< Numeri 21 >

1 Mfumu ya Akanaani ya ku Aradi, imene inkakhala ku Negevi, itamva kuti Aisraeli akubwera kudzera msewu wopita ku Atarimu, inachita nkhondo ndi Aisraeli nigwira ena mwa iwo.
پادشاه کنعانی سرزمین عراد (واقع در نگب کنعان) وقتی شنید اسرائیلی‌ها از راه اتاریم می‌آیند، سپاه خود را بسیج نموده، به قوم اسرائیل حمله کرد و عده‌ای از ایشان را به اسیری گرفت.
2 Ndipo Israeli anachita lonjezo ili kwa Yehova: “Mukapereka anthu awa mʼdzanja lathu ife tidzawonongeratu mizinda yawo.”
پس قوم اسرائیل به خداوند نذر کردند که اگر خداوند ایشان را یاری دهد تا بر پادشاه عراد و مردمش پیروز شوند، تمامی شهرهای آن مرزوبوم را به کلی نابود کنند.
3 Yehova anamva pempho la Aisraeli ndipo anapereka Akanaaniwo kwa iwo. Anawawononga pamodzi ndi mizinda yawo. Kotero malowo anatchedwa Horima.
خداوند دعای ایشان را شنیده کنعانی‌ها را شکست داد، و اسرائیلی‌ها آنان و شهرهای ایشان را به کلی نابود کردند. از آن پس، آن ناحیه «حرمه» (یعنی «نابودی») نامیده شد.
4 Aisraeli anayenda kuchokera ku phiri la Hori kudzera njira ya ku Nyanja Yofiira kuzungulira dziko la Edomu. Koma anthu anataya mtima mʼnjiramo
سپس قوم اسرائیل از کوه هور رهسپار شدند تا از راهی که به دریای سرخ ختم می‌شد سرزمین ادوم را دور بزنند. اما قوم اسرائیل در این سفر طولانی به ستوه آمدند
5 ndipo anayankhula motsutsana ndi Mulungu ndi Mose, nati, “Chifukwa chiyani munatitulutsa kuchoka mʼdziko la Igupto kuti tidzafere mʼchipululu muno? Kuno kulibe chakudya, kulibe madzi ndipo chakudya cha chabechabechi tatopa nacho.”
و به خدا و موسی اعتراض کرده گفتند: «چرا ما را از مصر بیرون آوردید تا در این بیابان بمیریم؟ در اینجا نه چیزی برای خوردن هست و نه چیزی برای نوشیدن! ما از خوردن این مَنّای بی‌مزه خسته شده‌ایم!»
6 Choncho Yehova anatumiza njoka zaululu pakati pawo. Zinaluma anthu ndipo Aisraeli ambiri anafa.
پس خداوند مارهای سمی به میان ایشان فرستاد و مارها عدهٔ زیادی از ایشان را گزیده، هلاک کردند.
7 Anthuwo anabwera kwa Mose ndi kunena kuti, “Tachimwa chifukwa tayankhula motsutsana ndi Yehova komanso inu. Pempherani kwa Yehova kuti atichotsere njokazi.” Tsono Mose anapempherera anthuwo.
آنگاه قوم اسرائیل پیش موسی آمده، فریاد برآوردند: «ما گناه کرده‌ایم، چون بر ضد خداوند و بر ضد تو سخن گفته‌ایم. از خداوند درخواست کن تا این مارها را از ما دور کند.» موسی برای قوم دعا کرد.
8 Yehova anati kwa Mose, “Upange njoka yaululu ndipo uyipachike pa mtengo. Aliyense amene walumidwa akangoyangʼana njokayo adzakhala ndi moyo.”
خداوند به وی فرمود: «یک مار مفرغین شبیه یکی از این مارها بساز و آن را بر سر یک تیر بیاویز. هر مارگزیده‌ای که به آن نگاه کند، زنده خواهد ماند!»
9 Pamenepo Mose anapanga njoka yamkuwa ndi kuyipachika pa mtengo. Ndipo aliyense wolumidwa akayangʼana njoka yamkuwayo ankakhala ndi moyo.
پس موسی یک مار مفرغین درست کرد و آن را بر سر تیری آویخت. به محض اینکه مار گزیده‌ای به آن نگاه می‌کرد، شفا می‌یافت!
10 Aisraeli anayendabe nakamanga misasa yawo ku Oboti.
قوم اسرائیل به اوبوت کوچ کردند و در آنجا اردو زدند.
11 Kenaka anasamuka ku Oboti nakamanga misasa yawo ku Iye-Abarimu, mʼchipululu chimene chili kummawa kwa Mowabu, kotulukira dzuwa.
سپس از آنجا به عیی‌عباریم که در بیابان و در فاصلهٔ کمی از شرق موآب قرار داشت، رفتند.
12 Kuchoka kumeneko anayendabe nakamanga misasa yawo mʼchigwa cha Zeredi.
از آنجا به وادی زارد کوچ کرده، اردو زدند.
13 Anasamukanso kumeneko nakamanga moyandikana ndi Arinoni mʼdera limene lili mʼchipululu chimene chimafika mʼdziko la Aamori. Arinoni ndiwo malire a Mowabu ndi Aamori.
بعد به طرف شمال رود ارنون نزدیک مرزهای اموری‌ها نقل مکان کردند. (رود ارنون، خط مرزی بین موآبی‌ها و اموری‌هاست.
14 Nʼchifukwa chake Buku la Nkhondo za Yehova limati, “Mzinda wa Wahebu uli mu Sufa, mu zigwa za Arinoni,
در کتاب «جنگهای خداوند» به این امر اشاره شده که درهٔ رود ارنون و شهر واهیب
15 ku matsitso a zigwa amene afika mpaka ku Ari nakhudza malire a dziko la Mowabu.”
بین اموری‌ها و موآبی‌ها قرار دارند.)
16 Kuchokera kumeneko anapitirira mpaka ku Beeri, pa chitsime chomwe Yehova anawuza Mose kuti, “Sonkhanitsa anthu pamodzi ndipo ndidzawapatsa madzi.”
سپس قوم اسرائیل به «بئر» (یعنی «چاه») کوچ کردند. این همان جایی است که خداوند به موسی فرمود: «قوم را جمع کن و من به ایشان آب خواهم داد.»
17 Pamenepo Aisraeli anayimba nyimbo iyi: “Tulutsa madzi, chitsime iwe! Chiyimbireni nyimbo,
آنگاه قوم اسرائیل این سرود را خواندند: «ای چاه، بجوش آی! در وصف این چاه بسرایید! این است چاهی که رهبران آن را کندند، بله، بزرگان اسرائیل با عصاهایشان آن را کندند!» قوم اسرائیل از بیابان به مَتّانه کوچ کردند،
18 chitsime chomwe anakumba mafumu, chomwe anakumba anthu omveka, ndi ndodo zawo zaufumu ndi ndodo zawo zoyendera.” Kenaka anachoka ku chipululu ndi kupita ku Matana.
19 Kuchoka ku Matana anapita ku Nahalieli, kuchoka ku Nahalieli anapita ku Bamoti,
و از مَتّانه به نحلیئیل، و از نحلیئیل به باموت
20 ndipo atachoka ku Bamoti anapita ku chigwa cha dziko la Mowabu kudzera njira ya pamwamba pa phiri la Pisiga, moyangʼanana ndi Yesimoni.
و از باموت به دره‌ای که در موآب قرار دارد و مشرف به بیابان و کوه پیسگاه است.
21 Aisraeli anatumiza amithenga kwa Sihoni mfumu ya Aamori, kuti,
در این وقت قوم اسرائیل سفیرانی نزد سیحون، پادشاه اموری‌ها فرستادند.
22 “Tiloleni kuti tidutse mʼdziko mwanu. Sitidzapatukira mʼminda mwanu kapena mu mpesa wanu kapena kumwa madzi mʼchitsime chili chonse. Tidzayenda mu msewu waukulu wa mfumu mpaka titadutsa malire a dziko lanu.”
فرستادگان درخواست کرده گفتند: «اجازه دهید از سرزمین شما عبور کنیم. ما قول می‌دهیم از شاهراه برویم و تا زمانی که از مرزتان نگذشته‌ایم از راهی که در آن می‌رویم خارج نشویم. به مزرعه‌ها و تاکستانهای شما وارد نخواهیم شد و آب شما را نیز نخواهیم نوشید.»
23 Koma Sihoni sanalole kuti Aisraeli adutse mʼdziko mwake. Iye anasonkhanitsa pamodzi ankhondo ake onse kuti akamenyane ndi Aisraeli mʼchipululu. Atafika pa Yahazi anamenyana ndi Aisraeli.
ولی سیحون پادشاه موافقت نکرد. در عوض، او سپاه خود را در بیابان در مقابل قوم اسرائیل بسیج کرد و در ناحیهٔ یاهص با ایشان وارد جنگ شد.
24 Koma Aisraeli anamupha ndi kulanda dziko lake kuchokera ku Arinoni mpaka ku Yaboki, kulekezera mʼmalire a dziko la Aamoni, chifukwa malire a dziko la Aamoni anali otetezedwa.
در این جنگ، بنی‌اسرائیل آنها را از دم شمشیر گذراندند و سرزمینشان را از رود ارنون تا رود یبوق و تا مرز سرزمین بنی‌عمون تصرف کردند، اما نتوانستند جلوتر بروند، زیرا مرز بنی‌عمون مستحکم بود.
25 Ndipo Aisraeli analanda mizinda yonse ya Aamori, nakhalamo kuphatikizapo Hesiboni ndi midzi yake yozungulira.
به این ترتیب، قوم اسرائیل تمام شهرهای اموری‌ها منجمله شهر حِشبون و تمام روستاهای اطرافش را تصرف کردند و در آنها ساکن شدند.
26 Hesiboni unali mzinda wa Sihoni mfumu ya Aamori, yemwe anamenyana ndi mfumu yakale ya dziko la Mowabu. Lonselo linakhala dziko lake mpaka ku Arinoni.
حِشبون پایتخت سیحون پادشاه اموری‌ها بود. او پیش از آن، پادشاه قبلی موآب را شکست داده، تمام سرزمینش را تا به اَرنون به تصرف درآورده بود.
27 Nʼchifukwa chake alakatuli amati: “Bwerani ku Hesiboni, mzindawo umangidwenso; mzinda wa Sihoni ukhazikike.
از همین رو شعرا در مورد سیحون پادشاه چنین گفته‌اند: «به حشبون بیایید، بگذارید بنا شود، بگذارید شهر سیحون پادشاه بازسازی شود.
28 “Moto unabuka ku Hesiboni, malawi a moto kuchokera mu mzinda wa Sihoni. Unanyeketsa Ari mzinda wa ku Mowabu, nzika za ku malo okwera a Arinoni.
زیرا آتشی از حِشبون افروخته شده، و شعله‌ای از شهر سیحون. شهر عارِ موآب را سوزانده، و حاکمان بلندیهای ارنون را هلاک کرده.
29 Tsoka kwa iwe Mowabu! Mwawonongedwa inu anthu a ku Kemosi! Ana ake aamuna wawasandutsa ngati anthu othawathawa ndipo ana ake aakazi ngati akapolo, akapolo a Sihoni, mfumu ya Aamori.
وای بر تو ای موآب! تو هلاک شدی، ای قومی که کموش را می‌پرستید! کموش پسران خود را همچون فراریان تسلیم کرد، و دخترانش را به اسارت سیحون، پادشاه اموری‌ها فرستاد.
30 “Koma ife tawagonjetsa; Hesiboni wawonongedwa mʼnjira monse mpaka kufika ku Diboni. Tawaphwasula mpaka ku mzinda wa Nofa, mzinda womwe umafika ku Medeba.
اما ما آنها را هلاک کرده‌ایم از حشبون تا دیبون، و تا نوفح که نزدیک میدبا است.»
31 “Choncho Aisraeli anakhala mʼdziko la Aamori.”
بدین ترتیب قوم اسرائیل در سرزمین اموری‌ها ساکن شدند.
32 Mose atatumiza azondi ku Yazeri, Aisraeliwo analanda midzi yozungulira ndi kuthamangitsa Aamori omwe ankakhala kumeneko.
موسی افرادی به ناحیهٔ یعزیز فرستاد تا وضع آنجا را بررسی کنند. پس از آن، قوم اسرائیل به آن ناحیه حمله بردند و آن را با روستاهای اطرافش گرفتند و اموری‌ها را بیرون راندند.
33 Kenaka anabwerera, nadzera njira ya ku Basani. Choncho Ogi mfumu ya ku Basani ndi gulu lake lonse lankhondo anatuluka kukakumana nawo ndipo anamenyana nawo ku Ederi.
سپس بنی‌اسرائیل بازگشتند و راهی را که به باشان منتهی می‌شد در پیش گرفتند؛ اما عوج، پادشاه باشان، برای جنگ با آنها، با سپاه خود به ادرعی آمد.
34 Yehova anati kwa Mose, “Usachite naye mantha pakuti ndamupereka mʼmanja mwako pamodzi ndi gulu lake lonse lankhondo ndi dziko lake lomwe. Ndipo uchite kwa iye zimene unachita Sihoni mfumu ya Aamori, amene ankalamulira ku Hesiboni.”
خداوند به موسی فرمود: «از او نترس، زیرا او را با همۀ قوم و سرزمینش به دست تو تسلیم کرده‌ام. همان بلایی به سر عوج پادشاه می‌آید که در حشبون به سر سیحون، پادشاه اموری‌ها آمد.»
35 Choncho Aisraeli anapha Ogi pamodzi ndi ana ake aamuna ndi gulu lake lonse la nkhondo. Palibe ndi mmodzi yemwe amene anatsala wamoyo, ndipo analanda dziko lakelo.
پس قوم اسرائیل، عوجِ پادشاه را همراه با پسرانش و اهالی سرزمینش کشتند، به طوری که یکی از آنها هم زنده نماند. سپس قوم اسرائیل آن سرزمین را تصرف کردند.

< Numeri 21 >