< Numeri 22 >

1 Aisraeli anayenda kupita ku zigwa za Mowabu nakamanga misasa yawo tsidya lina la Yorodani moyangʼanana ndi Yeriko.
and to set out son: descendant/people Israel and to camp in/on/with Plains (of Moab) (Plains of) Moab from side: beyond to/for Jordan Jericho
2 Tsono Balaki mwana wa Zipori anaona zonse zimene Aisraeli anachitira Aamori,
and to see: see Balak son: child Zippor [obj] all which to make: do Israel to/for Amorite
3 ndipo Amowabu anaopa anthuwo chifukwa analipo ambiri. Amowabuwo anachita mantha kwambiri mpaka ananjenjemera chifukwa cha Aisraeli.
and to dread Moab from face: because [the] people much for many he/she/it and to loathe Moab from face: because son: descendant/people Israel
4 Iwo anati kwa akuluakulu a ku Midiyani, “Gulu ili lidzabudula zonse zimene zatizungulira monga momwe ngʼombe yothena imathera udzu wa ku tchire.” Tsono Balaki mwana wa Zipori, yemwe anali mfumu ya Mowabu pa nthawi imeneyo,
and to say Moab to(wards) old: elder Midian now to lick [the] assembly [obj] all around us like/as to lick [the] cattle [obj] green [the] land: country and Balak son: child Zippor king to/for Moab in/on/with time [the] he/she/it
5 anatumiza amithenga kwa Balaamu mwana wa Beori, yemwe anali ku Petori, pafupi ndi mtsinje, mʼdziko la kwawo kuti akamuyitane. Balaki anati: “Taonani, anthu ochokera ku Igupto abwera, adzaza dziko lonse ndipo akufuna kuchita nane nkhondo.
and to send: depart messenger to(wards) Balaam son: child Beor Pethor [to] which upon [the] River land: country/planet son: descendant/people people his to/for to call: call to to/for him to/for to say behold people to come out: come from Egypt behold to cover [obj] eye: before(the eyes) [the] land: country/planet and he/she/it to dwell from opposite me
6 Tsopano bwera, utemberere anthu amenewa chifukwa ndi amphamvu kwambiri kuposa ine. Mwina ndingadzawagonjetse ndi kuwatulutsira kunja kwa dzikoli chifukwa ndikudziwa kuti amene umawadalitsa amadalitsika, ndipo amene umawatemberera amatembereredwa.”
and now to go: come! [emph?] please to curse [emph?] to/for me [obj] [the] people [the] this for mighty he/she/it from me perhaps be able to smite in/on/with him and to drive out: drive out him from [the] land: country/planet for to know [obj] which to bless to bless and which to curse to curse
7 Akuluakulu a Mowabu ndi akuluakulu a Midiyani ananyamuka atatenga ndalama zokalipirira mawula. Atafika kwa Balaamu, anamuwuza zomwe Balaki ananena.
and to go: went old: elder Moab and old: elder Midian and divination in/on/with hand: power their and to come (in): come to(wards) Balaam and to speak: speak to(wards) him word Balak
8 Balaamu anawawuza kuti, “Mugone konkuno usiku uno, ndipo ndikuyankhani zomwe Yehova andiwuze.” Choncho akuluakulu a Amowabu anagona kwa Balaamu.
and to say to(wards) them to lodge here [the] night and to return: return [obj] you word like/as as which to speak: speak LORD to(wards) me and to dwell ruler Moab with Balaam
9 Mulungu anabwera kwa Balaamu namufunsa kuti, “Kodi anthu ali ndi iwewa ndani?”
and to come (in): come God to(wards) Balaam and to say who? [the] human [the] these with you
10 Balaamu anayankha Mulungu kuti, “Balaki mwana wa Zipori, mfumu ya Mowabu, ananditumizira uthenga uwu:
and to say Balaam to(wards) [the] God Balak son: child Zippor king Moab to send: depart to(wards) me
11 ‘Taonani, anthu amene achokera ku dziko la Igupto adzaza dziko lonse. Tsopano bwera udzawatemberere mʼmalo mwanga. Mwina ndidzatha kumenyana nawo ndi kuwatulutsa.’”
behold [the] people [the] to come out: come from Egypt and to cover [obj] eye: before(the eyes) [the] land: country/planet now to go: come! [emph?] to curse [emph?] to/for me [obj] him perhaps be able to/for to fight in/on/with him and to drive out: drive out him
12 Koma Mulungu anawuza Balaamu kuti, “Usapite nawo. Usawatemberere anthu amenewo chifukwa ndi odalitsika.”
and to say God to(wards) Balaam not to go: went with them not to curse [obj] [the] people for to bless he/she/it
13 Mmawa mwake Balaamu anadzuka ndi kuwuza akuluakulu a Balaki aja kuti, “Bwererani ku dziko la kwanu chifukwa Yehova sanandilole kuti ndipite nanu.”
and to arise: rise Balaam in/on/with morning and to say to(wards) ruler Balak to go: went to(wards) land: country/planet your for to refuse LORD to/for to give: allow me to/for to go: went with you
14 Kotero akuluakulu a Mowabu anabwerera kwa Balaki ndi kukanena kuti, “Balaamu wakana kubwera nafe.”
and to arise: rise ruler Moab and to come (in): come to(wards) Balak and to say to refuse Balaam to go: come with us
15 Kenaka Balaki anatumanso akuluakulu ena ambiri ndi olemekezeka kwambiri kuposa oyamba aja ndipo
and to add: again still Balak to send: depart ruler many and to honor: honour from these
16 anafika kwa Balaamu nati; “Zomwe Balaki mwana wa Zipori akunena ndi izi: ‘Usalole kuti china chilichonse chikulepheretse kubwera kwa ine,
and to come (in): come to(wards) Balaam and to say to/for him thus to say Balak son: child Zippor not please to withhold from to go: come to(wards) me
17 chifukwa ndidzakulipira bwino kwambiri ndipo ndidzakuchitira chilichonse chimene unganene. Bwera ndipo uwatemberere anthu amenewa mʼmalo mwanga.’”
for to honor: honour to honor: honour you much and all which to say to(wards) me to make: do and to go: come! [emph?] please to curse [emph?] to/for me [obj] [the] people [the] this
18 Koma Balaamu anayankha atumiki a Balaki kuti, “Ngakhale Balaki atandipatsa nyumba yaufumu yodzaza ndi siliva ndi golide sindingachite chilichonse chachikulu kapena chachingʼono kuposa kuchita lamulo la Yehova Mulungu wanga.
and to answer Balaam and to say to(wards) servant/slave Balak if to give: give to/for me Balak fullness house: home his silver: money and gold not be able to/for to pass: trespass [obj] lip: word LORD God my to/for to make: do small or great: large
19 Tsopano mukhale kuno usiku uno monga ena anachitira, ndidzaona chimene Yehova adzandiwuza.”
and now to dwell please in/on/with this also you(m. p.) [the] night and to know what? to add LORD to speak: speak with me
20 Usiku umenewo Mulungu anabwera kwa Balaamu ndipo anati, “Popeza anthu awa abwera kudzakuyitana, nyamuka, pita nawo koma ukachite zokhazo zimene ndikuwuze.”
and to come (in): come God to(wards) Balaam night and to say to/for him if to/for to call: call to to/for you to come (in): come [the] human to arise: rise to go: went with them and surely [obj] [the] word which to speak: speak to(wards) you [obj] him to make: do
21 Balaamu anadzuka mmawa, namanga bulu wake wamkazi ndipo anapita ndi akuluakulu a Mowabu.
and to arise: rise Balaam in/on/with morning and to saddle/tie [obj] she-ass his and to go: went with ruler Moab
22 Koma Mulungu anakwiya kwambiri pamene ankapita ndipo mngelo wa Yehova anayima pa njira kutsutsana naye. Balaamu anakwera bulu wake wamkazi ndipo antchito ake awiri anali naye.
and to be incensed face: anger God for to go: went he/she/it and to stand messenger: angel LORD in/on/with way: journey to/for Satan to/for him and he/she/it to ride upon she-ass his and two youth his with him
23 Pamene buluyo anaona mngelo wa Yehova atayima pa njira ndi lupanga mʼmanja mwake, anapatukira kumbali kwa msewu napita kutchire. Balaamu anamumenya kuti abwerere mu msewu.
and to see: see [the] she-ass [obj] messenger: angel LORD to stand in/on/with way: road and sword his to draw in/on/with hand: power his and to stretch [the] she-ass from [the] way: road and to go: went in/on/with land: country and to smite Balaam [obj] [the] she-ass to/for to stretch her [the] way: road
24 Kenaka mngelo wa Yehova anayima mʼkanjira kakangʼono pakati pa minda iwiri ya mpesa yokhala ndi makoma mbali zonse
and to stand: stand messenger: angel LORD in/on/with passage [the] vineyard wall from this and wall from this
25 Bulu uja ataona mngelo wa Yehova anadzipanikiza ku khoma, kukhukhuza phazi la Balaamu kukhomako. Ndipo pomwepo Balaamu anamenya buluyo kachiwiri.
and to see: see [the] she-ass [obj] messenger: angel LORD and to oppress to(wards) [the] wall and to oppress [obj] foot Balaam to(wards) [the] wall and to add: again to/for to smite her
26 Kenaka mngelo wa Yehova anapita patsogolo ndi kuyima pamalo opanikizika pomwe panalibe poti nʼkutembenukira ku dzanja lamanja kapena lamanzere.
and to add messenger: angel LORD to pass and to stand: stand in/on/with place narrow which nothing way: journey to/for to stretch right and left
27 Buluyo ataonanso mngelo wa Yehova uja, anagona pansi Balaamu ali pa msana, ndipo iye anakwiya ndi kumumenya ndi ndodo yake.
and to see: see [the] she-ass [obj] messenger: angel LORD and to stretch underneath: under Balaam and to be incensed face: anger Balaam and to smite [obj] [the] she-ass in/on/with rod
28 Pamenepo Yehova anayankhulitsa bulu uja, ndipo buluyo anati kwa Balaamu, “Ndakuchitirani chiyani kuti mundimenye katatuka?”
and to open LORD [obj] lip [the] she-ass and to say to/for Balaam what? to make: do to/for you for to smite me this three foot
29 Balaamu anati kwa buluyo, “Wandipusitsa, ndikanakhala ndi lupanga mʼmanja mwanga, ndikanakupha pomwe pano.”
and to say Balaam to/for she-ass for to abuse in/on/with me if there sword in/on/with hand my for now to kill you
30 Buluyo anati kwa Balaamu, “Kodi sindine bulu wanu, amene mumakwera nthawi zonse kufikira lero? Kodi ndinakuchitiranipo zoterezi?” Iye anati “Ayi.”
and to say [the] she-ass to(wards) Balaam not I she-ass your which to ride upon me from still your till [the] day [the] this be useful be useful to/for to make: do to/for you thus and to say not
31 Pomwepo Yehova anatsekula maso Balaamu ndipo anaona mngelo wa Yehovayo ali chiyimire pa njira ndi lupanga losolola. Tsono iye anawerama nalambira pamaso pake.
and to reveal: uncover LORD [obj] eye Balaam and to see: see [obj] messenger: angel LORD to stand in/on/with way: journey and sword his to draw in/on/with hand his and to bow and to bow to/for face his
32 Mngelo wa Yehova anamufunsa kuti, “Chifukwa chiyani wamenya bulu wako katatu? Taona, Ine ndabwera kudzakutsutsa chifukwa ulendo wakowu ndi woyipa pamaso panga.
and to say to(wards) him messenger: angel LORD upon what? to smite [obj] she-ass your this three foot behold I to come out: come to/for Satan for to push [the] way: conduct to/for before me
33 Buluyu anandiona ndi kupatuka katatu aka. Akanakhala kuti sanapatuke, ndikanakupha tsopano, koma buluyu nʼkanamusiya ndi moyo.”
and to see: see me [the] she-ass and to stretch to/for face: before my this three foot perhaps to stretch from face: before my for now also [obj] you to kill and [obj] her to live
34 Balaamu anati kwa mngelo wa Yehova uja, “Ndachimwa. Sindinadziwe kuti munayima pa njira kunditsutsa. Tsopano ngati Inu simunakondwe, ineyo ndibwerera.”
and to say Balaam to(wards) messenger: angel LORD to sin for not to know for you(m. s.) to stand to/for to encounter: toward me in/on/with way: road and now if be evil in/on/with eye: seeing your to return: return to/for me
35 Mngelo wa Yehova anati kwa Balaamu, “Pita ndi anthuwa koma ukayankhule zokhazo zimene ndikakuwuze.” Choncho Balaamu anapita ndi akuluakulu a Balaki.
and to say messenger: angel LORD to(wards) Balaam to go: went with [the] human and end [obj] [the] word which to speak: speak to(wards) you [obj] him to speak: speak and to go: went Balaam with ruler Balak
36 Balaki atamva kuti Balaamu akubwera, anapita kukakumana naye ku mzinda wa Mowabu umene unali mʼmalire a Arinoni, mʼmphepete mwa dziko lake.
and to hear: hear Balak for to come (in): come Balaam and to come out: come to/for to encounter: meet him to(wards) city Moab which upon border: boundary Arnon which in/on/with end [the] border: boundary
37 Balaki anati kwa Balaamu, “Kodi sindinakutumizire uthenga woti ubwere msanga? Chifukwa chiyani sunabwere kwa ine? Kodi sindingathe kukulipira mokwanira?”
and to say Balak to(wards) Balaam not to send: depart to send: depart to(wards) you to/for to call: call to to/for you to/for what? not to go: come to(wards) me truly not be able to honor: honour you
38 Balaamu anayankha Balaki kuti, “Taonani, ndabwera kwa inu lero, kodi ine ndili ndi mphamvu zoti nʼkuyankhula chilichonse? Inetu ndiyenera kuyankhula zokhazo zimene Mulungu wandiwuza.”
and to say Balaam to(wards) Balak behold to come (in): come to(wards) you now be able be able to speak: speak anything [the] word which to set: put God in/on/with lip my [obj] him to speak: speak
39 Pamenepo Balaamu anapita pamodzi ndi Balaki ku Kiriati-Huzoti.
and to go: went Balaam with Balak and to come (in): come Kiriath-huzoth Kiriath-huzoth
40 Balaki anapereka nsembe ngʼombe ndi nkhosa, ndipo anapereka zina kwa Balaamu ndi kwa akuluakulu omwe anali naye.
and to sacrifice Balak cattle and flock and to send: depart to/for Balaam and to/for ruler which with him
41 Mmawa mwake Balaki anatenga Balaamu napita limodzi ku Bamoti Baala, ndipo kumeneko anakaonako gulu lina la Aisraeliwo.
and to be in/on/with morning and to take: take Balak [obj] Balaam and to ascend: establish him Bamoth (Bamoth)-baal and to see: see from there end [the] people

< Numeri 22 >