< Numeri 20 >

1 Pa mwezi woyamba gulu lonse la Aisraeli linafika ku chipululu cha Zini, ndipo anakhala ku Kadesi. Miriamu anafera kumeneko ndipo anayikidwa mʼmanda.
И приидоша сынове Израилтестии, весь сонм, в пустыню Син, в месяц первый, и пребываху людие в Кадисе: и скончася ту Мариам, и погребеся тамо.
2 Kunalibe madzi woti anthu onse ndi kumwa, choncho anthuwo anasonkhana motsutsana ndi Mose ndi Aaroni.
И не бяше воды сонму: и собрашася на Моисеа и Аарона,
3 Anakangana ndi Mose kuti, “Kunali bwino ifenso tikanangofa pamene abale athu anafa pamaso pa Yehova!
и ропташа людие на Моисеа, глаголюще: о, дабы умерли быхом в погибели братии нашея пред Господем:
4 Chifukwa chiyani unabweretsa gulu la Yehova mʼchipululu muno, kuti ife ndi ziweto zathu tife kuno?
и вскую введосте сонм Господнь в пустыню сию, погубити ны и скоты нашы?
5 Nʼchifukwa chiyani unatitulutsa mʼdziko la Igupto ndi kutibweretsa kumalo woyipa ano? Kuno kulibe tirigu kapena nkhuyu, mphesa kapena makangadza. Ndipo kuno kulibenso madzi akumwa!”
И вскую сие? Изведосте ны из Египта, еже приити (нам) на место злое сие, место, в немже не сеется, ни смокви, ни винограды, ниже яблоки, ниже вода есть пити.
6 Mose ndi Aaroni anachoka mu msonkhano ndi kupita pa khomo la tenti ya msonkhano, nagwa pansi chafufumimba ndipo ulemerero wa Yehova unaonekera.
И прииде Моисей и Аарон от лица сонма пред двери скинии свидения, и падоста ниц: и явися слава Господня над ними.
7 Yehova anati kwa Mose,
И рече Господь к Моисею, глаголя:
8 “Tenga ndodo, ndipo iwe ndi mʼbale wako Aaroni musonkhanitse anthu onse pamodzi. Uyankhule ndi thanthwe ilo iwo akuona ndipo lidzatulutsa madzi ake. Udzatulutsa madzi mʼthanthwe limeneli kuti anthu onse ndi ziweto zawo amwe.”
возми жезл твой и созови сонм ты и Аарон, брат твой, и рцыте ко каменю пред ними, и даст воды своя: и изведете им воды из камене, и напойте сонм и скоты их.
9 Choncho Mose anatenga ndodo pamaso pa Yehova monga momwe anamulamulira.
И взя Моисей жезл иже пред Господем, якоже повеле Господь.
10 Mose ndi Aaroni anasonkhanitsa anthuwo pamodzi ku thanthwelo ndipo Mose anawawuza kuti, “Tamverani osamvera inu, kodi tikupatseni madzi kuchokera ku thanthwe ili?”
И созва Моисей и Аарон сонм пред камень, и рече к ним: послушайте мене, непокоривии: еда из камене сего изведем вам воду?
11 Choncho Mose anatukula dzanja lake ndi kumenya thanthwelo kawiri ndi ndodo yake ndipo madzi ambiri anatuluka mwamphamvu, ndipo anthu ndi ziweto zawo anamwa.
И воздвиг Моисей руку свою, удари в камень жезлом дважды: и изыде вода многа, и напися сонм (весь) и скоты их.
12 Koma Yehova anati kwa Mose ndi Aaroni, “Chifukwa chakuti simunandikhulupirire ndiponso simunandilemekeze monga Woyera pamaso pa Aisraeli, simudzalowetsa anthuwa mʼdziko limene ndikupereka kwa iwo.”
И рече Господь к Моисею и Аарону: понеже не веровасте освятити Мя пред сынми Израилтескими, сего ради не введете вы сонма сего в землю, юже дах им:
13 Awa anali madzi a ku Meriba, kumene Aisraeli anakangana ndi Yehova ndiponso kumene Yehovayo anadzionetsa yekha kuti ndi Woyera pakati pawo.
сия вода Пререкания, яко возропташа сынове Израилтестии пред Господем, и освятися в них.
14 Mose anatumiza amithenga kuchokera ku Kadesi kupita kwa mfumu ya ku Edomu, kukanena kuti, “Mʼbale wako Israeli akunena izi: Inuyo mukudziwa za mavuto onse amene anatigwera.
И посла Моисей послы от Кадиса к Царю Едомскому, глаголя: тако глаголет брат твой Израиль: ты веси весь труд обретший нас:
15 Makolo athu anapita ku Igupto ndipo tinakhala kumeneko zaka zambiri. Aigupto anatizunza pamodzi ndi makolo athuwo,
и снидоша отцы наши в Египет, и жихом во Египте дни многи, и озлобиша нас Египтяне и отцев наших:
16 koma titalirira Yehova, Iyeyo anamva kulira kwathuko ndipo anatitumizira mngelo amene anatitulutsa ku Igupto.” “Taonani, tsopano tili pano pa Kadesi, mzinda wa mʼmalire a dziko lanu.
и возопихом ко Господу, и услыша Господь глас наш, и послав Ангела, изведе ны из Египта: и ныне есмы в Кадисе граде, на конце предел твоих:
17 Chonde mutilole tidutse mʼdziko lanu. Sitidzera mʼminda yanu kapena mu mpesa wanu, kapenanso kumwa madzi mʼchitsime chilichonse. Tidzayenda kutsata msewu waukulu wa mfumu ndipo sitidzapatukira ku dzanja lamanja kapena lamanzere mpaka titadutsa malire a dziko lanu.”
да прейдем сквозе землю твою: не пройдем сквозе села, ни сквозе винограды, ни пием воды в потоцех твоих: путем царским пойдем, не совратимся ни на десно, ни на лево, дондеже прейдем пределы твоя.
18 Koma Edomu anayankha kuti, “Musadutse kuno: Mukangoyesera tidzabwera ndi kumenyana nanu ndi lupanga.”
И рече к ним Едом: не пройдеши сквозе мене: аще же ни, ратию изыду противу тебе.
19 Aisraeli anayankha kuti, “Tidzayenda motsata msewu waukulu. Ndipo ngati ife kapena ziweto zathu tidzamwa madzi anu tidzalipira. Tikungofuna tidutse nawo, palibenso china.”
И рекоша к нему сынове Израилевы: под горою пройдем: аще же от воды твоея испием аз и скоты моя, дам цену тебе: но вещь сия ничтоже есть, под горою да пройдем.
20 Koma Edomu anayankhanso kuti, “Musadutse.” Kenaka Edomu anatuluka ndi gulu lankhondo lalikulu komanso lamphamvu.
Он же рече: не пройдеши сквозе мене. И изыде противу им Едом с народом тяжким и рукою крепкою.
21 Edomu anakaniza Israeli kuti adutse mʼdziko lake, choncho Israeli anabwerera.
И не восхоте Едом дати Израилю проити сквозе пределы своя, и уклонися Израиль от него.
22 Gulu lonse la Aisraeli linachoka ku Kadesi ndipo linafika ku phiri la Hori.
И воздвигошася от Кадиса, и приидоша сынове Израилтестии, весь сонм, в гору Ор.
23 Ali pa phiri la Hori, pafupi ndi malire a Edomu, Yehova anati kwa Mose ndi Aaroni,
И рече Господь к Моисею и Аарону в горе Ор у предел земли Едомли, глаголя:
24 “Aaroni adzakakhala ndi anthu a mtundu wake, sadzalowa mʼdziko limene ndapereka kwa Aisraeli, chifukwa nonse munandiwukira motsutsana ndi malamulo anga ku madzi a ku Meriba.
да приложится Аарон к людем своим, яко не внидете в землю, юже дах сыном Израилевым в наследие, понеже преогорчисте Мя у воды Пререкания:
25 Tenga Aaroni ndi mwana wake wamwamuna Eliezara ndipo ukwere nawo ku phiri la Hori.
возми Аарона брата твоего и Елеазара сына его, и возведи я на Ор гору пред всем сонмом:
26 Uvule Aaroni zovala zake ndipo umuveke mwana wake Eliezara, pakuti Aaroni adzafera komweko, ndipo adzakakhala ndi anthu a mtundu wake.”
и совлецы Аарону ризы его и облецы Елеазара сына его, и Аарон приложився да умрет тамо.
27 Mose anachita monga Yehova anamulamulira: Anapita ku phiri la Hori gulu lonse likuona.
И сотвори Моисей, якоже повеле ему Господь: и возведе я на Ор гору пред всем сонмом,
28 Pamenepo Mose anavula Aaroni zovala zake ndi kuveka mwana wake Eliezara. Aaroni anafa kumeneko pamwamba pa phirilo. Koma Mose ndi Eliezara anatsika ku phiriko,
и совлече Аарона с риз его, и облече в ня Елеазара сына его:
29 ndipo pamene anthu onse anamva kuti Aaroni wafa, nyumba yonse ya Israeli inamulira Aaroniyo masiku makumi atatu.
и умре Аарон тамо на версе горы: и сниде Моисей и Елеазар с горы. И виде весь сонм, яко умре Аарон: и плакашася по Аароне тридесять дний весь дом Израилев.

< Numeri 20 >