< Numeri 21 >

1 Mfumu ya Akanaani ya ku Aradi, imene inkakhala ku Negevi, itamva kuti Aisraeli akubwera kudzera msewu wopita ku Atarimu, inachita nkhondo ndi Aisraeli nigwira ena mwa iwo.
And he heard the Canaanite [the] king of Arad [who] dwelt the Negev that it had come Israel [the] way of the Atharim and he engaged in battle against Israel and he took captive - some of it captive[s].
2 Ndipo Israeli anachita lonjezo ili kwa Yehova: “Mukapereka anthu awa mʼdzanja lathu ife tidzawonongeratu mizinda yawo.”
And it vowed Israel a vow to Yahweh and it said certainly [if] you will give the people this in hand my and I will totally destroy cities their.
3 Yehova anamva pempho la Aisraeli ndipo anapereka Akanaaniwo kwa iwo. Anawawononga pamodzi ndi mizinda yawo. Kotero malowo anatchedwa Horima.
And he listened Yahweh to [the] voice of Israel and he delivered up the Canaanite[s] and it totally destroyed them and cities their and someone called [the] name of the place Hormah.
4 Aisraeli anayenda kuchokera ku phiri la Hori kudzera njira ya ku Nyanja Yofiira kuzungulira dziko la Edomu. Koma anthu anataya mtima mʼnjiramo
And they set out from Hor the mountain [the] direction of [the] sea of reed[s] to go around [the] land of Edom and it became short [the] self of the people on the way.
5 ndipo anayankhula motsutsana ndi Mulungu ndi Mose, nati, “Chifukwa chiyani munatitulutsa kuchoka mʼdziko la Igupto kuti tidzafere mʼchipululu muno? Kuno kulibe chakudya, kulibe madzi ndipo chakudya cha chabechabechi tatopa nacho.”
And it spoke the people against God and against Moses why? have you brought up us from Egypt to die in the wilderness for there not [is] food and there not [is] water and self our it loathes the food worthless.
6 Choncho Yehova anatumiza njoka zaululu pakati pawo. Zinaluma anthu ndipo Aisraeli ambiri anafa.
And he sent Yahweh among the people the snakes the saraphs and they bit the people and it died a people numerous from Israel.
7 Anthuwo anabwera kwa Mose ndi kunena kuti, “Tachimwa chifukwa tayankhula motsutsana ndi Yehova komanso inu. Pempherani kwa Yehova kuti atichotsere njokazi.” Tsono Mose anapempherera anthuwo.
And it came the people to Moses and they said we have sinned for we have spoken against Yahweh and against you pray to Yahweh so may he remove from on us the snake[s] and he prayed Moses for the people.
8 Yehova anati kwa Mose, “Upange njoka yaululu ndipo uyipachike pa mtengo. Aliyense amene walumidwa akangoyangʼana njokayo adzakhala ndi moyo.”
And he said Yahweh to Moses make for yourself a saraph and put it on a standard and it will be every [one who] is bitten and he will see it and he will live.
9 Pamenepo Mose anapanga njoka yamkuwa ndi kuyipachika pa mtengo. Ndipo aliyense wolumidwa akayangʼana njoka yamkuwayo ankakhala ndi moyo.
And he made Moses a snake of bronze and he put it on the standard and it was if it had bitten the snake anyone and he looked to [the] snake of bronze and he lived.
10 Aisraeli anayendabe nakamanga misasa yawo ku Oboti.
And they set out [the] people of Israel and they encamped in Oboth.
11 Kenaka anasamuka ku Oboti nakamanga misasa yawo ku Iye-Abarimu, mʼchipululu chimene chili kummawa kwa Mowabu, kotulukira dzuwa.
And they set out from Oboth and they encamped at Iye Abarim in the wilderness which [is] on [the] face of Moab from [the] rising of the sun.
12 Kuchoka kumeneko anayendabe nakamanga misasa yawo mʼchigwa cha Zeredi.
From there they set out and they encamped in [the] wadi of Zered.
13 Anasamukanso kumeneko nakamanga moyandikana ndi Arinoni mʼdera limene lili mʼchipululu chimene chimafika mʼdziko la Aamori. Arinoni ndiwo malire a Mowabu ndi Aamori.
From there they set out and they encamped from [the] other side of Arnon which [is] in the wilderness which goes out from [the] border of the Amorite[s] that Arnon [is] [the] border of Moab between Moab and between the Amorite[s].
14 Nʼchifukwa chake Buku la Nkhondo za Yehova limati, “Mzinda wa Wahebu uli mu Sufa, mu zigwa za Arinoni,
There-fore it is said in [the] book of [the] wars of Yahweh Waheb in Suphah and the wadis Arnon.
15 ku matsitso a zigwa amene afika mpaka ku Ari nakhudza malire a dziko la Mowabu.”
And [the] slope of the wadis which it extends to [the] dwelling of Ar and it leans to [the] border of Moab.
16 Kuchokera kumeneko anapitirira mpaka ku Beeri, pa chitsime chomwe Yehova anawuza Mose kuti, “Sonkhanitsa anthu pamodzi ndipo ndidzawapatsa madzi.”
And from there Beer towards that [is] the well which he said Yahweh to Moses gather the people so let me give to them water.
17 Pamenepo Aisraeli anayimba nyimbo iyi: “Tulutsa madzi, chitsime iwe! Chiyimbireni nyimbo,
Then it sang Israel the song this spring up O well sing of it.
18 chitsime chomwe anakumba mafumu, chomwe anakumba anthu omveka, ndi ndodo zawo zaufumu ndi ndodo zawo zoyendera.” Kenaka anachoka ku chipululu ndi kupita ku Matana.
A well [which] they dug it [the] leaders [which] they dug it [the] noble [people] of the people with a ruler's staff with staffs their and from [the] wilderness Mattanah.
19 Kuchoka ku Matana anapita ku Nahalieli, kuchoka ku Nahalieli anapita ku Bamoti,
And from Mattanah Nahaliel and from Nahaliel Bamoth.
20 ndipo atachoka ku Bamoti anapita ku chigwa cha dziko la Mowabu kudzera njira ya pamwamba pa phiri la Pisiga, moyangʼanana ndi Yesimoni.
And from Bamoth the valley which [is] in [the] region of Moab [the] top of Pisgah and it looked down over [the] face of the desolate place.
21 Aisraeli anatumiza amithenga kwa Sihoni mfumu ya Aamori, kuti,
And it sent Israel messengers to Sihon [the] king of the Amorite[s] saying.
22 “Tiloleni kuti tidutse mʼdziko mwanu. Sitidzapatukira mʼminda mwanu kapena mu mpesa wanu kapena kumwa madzi mʼchitsime chili chonse. Tidzayenda mu msewu waukulu wa mfumu mpaka titadutsa malire a dziko lanu.”
Let me pass in land your not we will turn aside in a field and in a vineyard not we will drink water of a well on [the] way of the king we will go until that we will pass through territory your.
23 Koma Sihoni sanalole kuti Aisraeli adutse mʼdziko mwake. Iye anasonkhanitsa pamodzi ankhondo ake onse kuti akamenyane ndi Aisraeli mʼchipululu. Atafika pa Yahazi anamenyana ndi Aisraeli.
And not he permitted Sihon Israel to pass in territory his and he gathered Sihon all people his and he went out to meet Israel the wilderness towards and he came Jahaz towards and he engaged in battle against Israel.
24 Koma Aisraeli anamupha ndi kulanda dziko lake kuchokera ku Arinoni mpaka ku Yaboki, kulekezera mʼmalire a dziko la Aamoni, chifukwa malire a dziko la Aamoni anali otetezedwa.
And it struck him Israel to [the] mouth of [the] sword and it took possession of land his from Arnon to Jabbok to [the] descendants of Ammon for [was] strong [the] border of [the] descendants of Ammon.
25 Ndipo Aisraeli analanda mizinda yonse ya Aamori, nakhalamo kuphatikizapo Hesiboni ndi midzi yake yozungulira.
And it took Israel all the cities these and it dwelt Israel in all [the] cities of the Amorite[s] in Heshbon and in all daughters its.
26 Hesiboni unali mzinda wa Sihoni mfumu ya Aamori, yemwe anamenyana ndi mfumu yakale ya dziko la Mowabu. Lonselo linakhala dziko lake mpaka ku Arinoni.
For Heshbon [was] [the] city of Sihon [the] king of the Amorite[s] it and he he had waged war against [the] king of Moab former and he had taken all land his from hand his to Arnon.
27 Nʼchifukwa chake alakatuli amati: “Bwerani ku Hesiboni, mzindawo umangidwenso; mzinda wa Sihoni ukhazikike.
There-fore they say those [who] speak proverbs come Heshbon let it be rebuilt and it may be established [the] city of Sihon.
28 “Moto unabuka ku Hesiboni, malawi a moto kuchokera mu mzinda wa Sihoni. Unanyeketsa Ari mzinda wa ku Mowabu, nzika za ku malo okwera a Arinoni.
For fire it went out from Heshbon flame from [the] town of Sihon it consumed Ar of Moab [the] citizens of [the] high places of Arnon.
29 Tsoka kwa iwe Mowabu! Mwawonongedwa inu anthu a ku Kemosi! Ana ake aamuna wawasandutsa ngati anthu othawathawa ndipo ana ake aakazi ngati akapolo, akapolo a Sihoni, mfumu ya Aamori.
Woe! to you O Moab you have perished O people of Chemosh he has made sons his fugitives and daughters his in captivity of [the] king of [the] Amorite[s] Sihon.
30 “Koma ife tawagonjetsa; Hesiboni wawonongedwa mʼnjira monse mpaka kufika ku Diboni. Tawaphwasula mpaka ku mzinda wa Nofa, mzinda womwe umafika ku Medeba.
And we shot at them it has perished Heshbon to Dibon and we have devastated to Nophah which [is] to Medeba.
31 “Choncho Aisraeli anakhala mʼdziko la Aamori.”
And it dwelt Israel in [the] land of the Amorite[s].
32 Mose atatumiza azondi ku Yazeri, Aisraeliwo analanda midzi yozungulira ndi kuthamangitsa Aamori omwe ankakhala kumeneko.
And he sent Moses to spy out Jazer and they captured daughters its (and it dispossessed *Q(K)*) the Amorite[s] who [was] there.
33 Kenaka anabwerera, nadzera njira ya ku Basani. Choncho Ogi mfumu ya ku Basani ndi gulu lake lonse lankhondo anatuluka kukakumana nawo ndipo anamenyana nawo ku Ederi.
And they turned and they went up [the] direction of Bashan and he went out Og [the] king of Bashan to meet them he and all people his for battle Edrei.
34 Yehova anati kwa Mose, “Usachite naye mantha pakuti ndamupereka mʼmanja mwako pamodzi ndi gulu lake lonse lankhondo ndi dziko lake lomwe. Ndipo uchite kwa iye zimene unachita Sihoni mfumu ya Aamori, amene ankalamulira ku Hesiboni.”
And he said Yahweh to Moses may not you fear him for in hand your I have given him and all people his and land his and you will do to him just as you did to Sihon [the] king of the Amorite[s] who [was] dwelling in Heshbon.
35 Choncho Aisraeli anapha Ogi pamodzi ndi ana ake aamuna ndi gulu lake lonse la nkhondo. Palibe ndi mmodzi yemwe amene anatsala wamoyo, ndipo analanda dziko lakelo.
And they struck down him and sons his and all people his until not he had left to him a survivor and they took possession of land his.

< Numeri 21 >