsembe yake pamodzi ndi akuluakulu a ku Mowabu. Balaki anafunsa Balaamu kuti, “Yehova wayankhula chiyani?”
So he came in unto him and, there he was-stationed by his ascending-sacrifice, and the princes of Moab with him. And Balak said unto him, What hath Yahweh spoken?
18 Pamenepo Balaamu ananena uthenga wake: “Nyamuka Balaki ndipo tamvera; Undimvere iwe mwana wa Zipori.
Then took he up his parable and said, —Rise, Balak, and hear, Give ear unto me son of Zippor!
19 Mulungu si munthu kuti aname, kapena mwana wa munthu kuti asinthe maganizo ake. Kodi amayankhula koma osachita? Kodi amalonjeza koma osakwaniritsa?
GOD is, not a man, that he should lie, Nor a son of Adam, that he should repent, —Hath, he, said, and will not perform? Yea spoken, and will not make it stand fast?
20 Wandilamula kuti ndidalitse, Iyeyo wadalitsa ndipo sindingasinthe.
Lo! to bless, have I received [command], —And I will bless, nor will I take it back.
21 “Palibe kuwukira kulikonse kumene wakuona mwa Yakobo, sanaone chovuta mu Israeli. Yehova Mulungu wawo ali nawo: mfuwu wa mfumu uli pakati pawo.
He hath not discovered trouble in Jacob, Neither hath he seen wretchedness in Israel, —Yahweh, his God, is with him, And, the acclaim of a king, in his midst:
22 Mulungu wowatulutsa mʼdziko la Igupto, ali ndi mphamvu ngati za njati.
GOD having brought them forth out of Egypt, The very horns of the buffalo, are his:
23 Palibe matsenga amene angalimbane ndi Yakobo, palibe mawula amene angalimbane ndi Israeli. Tsopano za Yakobo ndi Israeli adzanena kuti, ‘Onani zimene Mulungu wachita!’
Surely, there is no enchantment against Jacob, Nor divination against Israel, —Now, shall it be said—Of Jacob and of Israel, What hath GOD wrought!
24 Taonani, anthu anyamuka ngati mkango waukazi; adzuka okha ngati mkango waumuna umene supuma mpaka utadya nyama imene wagwira ndi kumwa magazi a nyama yogwidwayo.”
Lo, a people, like a lioness, shall rise, And like a strong lion, shall rouse himself up; He will not lie down till he eat the torn, And the blood of the slain, he drink.
25 Ndipo Balaki anati kwa Balaamu, “Usawatemberere ndi pangʼono pomwe kapena kuwadalitsa!
Then said Balak unto Balaam, Thou shalt neither revile, him, —nor bless him.
26 “Balaamu anayankha Balaki kuti, ‘Kodi sindinakuwuzeni kuti ndiyenera kuchita zimene Yehova wanena?’”
And Balaam responded, and said unto Balak, —Spake I not unto thee, saying, All that Yahweh shall speak, that, must I do?
27 Kenaka Balaki anati kwa Balaamu, “Bwera ndikutengere ku malo ena. Mwina chidzamukondweretsa Mulungu kuti uwatemberere kumeneko mʼmalo mwanga.”
And Balak said unto Balaam, Come, I pray thee! let me take thee unto another place, —peradventure, it may be right in the eyes of God, that thou revile me him. from thence.
28 Ndipo Balaki anamutengera Balaamu pamwamba pa Peori, poyangʼanana ndi chipululu.
So Balak took Balaam, —unto the head of Peor, that looketh over the face of the Jeshimon.
29 Balaamu anati kwa Balaki, “Mundimangire maguwa ansembe asanu ndi awiri pano ndipo mundikonzere ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri.”
And Balaam said unto Balak, Build me here, seven altars, —and prepare me here, seven bullocks and seven rams.
30 Balaki anachita monga Balaamu ananenera ndipo anapereka nsembe ngʼombe imodzi yayimuna ndi nkhosa imodzi yayimuna pa guwa lililonse.
And Balak did as Balaam said, —and caused to ascend a bullock and a ram on each altar.

< Numeri 23 >