< Numeri 21 >

1 Mfumu ya Akanaani ya ku Aradi, imene inkakhala ku Negevi, itamva kuti Aisraeli akubwera kudzera msewu wopita ku Atarimu, inachita nkhondo ndi Aisraeli nigwira ena mwa iwo.
A LOHE ae la ke alii o Arada ka Kanaana, e noho ana ma ke kukuluhema, e hele mai ana ka Iseraela ma ke ala e hiki ai i na wahi ona, alaila, kaua mai la ia i ka Iseraela, a lawe pio aku la i kekahi poe o lakou.
2 Ndipo Israeli anachita lonjezo ili kwa Yehova: “Mukapereka anthu awa mʼdzanja lathu ife tidzawonongeratu mizinda yawo.”
Hoohiki aku la ka Iseraela ia Iehova, i aku la, Ina paha e haawi mai oe i keia poe kanaka iloko o ko'u lima, alaila e luku loa aku no au i na kulanakauhale o lakou.
3 Yehova anamva pempho la Aisraeli ndipo anapereka Akanaaniwo kwa iwo. Anawawononga pamodzi ndi mizinda yawo. Kotero malowo anatchedwa Horima.
Hoolohe mai la o Iehova i ka leo o ka Iseraela, a hoolilo mai la i ka poe Kanaana: a luku loa aku la lakou ia lakou la, a me na kulanakauhale o lakou; a kapa aku la ia i ka inoa o ia wahi o Horema.
4 Aisraeli anayenda kuchokera ku phiri la Hori kudzera njira ya ku Nyanja Yofiira kuzungulira dziko la Edomu. Koma anthu anataya mtima mʼnjiramo
Hele aku la lakou mai ke kuahiwi o Hora aku, ma ke alanui o ke Kaiula, e puni i ka aina o Edoma: a ua pau ke aho o na kanaka no ke alanui.
5 ndipo anayankhula motsutsana ndi Mulungu ndi Mose, nati, “Chifukwa chiyani munatitulutsa kuchoka mʼdziko la Igupto kuti tidzafere mʼchipululu muno? Kuno kulibe chakudya, kulibe madzi ndipo chakudya cha chabechabechi tatopa nacho.”
Olelo ino aku la na kanaka i ke Akua, a ia Mose, No ke aha la olua i kai mai nei ia makou mailoko mai o Aigupita e make ma ka waonahele? no ka mea, aohe berena, aole hoi ho wai; a ke hoopailua nei ko makou naau i keia ai mama.
6 Choncho Yehova anatumiza njoka zaululu pakati pawo. Zinaluma anthu ndipo Aisraeli ambiri anafa.
Hoouna mai la o Iehova i na nahesa wela iwaena o na kanaka, a nahu mai la lakou i na kanaka; a he nui na kanaka o ka Iseraela i make.
7 Anthuwo anabwera kwa Mose ndi kunena kuti, “Tachimwa chifukwa tayankhula motsutsana ndi Yehova komanso inu. Pempherani kwa Yehova kuti atichotsere njokazi.” Tsono Mose anapempherera anthuwo.
No ia mea, hele mai la na kanaka io Mose la, i mai la, Ua haua hewa makou; no ka mea, ua olelo ino aku makou ia Iehova a ia oe: e pule aku oe ia Iehova, e lawe aku ia i na nahesa mai o makou aku nei. A pule aku la o Mose no na kanaka.
8 Yehova anati kwa Mose, “Upange njoka yaululu ndipo uyipachike pa mtengo. Aliyense amene walumidwa akangoyangʼana njokayo adzakhala ndi moyo.”
Olelo mai la o Iehova ia Mose, E hana oe nau i nahesa wela, a e kau aku ia maluna o ka laau, a o kela mea keia mea i nahuia, i ka wa e nana aku ai oia ia mea, e ola no ia.
9 Pamenepo Mose anapanga njoka yamkuwa ndi kuyipachika pa mtengo. Ndipo aliyense wolumidwa akayangʼana njoka yamkuwayo ankakhala ndi moyo.
A hana iho la o Mose i nahesa keleawe, a kau aku la ia maluna o ka laau; a o ke kanaka i nahuia i ka nahesa wela, i ka wa i nana aku ai oia i ka nahesa keleawe, ua ola ia.
10 Aisraeli anayendabe nakamanga misasa yawo ku Oboti.
A hele aku la na mamo a Iseraela, a hoomoana iho la ma Obota.
11 Kenaka anasamuka ku Oboti nakamanga misasa yawo ku Iye-Abarimu, mʼchipululu chimene chili kummawa kwa Mowabu, kotulukira dzuwa.
A hele lakou mai Obota aku, a hoomoana iho la ma Iieabarima, i ka waonahele ma ke alo o Moaba, ma ka hikina o ka la.
12 Kuchoka kumeneko anayendabe nakamanga misasa yawo mʼchigwa cha Zeredi.
Mailaila aku lakou i hele ai, a hoomoana iho la ma ke kahawai o Zareda.
13 Anasamukanso kumeneko nakamanga moyandikana ndi Arinoni mʼdera limene lili mʼchipululu chimene chimafika mʼdziko la Aamori. Arinoni ndiwo malire a Mowabu ndi Aamori.
Mailaila aku lakou i hele ai, a hoomoana iho la ma hela aoao o Arenona, ma ka waonahele e hele mai ana mailoko mai o na palena o ka Amora; no ka mea, o Arenona oia ka palena o Moaba, mawaena o Moaba a me ka Amora.
14 Nʼchifukwa chake Buku la Nkhondo za Yehova limati, “Mzinda wa Wahebu uli mu Sufa, mu zigwa za Arinoni,
Nolaila, ua olelo ia maloko o ka buke o na kaua a Iehova, ma Vaheba ma Supa, a ma na kahawai o Arenona,
15 ku matsitso a zigwa amene afika mpaka ku Ari nakhudza malire a dziko la Mowabu.”
A ma ke kahe ana o na kahawai, ka mea hele ma ka noho ana o Ara, a moe iho ma ka palena o Moaba.
16 Kuchokera kumeneko anapitirira mpaka ku Beeri, pa chitsime chomwe Yehova anawuza Mose kuti, “Sonkhanitsa anthu pamodzi ndipo ndidzawapatsa madzi.”
Mailaila aku lakou a Beera; oia ka punawai kahi a Iehova i olelo mai ai ia Mose, E hoakoakoa i na kanaka, a e haawi aku no wau i wai no lakou.
17 Pamenepo Aisraeli anayimba nyimbo iyi: “Tulutsa madzi, chitsime iwe! Chiyimbireni nyimbo,
Alaila mele aku la ka Iseraela i keia mele, E huahuai mai, e ka punawai; E mele aku oukou ia ia:
18 chitsime chomwe anakumba mafumu, chomwe anakumba anthu omveka, ndi ndodo zawo zaufumu ndi ndodo zawo zoyendera.” Kenaka anachoka ku chipululu ndi kupita ku Matana.
O na luna ka i kohi iho i ka punawai, O na'lii o na kanaka i eli iho ia, Mamuli o ka Lunakanawai, me na kookoo o lakou. A mai ka waonahele aku lakou a Matana;
19 Kuchoka ku Matana anapita ku Nahalieli, kuchoka ku Nahalieli anapita ku Bamoti,
A mai Matana aku a Nahaliela; a mai Nahaliela aku a Bamota:
20 ndipo atachoka ku Bamoti anapita ku chigwa cha dziko la Mowabu kudzera njira ya pamwamba pa phiri la Pisiga, moyangʼanana ndi Yesimoni.
A mai Bamota aku lakou a i ke awawa ma ke kula o Moaba, malalo o ka puu o Pisega, ma ka aoao e huli ana i ka waonahele.
21 Aisraeli anatumiza amithenga kwa Sihoni mfumu ya Aamori, kuti,
Hoouna aku la ka Iseraela i na elele io Sihona la ke alii o ka Amora, i aku la,
22 “Tiloleni kuti tidutse mʼdziko mwanu. Sitidzapatukira mʼminda mwanu kapena mu mpesa wanu kapena kumwa madzi mʼchitsime chili chonse. Tidzayenda mu msewu waukulu wa mfumu mpaka titadutsa malire a dziko lanu.”
E ae mai oe e hele aku wau mawaena o kou aina: aole makou e kipa ma na mahinaai, aole hoi ma na pawaina: aole makou e inu i ka wai o ka punawai; e hele aku no makou ma ke alanui o ke alii, a hala aku la makou mai kou mau palena aku.
23 Koma Sihoni sanalole kuti Aisraeli adutse mʼdziko mwake. Iye anasonkhanitsa pamodzi ankhondo ake onse kuti akamenyane ndi Aisraeli mʼchipululu. Atafika pa Yahazi anamenyana ndi Aisraeli.
Aole no i ae mai o Sihona e hele aku ka Iseraela mawaena o kona mau palena: aku, hoakoakoa ae la o Sihona i kona poe kanaka a pau, a hele aku la iloko o ka waonahele e ku e i ka Iseraela: a hele mai la ia i Iahaza, a kaua mai la i ka Iseraela.
24 Koma Aisraeli anamupha ndi kulanda dziko lake kuchokera ku Arinoni mpaka ku Yaboki, kulekezera mʼmalire a dziko la Aamoni, chifukwa malire a dziko la Aamoni anali otetezedwa.
Luku aku la ka Iseraela la ia i ka pahikaua, a komo aku la i kona aina mai Arenona a Iaboka, a hiki i na mamo a Amona: no ka mea, ua paa ka palena o na mamo a Amona.
25 Ndipo Aisraeli analanda mizinda yonse ya Aamori, nakhalamo kuphatikizapo Hesiboni ndi midzi yake yozungulira.
Lawe pio ae la ka Iseraela i keia mau kulanakauhale a pau: a noho iho la ka Iseraela ma na kulanakauhale a pau o ka Amora, i Hesebona, a i na kauhale a pau o ia wahi.
26 Hesiboni unali mzinda wa Sihoni mfumu ya Aamori, yemwe anamenyana ndi mfumu yakale ya dziko la Mowabu. Lonselo linakhala dziko lake mpaka ku Arinoni.
No ka mea, o Hesebona ke kulanakauhale o Sihona ke alii o ka Amora, nana i kaua aku mamua i ke alii o Moaba, a lawe ae la i kona aina a pau mai kona lima aku, a hiki i Arenona.
27 Nʼchifukwa chake alakatuli amati: “Bwerani ku Hesiboni, mzindawo umangidwenso; mzinda wa Sihoni ukhazikike.
No ia mea, i mai la na hakumele, E hele oukou iloko o Hesebona, e hana hou ia Ke kulanakauhale o Sihona e hookumuia:
28 “Moto unabuka ku Hesiboni, malawi a moto kuchokera mu mzinda wa Sihoni. Unanyeketsa Ari mzinda wa ku Mowabu, nzika za ku malo okwera a Arinoni.
No ka mea, mai Hesebona i hele aku ai ke ahi, He lapalapa ahi ma ke kulanakauhale o Sihona aku: Ua hoopau oia ia Ara o Moaba, A me na haku o na wahi kiekie o Arenona.
29 Tsoka kwa iwe Mowabu! Mwawonongedwa inu anthu a ku Kemosi! Ana ake aamuna wawasandutsa ngati anthu othawathawa ndipo ana ake aakazi ngati akapolo, akapolo a Sihoni, mfumu ya Aamori.
Auwe oe, e Moaba! ua make no oe! E na kanaka o Kemosa! Ua haawi aku ia i kana mau keikikane i pakele, A me kana mau kaikamahine, i poe pio No ke alii o ka Amora, no Sihona.
30 “Koma ife tawagonjetsa; Hesiboni wawonongedwa mʼnjira monse mpaka kufika ku Diboni. Tawaphwasula mpaka ku mzinda wa Nofa, mzinda womwe umafika ku Medeba.
Ua pana pua aku makou ia lakou; Ua lukuia o Hesebona a hiki i Dibona, Ua hooneoneo makou a hiki aku i Nopa, A hiki hoi i Medeba.
31 “Choncho Aisraeli anakhala mʼdziko la Aamori.”
A noho iho la ka Iseraela ma ka aina o ka Amora.
32 Mose atatumiza azondi ku Yazeri, Aisraeliwo analanda midzi yozungulira ndi kuthamangitsa Aamori omwe ankakhala kumeneko.
A hoouna aku la o Mose e makaikai ia Iaazera, a komo lakou i na kulanakauhale o ia wahi, a hookuke aku la i ka Amora malaila.
33 Kenaka anabwerera, nadzera njira ya ku Basani. Choncho Ogi mfumu ya ku Basani ndi gulu lake lonse lankhondo anatuluka kukakumana nawo ndipo anamenyana nawo ku Ederi.
Haliu ae la lakou, a pii aku la ma ke alanui o Basana: a hele mai la o Oga ke alii o Basana e ku e mai ia lakou, oia a me kona poe kanaka a pau, i ke kaua ma Ederei.
34 Yehova anati kwa Mose, “Usachite naye mantha pakuti ndamupereka mʼmanja mwako pamodzi ndi gulu lake lonse lankhondo ndi dziko lake lomwe. Ndipo uchite kwa iye zimene unachita Sihoni mfumu ya Aamori, amene ankalamulira ku Hesiboni.”
Olelo mai la o Iehova ia Mose, Mai makau oe ia ia; no ka mea, ua haawi aku no wau ia ia iloko o kou lima, me kona kanaka a pau, a me kona aina: a e hana aku oe ia ia me kau i hana aku ai ia Sihona ke alii o ka Amora i noho ma Hesebona.
35 Choncho Aisraeli anapha Ogi pamodzi ndi ana ake aamuna ndi gulu lake lonse la nkhondo. Palibe ndi mmodzi yemwe amene anatsala wamoyo, ndipo analanda dziko lakelo.
A luku aku la lakou ia ia, me kana mau keikikane, a me kona poe kanaka a pau, aole i koe kekahi e ola ana nona: a komo aku la lakou i kona aina.

< Numeri 21 >