< Numeri 22 >

1 Aisraeli anayenda kupita ku zigwa za Mowabu nakamanga misasa yawo tsidya lina la Yorodani moyangʼanana ndi Yeriko.
Derefter brød Israeliterne op derfra og slog Lejer paa Moabs Sletter hinsides Jordan over for Jeriko.
2 Tsono Balaki mwana wa Zipori anaona zonse zimene Aisraeli anachitira Aamori,
Da Balak, Zippors Søn, saa alt, hvad Israel havde gjort ved Amoriterne,
3 ndipo Amowabu anaopa anthuwo chifukwa analipo ambiri. Amowabuwo anachita mantha kwambiri mpaka ananjenjemera chifukwa cha Aisraeli.
grebes Moab af Rædsel for Folket, fordi det var saa talrigt, og Moab gruede for Israeliterne.
4 Iwo anati kwa akuluakulu a ku Midiyani, “Gulu ili lidzabudula zonse zimene zatizungulira monga momwe ngʼombe yothena imathera udzu wa ku tchire.” Tsono Balaki mwana wa Zipori, yemwe anali mfumu ya Mowabu pa nthawi imeneyo,
Da sagde Moab til Midjaniternes Ældste: »Nu vil denne Menneskemasse opæde alt, hvad der er rundt omkring os, som Okserne opæder Græsset paa Marken!« Paa den Tid var Balak, Zippors Søn, Konge over Moab.
5 anatumiza amithenga kwa Balaamu mwana wa Beori, yemwe anali ku Petori, pafupi ndi mtsinje, mʼdziko la kwawo kuti akamuyitane. Balaki anati: “Taonani, anthu ochokera ku Igupto abwera, adzaza dziko lonse ndipo akufuna kuchita nane nkhondo.
Han sendte nu Sendebud til Bileam, Beors Søn, i Petor, der ligger ved Floden, til Ammoniternes Land, og bad ham komme til sig, idet han lod sige: »Se, et Folk er udvandret fra Ægypten; se, det har oversvømmet Landet og slaaet sig ned lige over for mig.
6 Tsopano bwera, utemberere anthu amenewa chifukwa ndi amphamvu kwambiri kuposa ine. Mwina ndingadzawagonjetse ndi kuwatulutsira kunja kwa dzikoli chifukwa ndikudziwa kuti amene umawadalitsa amadalitsika, ndipo amene umawatemberera amatembereredwa.”
Kom nu og forband mig det Folk, thi det er mig for mægtigt: maaske jeg da kan slaa det og jage det ud af Landet. Thi jeg ved, at den, du velsigner, er velsignet, og den, du forbander, forbandet!«
7 Akuluakulu a Mowabu ndi akuluakulu a Midiyani ananyamuka atatenga ndalama zokalipirira mawula. Atafika kwa Balaamu, anamuwuza zomwe Balaki ananena.
Da gav Moabs og Midjans Ældste sig paa Vej, forsynede med Spaamandsløn, og da de kom til Bileam, overbragte de ham Balaks Ord.
8 Balaamu anawawuza kuti, “Mugone konkuno usiku uno, ndipo ndikuyankhani zomwe Yehova andiwuze.” Choncho akuluakulu a Amowabu anagona kwa Balaamu.
Han sagde til dem: »Bliv her Natten over, saa skal jeg give eder Svar, efter som HERREN vil tale til mig!« Moabs Høvdinger blev da hos Bileam.
9 Mulungu anabwera kwa Balaamu namufunsa kuti, “Kodi anthu ali ndi iwewa ndani?”
Men Gud kom til Bileam og spurgte: »Hvem er de Mænd, som er hos dig?«
10 Balaamu anayankha Mulungu kuti, “Balaki mwana wa Zipori, mfumu ya Mowabu, ananditumizira uthenga uwu:
Men Bileam svarede Gud: »Zippors Søn, Kong Balak af Moab, har sendt mig det Bud:
11 ‘Taonani, anthu amene achokera ku dziko la Igupto adzaza dziko lonse. Tsopano bwera udzawatemberere mʼmalo mwanga. Mwina ndidzatha kumenyana nawo ndi kuwatulutsa.’”
Se, et Folk er udvandret fra Ægypten og har oversvømmet Landet! Kom nu og forband mig det, maaske jeg da kan overvinde det og jage det bort!«
12 Koma Mulungu anawuza Balaamu kuti, “Usapite nawo. Usawatemberere anthu amenewo chifukwa ndi odalitsika.”
Men Gud sagde til Bileam: »Du maa ikke gaa med dem, du maa ikke forbande det Folk, thi det er velsignet!«
13 Mmawa mwake Balaamu anadzuka ndi kuwuza akuluakulu a Balaki aja kuti, “Bwererani ku dziko la kwanu chifukwa Yehova sanandilole kuti ndipite nanu.”
Næste Morgen stod Bileam op og sagde til Balaks Høvdinger: »Vend tilbage til eders Land, thi HERREN vægrer sig ved at give mig Tilladelse til at følge med eder!«
14 Kotero akuluakulu a Mowabu anabwerera kwa Balaki ndi kukanena kuti, “Balaamu wakana kubwera nafe.”
Da brød Moabs Høvdinger op, og de kom til Balak og meldte: »Bileam vægrede sig ved at følge med os!«
15 Kenaka Balaki anatumanso akuluakulu ena ambiri ndi olemekezeka kwambiri kuposa oyamba aja ndipo
Men Balak sendte paa ny Høvdinger af Sted, flere og mere ansete end de forrige;
16 anafika kwa Balaamu nati; “Zomwe Balaki mwana wa Zipori akunena ndi izi: ‘Usalole kuti china chilichonse chikulepheretse kubwera kwa ine,
og de kom til Bileam og sagde til ham: »Saaledes siger Balak, Zippors Søn: Undslaa dig ikke for at komme til mig!
17 chifukwa ndidzakulipira bwino kwambiri ndipo ndidzakuchitira chilichonse chimene unganene. Bwera ndipo uwatemberere anthu amenewa mʼmalo mwanga.’”
Jeg vil lønne dig rigeligt og gøre alt, hvad du kræver af mig. Kom nu og forband mig det Folk!«
18 Koma Balaamu anayankha atumiki a Balaki kuti, “Ngakhale Balaki atandipatsa nyumba yaufumu yodzaza ndi siliva ndi golide sindingachite chilichonse chachikulu kapena chachingʼono kuposa kuchita lamulo la Yehova Mulungu wanga.
Men Bileam svarede Balaks Folk: »Om Balak saa giver mig alt det Sølv og Guld, han har i sit Hus, formaar jeg dog hverken at gøre lidt eller meget imod HERREN min Guds Befaling;
19 Tsopano mukhale kuno usiku uno monga ena anachitira, ndidzaona chimene Yehova adzandiwuza.”
bliv derfor ogsaa I her Natten over, for at jeg kan faa at vide, hvad HERREN yderligere vil tale til mig!«
20 Usiku umenewo Mulungu anabwera kwa Balaamu ndipo anati, “Popeza anthu awa abwera kudzakuyitana, nyamuka, pita nawo koma ukachite zokhazo zimene ndikuwuze.”
Da kom Gud om Natten til Bileam og sagde til ham: »Er disse Mænd kommet til dig for at hente dig, saa følg med dem; men du maa ikke gøre andet, end hvad jeg siger dig!«
21 Balaamu anadzuka mmawa, namanga bulu wake wamkazi ndipo anapita ndi akuluakulu a Mowabu.
Saa stod Bileam op næste Morgen og sadlede sit Æsel og fulgte med Moabs Høvdinger.
22 Koma Mulungu anakwiya kwambiri pamene ankapita ndipo mngelo wa Yehova anayima pa njira kutsutsana naye. Balaamu anakwera bulu wake wamkazi ndipo antchito ake awiri anali naye.
Men Guds Vrede blussede op, fordi han fulgte med, og HERRENS Engel stillede sig paa Vejen for at staa ham imod, da han kom ridende paa sit Æsel fulgt af sine to Tjenere.
23 Pamene buluyo anaona mngelo wa Yehova atayima pa njira ndi lupanga mʼmanja mwake, anapatukira kumbali kwa msewu napita kutchire. Balaamu anamumenya kuti abwerere mu msewu.
Da nu Æselet saa HERRENS Engel staa paa Vejen med draget Sværd i Haanden, veg det ud fra Vejen og gik ind paa Marken; men Bileam slog Æselet for at tvinge det tilbage paa Vejen.
24 Kenaka mngelo wa Yehova anayima mʼkanjira kakangʼono pakati pa minda iwiri ya mpesa yokhala ndi makoma mbali zonse
Da stillede HERRENS Engel sig i Hulvejen mellem Vingaardene, hvor der var Mure paa begge Sider;
25 Bulu uja ataona mngelo wa Yehova anadzipanikiza ku khoma, kukhukhuza phazi la Balaamu kukhomako. Ndipo pomwepo Balaamu anamenya buluyo kachiwiri.
og da Æselet saa HERRENS Engel, trykkede det sig op til Muren, saa det trykkede Bileams Fod op mod Muren, og han gav sig atter til at slaa det.
26 Kenaka mngelo wa Yehova anapita patsogolo ndi kuyima pamalo opanikizika pomwe panalibe poti nʼkutembenukira ku dzanja lamanja kapena lamanzere.
HERRENS Engel gik nu længere frem og stillede sig i en Snævring, hvor det ikke var muligt at komme til Siden, hverken til højre eller venstre.
27 Buluyo ataonanso mngelo wa Yehova uja, anagona pansi Balaamu ali pa msana, ndipo iye anakwiya ndi kumumenya ndi ndodo yake.
Da Æselet saa HERRENS Engel, lagde det sig ned med Bileam. Da blussede Bileams Vrede op, og han gav sig til at slaa Æselet med Stokken.
28 Pamenepo Yehova anayankhulitsa bulu uja, ndipo buluyo anati kwa Balaamu, “Ndakuchitirani chiyani kuti mundimenye katatuka?”
Men HERREN aabnede Æselets Mund, og det sagde til Bileam: »Hvad har jeg gjort dig, siden du nu har slaaet mig tre Gange?«
29 Balaamu anati kwa buluyo, “Wandipusitsa, ndikanakhala ndi lupanga mʼmanja mwanga, ndikanakupha pomwe pano.”
Bileam svarede Æselet: »Du har drillet mig; havde jeg haft et Sværd i Haanden, havde jeg slaaet dig ihjel!«
30 Buluyo anati kwa Balaamu, “Kodi sindine bulu wanu, amene mumakwera nthawi zonse kufikira lero? Kodi ndinakuchitiranipo zoterezi?” Iye anati “Ayi.”
Men Æselet sagde til Bileam: »Er jeg ikke dit eget Æsel, som du har redet al din Tid indtil i Dag? Har jeg ellers haft for Vane at bære mig saaledes ad over for dig?« Han svarede: »Nej!«
31 Pomwepo Yehova anatsekula maso Balaamu ndipo anaona mngelo wa Yehovayo ali chiyimire pa njira ndi lupanga losolola. Tsono iye anawerama nalambira pamaso pake.
Da aabnede HERREN Bileams Øjne, og han saa HERRENS Engel staa paa Vejen med draget Sværd i Haanden; og han bøjede sig og kastede sig ned paa sit Ansigt.
32 Mngelo wa Yehova anamufunsa kuti, “Chifukwa chiyani wamenya bulu wako katatu? Taona, Ine ndabwera kudzakutsutsa chifukwa ulendo wakowu ndi woyipa pamaso panga.
Men HERRENS Engel sagde til ham: »Hvorfor slog du dit Æsel de tre Gange? Se, jeg er gaaet ud for at staa dig imod, thi du handlede overilet ved at rejse imod min Vilje.
33 Buluyu anandiona ndi kupatuka katatu aka. Akanakhala kuti sanapatuke, ndikanakupha tsopano, koma buluyu nʼkanamusiya ndi moyo.”
Æselet saa mig og veg tre Gange til Side for mig; og var det ikke veget til Side for mig, havde jeg slaaet dig ihjel, men skaanet dets Liv!«
34 Balaamu anati kwa mngelo wa Yehova uja, “Ndachimwa. Sindinadziwe kuti munayima pa njira kunditsutsa. Tsopano ngati Inu simunakondwe, ineyo ndibwerera.”
Da sagde Bileam til HERRENS Engel: »Jeg har syndet, jeg vidste jo ikke, at det var dig, der traadte i Vejen for mig. Men hvis det er dig imod, vil jeg atter vende tilbage.«
35 Mngelo wa Yehova anati kwa Balaamu, “Pita ndi anthuwa koma ukayankhule zokhazo zimene ndikakuwuze.” Choncho Balaamu anapita ndi akuluakulu a Balaki.
HERRENS Engel sagde til Bileam: »Følg blot med disse Mænd, men du maa kun sige de Ord, jeg siger dig!« Saa fulgte Bileam med Balaks Høvdinger.
36 Balaki atamva kuti Balaamu akubwera, anapita kukakumana naye ku mzinda wa Mowabu umene unali mʼmalire a Arinoni, mʼmphepete mwa dziko lake.
Da Balak nu hørte, at Bileam var undervejs, gik han ham i Møde til Ar Moab ved den Grænse, Arnon danner, den yderste Grænse.
37 Balaki anati kwa Balaamu, “Kodi sindinakutumizire uthenga woti ubwere msanga? Chifukwa chiyani sunabwere kwa ine? Kodi sindingathe kukulipira mokwanira?”
Og Balak sagde til Bileam: »Sendte jeg dig ikke Bud og bad dig komme? Hvorfor kom du da ikke til mig? Skulde jeg virkelig være ude af Stand til at lønne dig?«
38 Balaamu anayankha Balaki kuti, “Taonani, ndabwera kwa inu lero, kodi ine ndili ndi mphamvu zoti nʼkuyankhula chilichonse? Inetu ndiyenera kuyankhula zokhazo zimene Mulungu wandiwuza.”
Bileam sagde til Balak: »Se, nu er jeg kommet til dig; men mon det staar i min Magt at sige noget? Det Ord, Gud lægger mig i Munden, maa jeg tale!«
39 Pamenepo Balaamu anapita pamodzi ndi Balaki ku Kiriati-Huzoti.
Da fulgte Bileam med Balak, og de kom til Kirjat-Huzot.
40 Balaki anapereka nsembe ngʼombe ndi nkhosa, ndipo anapereka zina kwa Balaamu ndi kwa akuluakulu omwe anali naye.
Balak ofrede her Hornkvæg og Smaakvæg og sendte noget til Bileam og Høvdingerne, der var hos ham.
41 Mmawa mwake Balaki anatenga Balaamu napita limodzi ku Bamoti Baala, ndipo kumeneko anakaonako gulu lina la Aisraeliwo.
Næste Morgen tog Balak Bileam med sig og førte ham op til Bamot-Ba'al, hvorfra han kunde øjne den yderste Del af Folket.

< Numeri 22 >