< Numeri 23 >

1 Balaamu anati kwa Balaki, “Mundimangire maguwa ansembe asanu ndi awiri pano, ndipo mukonzenso ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri ndi nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri.”
And Bil'am said unto Balak, Build me here seven altars, and prepare me here seven bullocks and seven rams.
2 Balaki anachita monga Balaamu ananenera ndipo awiriwo anapereka ngʼombe imodzi ndi nkhosa yayimuna imodzi pa guwa lansembe lililonse.
And Balak did as Bil'am had spoken; and Balak and Bil'am offered a bullock and a ram on every altar.
3 Kenaka Balaamu anati kwa Balaki, “Khalani pano pafupi ndi nsembe yanu ineyo ndipite pambali. Mwina Yehova adzabwera kuti akumane nane. Chilichonse chimene akandionetse ndidzakuwuzani” Choncho anapita ku malo okwera a chipululu.
And Bil'am said unto Balak, Place thyself by thy burnt-offering; and I will go, peradventure the Lord will come to meet me, and whatsoever he may show me I will tell thee: and he went thoughtfully alone.
4 Mulungu anakumana naye ndipo Balaamu anati, “Ndakonza maguwa asanu ndi awiri ndipo pa guwa lililonse ndaperekapo nsembe ya ngʼombe yayimuna imodzi ndi nkhosa yayimuna imodzinso.”
And God met Bil'am: and he said unto him, The seven altars have I made ready, and I have offered a bullock and a ram upon every altar.
5 Yehova anawuza Balaamu kuti, “Bwerera kwa Balaki ndipo ukamuwuze uthenga uwu.”
And the Lord put a word in Bil'am's mouth, and said, Return unto Balak, and thus shalt thou speak.
6 Ndipo anabwerera kwa iye namupeza atayima pafupi ndi nsembe yake pamodzi ndi akuluakulu onse a Mowabu.
And he returned unto him, and, lo, he was standing by his burnt-offering, he, and all the princes of Moab.
7 Ndipo Balaamu ananena uthenga wake: “Balaki ananditenga kuchoka ku Aramu, mfumu ya ku Mowabu kuchokera ku mapiri a kummawa. Iye anati, ‘Bwera, temberera Yakobo mʼmalo mwanga, pita nyoza Israeli.’
And he took up his parable, and said, From Aram did Balak send for me, the king of Moab, out of the mountains of the east, Come, curse me Jacob, and come, defy Israel.
8 Ndingatemberere bwanji amene Mulungu sanawatemberere? Ndinganyoze bwanji amene Yehova sanawanyoze?
How shall I denounce, whom God hath not denounced? and how shall I defy, whom the Lord hath not defied?
9 Kuchokera pamwamba pa mapiri ndikuona anthu, ndikuwaona kuchokera pa zitunda. Ndikuona anthu okhala pawokha, osakhala mʼgulu limodzi ndi mitundu ina.
For from the top of rocks I see him, and from hills I behold him: lo, it is a people that shall dwell alone, and among the nations it shall not be reckoned.
10 Ndani angawerenge zidzukulu za Yakobo zochuluka ngati fumbi, kapena chimodzi mwa zigawo zinayi za Israeli? Lekeni ndife imfa ya oyera mtima, ndi chimaliziro changa chikhale ngati chawo!”
Who can count the dust of Jacob, and number the fourth part of Israel? May my soul die the death of the righteous, and may my last end be like his!
11 Balaki anati kwa Balaamu, “Wandichitira chiyani? Ndinakuyitana kuti utemberere adani anga, ndipo taona, sunachite chilichonse koma kuwadalitsa!”
And Balak said unto Bil'am, What hast thou done unto me? to denounce my enemies did I take thee, and, behold, thou hast even blessed them.
12 Iye anayankha kuti, “Kodi sindinayenera kuyankhula zimene Yehova anandiwuza?”
And he answered and said, Must I not take heed to speak that only which the Lord may put in my mouth?
13 Kenaka Balaki anawuza Balaamu kuti, “Tiye tipite limodzi ku malo ena komwe ungawaone. Udzangoona gulu limodzi osati onsewo. Ndipo pamenepo, ukawatemberere mʼmalo mwanga.”
And Balak said unto him, Come, I pray thee, with me unto another place, from where thou canst see them; nevertheless a portion of them only wilt thou see, but the whole of them thou wilt not see: and denounce them for me from there.
14 Tsono anamutengera ku munda wa Zofimu pamwamba pa phiri la Pisiga ndipo kumeneko anamanga maguwa ansembe asanu ndi awiri ndipo anapereka nsembe ngʼombe yayimuna imodzi ndi nkhosa yayimuna imodzi pa guwa lansembe lililonse.
And he brought him to the field of the watchmen, on the top of Pisgah, and he built seven altars, and offered a bullock and a ram on every altar.
15 Balaamu anawuza Balaki kuti, “Khalani pano pafupi ndi nsembe yanu pamene ine ndikukakumana ndi Mulungu cha uko.”
And he said unto Balak, Place thyself here by thy burnt-offering, while I will repair to yonder place.
16 Yehova anakumana ndi Balaamu ndipo anamuyankhula kuti, “Bwerera kwa Balaki ndipo ukamuwuze uthenga uwu.”
And the Lord met Bil'am, and put a word in his mouth, and said, Return unto Balak, and thus shalt thou speak.
17 Ndipo anapita kwa iye ndipo anamupeza atayimirira pafupi ndi nsembe yake pamodzi ndi akuluakulu a ku Mowabu. Balaki anafunsa Balaamu kuti, “Yehova wayankhula chiyani?”
And he came to him, and, behold, he was standing by his burnt-offering, and the princes of Moab with him; and Balak said unto him: What hath the Lord spoken?
18 Pamenepo Balaamu ananena uthenga wake: “Nyamuka Balaki ndipo tamvera; Undimvere iwe mwana wa Zipori.
And he took up his parable, and said, Rise up, Balak, and hear; bend hither thy ear unto me, son of Zippor!
19 Mulungu si munthu kuti aname, kapena mwana wa munthu kuti asinthe maganizo ake. Kodi amayankhula koma osachita? Kodi amalonjeza koma osakwaniritsa?
God is not a man, that he should lie; nor a son of man, that he should repent: hath he said, and shall he not do it? and hath he spoken, and shall he not fulfill it?
20 Wandilamula kuti ndidalitse, Iyeyo wadalitsa ndipo sindingasinthe.
Behold, to bless I have received [the word]; and he hath blessed, and I cannot reverse it.
21 “Palibe kuwukira kulikonse kumene wakuona mwa Yakobo, sanaone chovuta mu Israeli. Yehova Mulungu wawo ali nawo: mfuwu wa mfumu uli pakati pawo.
He hath not beheld any wrong in Jacob, nor hath he seen perverseness in Israel: the Lord his God is with him, and the glory of the king dwelleth among him.
22 Mulungu wowatulutsa mʼdziko la Igupto, ali ndi mphamvu ngati za njati.
God, who brought them out of Egypt, is to them like the heights of the reem.
23 Palibe matsenga amene angalimbane ndi Yakobo, palibe mawula amene angalimbane ndi Israeli. Tsopano za Yakobo ndi Israeli adzanena kuti, ‘Onani zimene Mulungu wachita!’
For there is no enchantment in Jacob, nor is there any divination in Israel: at the proper time shall it be said to Jacob and to Israel, what God doth work.
24 Taonani, anthu anyamuka ngati mkango waukazi; adzuka okha ngati mkango waumuna umene supuma mpaka utadya nyama imene wagwira ndi kumwa magazi a nyama yogwidwayo.”
Behold, it is a people, that shall rise up as a lioness, and as a lion shall it raise itself: it will not lie down until it have eaten the prey, and have drunk the blood of the slain.
25 Ndipo Balaki anati kwa Balaamu, “Usawatemberere ndi pangʼono pomwe kapena kuwadalitsa!
And Balak said unto Bil'am, Neither shalt thou denounce them, nor shalt thou any wise bless them.
26 “Balaamu anayankha Balaki kuti, ‘Kodi sindinakuwuzeni kuti ndiyenera kuchita zimene Yehova wanena?’”
But Bil'am answered and said unto Balak, Have I not spoken unto thee, saying, all that the Lord will speak, that must I do.
27 Kenaka Balaki anati kwa Balaamu, “Bwera ndikutengere ku malo ena. Mwina chidzamukondweretsa Mulungu kuti uwatemberere kumeneko mʼmalo mwanga.”
And Balak said unto Bil'am, Come, I pray thee, I will take thee unto another place, peradventure it may be pleasing in the eyes of God that thou mayest denounce them for me from there.
28 Ndipo Balaki anamutengera Balaamu pamwamba pa Peori, poyangʼanana ndi chipululu.
And Balak took Bil'am unto the top of Peor, that looketh toward the desert.
29 Balaamu anati kwa Balaki, “Mundimangire maguwa ansembe asanu ndi awiri pano ndipo mundikonzere ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri.”
And Bil'am said unto Balak, Build me here seven altars, and prepare me here seven bullocks and seven rams.
30 Balaki anachita monga Balaamu ananenera ndipo anapereka nsembe ngʼombe imodzi yayimuna ndi nkhosa imodzi yayimuna pa guwa lililonse.
And Balak did as Bil'am had said, and he offered a bullock and a ram on every altar.

< Numeri 23 >